< Amosi 2 >

1 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Mowabu akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anatentha mafupa a mfumu ya ku Edomu, mpaka kuwasandutsa phulusa,
Saa siger Herren: For tre Overtrædelser af Moab og for fire — jeg tager det ikke tilbage — fordi han brændte Edoms Konges Ben til Kalk,
2 Ine ndidzatumiza moto pa Mowabu, umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Keriyoti. Mowabu adzafera pakati pa nkhondo yoopsa, mʼkati mwa mfuwu wa nkhondo ndi kuliza malipenga.
derfor vil jeg sende en Ild i Moab, den skal fortære Kirjoths Paladser; og Moab skal dø under Bulder, under Stormraab, under Trompetens Lyd.
3 Ndidzawononga wolamulira wake ndi kupha akuluakulu onse amene ali pamodzi ndi iye,” akutero Yehova.
Og jeg vil udrydde Dommeren af hans Midte og ihjelslaa alle hans Fyrster med ham, siger Herren.
4 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Yuda akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza iwo akana lamulo la Yehova ndipo sanasunge malangizo ake, popeza asocheretsedwa ndi milungu yabodza, milungu imene makolo awo ankayitsatira,
Saa siger Herren: For tre Overtrædelser af Juda og for fire — jeg tager det ikke tilbage — fordi de foragtede Herrens Lov og ikke holdt hans Skikke, saa at deres Løgne, efter hvilke deres Fædre havde vandret, førte dem vild,
5 Ine ndidzatumiza moto pa Yuda, umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Yerusalemu.”
derfor vil jeg sende en Ild i Juda, og den skal fortære Paladserne i Jerusalem.
6 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Israeli akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Iwo amagulitsa anthu olungama ndi siliva, ndi osauka ndi nsapato.
Saa siger Herren: For tre Overtrædelser af Israel og for fire — jeg tager det ikke tilbage — fordi de sælge den retfærdige for Penge og den fattige formedelst et Par Sko;
7 Amapondereza anthu osauka ngati akuponda fumbi, ndipo sawaweruza mwachilungamo anthu oponderezedwa. Abambo ndi mwana wawo amagonana ndi mtsikana mmodzi yemweyo, ndipo potero amanyozetsa dzina langa loyera.
fordi de hige efter at bringe Jordens Støv paa de ringes Hoved og forvende de sagtmodiges Vej, og en Mand og hans Fader gaa til samme Pige, for at vanhellige mit hellige Navn;
8 Anthuwo amakagonana mʼmbali mwa guwa lililonse la nsembe pa zovala zimene anatenga ngati chikole. Mʼnyumba ya mulungu wawo amamweramo vinyo amene analipiritsa anthu pa milandu.
og de strække sig paa Klæder, som de have faaet i Pant, ved hvert et Alter, og drikke Vin, som de have faaet i Bøder, i deres Guds Hus;
9 “Ine ndinawononga Aamori pamaso pawo, ngakhale iwo anali anthu ataliatali ngati mikungudza ndiponso amphamvu ngati mitengo ya thundu. Ndinawononga zipatso zawo ndiponso mizu yawo.
skønt jeg havde ødelagt Amoriten for deres Ansigt, ham, hvis Højde var som Cedres Højde, og som var stærk som Egene; og jeg ødelagde hans Frugt fra oven af og hans Rødder fra neden af;
10 “Ine ndinakutulutsani ku Igupto, ndipo ndinakutsogolerani mʼchipululu kwa zaka makumi anayi, kudzakupatsani dziko la Aamori.
og jeg havde ført eder op af Ægyptens Land og førte eder i Ørken fyrretyve Aar for at tage Amoritens Land i Eje;
11 Ine ndinawutsanso ena mwa ana ako kuti akhale aneneri, ndi ena mwa anyamata ako kuti akhale anaziri. Kodi si choncho, inu Aisraeli?” akutero Yehova.
og jeg opvakte nogle af eders Sønner til Profeter og nogle af eders unge Karle til Nasiræer, (mon det ikke er saa, Israels Børn? siger Herren);
12 “Koma inu munawamwetsa vinyo anaziri aja, ndipo munalamula aneneri kuti asanenere.
men I gave Nasiræerne Vin at drikke og gave Profeterne det Bud: I skulle ikke spaa: —
13 “Tsono Ine ndidzakupsinjani monga imapsinjikira ngolo imene yadzaza ndi tirigu.
Se, derfor vil jeg trykke eder ned, ligesom Vognen, der er fuld med Neg, trykker ned.
14 Munthu waliwiro sadzatha kuthawa, munthu wamphamvu sadzakhalanso ndi nyonga, wankhondo sadzapulumutsa moyo wake.
Og den lette skal ingen Tilflugt finde, og den stærke skal ikke lægge Kraft i sin Styrke, og den vældige skal ikke redde sit Liv,
15 Munthu wa uta sadzalimbika, msilikali wothamanga kwambiri sadzapulumuka, ndipo wokwera pa akavalo sadzapulumutsa moyo wake.
og den, som fører Buen, skal ikke bestaa, og den, som er let paa sine Fødder, skal ikke redde sig, og den, som rider paa Hesten, skal ikke redde sit Liv.
16 Ngakhale asilikali olimba mtima kwambiri adzathawa ali maliseche pa tsikulo,” akutero Yehova.
Og den, som er stærk i sit Hjerte, iblandt de vældige, han skal fly nøgen paa samme Dag, siger Herren.

< Amosi 2 >