< Machitidwe a Atumwi 28 >

1 Titapulumuka choncho, tinamva kuti chilumbacho chimatchedwa Melita.
ܘܡܢ ܒܬܪܟܢ ܝܠܦܢ ܕܡܠܝܛܐ ܡܬܩܪܝܐ ܗܝ ܓܙܪܬܐ
2 Anthu a pa chilumbacho anatichitira zokoma zimene sizichitika kawirikawiri. Iwo anakoleza moto natilandira tonse chifukwa kumagwa mvula ndipo kumazizira.
ܘܒܪܒܪܝܐ ܕܥܡܪܝܢ ܗܘܘ ܒܗ ܪܚܡܐ ܤܓܝܐܐ ܚܘܝܘ ܠܘܬܢ ܘܐܘܚܕܘ ܢܘܪܐ ܘܩܪܐܘܢ ܠܟܠܢ ܕܢܫܚܢ ܡܛܠ ܡܛܪܐ ܤܓܝܐܐ ܘܩܘܪܫܐ ܕܐܝܬ ܗܘܐ
3 Paulo anatola mtolo wankhuni, pamene amayika pa moto, munatulukamo njoka chifukwa cha kutentha, ndipo inamuluma pa dzanja.
ܘܦܘܠܘܤ ܫܩܠ ܤܘܓܐܐ ܕܚܒܘܒܐ ܘܤܡ ܥܠ ܢܘܪܐ ܘܢܦܩܬ ܡܢܗܘܢ ܐܟܕܢܐ ܡܢ ܪܬܚܐ ܕܢܘܪܐ ܘܢܟܬܬ ܒܐܝܕܗ
4 Anthu a pa chilumbacho ataona njokayo ili lende pa dzanja lake, iwo anawuzana kuti, “Munthu uyu akuyenera kukhala munthu wopha anthu; pakuti ngakhale wapulumuka pa nyanja, chilungamo sichinamulore kuti akhale ndi moyo.”
ܘܟܕ ܚܙܐܘܗ ܒܪܒܪܝܐ ܕܬܠܝܐ ܒܐܝܕܗ ܐܡܪܝܢ ܗܘܘ ܟܒܪ ܗܢܐ ܓܒܪܐ ܩܛܘܠܐ ܗܘ ܕܟܕ ܐܫܬܘܙܒ ܡܢ ܝܡܐ ܟܐܢܘܬܐ ܠܐ ܫܒܩܬܗ ܕܢܚܐ
5 Koma Paulo anayikutumulira pa moto njokayo, ndipo sanamve kupweteka.
ܗܘ ܕܝܢ ܦܘܠܘܤ ܐܢܝܦ ܐܝܕܗ ܘܫܕܗ ܠܐܟܕܢܐ ܒܢܘܪܐ ܘܡܕܡ ܕܤܢܐ ܠܐ ܗܘܝܗܝ
6 Anthu anayembekezera kuti thupi lake litupa kapena agwa ndi kufa mwadzidzidzi, koma anadikira nthawi yayitali. Ataona kuti palibe kanthu kachilendo kanamuchitikira anasintha maganizo awo nanena kuti iye ndi mulungu.
ܤܒܪܝܢ ܗܘܘ ܕܝܢ ܒܪܒܪܝܐ ܕܒܪ ܫܥܬܗ ܡܬܡܤܐ ܘܢܦܠ ܟܕ ܡܝܬ ܥܠ ܐܪܥܐ ܘܟܕ ܥܕܢܐ ܤܓܝܐܐ ܤܟܝܘ ܘܚܙܘ ܕܡܕܡ ܕܤܢܐ ܠܐ ܗܘܝܗܝ ܫܚܠܦܘ ܡܠܝܗܘܢ ܘܐܡܪܘ ܕܐܠܗܐ ܗܘ
7 Pafupi ndi malowa panali munda wa Popliyo, mkulu wa boma la pa chilumbacho. Iye anatilandira natisamala bwino masiku atatu.
ܐܝܬ ܗܘܐ ܕܝܢ ܩܘܪܝܐ ܒܗ ܒܗܘ ܐܬܪܐ ܠܓܒܪܐ ܚܕ ܕܫܡܗ ܗܘܐ ܦܘܦܠܝܘܤ ܕܗܘ ܗܘܐ ܪܫܗ ܕܓܙܪܬܐ ܘܩܒܠܢ ܒܒܝܬܗ ܬܠܬܐ ܝܘܡܝܢ ܚܕܝܐܝܬ
8 Abambo ake anali gone, chifukwa amadwala malungo ndi kamwazi. Paulo analowa mʼchipinda chake kukawaona, ndipo atapemphera, anasanjika manja ake pa iwo nawachiritsa.
ܐܒܘܗܝ ܕܝܢ ܕܦܘܦܠܝܘܤ ܒܐܫܬܐ ܘܒܟܐܒ ܡܥܝܐ ܟܪܝܗ ܗܘܐ ܘܥܠ ܠܘܬܗ ܦܘܠܘܤ ܘܨܠܝ ܘܤܡ ܥܠܘܗܝ ܐܝܕܗ ܘܐܚܠܡܗ
9 Zitachitika zimenezi, anthu onse odwala a pa chilumbacho anabwera ndipo anachiritsidwa.
ܘܟܕ ܗܘܬ ܗܕܐ ܐܦ ܫܪܟܐ ܐܝܠܝܢ ܕܐܝܬ ܗܘܘ ܒܗ ܒܓܙܪܬܐ ܟܪܝܗܐ ܩܪܒܝܢ ܗܘܘ ܠܘܬܗ ܘܡܬܐܤܝܢ ܗܘܘ
10 Anthuwo anatilemekeza ife mʼnjira zambiri ndipo pamene tinakonzeka kuti tiyambe ulendo, anatipatsa zonse zomwe tinazisowa.
ܘܐܝܩܪܐ ܪܘܪܒܐ ܝܩܪܘܢ ܘܟܕ ܢܦܩܝܢ ܗܘܝܢ ܡܢ ܬܡܢ ܙܘܕܘܢ
11 Patapita miyezi itatu, tinanyamuka pa sitima ina imene inakhala pa chilumbacho chifukwa cha kuzizira. Inali sitima ya ku Alekisandriya imene inali ndi chizindikiro cha milungu ya mapasa yotchedwa Kastro ndi Polikisi.
ܢܦܩܢ ܕܝܢ ܒܬܪ ܝܪܚܐ ܬܠܬܐ ܘܪܕܝܢ ܒܐܠܦܐ ܐܠܟܤܢܕܪܝܬܐ ܕܐܤܬܝܬ ܗܘܬ ܒܗ ܒܓܙܪܬܐ ܘܐܝܬ ܗܘܬ ܥܠܝܗ ܐܬܐ ܕܬܐܡܐ
12 Tinakafika ku Surakusa ndipo kumeneko tinakhalako masiku atatu.
ܘܐܬܝܢ ܠܤܪܩܘܤܐ ܡܕܝܢܬܐ ܘܩܘܝܢ ܬܡܢ ܝܘܡܬܐ ܬܠܬܐ
13 Kuchokera kumeneko tinayenda ndi kukafika ku Regio. Mmawa mwake mphepo yochokera kummwera inawomba, ndipo tsiku linalo tinakafika ku Potiyolo.
ܘܡܢ ܬܡܢ ܐܬܟܪܟܢ ܘܡܢܥܢ ܠܪܓܝܘܢ ܡܕܝܢܬܐ ܘܒܬܪ ܝܘܡܐ ܚܕ ܢܫܒܬ ܠܢ ܪܘܚܐ ܕܬܝܡܢܐ ܘܠܬܪܝܢ ܝܘܡܝܢ ܐܬܝܢ ܠܦܘܛܝܐܠܤ ܡܕܝܢܬܐ ܕܐܝܛܠܝܐ
14 Kumeneko tinapezako abale amene anatiyitana kuti tikhale nawo sabata limodzi. Ndipo kenaka tinapita ku Roma.
ܘܐܫܟܚܢ ܬܡܢ ܐܚܐ ܘܒܥܘ ܡܢܢ ܘܗܘܝܢ ܠܘܬܗܘܢ ܝܘܡܬܐ ܫܒܥܐ ܘܗܝܕܝܢ ܐܙܠܢ ܠܪܗܘܡܐ
15 Abale kumeneko atamva kuti tikubwera, anabwera kudzakumana nafe mpaka ku bwalo la Apiyo ndiponso ku nyumba za alendo zitatu. Atawaona anthu amenewa Paulo anayamika Mulungu ndipo analimbikitsidwa.
ܘܟܕ ܫܡܥܘ ܐܚܐ ܕܬܡܢ ܢܦܩܘ ܠܐܘܪܥܢ ܥܕܡܐ ܠܫܘܩܐ ܕܡܬܩܪܐ ܐܦܝܘܤ ܦܘܪܘܤ ܘܥܕܡܐ ܠܬܠܬ ܚܢܘܢ ܘܟܕ ܚܙܐ ܐܢܘܢ ܦܘܠܘܤ ܐܘܕܝ ܠܐܠܗܐ ܘܐܬܚܝܠ
16 Titafika ku Roma, Paulo analoledwa kukhala pa yekha ndi msilikali womulondera.
ܘܥܠܢ ܠܪܗܘܡܐ ܘܐܦܤ ܩܢܛܪܘܢܐ ܠܦܘܠܘܤ ܕܢܫܪܐ ܐܝܟܐ ܕܨܒܐ ܥܡ ܐܤܛܪܛܝܘܛܐ ܗܘ ܕܢܛܪ ܗܘܐ ܠܗ
17 Patapita masiku atatu, Paulo anasonkhanitsa pamodzi atsogoleri a Ayuda. Atasonkhana, Paulo anawawuza kuti, “Abale anga, ngakhale kuti ine sindinachite kanthu kalikonse kulakwira mtundu wathu kapena miyambo ya makolo athu, koma anandigwira mu Yerusalemu ndi kundipereka mʼmanja mwa Aroma.
ܘܡܢ ܒܬܪ ܬܠܬܐ ܝܘܡܝܢ ܫܕܪ ܦܘܠܘܤ ܩܪܐ ܠܪܫܢܝܗܘܢ ܕܝܗܘܕܝܐ ܘܟܕ ܐܬܟܢܫܘ ܐܡܪ ܠܗܘܢ ܓܒܪܐ ܐܚܝ ܐܢܐ ܟܕ ܒܡܕܡ ܠܐ ܩܡܬ ܠܘܩܒܠ ܥܡܐ ܘܢܡܘܤܐ ܕܐܒܗܝ ܒܐܤܘܪܐ ܐܫܬܠܡܬ ܡܢ ܐܘܪܫܠܡ ܒܐܝܕܐ ܕܪܗܘܡܝܐ
18 Iwo anandifufuza ndipo anafuna kundimasula chifukwa sanandipeze wopalamula mlandu woyenera kuphedwa.
ܘܗܢܘܢ ܟܕ ܫܐܠܘܢܝ ܨܒܘ ܕܢܫܪܘܢܢܝ ܡܛܠ ܕܠܐ ܐܫܟܚܘ ܒܬܪܝ ܪܫܝܢܐ ܡܕܡ ܕܫܘܐ ܠܡܘܬܐ
19 Koma Ayuda atakana, ine ndinakakamizidwa kupempha kuti ndikaonekere pamaso pa Kaisara, sikuti ndinali ndi kanthu konenezera mtundu wanga.
ܘܟܕ ܩܝܡܝܢ ܗܘܘ ܠܘܩܒܠܝ ܝܗܘܕܝܐ ܐܬܐܠܨܬ ܕܐܩܥܐ ܒܓܢ ܩܤܪ ܠܐ ܐܝܟ ܐܝܬ ܠܝ ܕܐܩܛܪܓ ܒܡܕܡ ܠܒܢܝ ܥܡܝ
20 Pa chifukwa ichi ndapempha kuti ndionane nanu ndi kuyankhula nanu. Pakuti nʼchifukwa cha chiyembekezo cha Israeli ndamangidwa unyolo uwu.”
ܡܛܠ ܗܢܐ ܒܥܝܬ ܡܢܟܘܢ ܕܬܐܬܘܢ ܘܐܚܙܝܟܘܢ ܘܐܫܬܥܐ ܠܟܘܢ ܗܠܝܢ ܡܛܠ ܤܒܪܐ ܓܝܪ ܕܐܝܤܪܝܠ ܐܤܝܪ ܐܢܐ ܒܫܫܠܬܐ ܗܕܐ
21 Iwo anayankha kuti, “Ife sitinalandire kalata iliyonse yochokera ku Yudeya yonena za iwe, ndipo palibe mmodzi wa abale amene anachokera kumeneko anafotokoza kapena kunena kalikonse koyipa ka iwe.
ܐܡܪܝܢ ܠܗ ܗܢܘܢ ܚܢܢ ܐܓܪܬܐ ܥܠܝܟ ܠܐ ܩܒܠܢ ܡܢ ܝܗܘܕ ܘܠܐ ܐܢܫ ܡܢ ܐܚܐ ܕܐܬܘ ܡܢ ܐܘܪܫܠܡ ܐܡܪܘ ܠܢ ܡܕܡ ܕܒܝܫ ܥܠܝܟ
22 Koma ife tikufuna kumva maganizo ako ndi otani, pakuti tikudziwa kuti ponseponse anthu akuyankhula zotsutsana ndi mpatuko umenewu.”
ܨܒܝܢܢ ܕܝܢ ܕܢܫܡܥ ܡܢܟ ܡܕܡ ܕܡܬܪܥܐ ܐܢܬ ܡܛܠ ܕܝܘܠܦܢܐ ܗܢܐ ܝܕܥܝܢܢ ܕܥܠ ܐܢܫ ܠܐ ܡܩܒܠ
23 Iwo anakonza tsiku lina loti akumane ndi Paulo, ndipo anabwera anthu ambiri ku nyumba kumene amakhala. Kuyambira mmawa mpaka madzulo, Paulo anawafotokozera ndi kuwawuza za ufumu wa Mulungu ndipo anayesa kuwakopa kuti akhulupirire Yesu kuchokera mʼMalamulo a Mose ndiponso mʼmabuku a Aneneri.
ܘܐܩܝܡܘ ܠܗ ܝܘܡܐ ܘܟܢܫܘ ܘܐܬܘ ܠܘܬܗ ܤܓܝܐܐ ܟܪ ܕܫܪܐ ܗܘܐ ܘܓܠܐ ܠܗܘܢ ܥܠ ܡܠܟܘܬܐ ܕܐܠܗܐ ܟܕ ܡܤܗܕ ܘܡܦܝܤ ܠܗܘܢ ܥܠ ܝܫܘܥ ܡܢ ܢܡܘܤܐ ܕܡܘܫܐ ܘܡܢ ܢܒܝܐ ܡܢ ܨܦܪܐ ܘܥܕܡܐ ܠܪܡܫܐ
24 Ena anakopeka ndi zimene Paulo ananena, koma enanso sanakhulupirire.
ܘܐܢܫܝܢ ܡܢܗܘܢ ܡܬܛܦܝܤܝܢ ܗܘܘ ܠܡܠܘܗܝ ܘܐܚܪܢܐ ܠܐ ܡܬܛܦܝܤܝܢ ܗܘܘ
25 Ndipo anayamba kuchoka popeza sanagwirizane pakati pawo Paulo atanena mawu awa omaliza akuti, “Mzimu Woyera anayankhula zoona za makolo anu pamene Iye ananena kudzera mwa Mneneri Yesaya kuti,
ܘܐܫܬܪܝܘ ܡܢ ܠܘܬܗ ܟܕ ܠܐ ܫܠܡܝܢ ܠܚܕܕܐ ܘܐܡܪ ܠܗܘܢ ܗܘ ܦܘܠܘܤ ܡܠܬܐ ܗܕܐ ܫܦܝܪ ܡܠܠ ܪܘܚܐ ܕܩܘܕܫܐ ܒܦܘܡ ܐܫܥܝܐ ܢܒܝܐ ܠܘܩܒܠ ܐܒܗܬܟܘܢ
26 “Pita kwa anthu awa ndi kuwawuza kuti, ‘Kumva mudzamva, koma osamvetsetsa; kupenya mudzapenya, koma osaona kanthu.’
ܟܕ ܐܡܪ ܕܙܠ ܠܘܬ ܥܡܐ ܗܢܐ ܘܐܡܪ ܠܗܘܢ ܕܫܡܥܐ ܬܫܡܥܘܢ ܘܠܐ ܬܤܬܟܠܘܢ ܘܬܚܙܘܢ ܘܠܐ ܬܒܚܪܘܢ
27 Pakuti mtima wa anthu ndi wokanika; mʼmakutu mwawo ndi mogontha, ndipo atsinzina kuti asaone kanthu. Mwina angapenye ndi maso awo, angamve ndi makutu awo, angamvetse ndi nzeru zawo ndi kutembenuka, Ineyo nʼkuwachiritsa.
ܐܬܥܒܝ ܠܗ ܓܝܪ ܠܒܗ ܕܥܡܐ ܗܢܐ ܘܡܫܡܥܬܗܘܢ ܐܘܩܪܘ ܘܥܝܢܝܗܘܢ ܥܡܨܘ ܕܠܐ ܢܚܙܘܢ ܒܥܝܢܝܗܘܢ ܘܢܫܡܥܘܢ ܒܐܕܢܝܗܘܢ ܘܢܤܬܟܠܘܢ ܒܠܒܗܘܢ ܘܢܬܘܒܘܢ ܠܘܬܝ ܘܐܫܒܘܩ ܠܗܘܢ
28 “Chifukwa chake ine ndikufuna mudziwe kuti chipulumutso cha Mulungu chatumizidwa kwa anthu a mitundu ina, ndipo iwo adzamvera.”
ܬܬܝܕܥ ܠܟܘܢ ܗܟܝܠ ܗܕܐ ܕܠܥܡܡܐ ܗܘ ܐܫܬܕܪ ܗܢܐ ܦܘܪܩܢܐ ܕܐܠܗܐ ܗܢܘܢ ܓܝܪ ܐܦ ܫܡܥܝܢ ܠܗ
29 Paulo atanena mawu amenewa, Ayuda aja anachoka akutsutsana kwambiri.
ܘܟܕ ܗܠܝܢ ܐܡܪ ܢܦܩܘ ܝܗܘܕܝܐ ܘܤܓܝ ܕܪܫܝܢ ܗܘܘ ܒܝܢܬܗܘܢ
30 Paulo anakhala kumeneko zaka ziwiri zathunthu mʼnyumba yobwereka yomwe amalipira ndipo ankalandira aliyense amene amabwera kudzamuona.
ܘܐܓܪ ܠܗ ܦܘܠܘܤ ܡܢ ܕܝܠܗ ܒܝܬܐ ܘܗܘܐ ܒܗ ܬܪܬܝܢ ܫܢܝܢ ܘܡܩܒܠ ܗܘܐ ܬܡܢ ܠܟܠܗܘܢ ܐܝܠܝܢ ܕܐܬܝܢ ܗܘܘ ܠܘܬܗ
31 Molimba mtima ndi popanda womuletsa, Paulo analalikira za ufumu wa Mulungu ndi kuphunzitsa za Ambuye Yesu Khristu.
ܘܡܟܪܙ ܗܘܐ ܥܠ ܡܠܟܘܬܗ ܕܐܠܗܐ ܘܡܠܦ ܗܘܐ ܥܝܢ ܒܓܠܐ ܥܠ ܡܪܢ ܝܫܘܥ ܡܫܝܚܐ ܕܠܐ ܟܠܝܢ

< Machitidwe a Atumwi 28 >