< Machitidwe a Atumwi 28 >
1 Titapulumuka choncho, tinamva kuti chilumbacho chimatchedwa Melita.
Og da vi nu vare reddede, saa fik vi at vide, at Øen hed Malta.
2 Anthu a pa chilumbacho anatichitira zokoma zimene sizichitika kawirikawiri. Iwo anakoleza moto natilandira tonse chifukwa kumagwa mvula ndipo kumazizira.
Og Barbarerne viste os en usædvanlig Menneskekærlighed; thi de tændte et Baal og toge sig af os alle for den frembrydende Regns og Kuldens Skyld.
3 Paulo anatola mtolo wankhuni, pamene amayika pa moto, munatulukamo njoka chifukwa cha kutentha, ndipo inamuluma pa dzanja.
Men da Paulus samlede en Bunke Ris og lagde paa Baalet, krøb der en Øgle ud paa Grund af Varmen og hængte sig fast ved hans Haand.
4 Anthu a pa chilumbacho ataona njokayo ili lende pa dzanja lake, iwo anawuzana kuti, “Munthu uyu akuyenera kukhala munthu wopha anthu; pakuti ngakhale wapulumuka pa nyanja, chilungamo sichinamulore kuti akhale ndi moyo.”
Da nu Barbarerne saa Dyret hænge ved hans Haand, sagde de til hverandre: „Sikkert er denne Mand en Morder, hvem Gengældelsen ikke har tilstedt at leve, skønt han er reddet fra Havet.‟
5 Koma Paulo anayikutumulira pa moto njokayo, ndipo sanamve kupweteka.
Men han rystede Dyret af i Ilden, og der skete ham intet ondt.
6 Anthu anayembekezera kuti thupi lake litupa kapena agwa ndi kufa mwadzidzidzi, koma anadikira nthawi yayitali. Ataona kuti palibe kanthu kachilendo kanamuchitikira anasintha maganizo awo nanena kuti iye ndi mulungu.
Men de ventede, at han skulde hovne op eller pludseligt falde død om. Men da de havde ventet længe og saa, at der ikke skete ham noget usædvanligt, kom de paa andre Tanker og sagde, at han var en Gud.
7 Pafupi ndi malowa panali munda wa Popliyo, mkulu wa boma la pa chilumbacho. Iye anatilandira natisamala bwino masiku atatu.
Men i Omegnen af dette Sted havde Øens fornemste Mand, ved Navn Publius, nogle Landejendomme. Han tog imod os og laante os venligt Herberge i tre Dage.
8 Abambo ake anali gone, chifukwa amadwala malungo ndi kamwazi. Paulo analowa mʼchipinda chake kukawaona, ndipo atapemphera, anasanjika manja ake pa iwo nawachiritsa.
Men det traf sig, at Publius's Fader laa syg af Feber og Blodgang. Til ham gik Paulus ind og bad og lagde Hænderne paa ham og helbredte ham.
9 Zitachitika zimenezi, anthu onse odwala a pa chilumbacho anabwera ndipo anachiritsidwa.
Da dette var sket, kom ogsaa de andre paa Øen, som havde Sygdomme, til ham og bleve helbredede.
10 Anthuwo anatilemekeza ife mʼnjira zambiri ndipo pamene tinakonzeka kuti tiyambe ulendo, anatipatsa zonse zomwe tinazisowa.
De viste os ogsaa megen Ære, og da vi sejlede bort, bragte de om Bord i Skibet, hvad vi trængte til.
11 Patapita miyezi itatu, tinanyamuka pa sitima ina imene inakhala pa chilumbacho chifukwa cha kuzizira. Inali sitima ya ku Alekisandriya imene inali ndi chizindikiro cha milungu ya mapasa yotchedwa Kastro ndi Polikisi.
Men efter tre Maaneders Forløb sejlede vi da bort i et aleksandrinsk Skib, som havde haft Vinterleje ved Øen og førte Tvillingernes Mærke.
12 Tinakafika ku Surakusa ndipo kumeneko tinakhalako masiku atatu.
Og vi løb ind til Syrakus, hvor vi bleve tre Dage.
13 Kuchokera kumeneko tinayenda ndi kukafika ku Regio. Mmawa mwake mphepo yochokera kummwera inawomba, ndipo tsiku linalo tinakafika ku Potiyolo.
Derfra sejlede vi videre og kom til Regium, og efter en Dags Forløb fik vi Søndenvind og kom den næste Dag til Puteoli.
14 Kumeneko tinapezako abale amene anatiyitana kuti tikhale nawo sabata limodzi. Ndipo kenaka tinapita ku Roma.
Der fandt vi Brødre og bleve opfordrede til at blive hos dem i syv Dage. Og saa droge vi til Rom.
15 Abale kumeneko atamva kuti tikubwera, anabwera kudzakumana nafe mpaka ku bwalo la Apiyo ndiponso ku nyumba za alendo zitatu. Atawaona anthu amenewa Paulo anayamika Mulungu ndipo analimbikitsidwa.
Og Brødrene derfra, som havde hørt om os, kom os i Møde til Appius's Forum og Tres-Tabernæ. Og da Paulus saa dem, takkede han Gud og fattede Mod.
16 Titafika ku Roma, Paulo analoledwa kukhala pa yekha ndi msilikali womulondera.
Men da vi kom til Rom, [overgav Høvedsmanden Fangerne til Høvdingen for Livvagten. Dog] blev det tilstedt Paulus at bo for sig selv sammen med den Stridsmand, der bevogtede ham.
17 Patapita masiku atatu, Paulo anasonkhanitsa pamodzi atsogoleri a Ayuda. Atasonkhana, Paulo anawawuza kuti, “Abale anga, ngakhale kuti ine sindinachite kanthu kalikonse kulakwira mtundu wathu kapena miyambo ya makolo athu, koma anandigwira mu Yerusalemu ndi kundipereka mʼmanja mwa Aroma.
Men efter tre Dages Forløb skete det, at han sammenkaldte de fornemste iblandt Jøderne. Men da de vare forsamlede, sagde han til dem: „I Mænd, Brødre! uagtet jeg intet har gjort imod vort Folk eller de fædrene Skikke, er jeg fra Jerusalem overgiven som Fange i Romernes Hænder,
18 Iwo anandifufuza ndipo anafuna kundimasula chifukwa sanandipeze wopalamula mlandu woyenera kuphedwa.
og disse vilde efter at have forhørt mig løslade mig, efterdi der ikke var nogen Dødsskyld hos mig.
19 Koma Ayuda atakana, ine ndinakakamizidwa kupempha kuti ndikaonekere pamaso pa Kaisara, sikuti ndinali ndi kanthu konenezera mtundu wanga.
Men da Jøderne gjorde Indsigelse, nødtes jeg til at skyde mig ind under Kejseren, dog ikke, som om jeg havde noget at anklage mit Folk for.
20 Pa chifukwa ichi ndapempha kuti ndionane nanu ndi kuyankhula nanu. Pakuti nʼchifukwa cha chiyembekezo cha Israeli ndamangidwa unyolo uwu.”
Af denne Aarsag har jeg altsaa ladet eder kalde hid for at se og tale med eder; thi for Israels Haabs Skyld er jeg sluttet i denne Lænke.‟
21 Iwo anayankha kuti, “Ife sitinalandire kalata iliyonse yochokera ku Yudeya yonena za iwe, ndipo palibe mmodzi wa abale amene anachokera kumeneko anafotokoza kapena kunena kalikonse koyipa ka iwe.
Men de sagde til ham: „Hverken have vi faaet Brev fra Judæa om dig, ikke heller er nogen af Brødrene kommen og har meddelt eller sagt noget ondt om dig.
22 Koma ife tikufuna kumva maganizo ako ndi otani, pakuti tikudziwa kuti ponseponse anthu akuyankhula zotsutsana ndi mpatuko umenewu.”
Men vi ønske at høre af dig, hvad du tænker; thi om dette Parti er det os bekendt, at det alle Vegne finder Modsigelse.‟
23 Iwo anakonza tsiku lina loti akumane ndi Paulo, ndipo anabwera anthu ambiri ku nyumba kumene amakhala. Kuyambira mmawa mpaka madzulo, Paulo anawafotokozera ndi kuwawuza za ufumu wa Mulungu ndipo anayesa kuwakopa kuti akhulupirire Yesu kuchokera mʼMalamulo a Mose ndiponso mʼmabuku a Aneneri.
Efter saa at have aftalt en Dag med ham, kom de til ham i Herberget i større Tal, og for dem forklarede han og vidnede om Guds Rige og søgte at overbevise dem om Jesus, baade ud af Mose Lov og af Profeterne, fra aarle om Morgenen indtil Aften.
24 Ena anakopeka ndi zimene Paulo ananena, koma enanso sanakhulupirire.
Og nogle lode sig overbevise af det, som blev sagt, men andre troede ikke.
25 Ndipo anayamba kuchoka popeza sanagwirizane pakati pawo Paulo atanena mawu awa omaliza akuti, “Mzimu Woyera anayankhula zoona za makolo anu pamene Iye ananena kudzera mwa Mneneri Yesaya kuti,
Og under indbyrdes Uenighed gik de bort, da Paulus havde sagt dette ene Ord: „Rettelig har den Helligaand talt ved Profeten Esajas til eders Fædre og sagt:
26 “Pita kwa anthu awa ndi kuwawuza kuti, ‘Kumva mudzamva, koma osamvetsetsa; kupenya mudzapenya, koma osaona kanthu.’
„Gaa hen til dette Folk og sig: I skulle høre med eders Øren og ikke forstaa og se med eders Øjne og ikke se;
27 Pakuti mtima wa anthu ndi wokanika; mʼmakutu mwawo ndi mogontha, ndipo atsinzina kuti asaone kanthu. Mwina angapenye ndi maso awo, angamve ndi makutu awo, angamvetse ndi nzeru zawo ndi kutembenuka, Ineyo nʼkuwachiritsa.
thi dette Folks Hjerte er blevet sløvet, og med Ørene høre de tungt, og deres Øjne have de tillukket, for at de ikke skulle se med Øjnene og høre med Ørene og forstaa med Hjertet og omvende sig, saa jeg kunde helbrede dem.‟
28 “Chifukwa chake ine ndikufuna mudziwe kuti chipulumutso cha Mulungu chatumizidwa kwa anthu a mitundu ina, ndipo iwo adzamvera.”
Derfor være det eder vitterligt, at denne Guds Frelse er sendt til Hedningerne; de skulle ogsaa høre.‟
29 Paulo atanena mawu amenewa, Ayuda aja anachoka akutsutsana kwambiri.
[Og da han havde sagt dette, gik Jøderne bort, og der var stor Trætte imellem dem indbyrdes.]
30 Paulo anakhala kumeneko zaka ziwiri zathunthu mʼnyumba yobwereka yomwe amalipira ndipo ankalandira aliyense amene amabwera kudzamuona.
Men han blev hele to Aar i sit lejede Herberge og modtog alle, som kom til ham,
31 Molimba mtima ndi popanda womuletsa, Paulo analalikira za ufumu wa Mulungu ndi kuphunzitsa za Ambuye Yesu Khristu.
idet han prædikede Guds Rige og lærte om den Herre Jesus med al Frimodighed, uhindret.