< Machitidwe a Atumwi 28 >

1 Titapulumuka choncho, tinamva kuti chilumbacho chimatchedwa Melita.
And when they had saved themselves, they then learned that the island was called Melita.
2 Anthu a pa chilumbacho anatichitira zokoma zimene sizichitika kawirikawiri. Iwo anakoleza moto natilandira tonse chifukwa kumagwa mvula ndipo kumazizira.
And the barbarians showed us no ordinary kindness; for they kindled a fire, and received us all, because of the rain which was falling, and because of the cold.
3 Paulo anatola mtolo wankhuni, pamene amayika pa moto, munatulukamo njoka chifukwa cha kutentha, ndipo inamuluma pa dzanja.
And when Paul had brought together a heap of brushwood, and laid it on the fire, a viper came out, by reason of the heat, and fastened itself on his hand.
4 Anthu a pa chilumbacho ataona njokayo ili lende pa dzanja lake, iwo anawuzana kuti, “Munthu uyu akuyenera kukhala munthu wopha anthu; pakuti ngakhale wapulumuka pa nyanja, chilungamo sichinamulore kuti akhale ndi moyo.”
And when the barbarians saw the reptile hanging from his hand, they said to one another: This man is certainly a murderer, whom, although he has saved himself from the sea, justice does not permit to live.
5 Koma Paulo anayikutumulira pa moto njokayo, ndipo sanamve kupweteka.
Then he shook the reptile from him into the fire, and suffered no harm.
6 Anthu anayembekezera kuti thupi lake litupa kapena agwa ndi kufa mwadzidzidzi, koma anadikira nthawi yayitali. Ataona kuti palibe kanthu kachilendo kanamuchitikira anasintha maganizo awo nanena kuti iye ndi mulungu.
But they were expecting that he would become inflamed and swollen, or would suddenly fall down dead; yet, after expecting it for a long time, and seeing no harm befall him, they changed their mind, and said he was a god.
7 Pafupi ndi malowa panali munda wa Popliyo, mkulu wa boma la pa chilumbacho. Iye anatilandira natisamala bwino masiku atatu.
Among the estates about that place were those of the chief man of the island, whose name was Publius, who took us to his house, and, for three days, entertained us kindly.
8 Abambo ake anali gone, chifukwa amadwala malungo ndi kamwazi. Paulo analowa mʼchipinda chake kukawaona, ndipo atapemphera, anasanjika manja ake pa iwo nawachiritsa.
And it happened that the father of Publius was lying sick with fever and dysentery. And Paul went in to him, and prayed, and laid his hands on him, and restored him to health.
9 Zitachitika zimenezi, anthu onse odwala a pa chilumbacho anabwera ndipo anachiritsidwa.
Therefore, after this had been clone, the rest also in the island who had diseases, came and were cured.
10 Anthuwo anatilemekeza ife mʼnjira zambiri ndipo pamene tinakonzeka kuti tiyambe ulendo, anatipatsa zonse zomwe tinazisowa.
And they also honored us with many honors; and, when we put to sea, they supplied us with such things as we needed.
11 Patapita miyezi itatu, tinanyamuka pa sitima ina imene inakhala pa chilumbacho chifukwa cha kuzizira. Inali sitima ya ku Alekisandriya imene inali ndi chizindikiro cha milungu ya mapasa yotchedwa Kastro ndi Polikisi.
After three months we put to sea in a ship of Alexandria, which had wintered in the island, whose sign was the Dioscuri.
12 Tinakafika ku Surakusa ndipo kumeneko tinakhalako masiku atatu.
And we landed at Syracuse, and remained there three days:
13 Kuchokera kumeneko tinayenda ndi kukafika ku Regio. Mmawa mwake mphepo yochokera kummwera inawomba, ndipo tsiku linalo tinakafika ku Potiyolo.
from which place, by coasting about, we came to Rhegium; and one day afterward, the south wind arose; and we came, on the next day, to Puteoli,
14 Kumeneko tinapezako abale amene anatiyitana kuti tikhale nawo sabata limodzi. Ndipo kenaka tinapita ku Roma.
where we found brethren, and were persuaded to remain with them seven days. And thus we went toward Home.
15 Abale kumeneko atamva kuti tikubwera, anabwera kudzakumana nafe mpaka ku bwalo la Apiyo ndiponso ku nyumba za alendo zitatu. Atawaona anthu amenewa Paulo anayamika Mulungu ndipo analimbikitsidwa.
And from this place, the brethren, having heard of us, came out as far as Appii Forum and the Three Taverns, to meet us. When Paul saw the brethren, he thanked God, and took courage.
16 Titafika ku Roma, Paulo analoledwa kukhala pa yekha ndi msilikali womulondera.
When we came to Rome, the centurion delivered the prisoners to the captain of the guard; but Paul was permitted to dwell by himself, with a soldier that guarded him.
17 Patapita masiku atatu, Paulo anasonkhanitsa pamodzi atsogoleri a Ayuda. Atasonkhana, Paulo anawawuza kuti, “Abale anga, ngakhale kuti ine sindinachite kanthu kalikonse kulakwira mtundu wathu kapena miyambo ya makolo athu, koma anandigwira mu Yerusalemu ndi kundipereka mʼmanja mwa Aroma.
And it came to pass, after three days, that he called together the chief men of the Jews; and when they had come, he said to them: Brethren, though I have done nothing against the people, or the customs of our fathers, yet I was delivered as a prisoner from Jerusalem into the hands of the Romans.
18 Iwo anandifufuza ndipo anafuna kundimasula chifukwa sanandipeze wopalamula mlandu woyenera kuphedwa.
They, after examination, would have released me, for they found no cause of death in me.
19 Koma Ayuda atakana, ine ndinakakamizidwa kupempha kuti ndikaonekere pamaso pa Kaisara, sikuti ndinali ndi kanthu konenezera mtundu wanga.
But because the Jews spoke against it, I was compelled to appeal to Cæsar: not that I have any accusation to bring against my own nation.
20 Pa chifukwa ichi ndapempha kuti ndionane nanu ndi kuyankhula nanu. Pakuti nʼchifukwa cha chiyembekezo cha Israeli ndamangidwa unyolo uwu.”
For this reason, I called for you, that I might see you and speak to you; for on account of the hope of Israel, I am bound with this chain.
21 Iwo anayankha kuti, “Ife sitinalandire kalata iliyonse yochokera ku Yudeya yonena za iwe, ndipo palibe mmodzi wa abale amene anachokera kumeneko anafotokoza kapena kunena kalikonse koyipa ka iwe.
And they said to him: We have neither received letters from Judea concerning you, nor has any one of the brethren come, and reported or spoken any evil of you.
22 Koma ife tikufuna kumva maganizo ako ndi otani, pakuti tikudziwa kuti ponseponse anthu akuyankhula zotsutsana ndi mpatuko umenewu.”
But we think it right to hear from you what you think: for, as it respects this sect, we know that it is everywhere spoken against.
23 Iwo anakonza tsiku lina loti akumane ndi Paulo, ndipo anabwera anthu ambiri ku nyumba kumene amakhala. Kuyambira mmawa mpaka madzulo, Paulo anawafotokozera ndi kuwawuza za ufumu wa Mulungu ndipo anayesa kuwakopa kuti akhulupirire Yesu kuchokera mʼMalamulo a Mose ndiponso mʼmabuku a Aneneri.
And when they had appointed him a day, many came to him at his lodging; to whom, from morning till evening; , he earnestly testified, and set forth the kingdom of God, persuading them concerning Jesus, both from the law of Moses, and from the prophets.
24 Ena anakopeka ndi zimene Paulo ananena, koma enanso sanakhulupirire.
And some believed the things that were spoken, and some believed not.
25 Ndipo anayamba kuchoka popeza sanagwirizane pakati pawo Paulo atanena mawu awa omaliza akuti, “Mzimu Woyera anayankhula zoona za makolo anu pamene Iye ananena kudzera mwa Mneneri Yesaya kuti,
And not agreeing among themselves, they departed, after Paul had spoken one word: Well did the Holy Spirit speak to our fathers by Isaiah the prophet,
26 “Pita kwa anthu awa ndi kuwawuza kuti, ‘Kumva mudzamva, koma osamvetsetsa; kupenya mudzapenya, koma osaona kanthu.’
saying: Go to this people and say, You shall surely hear, but you will not understand; and you shall surely see, but you will not perceive.
27 Pakuti mtima wa anthu ndi wokanika; mʼmakutu mwawo ndi mogontha, ndipo atsinzina kuti asaone kanthu. Mwina angapenye ndi maso awo, angamve ndi makutu awo, angamvetse ndi nzeru zawo ndi kutembenuka, Ineyo nʼkuwachiritsa.
For the heart of this people has become fat, and with their ears they hear heavily, and their eyes they have closed, lest they should see with their eyes, and hear with their ears, and understand with their heart, and should turn, and I should restore them to health.
28 “Chifukwa chake ine ndikufuna mudziwe kuti chipulumutso cha Mulungu chatumizidwa kwa anthu a mitundu ina, ndipo iwo adzamvera.”
Therefore, be it known to you, that the salvation of God is sent to the Gentiles, and they will hear.
29 Paulo atanena mawu amenewa, Ayuda aja anachoka akutsutsana kwambiri.
And when he had said these things, the Jews departed, and had great disputation among themselves.
30 Paulo anakhala kumeneko zaka ziwiri zathunthu mʼnyumba yobwereka yomwe amalipira ndipo ankalandira aliyense amene amabwera kudzamuona.
And Paul dwelt two whole years in his own rented house, and received all that came to him,
31 Molimba mtima ndi popanda womuletsa, Paulo analalikira za ufumu wa Mulungu ndi kuphunzitsa za Ambuye Yesu Khristu.
preaching the kingdom of God, and teaching the things concerning the Lord Jesus Christ, with all boldness and without hinderance.

< Machitidwe a Atumwi 28 >