< Machitidwe a Atumwi 26 >

1 Ndipo Agripa anawuza Paulo kuti, “Takulola kuti unene mawu ako.” Paulo anatambasula dzanja lake nayamba kudziteteza kuti,
Agrippa dit à Paul: « Tu peux parler en ton nom. » Alors Paul étendit la main, et prit sa défense.
2 “Mfumu Agripa ine ndikudziyesa wa mwayi kuyima pamaso panu lero lino ndi kudziteteza, kutsutsa zonse zimene Ayuda andinenera,
« Je m'estime heureux, roi Agrippa, d'avoir à me défendre aujourd'hui devant toi sur toutes les choses dont je suis accusé par les Juifs,
3 ndipo makamaka chifukwa inu mukudziwa bwino miyambo yonse ya Chiyuda ndiponso zonse zimene amatsutsana. Nʼchifukwa chake ndikukupemphani kuti mundimvetsere moleza mtima.
d'autant plus que tu es expert dans toutes les coutumes et dans toutes les questions qui se posent chez les Juifs. Je te prie donc de m'écouter avec patience.
4 “Ayuda onse akudziwa za moyo wanga mmene ndakhalira kuyambira ndili mwana, kuchokera pachiyambi cha moyo wanga mʼdziko lathu ndiponso mu Yerusalemu.
« En effet, tous les Juifs connaissent ma manière de vivre depuis ma jeunesse, qui a été dès le début parmi ma propre nation et à Jérusalem;
5 Iwo akundidziwa kuyambira kalekale ndipo angathe kuchitira umboni kuti ndakhala ndili Mfarisi moyo wanga wonse, mmodzi wa gulu limene limasamala chipembedzo chathu koposa.
m'ayant connu dès le début, s'ils veulent bien en témoigner, que selon la secte la plus stricte de notre religion j'ai vécu en pharisien.
6 Ndipo tsopano ndikuyimbidwa mlandu lero chifukwa cha chiyembekezo changa pa zimene Mulungu analonjeza makolo athu.
Maintenant, je me tiens ici pour être jugé à cause de l'espérance de la promesse faite par Dieu à nos pères,
7 Ili ndi lonjezo limene mafuko athu khumi ndi awiri akuyembekezera kuti likwaniritsidwe pamene akupembedza Mulungu molimbika usana ndi usiku. Wolemekezeka Mfumu, nʼchifukwa cha chiyembekezo chimenechi Ayuda kuti akundiyimba mlandu.
que nos douze tribus, servant avec ardeur nuit et jour, espèrent atteindre. C'est au sujet de cette espérance que je suis accusé par les Juifs, roi Agrippa!
8 Nʼchifukwa chiyani ena a inu mukuganiza kuti nʼkosatheka kuti Mulungu aukitse akufa?
Pourquoi jugez-vous incroyable que Dieu ressuscite les morts?
9 “Inenso ndimaganiza kuti ndimayenera kuchita zinthu zambiri pofuna kuthana ndi dzina la Yesu wa ku Nazareti.
« Moi-même, j'ai très certainement pensé que je devais faire beaucoup de choses contraires au nom de Jésus de Nazareth.
10 Ndipo izi ndi zimene ndinazichita ku Yerusalemu. Ndi ulamuliro wa akulu a ansembe, ine ndinayika mʼndende oyera mtima ambiri, ndipo pamene amaphedwa, ine ndimavomereza.
C'est aussi ce que j'ai fait à Jérusalem. J'ai fait enfermer dans des prisons un grand nombre de saints, ayant reçu l'autorité des principaux sacrificateurs; et quand on les mettait à mort, je votais contre eux.
11 Nthawi zambiri ndinkapita mʼsunagoge iliyonse kuti alangidwe, ndipo ndinayesera kuwakakamiza kuti achitire chipongwe Mulungu. Mu mkwiyo wangawo, ndimapita ngakhale ku mizinda yachilendo kuti ndikawazunze.
Les punissant souvent dans toutes les synagogues, je m'efforçais de les faire blasphémer. Étant extrêmement furieux contre eux, je les persécutais jusque dans les villes étrangères.
12 “Pa ulendo wina wotere, ndikupita ku Damasiko ndi mphamvu ndi ulamuliro ochokera kwa akulu a ansembe,
« Alors que je me rendais à Damas avec l'autorisation et la mission des chefs des prêtres,
13 Wolemekezeka Mfumu, nthawi ya masana pamene ndimayenda pa msewu, ndinaona kuwala kuchokera kumwamba koposa kuwala kwa dzuwa kutandizungulira ine pamodzi ndi anzangawo.
à midi, ô roi, je vis en chemin une lumière venant du ciel, plus brillante que le soleil, qui m'entourait ainsi que ceux qui voyageaient avec moi.
14 Tonse tinagwa pansi ndipo ndinamva mawu mʼChihebri akuti, ‘Saulo, Saulo chifukwa chiyani ukundizunza Ine? Nʼkovuta kulimbikira mtunda wopanda madzi.’”
Lorsque nous fûmes tous tombés à terre, j'entendis une voix qui me disait en hébreu: « Saul, Saul, pourquoi me persécutes-tu? Il t'est difficile de frapper contre les aiguillons ».
15 Ndipo ine ndinafunsa kuti, “Ndinu ndani Ambuye?” Ambuye anayankha kuti, “Ndine Yesu, amene iwe ukumuzunza.
« J'ai dit: « Qui es-tu, Seigneur? Il dit: « Je suis Jésus, que vous persécutez.
16 Tsopano dzuka ndipo imirira. Ine ndaonekera kwa iwe kuti ndikusankhe kuti ukhale mtumiki ndiponso mboni ya zimene waziona za Ine ndiponso zimene ndidzakuonetsa.
Mais lève-toi et tiens-toi sur tes pieds, car c'est dans ce but que je te suis apparu, pour t'établir serviteur et témoin des choses que tu as vues et de celles que je te révélerai,
17 Ine ndidzakulanditsa mʼmanja mwa anthu a mtundu wako ndiponso mwa anthu a mitundu ina. Ine ndikukutuma kwa iwo,
pour te délivrer du peuple et des païens vers lesquels je t'envoie,
18 kuti ukatsekule maso awo kuti atembenuke mtima kuchoka ku mdima ndi kulowa mʼkuwala, kuchoka ku mphamvu za Satana ndi kupita kwa Mulungu, kuti alandire chikhululukiro cha machimo awo ndi kukhala mʼgulu la amene akuyeretsedwa chifukwa chokhulupirira Ine.
pour leur ouvrir les yeux, afin qu'ils passent des ténèbres à la lumière et de la puissance de Satan à Dieu, pour qu'ils reçoivent la rémission des péchés et un héritage parmi ceux qui sont sanctifiés par la foi en moi.
19 “Nʼchifukwa chake Mfumu Agripa, sindinakane kumvera masomphenya wochokera kumwamba.
« C'est pourquoi, roi Agrippa, je n'ai pas désobéi à la vision céleste,
20 Kuyambira kwa anthu a ku Damasiko, a ku Yerusalemu, a ku Yudeya konse ndi kwa anthu a mitundu inanso, ndinalalikira kuti akuyenera kulapa ndi kutembenukira kwa Mulungu ndikuti aonetse kulapa kwawo mwa ntchito zawo.
mais j'ai annoncé d'abord à ceux de Damas, à Jérusalem, dans tout le pays de Judée, et aussi aux païens, qu'ils devaient se repentir et se tourner vers Dieu, en faisant des œuvres dignes de la repentance.
21 Ichi nʼchifukwa chake Ayuda anandigwira mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu nafuna kundipha.
C'est pourquoi les Juifs se sont emparés de moi dans le temple et ont voulu me faire mourir.
22 Koma Mulungu wakhala akundithandiza mpaka lero lino. Ine ndayima pano kuti ndichitire umboni kwa anthu onse otchuka ndi anthu wamba. Ine sindikunena zina zowonjezera koma zimene Aneneri ndi Mose ananena kuti zidzachitika.
Ayant donc obtenu le secours qui vient de Dieu, je me tiens jusqu'à ce jour pour rendre témoignage aux petits et aux grands, ne disant rien d'autre que ce que les prophètes et Moïse ont annoncé,
23 Iwo ananena kuti Khristu adzamva zowawa ndipo popeza Iye adzakhala woyamba kuuka kwa akufa, adzalalikira za kuwunika kwa anthu a mtundu wake ndiponso kwa anthu a mitundu ina.”
comment le Christ doit souffrir et comment, par la résurrection des morts, il sera le premier à annoncer la lumière à ce peuple et aux païens. »
24 Paulo akudziteteza, Festo anakweza mawu nati, “Wazungulira mutu Paulo! Kuphunzira kwako kwakuchititsa misala.”
Comme il prenait ainsi sa défense, Festus dit d'une voix forte: « Paul, tu es fou! Ton grand savoir te rend fou! »
25 Paulo anayankha nati, “Wolemekezeka Festo, sindine wozungulira mutu. Zimene ndikunena ndi zoona ndiponso za nzeru.
Mais il répondit: « Je ne suis pas fou, très excellent Festus, mais je dis hardiment des paroles de vérité et de raison.
26 Mfumu ikuzidziwa bwino zinthu izi, ndipo ndikuyankhula momasuka kwa iyo. Ine ndikukhulupirira kuti palibe kanthu nʼkamodzi komwe kamene sukukadziwa, chifukwa izi sizinachike mseri.
Car le roi est au courant de ces choses, et c'est à lui aussi que je parle librement. Car je suis persuadé qu'aucune de ces choses ne lui est cachée, puisque cela ne s'est pas fait dans un coin.
27 Mfumu Agripa, kodi mumakhulupirira mawu a aneneri? Ine ndikudziwa kuti mumakhulupirira.”
Roi Agrippa, crois-tu les prophètes? Je sais que tu crois. »
28 Kenaka Agripa anati kwa Paulo, “Kodi ukuganiza kuti mʼkanthawi kochepa kotere ungandikope kuti ndikhale Mkhristu?”
Agrippa dit à Paul: « Avec un peu de persuasion, essaies-tu de faire de moi un chrétien? »
29 Paulo anayankha kuti, “Ngakhale kanthawi kochepa kapena nthawi yayitali, ine ndikupempha kwa Mulungu kuti osati inu nokha koma aliyense amene akundimva lero lino akhale monga ine, kupatulapo maunyolo okhawa.”
Paul dit: « Je prie Dieu, afin que, soit avec peu, soit avec beaucoup, non seulement vous, mais aussi tous ceux qui m'écoutent aujourd'hui, deviennent tels que je suis, à l'exception de ces liens. »
30 Mfumu inayimirira pamodzi ndi bwanamkubwa ndi Bernisi ndiponso anthu onse amene anakhala nawo pamodzi.
Le roi se leva avec le gouverneur et Bérénice, et ceux qui étaient assis avec eux.
31 Inatuluka mʼchipindamo, ndipo pamene imayankhula inati, “Munthu uyu sanachite kanthu koyenera kuphedwa kapena kumangidwa.”
Quand ils se furent retirés, ils se parlèrent entre eux, disant: « Cet homme ne fait rien qui mérite la mort ou la prison. »
32 Agripa anati kwa Festo, “Munthu uyu akanamasulidwa akanakhala kuti sanapemphe zokaonekera kwa Kaisara.”
Agrippa dit à Festus: « Cet homme aurait pu être libéré s'il n'avait pas fait appel à César. »

< Machitidwe a Atumwi 26 >