< Amosi 1 >

1 Mawu a Amosi, mmodzi mwa anthu oweta nkhosa ku Tekowa. Zimene iye anaona mʼmasomphenya zokhudza Israeli patatsala zaka ziwiri kuti chivomerezi chichitike, nthawi imene Uziya anali mfumu ya Yuda ndipo Yeroboamu mwana wa Yowasi anali mfumu ya Israeli.
Les paroles d'Amos, qui était d'entre les bergers de Thékoa, lesquelles lui furent révélées touchant Israël aux jours d'Ozias, roi de Juda, et de Jéroboam, fils de Joas, roi d'Israël, deux ans avant le tremblement de terre.
2 Amosi anati: “Yehova akubangula mu Ziyoni ndipo akumveka ngati bingu mu Yerusalemu; msipu wa abusa ukulira, ndipo pamwamba pa Karimeli pakuwuma.”
Il dit: L'Éternel rugit de Sion; de Jérusalem il fait entendre sa voix; les pâturages des bergers sont en deuil, et le sommet du Carmel est desséché.
3 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Damasiko akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anapuntha Giliyadi ndi zopunthira za mano achitsulo,
Ainsi a dit l'Éternel: A cause de trois crimes de Damas et même de quatre, je ne le révoquerai point: parce qu'ils ont foulé Galaad avec des herses de fer;
4 Ine ndidzatumiza moto pa nyumba ya Hazaeli umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.
J'enverrai le feu dans la maison de Hasaël, et il dévorera les palais de Ben-Hadad;
5 Ndidzathyola chipata cha Damasiko; ndidzawononga mfumu yokhala ku Chigwa cha Aveni, ndiponso iye amene akugwira ndodo yaufumu mu Beti-Edeni. Anthu a ku Aramu adzapita ku ukapolo ku Kiri,” akutero Yehova.
Je briserai les barres de Damas; j'exterminerai de Bikath-Aven les habitants, et de Beth-Éden celui qui tient le sceptre, et le peuple de Syrie sera mené captif à Kir, dit l'Éternel.
6 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Gaza akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anatenga ukapolo mtundu wathunthu ndi kuwugulitsa ku Edomu,
Ainsi a dit l'Éternel: A cause de trois crimes de Gaza et même de quatre, je ne le révoquerai point: parce qu'ils ont emmené des captifs en grand nombre pour les livrer à Édom;
7 ndidzatumiza moto pa makoma a Gaza umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.
J'enverrai le feu dans les murs de Gaza, et il dévorera ses palais;
8 Ndidzawononga mfumu ya ku Asidodi komanso amene akugwira ndodo yaufumu ku Asikeloni. Ndidzalanga Ekroni, mpaka wotsala mwa Afilisti atafa,” akutero Ambuye Yehova.
J'exterminerai d'Asdod les habitants, et d'Askélon celui qui tient le sceptre; je tournerai ma main contre Ékron, et le reste des Philistins périra, dit le Seigneur, l'Éternel.
9 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Turo akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza iwo anagulitsa mtundu wathunthu ku ukapolo ku Edomu, osasunga pangano laubale lija,
Ainsi a dit l'Éternel: A cause de trois crimes de Tyr et même de quatre, je ne le révoquerai point: parce qu'ils ont livré à Édom des captifs en grand nombre, et ne se sont point souvenus de l'alliance fraternelle;
10 Ine ndidzatumiza moto pa makoma a Turo umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.”
J'enverrai le feu dans les murs de Tyr, et il dévorera ses palais.
11 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Edomu akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anathamangitsa mʼbale wake ndi lupanga, popanda nʼchifundo chomwe. Popeza mkwiyo wake unakulabe ndipo ukali wake sunatonthozeke,
Ainsi a dit l'Éternel: A cause de trois crimes d'Édom et même de quatre, je ne le révoquerai point: parce qu'il a poursuivi son frère avec l'épée, et qu'il a étouffé la compassion, parce que sa colère déchire sans cesse, et qu'il garde sa fureur à toujours;
12 Ine ndidzatumiza moto pa Temani umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za Bozira.”
J'enverrai le feu dans Théman, et il dévorera les palais de Botsra.
13 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Amoni akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anatumbula akazi oyembekezera a ku Giliyadi nʼcholinga choti akuze malire awo,
Ainsi a dit l'Éternel: A cause de trois crimes des enfants d'Ammon et même de quatre, je ne le révoquerai point: parce qu'ils ont fendu le ventre des femmes enceintes de Galaad, pour étendre leurs frontières;
14 Ine ndidzayatsa moto pa makoma a ku Raba umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu. Padzakhala kulira kwakukulu pa tsiku la nkhondoyo, kumenyana kudzakhala kwafumbi ngati mkuntho wa kamvuluvulu.
J'allumerai le feu dans les murs de Rabba, et il dévorera ses palais, au bruit des clameurs dans le jour du combat, au milieu de l'ouragan dans le jour de la tempête;
15 Mfumu yawo idzatengedwa kupita ku ukapolo, iyo pamodzi ndi akuluakulu ake,” akutero Yehova.
Et leur roi s'en ira en captivité, lui et ses chefs avec lui, dit l'Éternel.

< Amosi 1 >