< Amosi 1 >

1 Mawu a Amosi, mmodzi mwa anthu oweta nkhosa ku Tekowa. Zimene iye anaona mʼmasomphenya zokhudza Israeli patatsala zaka ziwiri kuti chivomerezi chichitike, nthawi imene Uziya anali mfumu ya Yuda ndipo Yeroboamu mwana wa Yowasi anali mfumu ya Israeli.
The wordis of Amos ben these, that was in the schepherdis thingis of Thecue, whiche he siy on Israel, in the daies of Osie, king of Juda, and in the daies of Jeroboam, sone of Joas, kyng of Israel, bifor twei yeeris of the erthe mouynge.
2 Amosi anati: “Yehova akubangula mu Ziyoni ndipo akumveka ngati bingu mu Yerusalemu; msipu wa abusa ukulira, ndipo pamwamba pa Karimeli pakuwuma.”
And he seide, The Lord schal rore fro Sion, and schal yyue his vois fro Jerusalem; and the faire thingis of schepherdis mourenyden, and the cop of Carmele was maad drie.
3 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Damasiko akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anapuntha Giliyadi ndi zopunthira za mano achitsulo,
The Lord seith these thingis, On thre grete trespassis of Damask, and on foure, I shal not conuerte it, for it threischide Galaad in irun waynes.
4 Ine ndidzatumiza moto pa nyumba ya Hazaeli umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.
And Y schal sende fier in to the hous of Asael, and it schal deuoure the housis of Benadab.
5 Ndidzathyola chipata cha Damasiko; ndidzawononga mfumu yokhala ku Chigwa cha Aveni, ndiponso iye amene akugwira ndodo yaufumu mu Beti-Edeni. Anthu a ku Aramu adzapita ku ukapolo ku Kiri,” akutero Yehova.
And Y schal al to-breke the barre of Damask, and Y schal leese a dwellere fro the feeld of idol, and hym that holdith the ceptre fro the hous of lust and of letcherie; and the puple of Sirie schal be translatid to Sirenen, seith the Lord.
6 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Gaza akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anatenga ukapolo mtundu wathunthu ndi kuwugulitsa ku Edomu,
The Lord seith these thingis, On thre grete trespassis of Gasa, and on foure, Y schal not conuerte it, for it translatide perfit caitifte, to close that togidere in Idumee.
7 ndidzatumiza moto pa makoma a Gaza umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.
And Y schal sende fier in to the wal of Gasa, and it schal deuoure the housis therof.
8 Ndidzawononga mfumu ya ku Asidodi komanso amene akugwira ndodo yaufumu ku Asikeloni. Ndidzalanga Ekroni, mpaka wotsala mwa Afilisti atafa,” akutero Ambuye Yehova.
And Y schal leese the dwelleris of Azotus, and hym that holdith the ceptre of Ascalon; and Y schal turne myn hond on Accaron, and the remenauntis of Filisteis schulen perische, seith the Lord God.
9 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Turo akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza iwo anagulitsa mtundu wathunthu ku ukapolo ku Edomu, osasunga pangano laubale lija,
The Lord God seith these thingis, On thre grete trespassis of Tire, and on foure, Y schal not conuerte it, for thei closiden togidere perfit caitifte in Idumee, and hadde not mynde on the boond of pees of britheren.
10 Ine ndidzatumiza moto pa makoma a Turo umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.”
And Y schal sende fier in to the wal of Tire, and it schal deuoure the housis therof.
11 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Edomu akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anathamangitsa mʼbale wake ndi lupanga, popanda nʼchifundo chomwe. Popeza mkwiyo wake unakulabe ndipo ukali wake sunatonthozeke,
The Lord seith these thingis, On thre grete trespassis of Edom, and on foure, Y schal not conuerte it, for it pursuede bi swerd his brother, and defoulide the merci of hym, and helde ferthere his woodnesse, and kepte his indignacioun `til in to the ende.
12 Ine ndidzatumiza moto pa Temani umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za Bozira.”
Y schal sende fier in to Theman, and it schal deuoure the housis of Bosra.
13 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Amoni akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anatumbula akazi oyembekezera a ku Giliyadi nʼcholinga choti akuze malire awo,
The Lord seith these thingis, On thre grete trespassis of the sones of Amon, and on foure, Y schal not conuerte hym, for he karf the wymmen with childe of Galaad, for to alarge his terme.
14 Ine ndidzayatsa moto pa makoma a ku Raba umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu. Padzakhala kulira kwakukulu pa tsiku la nkhondoyo, kumenyana kudzakhala kwafumbi ngati mkuntho wa kamvuluvulu.
And Y schal kyndle fier in the wal of Rabbe, and it schal deuoure the housis therof, in yellyng in the dai of batel, and in whirlwynd in the dai of mouyng togidere.
15 Mfumu yawo idzatengedwa kupita ku ukapolo, iyo pamodzi ndi akuluakulu ake,” akutero Yehova.
And Melchon schal go in to caitifte, he and hise princes togidere, seith the Lord.

< Amosi 1 >