< Amosi 2 >

1 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Mowabu akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anatentha mafupa a mfumu ya ku Edomu, mpaka kuwasandutsa phulusa,
Yahweh [also] said this: “[I will punish the people of] Moab because of the many sins [that they have committed]; I will not change my mind about punishing them, because they [dug up] the bones of the king of Edom and burned them completely, with the result that [the ashes became as white] as lime.
2 Ine ndidzatumiza moto pa Mowabu, umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Keriyoti. Mowabu adzafera pakati pa nkhondo yoopsa, mʼkati mwa mfuwu wa nkhondo ndi kuliza malipenga.
So I will cause a fire to completely burn the fortresses of Kerioth [city in Moab]. [People will hear soldiers] shouting and blowing trumpets [loudly] while I am causing Moab to be destroyed
3 Ndidzawononga wolamulira wake ndi kupha akuluakulu onse amene ali pamodzi ndi iye,” akutero Yehova.
[and while] I am getting rid of its king and all its leaders. [That will surely happen because I], Yahweh, have said it!”
4 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Yuda akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza iwo akana lamulo la Yehova ndipo sanasunge malangizo ake, popeza asocheretsedwa ndi milungu yabodza, milungu imene makolo awo ankayitsatira,
Yahweh [also] said this: “[I will also punish the people of] Judah because of the many sins [that they have committed]; I will not change my mind about punishing them, because they have rejected what I taught them and they have not obeyed my commands. They have been deceived [and persuaded to worship false gods], the same [gods] that their ancestors [worshiped].
5 Ine ndidzatumiza moto pa Yuda, umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Yerusalemu.”
So I will cause a fire to completely burn [everything in] Judah, including the fortresses in Jerusalem.”
6 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Israeli akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Iwo amagulitsa anthu olungama ndi siliva, ndi osauka ndi nsapato.
Yahweh [also] said this: “[I will punish the people of] Israel because of the many sins [that they have committed]; I will not change my mind about punishing them, because they sell righteous [people] to get [a small amount of] silver; they sell poor [people, causing them to become slaves], getting for [each of] them [only the amount of money with which they could buy] a pair of sandals.
7 Amapondereza anthu osauka ngati akuponda fumbi, ndipo sawaweruza mwachilungamo anthu oponderezedwa. Abambo ndi mwana wawo amagonana ndi mtsikana mmodzi yemweyo, ndipo potero amanyozetsa dzina langa loyera.
[It is as though] they trample the poor people into the dirt and do not allow those who are helpless to be treated fairly. Men and their fathers dishonor me [MTY] by both having sex [EUP] with the same [slave] girl.
8 Anthuwo amakagonana mʼmbali mwa guwa lililonse la nsembe pa zovala zimene anatenga ngati chikole. Mʼnyumba ya mulungu wawo amamweramo vinyo amene analipiritsa anthu pa milandu.
[When poor people borrow money], [the lenders force those people to give to them a piece of clothing] for them to keep until he can pay back the money. [But at the end of each day, instead of returning that garment as Yahweh had commanded them to], they lie down on that garment at the places where they worship [their gods]! They fine people, and with that money [they buy] wine and drink it in the temples of their gods!
9 “Ine ndinawononga Aamori pamaso pawo, ngakhale iwo anali anthu ataliatali ngati mikungudza ndiponso amphamvu ngati mitengo ya thundu. Ndinawononga zipatso zawo ndiponso mizu yawo.
[Long ago, ] to assist your ancestors, I got rid of the Amor people-group. They [seemed to be] as tall as cedar [trees] and as strong as oak [trees], but I got rid of them completely, [as easily as someone cuts off] [MET] the branches of a tree and then digs out all its roots.
10 “Ine ndinakutulutsani ku Igupto, ndipo ndinakutsogolerani mʼchipululu kwa zaka makumi anayi, kudzakupatsani dziko la Aamori.
I brought your [ancestors] out of Egypt, and [then] I led them through the desert for 40 years. And then I enabled them to conquer/possess the Amor area.
11 Ine ndinawutsanso ena mwa ana ako kuti akhale aneneri, ndi ena mwa anyamata ako kuti akhale anaziri. Kodi si choncho, inu Aisraeli?” akutero Yehova.
I chose some of you Israelis to be prophets, and I chose others to be Nazir-men [who were completely dedicated to me]. You people of Israel certainly [RHQ] know that what I have said is true!
12 “Koma inu munawamwetsa vinyo anaziri aja, ndipo munalamula aneneri kuti asanenere.
But you commanded the prophets to not speak the messages that [I gave to] them, and you persuaded the Nazir-men to drink wine, [which I told them never to do].
13 “Tsono Ine ndidzakupsinjani monga imapsinjikira ngolo imene yadzaza ndi tirigu.
So I will crush you like [SIM] [the wheels of] a wagon that is loaded with grain crushes [whatever it rolls over].
14 Munthu waliwiro sadzatha kuthawa, munthu wamphamvu sadzakhalanso ndi nyonga, wankhondo sadzapulumutsa moyo wake.
[Even] if you run fast, you will not escape; [even] if you are strong, [it will be as though] you are weak, and warriors will be unable to save themselves.
15 Munthu wa uta sadzalimbika, msilikali wothamanga kwambiri sadzapulumuka, ndipo wokwera pa akavalo sadzapulumutsa moyo wake.
[Even] if you are able to shoot arrows [well], you will be forced to retreat [LIT]; [even] if you run fast or if you ride [away] on a horse, you will not [be able to] save yourself.
16 Ngakhale asilikali olimba mtima kwambiri adzathawa ali maliseche pa tsikulo,” akutero Yehova.
[Even] warriors who are very brave will drop their weapons when they try to flee on the day [that I get rid of them]. [That will surely happen because I], Yahweh, have said it.”

< Amosi 2 >