< Machitidwe a Atumwi 26 >

1 Ndipo Agripa anawuza Paulo kuti, “Takulola kuti unene mawu ako.” Paulo anatambasula dzanja lake nayamba kudziteteza kuti,
So Agrippa said to Paul, “You may speak for yourself.” Then Paul stretched out his hand and made his defense.
2 “Mfumu Agripa ine ndikudziyesa wa mwayi kuyima pamaso panu lero lino ndi kudziteteza, kutsutsa zonse zimene Ayuda andinenera,
“I regard myself as happy, King Agrippa, to make my case before you today against all the accusations of the Jews;
3 ndipo makamaka chifukwa inu mukudziwa bwino miyambo yonse ya Chiyuda ndiponso zonse zimene amatsutsana. Nʼchifukwa chake ndikukupemphani kuti mundimvetsere moleza mtima.
especially, because you are an expert in all the Jewish customs and questions. So I ask you to hear me patiently.
4 “Ayuda onse akudziwa za moyo wanga mmene ndakhalira kuyambira ndili mwana, kuchokera pachiyambi cha moyo wanga mʼdziko lathu ndiponso mu Yerusalemu.
Truly, all the Jews know how I lived from my youth in my own nation and at Jerusalem.
5 Iwo akundidziwa kuyambira kalekale ndipo angathe kuchitira umboni kuti ndakhala ndili Mfarisi moyo wanga wonse, mmodzi wa gulu limene limasamala chipembedzo chathu koposa.
They knew me from the beginning and they should admit that I lived as a Pharisee, the strictest party of our religion.
6 Ndipo tsopano ndikuyimbidwa mlandu lero chifukwa cha chiyembekezo changa pa zimene Mulungu analonjeza makolo athu.
Now I stand here to be judged because of my certain hope in the promise made by God to our fathers.
7 Ili ndi lonjezo limene mafuko athu khumi ndi awiri akuyembekezera kuti likwaniritsidwe pamene akupembedza Mulungu molimbika usana ndi usiku. Wolemekezeka Mfumu, nʼchifukwa cha chiyembekezo chimenechi Ayuda kuti akundiyimba mlandu.
For this is the promise that our twelve tribes sought to receive as they earnestly worshiped God night and day. It is for this certain hope, King Agrippa, that the Jews accuse me.
8 Nʼchifukwa chiyani ena a inu mukuganiza kuti nʼkosatheka kuti Mulungu aukitse akufa?
Why should any of you think it is unbelievable that God raises the dead?
9 “Inenso ndimaganiza kuti ndimayenera kuchita zinthu zambiri pofuna kuthana ndi dzina la Yesu wa ku Nazareti.
Now indeed, I myself thought that I should do many things against the name of Jesus of Nazareth.
10 Ndipo izi ndi zimene ndinazichita ku Yerusalemu. Ndi ulamuliro wa akulu a ansembe, ine ndinayika mʼndende oyera mtima ambiri, ndipo pamene amaphedwa, ine ndimavomereza.
I did these in Jerusalem. I locked up many of the saints in prison by the authority I received from the chief priests, and when they were killed, I cast my vote against them.
11 Nthawi zambiri ndinkapita mʼsunagoge iliyonse kuti alangidwe, ndipo ndinayesera kuwakakamiza kuti achitire chipongwe Mulungu. Mu mkwiyo wangawo, ndimapita ngakhale ku mizinda yachilendo kuti ndikawazunze.
I punished them many times in all the synagogues and I tried to force them to blaspheme. I was furiously enraged against them and I persecuted them even to foreign cities.
12 “Pa ulendo wina wotere, ndikupita ku Damasiko ndi mphamvu ndi ulamuliro ochokera kwa akulu a ansembe,
While I was doing this, I went to Damascus with authority and orders from the chief priests;
13 Wolemekezeka Mfumu, nthawi ya masana pamene ndimayenda pa msewu, ndinaona kuwala kuchokera kumwamba koposa kuwala kwa dzuwa kutandizungulira ine pamodzi ndi anzangawo.
and on the way there, at midday, King, I saw a light from heaven that was brighter than the sun and it shone around both me and the men who were traveling with me.
14 Tonse tinagwa pansi ndipo ndinamva mawu mʼChihebri akuti, ‘Saulo, Saulo chifukwa chiyani ukundizunza Ine? Nʼkovuta kulimbikira mtunda wopanda madzi.’”
When we all fell to the ground, I heard a voice speaking to me that said in the Hebrew language, 'Saul, Saul, why do you persecute me? It is hard for you to kick a goad.'
15 Ndipo ine ndinafunsa kuti, “Ndinu ndani Ambuye?” Ambuye anayankha kuti, “Ndine Yesu, amene iwe ukumuzunza.
Then I said, 'Who are you, Lord?' The Lord replied, 'I am Jesus whom you persecute.
16 Tsopano dzuka ndipo imirira. Ine ndaonekera kwa iwe kuti ndikusankhe kuti ukhale mtumiki ndiponso mboni ya zimene waziona za Ine ndiponso zimene ndidzakuonetsa.
Now get up and stand on your feet; because for this purpose I appeared to you, to appoint you to be a servant and a witness concerning the things that you know about me now and the things that I will show to you later;
17 Ine ndidzakulanditsa mʼmanja mwa anthu a mtundu wako ndiponso mwa anthu a mitundu ina. Ine ndikukutuma kwa iwo,
and I will rescue you from the people and from the Gentiles to whom I am sending you,
18 kuti ukatsekule maso awo kuti atembenuke mtima kuchoka ku mdima ndi kulowa mʼkuwala, kuchoka ku mphamvu za Satana ndi kupita kwa Mulungu, kuti alandire chikhululukiro cha machimo awo ndi kukhala mʼgulu la amene akuyeretsedwa chifukwa chokhulupirira Ine.
to open their eyes and to turn them from darkness to light and from the power of Satan to God, so that they may receive from God the forgiveness of sins and the inheritance that I give to them who are sanctified by faith in me.'
19 “Nʼchifukwa chake Mfumu Agripa, sindinakane kumvera masomphenya wochokera kumwamba.
Therefore, King Agrippa, I did not disobey the heavenly vision;
20 Kuyambira kwa anthu a ku Damasiko, a ku Yerusalemu, a ku Yudeya konse ndi kwa anthu a mitundu inanso, ndinalalikira kuti akuyenera kulapa ndi kutembenukira kwa Mulungu ndikuti aonetse kulapa kwawo mwa ntchito zawo.
but, to those in Damascus first, and then at Jerusalem, and throughout all the country of Judea, and also to the Gentiles, I gave them the message that that they should repent and turn to God, doing deeds worthy of repentance.
21 Ichi nʼchifukwa chake Ayuda anandigwira mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu nafuna kundipha.
For this cause the Jews arrested me in the temple and tried to kill me.
22 Koma Mulungu wakhala akundithandiza mpaka lero lino. Ine ndayima pano kuti ndichitire umboni kwa anthu onse otchuka ndi anthu wamba. Ine sindikunena zina zowonjezera koma zimene Aneneri ndi Mose ananena kuti zidzachitika.
God has helped me until now, so I stand and testify to the common people and to the great ones about nothing more than what the prophets and Moses said would happen—
23 Iwo ananena kuti Khristu adzamva zowawa ndipo popeza Iye adzakhala woyamba kuuka kwa akufa, adzalalikira za kuwunika kwa anthu a mtundu wake ndiponso kwa anthu a mitundu ina.”
that Christ must suffer and that by being the first to rise from the dead, he would proclaim light to our own people and to the Gentiles.”
24 Paulo akudziteteza, Festo anakweza mawu nati, “Wazungulira mutu Paulo! Kuphunzira kwako kwakuchititsa misala.”
As Paul completed his defense, Festus said with a loud voice, “Paul, you are insane; your great learning makes you insane.”
25 Paulo anayankha nati, “Wolemekezeka Festo, sindine wozungulira mutu. Zimene ndikunena ndi zoona ndiponso za nzeru.
But Paul said, “I am not insane, most excellent Festus, but what I am declaring is true and rational.
26 Mfumu ikuzidziwa bwino zinthu izi, ndipo ndikuyankhula momasuka kwa iyo. Ine ndikukhulupirira kuti palibe kanthu nʼkamodzi komwe kamene sukukadziwa, chifukwa izi sizinachike mseri.
For the king knows about these things; and so, I speak freely to him, for I am persuaded that none of this is hidden from him; for this has not been done in a corner.
27 Mfumu Agripa, kodi mumakhulupirira mawu a aneneri? Ine ndikudziwa kuti mumakhulupirira.”
Do you believe the prophets, King Agrippa? I know that you believe.”
28 Kenaka Agripa anati kwa Paulo, “Kodi ukuganiza kuti mʼkanthawi kochepa kotere ungandikope kuti ndikhale Mkhristu?”
Agrippa said to Paul, “In a short time would you persuade me and make me a Christian?”
29 Paulo anayankha kuti, “Ngakhale kanthawi kochepa kapena nthawi yayitali, ine ndikupempha kwa Mulungu kuti osati inu nokha koma aliyense amene akundimva lero lino akhale monga ine, kupatulapo maunyolo okhawa.”
Paul said, “I pray to God, that whether in a short or long time, not you only, but also all that hear me today, would be like me, but without these prison chains.”
30 Mfumu inayimirira pamodzi ndi bwanamkubwa ndi Bernisi ndiponso anthu onse amene anakhala nawo pamodzi.
Then the king stood up, and the governor, and Bernice also, and those who were sitting with them;
31 Inatuluka mʼchipindamo, ndipo pamene imayankhula inati, “Munthu uyu sanachite kanthu koyenera kuphedwa kapena kumangidwa.”
when they left the hall, they talked to one another and said, “This man does nothing worthy of death or of bonds.”
32 Agripa anati kwa Festo, “Munthu uyu akanamasulidwa akanakhala kuti sanapemphe zokaonekera kwa Kaisara.”
Agrippa said to Festus, “This man could have been freed if he had not appealed to Caesar.”

< Machitidwe a Atumwi 26 >