< Machitidwe a Atumwi 4 >

1 Pamene Petro ndi Yohane amayankhula ndi anthu, kunabwera ansembe, mkulu woyangʼanira Nyumba ya Mulungu ndiponso Asaduki.
בשעה שפטרוס ויוחנן דברו אל העם, ניגשו אליהם בכעס הכוהנים, הקצין הממונה על משמר בית־המקדש וכן אחדים מהצדוקים,
2 Iwo anakhumudwa kwambiri chifukwa atumwiwo amaphunzitsa anthu ndi kumalalikira za kuuka kwa akufa mwa Yesu.
מכיוון שהשניים לימדו את העם שישוע המשיח קם לתחייה, וכך הוכיחו שאכן תהיה תחיית המתים.
3 Iwo anagwira Petro ndi Yohane, popeza kunali kutada, anawayika mʼndende mpaka mmawa mwake.
הם תפסו את פטרוס ויוחנן, ומאחר שכבר ירד הערב, הכניסו אותם לכלא עד יום המחרת.
4 Koma anthu ambiri amene anamva uthenga anakhulupirira, ndipo chiwerengero cha anthu chinakwana 5,000.
אולם רבים מאלה שהאזינו לפטרוס האמינו לדבריו, ומספר המאמינים במשיח הגיע ל־חמשת־אלפים איש.
5 Mmawa mwake olamulira, akulu ndi aphunzitsi a malamulo anasonkhana mu Yerusalemu.
למחרת התכנסו מנהיגי העם בירושלים, כדי לערוך ישיבה עם חנן הכוהן הגדול, קייפא, יוחנן, אלכסנדר ועוד רבים מקרובי משפחתו של הכהן הגדול.
6 Panali Anasi, Mkulu wa ansembe, Kayafa, Yohane ndi Alekisandro ndi ana a banja la mkulu wa ansembe.
7 Iwo anayimiritsa Petro ndi Yohane patsogolo pawo nayamba kuwafunsa kuti, “Kodi munachita zimenezi ndi mphamvu yanji kapena mʼdzina la yani?”
הם העמידו לפניהם את פטרוס ויוחנן, ושאלו אותם:”באיזה כוח ובאיזו סמכות עשיתם זאת?“
8 Petro wodzazidwa ndi Mzimu Woyera, anawawuza kuti, “Inu olamulira ndi akulu!
פטרוס שנמלא רוח הקודש, השיב:”מנהיגים וזקני־העם הנכבדים,
9 Ngati ife tikufunsidwa lero chifukwa cha ntchito yabwino imene yachitika pa munthu wolumala miyendo ndi mmene iye anachiritsidwira,
אם אתם מתכוונים לטובה שעשינו לאיש הפיסח הזה, אשר קם על רגליו בריא ושלם,
10 tsono dziwani izi inu ndi aliyense mu Israeli: munthuyu akuyima pamaso panu, wochiritsidwa kwathunthu, ndi chifukwa cha dzina la Yesu Khristu wa ku Nazareti amene munamupachika koma Mulungu anamuukitsa kwa akufa.
הרשו לי להצהיר בפניכם ולפני כל עם־ישראל: עשינו מה שעשינו בשמו ובכוחו של ישוע המשיח מנצרת. אתם אמנם צלבתם את ישוע, אולם אלוהים הקים אותו מן המתים! בשמו ובסמכותו עומד האיש הזה לפניכם בריא ושלם.
11 Iye ndi “‘Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana, umenewo wasanduka mwala wa pa ngodya!’
ישוע המשיח הוא אבן הפינה אשר אתם, הבונים, מאסתם בה, ואשר הייתה לראש פינה.
12 Chipulumutso sichipezeka mwa wina aliyense; pakuti palibe dzina lina pansi pa thambo limene lapatsidwa kwa anthu limene tiyenera kupulumutsidwa nalo.”
איש מלבדו אינו יכול להושיע! ואין עוד שם תחת השמים אשר בני־האדם יכולים לקרוא אליו כדי להיוושע!“
13 Ataona kulimba mtima kwa Petro ndi Yohane ndi kuzindikira kuti anali osaphunzira, anthu wamba, anadabwa kwambiri ndipo anazindikira kuti anthuwa anakhala pamodzi ndi Yesu.
כשראו הדיינים את אומץ לבם של פטרוס ויוחנן, ונוכחו לדעת שהם אנשים פשוטים, לא משכילים ולא”מקצועיים“, התפלאו מאוד. הם זיהו אותם, שבעבר היו יחד עם ישוע.
14 Koma popeza iwo amamuona munthu amene anachiritsidwa atayima pamodzi ndi iwo, palibe chimene akananena.
והדיינים לא יכלו להכחיש את עובדת ריפויו של הפיסח לשעבר, כי הוא עמד מולם בריא ושלם.
15 Chifukwa chake anawalamula kuti atuluke mʼbwalo la milandu ndipo akulu abwalowo anayamba kukambirana.
הדיינים, אובדי־עצות, ציוו על פטרוס ויוחנן לצאת מאולם המשפט, כדי שיוכלו להתייעץ ביניהם.
16 Iwo anafunsana kuti, “Kodi anthuwa tichite nawo chiyani? Pakuti aliyense okhala mu Yerusalemu akudziwa kuti achita chodabwitsachi, ndipo ife sitingathe kukana.
”מה נעשה בהם?“שאלו זה את זה.”איננו יכולים להכחיש שהם חוללו נס גדול, שהרי כל תושבי ירושלים שמעו על כך.
17 Koma kuti mbiriyi isapitirire kuwanda pakati pa anthu, ife tiwachenjeze anthu amenewa kuti asayankhulenso kwa wina aliyense mʼdzina la Yesu.”
אך אולי נוכל למנוע בעדם להמשיך להפיץ את התעמולה שלהם. נזהיר אותם שאם יעזו להמשיך להטיף בשם ישוע, נעניש אותם בחומרה רבה!“
18 Pamenepo anawayitananso ndipo anawalamula kuti asayankhule kapena kuphunzitsa konse mʼdzina la Yesu.
הם קראו לפטרוס ויוחנן לשוב לאולם, ודרשו מהם שלא לדבר שוב על ישוע לעולם.
19 Koma Petro ndi Yohane anayankha kuti, “Weruzani nokha ngati nʼkwabwino pamaso pa Mulungu kumvera inu koposa Mulungu.
אולם פטרוס ויוחנן השיבו:”החליטו אתם בעצמכם, האם אלוהים רוצה שנשמע לקולו או לקולכם?
20 Ife sitingaleke kuyankhula za zimene tinaziona ndi kuzimva.”
איננו יכולים להפסיק לספר על כל אשר ישוע עשה לנגד עינינו, או על הדברים ששמענו מפיו!“
21 Atawonjeza kuwaopseza anawamasula. Sanathe kugwirizana njira yowalangira, chifukwa anthu onse amayamika Mulungu chifukwa cha zimene zinachitika.
חברי הסנהדרין הוסיפו לגעור בהם ולאיים עליהם, אך לבסוף שחררו אותם, כי לא ידעו כיצד להענישם בלי לעורר מהומה בעם. שכן כל העם הלל את אלוהים על שחולל את הנס הנפלא הזה
22 Ndipo munthu amene anachiritsidwayo anali ndi zaka makumi anayi.
וריפא את האדם שהיה פיסח במשך ארבעים שנה.
23 Atamasulidwa Petro ndi Yohane anapita kwa anzawo ndipo anawafotokozera zonse zimene akulu a ansembe ndi akulu anawawuza.
מיד לאחר שחרורם מיהרו פטרוס ויוחנן אל אחיהם המאמינים וסיפרו להם את דברי הסנהדרין.
24 Anthu atamva zimenezi anafuwula ndi mtima umodzi napemphera kwa Mulungu. Iwo anati, “Ambuye wolamulira zonse, Inu munalenga kumwamba ndi dziko lapansi ndi nyanja ndiponso zonse zili mʼmenemo.
כששמעו המאמינים את הדבר, התפללו אל אלוהים בלב אחד:”אדוננו, בורא השמים, הארץ, הים וכל אשר בם –
25 Inu munayankhula mwa Mzimu Woyera kudzera pakamwa pa Davide kholo lathu, mtumiki wanu kuti, “‘Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu, ndipo akonzekera kuchita zopandapake?
עוד לפני זמן רב דיברת באמצעות רוח הקודש, בפי דוד המלך שהוא עבדך ואבינו, ואמרת:’למה רגשו גוים, ולאומים יהגו ריק?
26 Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo.’
יתיצבו מלכי ארץ ורוזנים נוסדו יחד על ה׳ ועל משיחו‘.
27 Zoonadi, Herode ndi Pontiyo Pilato anasonkhana pamodzi ndi amitundu ndiponso Aisraeli, mu mzinda muno, kupanga zolimbana ndi mtumiki wanu woyera Yesu, amene Inu munamudzoza.
”דבריך אלה התקיימו בעיר הזאת! שהרי המלך הורדוס ופונטיוס פילטוס כרתו ברית עם העמים השונים ועם בני־ישראל, וכולם יחד קמו נגד עבדך הקדוש ישוע המשיח.
28 Iwo anachita zimene munakonzeratu mwachifuniro chanu ndi mphamvu yanu kuti zichitike.
אולם הם עשו אך ורק את מה שבחוכמתך הרבה החלטת שיעשו.
29 Tsopano, Ambuye taonani kuti atiopseza, tithandizeni ife atumiki anu, kuti tiyankhule mawu anu molimba mtima.
ועתה, ה׳, שמע נא את איומיהם, ותן לעבדיך אומץ־לב לבשר את דברך.
30 Tambasulani dzanja lanu kuchiritsa anthu ndipo kuti, zizindikiro zodabwitsa zichitike mʼdzina la mtumiki wanu woyera Yesu.”
שלח נא את כוחך המרפא, והנח לנו לחולל נסים ונפלאות רבים בשמו של עבדך הקדוש ישוע המשיח.“
31 Iwo atatha kupemphera, malo amene anasonkhanapo anagwedezeka. Ndipo iwo onse anadzazidwa ndi Mzimu Woyera ndipo anayankhula Mawu a Mulungu molimba mtima.
לאחר שסיימו להתפלל הזדעזע הבית שבו ישבו. כולם נמלאו ברוח הקודש ובישרו את דבר ה׳ באומץ ובביטחון.
32 Okhulupirira onse anali a mtima umodzi, ndi maganizo amodzi. Palibe munthu amene amati zomwe anali nazo zinali zake zokha, koma amagawana chilichonse chimene anali nacho.
כל המאמינים היו מאוחדים בלב אחד ובדעה אחת, ואיש לא התייחס אל אשר בידו כאל רכושו הפרטי; הכול היה משותף לכולם.
33 Atumwi anapitirira kuchitira umboni mwa mphamvu zakuuka kwa Ambuye Yesu, ndipo pa iwo panali chisomo chochuluka.
השליחים דיברו בכוח ובגבורה על תקומתו של האדון ישוע, ואלוהים ברך אותם בכל מעשיהם.
34 Panalibe anthu osowa kanthu pakati pawo. Pakuti amene anali ndi malo, kapena nyumba amagulitsa ndi kubweretsa ndalamazo
לא היה ביניהם אף עני אחד, כי בעלי השדות ובעלי הבתים מכרו את נכסיהם ונתנו את הכסף לשליחים, כדי שיחלקו לאחרים לפי הצורך.
35 ndi kuzipereka kwa atumwi, ndipo zimagawidwa kwa aliyense amene anali ndi chosowa.
36 Yosefe, wa fuko la Levi, wochokera ku Kupro amene atumwi anamutcha Barnaba, kutanthauza kuti mwana wachilimbikitso,
היה ביניהם, למשל, אדם בשם יוסף (זה שהשליחים קראו לו”בר־נבא“או”בן־הנחמה“), משבט לוי, יליד קפריסין.
37 anagulitsa munda wake ndipo anadzapereka ndalamazo kwa atumwi.
גם הוא מכר את השדה שלו, ואת הכסף הביא לשליחים כדי שיחלקו לנזקקים.

< Machitidwe a Atumwi 4 >