< Machitidwe a Atumwi 6 >
1 Mʼmasiku amenewo pamene chiwerengero cha ophunzira chinkachuluka, Ayuda a Chihelene pakati pawo anadandaula chifukwa cha Ayuda a Chihebri chifukwa amasiye awo samawagawira chakudya cha tsiku ndi tsiku.
În zilele acelea, când numărul ucenicilor se înmulțea, s-a ridicat o plângere din partea elinilor împotriva evreilor, pentru că văduvele lor erau neglijate în slujba zilnică.
2 Tsono Atumwi khumi ndi awiriwo anasonkhanitsa ophunzira onse pamodzi ndipo anati, “Nʼkosayenera kuti ife tisiye kulalikira Mawu a Mulungu ndi kuyangʼanira za chakudya.
Cei doisprezece au convocat mulțimea discipolilor și au spus: “Nu se cuvine ca noi să părăsim cuvântul lui Dumnezeu și să servim la mese.
3 Choncho abale, sankhani pakati panu anthu asanu ndi awiri a mbiri yabwino, odzazidwa ndi Mzimu Woyera ndi anzeru. Ife tidzawapatsa udindo oyangʼanira.
De aceea, fraților, alegeți dintre voi șapte bărbați de bună reputație, plini de Duhul Sfânt și de înțelepciune, pe care să îi numim în fruntea acestei afaceri.
4 Koma ife tidzadzipereka kuti tizipemphera ndi kulalikira mawu.”
Dar noi vom continua cu stăruință în rugăciune și în slujirea cuvântului.”
5 Mawu amenewa anakondweretsa gulu lonse la anthu. Iwo anasankha, Stefano, munthu wodzazidwa ndi chikhulupiriro ndiponso Mzimu Woyera; anasankhanso Filipo, Prokoro, Nikanora, Timo, Parmena ndi Nikolao amene anatembenuka mtima ndi kulowa Chiyuda kuchokera kwa Antiokeya.
Aceste cuvinte au plăcut întregii mulțimi. Ei au ales pe Ștefan, un om plin de credință și de Duhul Sfânt, pe Filip, Prohor, Nicanor, Timon, Parmenas și Nicolae, un prozelit din Antiohia,
6 Iwo anapereka anthuwa kwa atumwi amene anawapempherera ndi kuwasanjika manja.
pe care i-au pus înaintea apostolilor. După ce s-au rugat, aceștia și-au pus mâinile peste ei.
7 Ndipo Mawu a Mulungu anapitirira kufalikira. Chiwerengero cha ophunzira mu Yerusalemu chinakula mofulumira ndipo ansembe ochuluka anakhulupirira.
Cuvântul lui Dumnezeu creștea și numărul ucenicilor se înmulțea foarte mult în Ierusalim. O mare mulțime de preoți se supuneau credinței.
8 Stefano, munthu wodzazidwa ndi chisomo cha Mulungu ndi mphamvu anachita zodabwitsa ndiponso zizindikiro zazikulu pakati pa anthu.
Ștefan, plin de credință și de putere, făcea minuni și semne mari în popor.
9 Panauka mtsutso kuchokera kwa anthu a ku Kurene ndi a ku Alekisandriya komanso a ku dera la Silisiya ndi Asiya, otchedwa a Sunagoge ya Mfulu. Anthu amenewa anayamba kutsutsana ndi Stefano.
Dar unii dintre cei din sinagoga numită “Libertinii”, dintre cireni, dintre alexandrini și dintre cei din Cilicia și din Asia s-au sculat, certându-se cu Ștefan.
10 Koma iwo sanathe kumugonjetsa chifukwa iye ankayankhula ndi nzeru zimene Mzimu Woyera anamupatsa.
Ei nu au putut să reziste înțelepciunii și Duhului prin care vorbea el.
11 Iwo ananyengerera anthu ena mwamseri kuti anene kuti, “Ife tinamva Stefano akuchitira chipongwe Mose ndiponso Mulungu.”
Atunci au determinat pe ascuns pe oameni să spună: “L-am auzit spunând cuvinte blasfemiatoare împotriva lui Moise și a lui Dumnezeu”.
12 Motero anawutsa mitima ya anthu, akulu ndi aphunzitsi amalamulo. Anamugwira Stefano ndi kumubweretsa ku Bwalo Lalikulu.
Au stârnit poporul, bătrânii și cărturarii, au venit împotriva lui și l-au prins, apoi l-au adus în consiliu,
13 Iwo anabweretsa mboni zonama zimene zinati, “Munthu uyu akupitirirabe kuyankhula mawu onyoza malo oyera ndi malamulo.
și au pus martori falși care spuneau: “Omul acesta nu încetează să rostească cuvinte blasfemiatoare împotriva acestui loc sfânt și a Legii.
14 Pakuti tinamumva akunena kuti Yesu uja wa ku Nazareti adzawononga malo ano ndiponso kusintha miyambo imene Mose anatipatsa.”
Căci l-am auzit spunând că acest Isus din Nazaret va distruge acest loc și va schimba obiceiurile pe care ni le-a dat Moise.”
15 Onse amene anakhala pansi Mʼbwalo Lalikulu anamuyangʼanitsitsa Stefano, ndipo anaona kuti nkhope yake ikuwala ngati ya mngelo.
Toți cei care stăteau în consiliu, fixându-și ochii asupra lui, i-au văzut fața ca pe cea a unui înger.