< Amosi 1 >

1 Mawu a Amosi, mmodzi mwa anthu oweta nkhosa ku Tekowa. Zimene iye anaona mʼmasomphenya zokhudza Israeli patatsala zaka ziwiri kuti chivomerezi chichitike, nthawi imene Uziya anali mfumu ya Yuda ndipo Yeroboamu mwana wa Yowasi anali mfumu ya Israeli.
Paroles d’Amos, un des éleveurs de troupeaux à Tekoa, qui prophétisa sur Israël durant le règne d’Ouzia, roi de Juda, et de Jéroboam, roi d’Israël, deux ans avant le tremblement de terre.
2 Amosi anati: “Yehova akubangula mu Ziyoni ndipo akumveka ngati bingu mu Yerusalemu; msipu wa abusa ukulira, ndipo pamwamba pa Karimeli pakuwuma.”
Il dit: "L’Eternel rugit de Sion, de Jérusalem il fait entendre sa voix: les pacages des bergers en sont assombris, le sommet du Carmel en est desséché."
3 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Damasiko akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anapuntha Giliyadi ndi zopunthira za mano achitsulo,
Ainsi parle l’Eternel: "A cause du triple, du quadruple crime de Damas, je ne le révoquerai pas, mon arrêt: parce qu’ils ont foulé le pays de Galaad avec des herses de fer.
4 Ine ndidzatumiza moto pa nyumba ya Hazaeli umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.
Aussi déchaînerai-je le feu contre la maison de Hazaël, pour qu’il dévore les palais de Ben-Hadad.
5 Ndidzathyola chipata cha Damasiko; ndidzawononga mfumu yokhala ku Chigwa cha Aveni, ndiponso iye amene akugwira ndodo yaufumu mu Beti-Edeni. Anthu a ku Aramu adzapita ku ukapolo ku Kiri,” akutero Yehova.
Je briserai les verrous de Damas, j’exterminerai les habitants du Val de Perversité et le porte-sceptre de la maison de Délices. Le peuple d’Aram ira en exil à Kir, dit l’Eternel."
6 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Gaza akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anatenga ukapolo mtundu wathunthu ndi kuwugulitsa ku Edomu,
Ainsi parle l’Eternel: "A cause du triple, du quadruple crime de Gaza, je ne le révoquerai pas, mon arrêt: parce qu’ils ont déporté des exilés en masse pour les livrer à Edom.
7 ndidzatumiza moto pa makoma a Gaza umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.
Aussi déchaînerai-je le feu contre les murs de Gaza, pour qu’il en dévore les palais.
8 Ndidzawononga mfumu ya ku Asidodi komanso amene akugwira ndodo yaufumu ku Asikeloni. Ndidzalanga Ekroni, mpaka wotsala mwa Afilisti atafa,” akutero Ambuye Yehova.
J’Exterminerai les habitants d’Asdod et le porte-sceptre d’Ascalon; je dirigerai ma main contre Ekron, pour que périsse le reste des Philistins, dit le Seigneur Dieu."
9 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Turo akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza iwo anagulitsa mtundu wathunthu ku ukapolo ku Edomu, osasunga pangano laubale lija,
Ainsi parle l’Eternel: "A cause du triple, du quadruple crime de Tyr, je ne le révoquerai pas, mon arrêt: parce qu’ils ont livré des captifs en masse à Edom, sans se souvenir de la fraternelle alliance.
10 Ine ndidzatumiza moto pa makoma a Turo umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.”
Aussi déchaînerai-je le feu contre les murs de Tyr, pour qu’il en dévore les palais."
11 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Edomu akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anathamangitsa mʼbale wake ndi lupanga, popanda nʼchifundo chomwe. Popeza mkwiyo wake unakulabe ndipo ukali wake sunatonthozeke,
Ainsi parle l’Eternel: "A cause du triple, du quadruple crime d’Edom, je ne le révoquerai pas, mon arrêt: parce qu’il a poursuivi son frère avec l’épée, étouffant toute pitié; parce que sa colère ne cesse de faire des victimes, et qu’il se complaît dans une haine sans fin.
12 Ine ndidzatumiza moto pa Temani umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za Bozira.”
Aussi déchaînerai-je le feu contre Têmân, pour qu’il dévore les palais de Boçra."
13 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Amoni akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anatumbula akazi oyembekezera a ku Giliyadi nʼcholinga choti akuze malire awo,
Ainsi parle l’Eternel: "A cause du triple, du quadruple crime des fils d’Ammon, je ne le révoquerai pas, mon arrêt: parce qu’ils ont éventré les femmes enceintes de Galaad, en vue d’étendre leur territoire.
14 Ine ndidzayatsa moto pa makoma a ku Raba umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu. Padzakhala kulira kwakukulu pa tsiku la nkhondoyo, kumenyana kudzakhala kwafumbi ngati mkuntho wa kamvuluvulu.
Aussi mettrai-je le feu aux murs de Rabba, pour qu’il en dévore les palais, au milieu des cris de guerre, au jour du combat, au milieu de la tempête, au jour de l’ouragan.
15 Mfumu yawo idzatengedwa kupita ku ukapolo, iyo pamodzi ndi akuluakulu ake,” akutero Yehova.
Malcom ira en exil, lui et ses dignitaires, tous ensemble, dit l’Eternel."

< Amosi 1 >