< Machitidwe a Atumwi 3 >

1 Tsiku lina Petro ndi Yohane ankapita ku Nyumba ya Mulungu kukapemphera nthawi ya 3 koloko masana.
Chiengʼ moro achiel, kar sa ochiko odhiambo, mane en sa mar lemo noyudo ka Petro gi Johana odhi e hekalu.
2 Ndipo munthu wolumala chibadwire ankanyamulidwa tsiku ndi tsiku kukayikidwa pa khomo la Nyumbayo lotchedwa Khomo Lokongola kuti azikapempha amene amalowa ku bwalo la Nyumbayo.
To e sechego noyudo otingʼ ngʼat moro maputh kitero e ranga hekalu miluongo ni Malongʼo, kama ne ojaketee pile pile, mondo okwa kony kuom joma donjo ei hekalu.
3 Ataona Petro ndi Yohane ali pafupi kulowa anawapempha ndalama.
Kane ngʼatno oneno Petro gi Johana kadonjo ei hekalu, nokwayogi kony.
4 Iwo anamuyangʼanitsitsa iye. Kenaka Petro anati, “Tiyangʼane!”
To Petro gi Johana ne ongʼiyo wangʼe tir, mi Petro owachone niya, “Ngʼiwa ane!”
5 Munthuyo anawayangʼanitsitsa kuyembekezera kuti alandira kanthu kuchokera kwa iwo.
Ngʼatno nongʼiyogi, kogeno yudo gimoro kuomgi.
6 Petro anati kwa iye, “Ine ndilibe siliva kapena golide, koma chimene ndili nacho ndikupatsa. Mʼdzina la Yesu Khristu wa ku Nazareti, yenda.”
Eka Petro nowachone niya, “Fedha gi dhahabu aongego, to gima an-go ema amiyi. E nying Yesu Kristo ja-Nazareth, chungi iwuothi.”
7 Ndipo anamugwira dzanja lamanja, namuthandiza kuti ayimirire ndipo nthawi yomweyo mapazi ake ndi akakolo ake analimba.
Nomako bad ngʼatno, mi okonye aa malo, kendo gikanyo tiend ngʼatno gi ombongʼne noyudo teko.
8 Iye analumpha ndi kuyamba kuyenda. Kenaka analowa nawo pamodzi mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu, akuyenda ndi kulumpha ndiponso kuyamika Mulungu.
Ngʼatno nochikore malo mi ochako wuoth. Bangʼe nodhi kodgi ei laru mar hekalu, kowuotho kendo kochikore kendo kopako Nyasaye.
9 Anthu onse atamuona akuyenda ndiponso kuyamika Mulungu,
Ka ji duto nonene kowuotho kendo kopako Nyasaye,
10 anamuzindikira kuti ndi yemwe uja ankakhala pa khomo la Nyumbayo lotchedwa Khomo Lokongola, ndipo anazizwa ndi kudabwa ndi zimene zinamuchitikira.
negifwenyo ni en e ngʼat mane jabedo kakwecho e dhoranga hekalu miluongo ni Malongʼo, omiyo ne giwuoro kendo dhogi nomoko kuom gima notimorene.
11 Wopempha uja akuyenda pamodzi ndi Petro ndi Yohane, anthu onse anadabwa ndipo anawathamangira iwo kumalo wotchedwa Khonde la Solomoni.
Kane jakwechono pod otwere kuom Petro gi Johana, ji duto nohum nono. Negibiro gingʼwech ir jootego nyaka kama iluongo ni Agoch Solomon.
12 Petro ataona zimenezi anawawuza kuti, “Inu Aisraeli, chifukwa chiyani mukudabwa ndi zimene zachitikazi? Bwanji mukuyangʼana ife ngati kuti tamuyendetsa munthuyu ndi mphamvu yathu kapena chifukwa cha kupembedza kwathu?
Kane Petro onenogi, nowachonegi niya, “Un jo-Israel, angʼo momiyo gima otimoreni obwogou? Angʼo momiyo uchomo wangʼu kungʼiyowa mana ka gima tekowa wawegi kata timwa makare ema omiyo ngʼatni owuotho?
13 Mulungu wa Abrahamu, Isake ndi Yakobo, Mulungu wa makolo athu, wamulemekeza mtumiki wake Yesu. Amene inu munamukana pamaso pa Pilato ndi kumupereka Iye kuti aphedwe, ngakhale kuti Pilato anafuna kuti amumasule.
Nyasach Ibrahim gi Isaka kod Jakobo, ma en Nyasach kwerewa, ema osemiyo Yesu jatichne duongʼ. Ne uchiwe mondo onege, kendo ne ukwede e nyim Pilato, kata obedo ni Pilato ne dwaro gonye.
14 Koma inu munamukana Woyera ndi Wolungamayo ndipo munapempha kuti akumasulireni munthu wakupha anthu.
Ne ukwedo Ngʼama Ler kendo makare, to ukwayo mondo ogonynu janek.
15 Inu munapha mwini moyo, koma Mulungu anamuukitsa kwa akufa. Ife ndife mboni za zimenezi.
Ne unego wuon ngima, to Nyasaye nochiere oa kuom joma otho. Wan wawegi wan joneno kuom wachni.
16 Mwachikhulupiriro mʼdzina la Yesu, munthu uyu amene mukumuona ndi kumudziwa analimbikitsidwa. Mʼdzina la Yesu ndi chikhulupiriro chimene chili mwa iye chamuchiritsa kwathunthu, monga nonse mukuona.
Kuom yie e nying Yesu, ema ngʼat munenoni kendo ungʼeyoni oseyudoe chang. En mana nying Yesu, kaachiel kod yie maa kuome, ema osemiyo ngʼatni resruok moromo chuth, mana kaka un duto unenoni.
17 “Tsopano abale ine ndikudziwa kuti inu munachita zimenezi mosadziwa, monga momwenso anachitira atsogoleri anu.
“To koro, owetena, angʼeyo ni ne utimo gigo ka ok ungʼeyo, mana kaka jotendu bende notimogi kane ok gingʼeyo.
18 Koma umu ndi mmene Mulungu anakwaniritsira zimene zinanenedwa kale ndi aneneri onse, kuti Khristu adzamva zowawa.
To ma e yo ma Nyasaye nochopogo chenrone mane osenyiso chon gi dho jonabi duto, kowacho ni Kristo nyaka sandi.
19 Chifukwa chake, lapani, bwererani kwa Mulungu, kuti machimo anu afafanizidwe, kuti nthawi ya kutsitsimuka ibwere kuchokera kwa Ambuye,
Koro lokreuru uwe richou, udog ir Nyasaye, mondo richou owenu, eka Ruoth noduog chunyu mi uyud kwe,
20 ndi kuti Iye atumize Yesu Khristu amene anasankhidwa chifukwa cha inu.
bangʼe enoornu Yesu Kristo, Jal mane owalnu.
21 Iye ayenera kukhalabe kumwamba mpaka nthawi ya kukonzanso zinthu zonse monga Mulungu analonjeza kale kudzera mwa aneneri ake oyera mtima. (aiōn g165)
To pod nyaka obedie e polo nyaka chop kinde ma Nyasaye ketoe gik moko duto kare, mana kaka nosesingore chon gi dho jonabi mage maler. (aiōn g165)
22 Pakuti Mose anati, ‘Ambuye Mulungu wanu adzakuukitsirani mneneri monga ine kuchokera pakati pa anthu anu; mumvere zonse zimene iye akuwuzeni.
Musa nowacho ni, ‘Jehova Nyasaye ma Nyasachu biro miyou janabi machal koda kowuok e dier ogandau, kendo un bende nyaka uwinj gimoro amora mowachonu.
23 Aliyense amene sadzamvera mawu a mneneriyo, adzayenera kuchotsedwa pakati pa abale ake.’
Ngʼato angʼata ma ok winje, to nongʼad kare oko chuth e kind ogandane.’
24 “Ndipo aneneri onse ambiri amene anayankhula kuyambira Samueli, ananeneratu za masiku ano.
“Chutho, jonabi duto, kochakore ndalo Samuel gi jonabi mane oluwo bangʼe kaachiel gi ji duto mane owuoyo, bende nokoro gik matinde timore ndaloni.
25 Inu ndinu ana a aneneri ndiponso ana apangano limene Mulungu anachita ndi makolo anu. Iye anati kwa Abrahamu, ‘Anthu onse a pa dziko lapansi adzadalitsika kudzera mwa zidzukulu zako.’
To un e nyikwa jonabigo, kendo un e weg singruok ma Nyasaye notimo gi kwereu. Nyasaye nowachone Ibrahim ni, ‘joma ok jo-Yahudi duto mag piny noyud gweth koa kuom kothi.’
26 Pamene Mulungu anaukitsa mtumiki wake, anamutuma Iye poyamba kwa inu kuti akudalitseni pobweza aliyense wa inu ku zoyipa zake.”
Kane Nyasaye ooro Jatichne, to noore mokwongo ne un, mondo ogwedhu, ka oloko ngʼato ka ngʼato weyo yorene maricho.”

< Machitidwe a Atumwi 3 >