< Amosi 1 >

1 Mawu a Amosi, mmodzi mwa anthu oweta nkhosa ku Tekowa. Zimene iye anaona mʼmasomphenya zokhudza Israeli patatsala zaka ziwiri kuti chivomerezi chichitike, nthawi imene Uziya anali mfumu ya Yuda ndipo Yeroboamu mwana wa Yowasi anali mfumu ya Israeli.
Paroles d’Amos, qui fut un des pasteurs de Thécué, paroles relatives aux choses qu’il a vues touchant Israël, au temps d’Ozias, roi de Juda, et de Jéroboam, fils de Joas, roi d’Israël, deux ans avant le tremblement de terre.
2 Amosi anati: “Yehova akubangula mu Ziyoni ndipo akumveka ngati bingu mu Yerusalemu; msipu wa abusa ukulira, ndipo pamwamba pa Karimeli pakuwuma.”
Et il dit: Le Seigneur rugira de Sion, et de Jérusalem il fera entendre sa voix; et les beaux pâturages des pasteurs ont été dans le deuil, et la cîme du Carmel a été desséchée.
3 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Damasiko akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anapuntha Giliyadi ndi zopunthira za mano achitsulo,
Voici ce que dit le Seigneur: à cause des trois et même des quatre crimes de Damas, je ne le convertirai pas; parce qu’ils ont écrasé Galaad sous des chariots armés de fer,
4 Ine ndidzatumiza moto pa nyumba ya Hazaeli umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.
Et j’enverrai un feu dans la maison d’Azaël, et il dévorera les maisons de Bénadad.
5 Ndidzathyola chipata cha Damasiko; ndidzawononga mfumu yokhala ku Chigwa cha Aveni, ndiponso iye amene akugwira ndodo yaufumu mu Beti-Edeni. Anthu a ku Aramu adzapita ku ukapolo ku Kiri,” akutero Yehova.
Et je briserai le verrou de Damas, et j’exterminerai du champ de l’idole l’habitant, et de la maison de plaisir celui qui tient le sceptre; et le peuple de Syrie sera transporté à Cyrène, dit le Seigneur.
6 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Gaza akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anatenga ukapolo mtundu wathunthu ndi kuwugulitsa ku Edomu,
Voici ce que dit le Seigneur: À cause des trois et quatre crimes de Gaza, je ne le convertirai pas, parce qu’ils ont transféré tous les captifs, afin de les renfermer dans l’Idumée.
7 ndidzatumiza moto pa makoma a Gaza umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.
Et j’enverrai un feu contre le mur de Gaza, et il dévorera ses édifices.
8 Ndidzawononga mfumu ya ku Asidodi komanso amene akugwira ndodo yaufumu ku Asikeloni. Ndidzalanga Ekroni, mpaka wotsala mwa Afilisti atafa,” akutero Ambuye Yehova.
J’exterminerai d’Azot l’habitant, et d’Ascalon celui qui tient le sceptre; et je tournerai ma main sur Accaron, et les restes des Philistins seront détruits, dit le Seigneur Dieu.
9 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Turo akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza iwo anagulitsa mtundu wathunthu ku ukapolo ku Edomu, osasunga pangano laubale lija,
Voici ce que dit le Seigneur: À cause des trois et même des quatre crimes de Tyr, je ne le convertirai pas, parce qu’ils ont renfermé tous les captifs dans l’Idumée, et qu’ils ne se sont pas souvenus de l’alliance faite avec leurs frères.
10 Ine ndidzatumiza moto pa makoma a Turo umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.”
Et j’enverrai un feu contre les murs de Tyr, et il dévorera ses édifices.
11 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Edomu akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anathamangitsa mʼbale wake ndi lupanga, popanda nʼchifundo chomwe. Popeza mkwiyo wake unakulabe ndipo ukali wake sunatonthozeke,
Voici ce que dit le Seigneur: À cause des trois et même des quatre crimes d’Edom, je ne le convertirai pas, parce qu’il a poursuivi son frère par le glaive, qu’il a violé envers lui la miséricorde, qu’il n’a pas mis de bornes à sa fureur, et qu’il a conservé le ressentiment de sa colère jusqu’à la fin.
12 Ine ndidzatumiza moto pa Temani umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za Bozira.”
J’enverrai un feu dans Théman, et il dévorera les édifices de Bosra.
13 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Amoni akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anatumbula akazi oyembekezera a ku Giliyadi nʼcholinga choti akuze malire awo,
Voici ce que dit le Seigneur: À cause des trois et même des quatre crimes des fils d’Ammon, je ne les convertirai pas, parce qu’ils ont ouvert le sein des femmes enceintes de Galaad pour étendre leurs frontières.
14 Ine ndidzayatsa moto pa makoma a ku Raba umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu. Padzakhala kulira kwakukulu pa tsiku la nkhondoyo, kumenyana kudzakhala kwafumbi ngati mkuntho wa kamvuluvulu.
J’allumerai un feu dans les murs de Rabba, et il dévorera ses édifices parmi les cris, en un jour de combat, parmi la tourmente, en un jour de bouleversement.
15 Mfumu yawo idzatengedwa kupita ku ukapolo, iyo pamodzi ndi akuluakulu ake,” akutero Yehova.
Et Melchom ira en captivité, lui et ses princes avec lui, dit le Seigneur.

< Amosi 1 >