< Machitidwe a Atumwi 26 >

1 Ndipo Agripa anawuza Paulo kuti, “Takulola kuti unene mawu ako.” Paulo anatambasula dzanja lake nayamba kudziteteza kuti,
Then Agrippa said to Paul, "You have permission to speak about yourself." So Paul, with outstretched arm, proceeded to make his defence.
2 “Mfumu Agripa ine ndikudziyesa wa mwayi kuyima pamaso panu lero lino ndi kudziteteza, kutsutsa zonse zimene Ayuda andinenera,
"As regards all the accusations brought against me by the Jews," he said, "I think myself fortunate, King Agrippa, in being about to defend myself to-day before you,
3 ndipo makamaka chifukwa inu mukudziwa bwino miyambo yonse ya Chiyuda ndiponso zonse zimene amatsutsana. Nʼchifukwa chake ndikukupemphani kuti mundimvetsere moleza mtima.
who are so familiar with all the customs and speculations that prevail among the Jews; and for this reason, I pray you, give me a patient hearing.
4 “Ayuda onse akudziwa za moyo wanga mmene ndakhalira kuyambira ndili mwana, kuchokera pachiyambi cha moyo wanga mʼdziko lathu ndiponso mu Yerusalemu.
"The kind of life I have lived from my youth upwards, as exemplified in my early days among my nation and in Jerusalem, is known to all the Jews.
5 Iwo akundidziwa kuyambira kalekale ndipo angathe kuchitira umboni kuti ndakhala ndili Mfarisi moyo wanga wonse, mmodzi wa gulu limene limasamala chipembedzo chathu koposa.
For they all know me of old--if they would but testify to the fact--how, being an adherent of the strictest sect of our religion, my life was that of a Pharisee.
6 Ndipo tsopano ndikuyimbidwa mlandu lero chifukwa cha chiyembekezo changa pa zimene Mulungu analonjeza makolo athu.
And now I stand here impeached because of my hope in the fulfilment of the promise made by God to our forefathers--
7 Ili ndi lonjezo limene mafuko athu khumi ndi awiri akuyembekezera kuti likwaniritsidwe pamene akupembedza Mulungu molimbika usana ndi usiku. Wolemekezeka Mfumu, nʼchifukwa cha chiyembekezo chimenechi Ayuda kuti akundiyimba mlandu.
the promise which our twelve tribes, worshipping day and night with intense devotedness, hope to have made good to them. It is on the subject of this hope, Sir, that I am accused by the Jews.
8 Nʼchifukwa chiyani ena a inu mukuganiza kuti nʼkosatheka kuti Mulungu aukitse akufa?
Why is it deemed with all of you a thing past belief if God raises the dead to life?
9 “Inenso ndimaganiza kuti ndimayenera kuchita zinthu zambiri pofuna kuthana ndi dzina la Yesu wa ku Nazareti.
"I myself, however, thought it a duty to do many things in hostility to the name of Jesus, the Nazarene.
10 Ndipo izi ndi zimene ndinazichita ku Yerusalemu. Ndi ulamuliro wa akulu a ansembe, ine ndinayika mʼndende oyera mtima ambiri, ndipo pamene amaphedwa, ine ndimavomereza.
And that was how I acted in Jerusalem. Armed with authority received from the High Priests I shut up many of God's people in various prisons, and when they were about to be put to death I gave my vote against them.
11 Nthawi zambiri ndinkapita mʼsunagoge iliyonse kuti alangidwe, ndipo ndinayesera kuwakakamiza kuti achitire chipongwe Mulungu. Mu mkwiyo wangawo, ndimapita ngakhale ku mizinda yachilendo kuti ndikawazunze.
In all the synagogues also I punished them many a time, and tried to make them blaspheme; and in my wild fury I chased them even to foreign towns.
12 “Pa ulendo wina wotere, ndikupita ku Damasiko ndi mphamvu ndi ulamuliro ochokera kwa akulu a ansembe,
"While thus engaged, I was travelling one day to Damascus armed with authority and a commission from the High Priests,
13 Wolemekezeka Mfumu, nthawi ya masana pamene ndimayenda pa msewu, ndinaona kuwala kuchokera kumwamba koposa kuwala kwa dzuwa kutandizungulira ine pamodzi ndi anzangawo.
and on the journey, at noon, Sir, I saw a light from Heaven--brighter than the brightness of the sun--shining around me and around those who were travelling with me.
14 Tonse tinagwa pansi ndipo ndinamva mawu mʼChihebri akuti, ‘Saulo, Saulo chifukwa chiyani ukundizunza Ine? Nʼkovuta kulimbikira mtunda wopanda madzi.’”
We all fell to the ground; and I heard a voice which said to me in Hebrew, "'Saul, Saul, why are you persecuting Me? You are finding it painful to kick against the ox-goad.'
15 Ndipo ine ndinafunsa kuti, “Ndinu ndani Ambuye?” Ambuye anayankha kuti, “Ndine Yesu, amene iwe ukumuzunza.
"'Who art Thou, Lord?' I asked. "'I am Jesus whom you are persecuting,' the Lord replied.
16 Tsopano dzuka ndipo imirira. Ine ndaonekera kwa iwe kuti ndikusankhe kuti ukhale mtumiki ndiponso mboni ya zimene waziona za Ine ndiponso zimene ndidzakuonetsa.
'But rise, and stand on your feet; for I have appeared to you for the very purpose of appointing you My servant and My witness both as to the things you have already seen and as to those in which I will appear to you.
17 Ine ndidzakulanditsa mʼmanja mwa anthu a mtundu wako ndiponso mwa anthu a mitundu ina. Ine ndikukutuma kwa iwo,
I will save you from the Jewish people and from the Gentiles, to whom I send you to open their eyes,
18 kuti ukatsekule maso awo kuti atembenuke mtima kuchoka ku mdima ndi kulowa mʼkuwala, kuchoka ku mphamvu za Satana ndi kupita kwa Mulungu, kuti alandire chikhululukiro cha machimo awo ndi kukhala mʼgulu la amene akuyeretsedwa chifukwa chokhulupirira Ine.
that they may turn from darkness to light and from the obedience to Satan to God, in order to receive forgiveness of sins and an inheritance among those who are sanctified through faith in Me.'
19 “Nʼchifukwa chake Mfumu Agripa, sindinakane kumvera masomphenya wochokera kumwamba.
"Therefore, King Agrippa, I was not disobedient to the heavenly vision;
20 Kuyambira kwa anthu a ku Damasiko, a ku Yerusalemu, a ku Yudeya konse ndi kwa anthu a mitundu inanso, ndinalalikira kuti akuyenera kulapa ndi kutembenukira kwa Mulungu ndikuti aonetse kulapa kwawo mwa ntchito zawo.
but I proceeded to preach first to the people in Damascus, and then to those in Jerusalem and in all Judaea, and to the Gentiles, that they must repent and turn to God, and live lives consistent with such repentance.
21 Ichi nʼchifukwa chake Ayuda anandigwira mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu nafuna kundipha.
"It was on this account that the Jews seized me in the Temple and tried to kill me.
22 Koma Mulungu wakhala akundithandiza mpaka lero lino. Ine ndayima pano kuti ndichitire umboni kwa anthu onse otchuka ndi anthu wamba. Ine sindikunena zina zowonjezera koma zimene Aneneri ndi Mose ananena kuti zidzachitika.
Having, however, obtained the help which is from God, I have stood firm until now, and have solemnly exhorted rich and poor alike, saying nothing except what the Prophets and Moses predicted as soon to happen,
23 Iwo ananena kuti Khristu adzamva zowawa ndipo popeza Iye adzakhala woyamba kuuka kwa akufa, adzalalikira za kuwunika kwa anthu a mtundu wake ndiponso kwa anthu a mitundu ina.”
since the Christ was to be a suffering Christ, and by coming back from the dead was then to be the first to proclaim a message of light both to the Jewish people and to the Gentiles."
24 Paulo akudziteteza, Festo anakweza mawu nati, “Wazungulira mutu Paulo! Kuphunzira kwako kwakuchititsa misala.”
As Paul thus made his defence, Festus exclaimed in a loud voice, "You are raving mad, Paul; and great learning is driving you mad."
25 Paulo anayankha nati, “Wolemekezeka Festo, sindine wozungulira mutu. Zimene ndikunena ndi zoona ndiponso za nzeru.
"I am not mad, most noble Festus," replied Paul; "I am speaking words of sober truth.
26 Mfumu ikuzidziwa bwino zinthu izi, ndipo ndikuyankhula momasuka kwa iyo. Ine ndikukhulupirira kuti palibe kanthu nʼkamodzi komwe kamene sukukadziwa, chifukwa izi sizinachike mseri.
For the King, to whom I speak freely, knows about these matters. I am not to be persuaded that any detail of them has escaped his notice; for these things have not been done in a corner.
27 Mfumu Agripa, kodi mumakhulupirira mawu a aneneri? Ine ndikudziwa kuti mumakhulupirira.”
King Agrippa, do you believe the Prophets? I know that you believe them."
28 Kenaka Agripa anati kwa Paulo, “Kodi ukuganiza kuti mʼkanthawi kochepa kotere ungandikope kuti ndikhale Mkhristu?”
Agrippa answered, "In brief, you are doing your best to persuade me to become a Christian."
29 Paulo anayankha kuti, “Ngakhale kanthawi kochepa kapena nthawi yayitali, ine ndikupempha kwa Mulungu kuti osati inu nokha koma aliyense amene akundimva lero lino akhale monga ine, kupatulapo maunyolo okhawa.”
"My prayer to God, whether briefly or at length," replied Paul, "would be that not only you but all who are my hearers to-day, might become such as I am--except these chains."
30 Mfumu inayimirira pamodzi ndi bwanamkubwa ndi Bernisi ndiponso anthu onse amene anakhala nawo pamodzi.
So the King rose, and the Governor, and Bernice, and those who were sitting with them;
31 Inatuluka mʼchipindamo, ndipo pamene imayankhula inati, “Munthu uyu sanachite kanthu koyenera kuphedwa kapena kumangidwa.”
and, having withdrawn, they talked to one another and said, "This man is doing nothing for which he deserves death or imprisonment."
32 Agripa anati kwa Festo, “Munthu uyu akanamasulidwa akanakhala kuti sanapemphe zokaonekera kwa Kaisara.”
And Agrippa said to Festus, "He might have been set at liberty, if he had not appealed to Caesar."

< Machitidwe a Atumwi 26 >