< Amosi 2 >
1 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Mowabu akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anatentha mafupa a mfumu ya ku Edomu, mpaka kuwasandutsa phulusa,
Nanku okutshiwo nguThixo: “Ngenxa yezono ezintathu zaseMowabi loba ngenxa yezine, kangiyikulunqanda ulaka lwami, ngoba utshise amathambo enkosi yase-Edomi aze afana lekalaga,
2 Ine ndidzatumiza moto pa Mowabu, umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Keriyoti. Mowabu adzafera pakati pa nkhondo yoopsa, mʼkati mwa mfuwu wa nkhondo ndi kuliza malipenga.
ngizathumela umlilo kuMowabi ozalobisa izinqaba zaseKheriyothi. UMowabi uzachitheka kulokuxokozela okukhulu lokumenyezelwa kwezitsho zempi lokukhala kwecilongo.
3 Ndidzawononga wolamulira wake ndi kupha akuluakulu onse amene ali pamodzi ndi iye,” akutero Yehova.
Ngizaqothula ababusi bakhe ngibulale zonke izikhulu zakhe kanye laye,” kutsho uThixo.
4 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Yuda akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza iwo akana lamulo la Yehova ndipo sanasunge malangizo ake, popeza asocheretsedwa ndi milungu yabodza, milungu imene makolo awo ankayitsatira,
Nanku okutshiwo nguThixo: “Ngenxa yezono ezintathu zikaJuda loba ngenxa yezine, kangiyikulunqanda ulaka lwami, ngoba bawalile umthetho kaThixo kabaze bagcina lezimiso zakhe, ngoba badukiswe ngonkulunkulu bamanga, onkulunkulu abalandelwa ngokhokho babo.
5 Ine ndidzatumiza moto pa Yuda, umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Yerusalemu.”
Ngizathumela umlilo koJuda ozalobisa izinqaba zaseJerusalema.”
6 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Israeli akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Iwo amagulitsa anthu olungama ndi siliva, ndi osauka ndi nsapato.
Nanku okutshiwo nguThixo: “Ngenxa yezono ezintathu zika-Israyeli loba ngenxa yezine, kangiyikulunqanda ulaka lwami ngoba bathengisa abalungileyo ngesiliva, labaswelayo ngamanyathelo.
7 Amapondereza anthu osauka ngati akuponda fumbi, ndipo sawaweruza mwachilungamo anthu oponderezedwa. Abambo ndi mwana wawo amagonana ndi mtsikana mmodzi yemweyo, ndipo potero amanyozetsa dzina langa loyera.
Banyathela phezu kwamakhanda abayanga njengaphezu kothuli lomhlabathi banqabele imfanelo yabancindezelweyo. Uyise lendodana bembatha lentombi yinye kanjalo bangcolise ibizo lami elingcwele.
8 Anthuwo amakagonana mʼmbali mwa guwa lililonse la nsembe pa zovala zimene anatenga ngati chikole. Mʼnyumba ya mulungu wawo amamweramo vinyo amene analipiritsa anthu pa milandu.
Bacambalala phansi emaceleni ama-alithare wonke, phezu kwezembatho ezithethwe ziyizibambiso. Endlini kankulunkulu wabo banatha iwayini elithethwe njengenhlawulo.
9 “Ine ndinawononga Aamori pamaso pawo, ngakhale iwo anali anthu ataliatali ngati mikungudza ndiponso amphamvu ngati mitengo ya thundu. Ndinawononga zipatso zawo ndiponso mizu yawo.
Ngachitha umʼAmori phambi kwabo, lanxa wayemude njengemisedari njalo eqine njengomʼokhi. Ngachitha izithelo zakhe phezulu kanye lempande zakhe ngaphansi.
10 “Ine ndinakutulutsani ku Igupto, ndipo ndinakutsogolerani mʼchipululu kwa zaka makumi anayi, kudzakupatsani dziko la Aamori.
Ngalikhupha eGibhithe ngalikhokhela iminyaka engamatshumi amane enkangala ukuba ngilinike ilizwe lama-Amori.
11 Ine ndinawutsanso ena mwa ana ako kuti akhale aneneri, ndi ena mwa anyamata ako kuti akhale anaziri. Kodi si choncho, inu Aisraeli?” akutero Yehova.
Ngakhupha labaphrofethi bephuma phakathi kwamadodana enu, kanye lamaNaziri ephuma phakathi kwezinsizwa zenu. Lokhu akuqotho na, bantu bako-Israyeli?” kutsho uThixo.
12 “Koma inu munawamwetsa vinyo anaziri aja, ndipo munalamula aneneri kuti asanenere.
“Kodwa lanathisa amaNaziri iwayini, lalaya abaphrofethi ukuba bangaphrofethi.
13 “Tsono Ine ndidzakupsinjani monga imapsinjikira ngolo imene yadzaza ndi tirigu.
Khathesi-ke mina ngizalichoboza njengokuchoboza kwenqola ithwele amabele.
14 Munthu waliwiro sadzatha kuthawa, munthu wamphamvu sadzakhalanso ndi nyonga, wankhondo sadzapulumutsa moyo wake.
Olejubane kayikubaleka, oqinileyo uzawaswela amandla akhe, lebutho kaliyikusindisa impilo yalo.
15 Munthu wa uta sadzalimbika, msilikali wothamanga kwambiri sadzapulumuka, ndipo wokwera pa akavalo sadzapulumutsa moyo wake.
Umtshoki akayikugxila, ibutho elilejubane kaliyikuphunyuka lomgadi webhiza kayikusindisa impilo yakhe.
16 Ngakhale asilikali olimba mtima kwambiri adzathawa ali maliseche pa tsikulo,” akutero Yehova.
Lebutho elilesibindi kakhulu, ngalolosuku lizabaleka linqunu,” kutsho uThixo.