< Machitidwe a Atumwi 26 >

1 Ndipo Agripa anawuza Paulo kuti, “Takulola kuti unene mawu ako.” Paulo anatambasula dzanja lake nayamba kudziteteza kuti,
Men Agrippa sagde til Paulus: "Det tilstedes dig at tale om dig selv." Da udrakte Paulus Hånden og forsvarede sig således:
2 “Mfumu Agripa ine ndikudziyesa wa mwayi kuyima pamaso panu lero lino ndi kudziteteza, kutsutsa zonse zimene Ayuda andinenera,
"Jeg agter mig selv lykkelig, fordi jeg i Dag skal forsvare mig for dig angående alle de Ting, for hvilke jeg anklages af Jøderne, Kong Agrippa!
3 ndipo makamaka chifukwa inu mukudziwa bwino miyambo yonse ya Chiyuda ndiponso zonse zimene amatsutsana. Nʼchifukwa chake ndikukupemphani kuti mundimvetsere moleza mtima.
navnlig fordi du er kendt med alle Jødernes Skikke og Stridsspørgsmål; derfor beder jeg dig om, at du tålmodigt vil høre mig.
4 “Ayuda onse akudziwa za moyo wanga mmene ndakhalira kuyambira ndili mwana, kuchokera pachiyambi cha moyo wanga mʼdziko lathu ndiponso mu Yerusalemu.
Mit Levned fra Ungdommen af, som fra Begyndelsen har været ført iblandt mit Folk og i Jerusalem, vide alle Jøderne Besked om;
5 Iwo akundidziwa kuyambira kalekale ndipo angathe kuchitira umboni kuti ndakhala ndili Mfarisi moyo wanga wonse, mmodzi wa gulu limene limasamala chipembedzo chathu koposa.
thi de kende mig i Forvejen lige fra først af (om de ellers ville vidne), at jeg har levet som Farisæer efter det strengeste Parti i vor Gudsdyrkelse.
6 Ndipo tsopano ndikuyimbidwa mlandu lero chifukwa cha chiyembekezo changa pa zimene Mulungu analonjeza makolo athu.
Og nu står jeg her og dømmes for Håbet på den Forjættelse, som er given af Gud til vore Fædre,
7 Ili ndi lonjezo limene mafuko athu khumi ndi awiri akuyembekezera kuti likwaniritsidwe pamene akupembedza Mulungu molimbika usana ndi usiku. Wolemekezeka Mfumu, nʼchifukwa cha chiyembekezo chimenechi Ayuda kuti akundiyimba mlandu.
og som vort Tolvstammefolk håber at nå frem til, idet de tjene Gud uafladeligt Nat og Dag; for dette Håbs Skyld anklages jeg af Jøder, o Konge!
8 Nʼchifukwa chiyani ena a inu mukuganiza kuti nʼkosatheka kuti Mulungu aukitse akufa?
Hvor kan det holdes for utroligt hos eder, at Gud oprejser døde?
9 “Inenso ndimaganiza kuti ndimayenera kuchita zinthu zambiri pofuna kuthana ndi dzina la Yesu wa ku Nazareti.
Jeg selv mente nu også at burde gøre meget imod Jesu, Nazaræerens Navn,
10 Ndipo izi ndi zimene ndinazichita ku Yerusalemu. Ndi ulamuliro wa akulu a ansembe, ine ndinayika mʼndende oyera mtima ambiri, ndipo pamene amaphedwa, ine ndimavomereza.
og det gjorde jeg også i Jerusalem; og jeg indespærrede mange af de hellige i Fængsler, da jeg havde fået Fuldmagt dertil af Ypperstepræsterne, og når de bleve slåede ihjel, gav jeg min Stemme dertil.
11 Nthawi zambiri ndinkapita mʼsunagoge iliyonse kuti alangidwe, ndipo ndinayesera kuwakakamiza kuti achitire chipongwe Mulungu. Mu mkwiyo wangawo, ndimapita ngakhale ku mizinda yachilendo kuti ndikawazunze.
Og i alle Synagogerne lod jeg dem ofte straffe og tvang dem til at tale bespotteligt, og rasende end mere imod dem forfulgte jeg dem endog til de udenlandske Byer.
12 “Pa ulendo wina wotere, ndikupita ku Damasiko ndi mphamvu ndi ulamuliro ochokera kwa akulu a ansembe,
Da jeg i dette Øjemed drog til Damaskus med Fuldmagt og Myndighed fra Ypperstepræsterne,
13 Wolemekezeka Mfumu, nthawi ya masana pamene ndimayenda pa msewu, ndinaona kuwala kuchokera kumwamba koposa kuwala kwa dzuwa kutandizungulira ine pamodzi ndi anzangawo.
så jeg undervejs midt på Dagen, o Konge! et Lys fra Himmelen, som overgik Solens Glans, omstråle mig og dem, som rejste med mig.
14 Tonse tinagwa pansi ndipo ndinamva mawu mʼChihebri akuti, ‘Saulo, Saulo chifukwa chiyani ukundizunza Ine? Nʼkovuta kulimbikira mtunda wopanda madzi.’”
Men da vi alle faldt til Jorden, hørte jeg en Røst, som sagde til mig i det hebraiske Sprog: Saul! Saul! hvorfor forfølger du mig? det bliver dig hårdt at stampe imod Brodden.
15 Ndipo ine ndinafunsa kuti, “Ndinu ndani Ambuye?” Ambuye anayankha kuti, “Ndine Yesu, amene iwe ukumuzunza.
Og jeg sagde: Hvem er du, Herre? Men Herren sagde: Jeg er Jesus, som du forfølger.
16 Tsopano dzuka ndipo imirira. Ine ndaonekera kwa iwe kuti ndikusankhe kuti ukhale mtumiki ndiponso mboni ya zimene waziona za Ine ndiponso zimene ndidzakuonetsa.
Men rejs dig og stå på dine Fødder; thi derfor har jeg vist mig for dig, for at udkåre dig til Tjener og Vidne, både om det, som du har set, og om mine kommende Åbenbaringer for dig,
17 Ine ndidzakulanditsa mʼmanja mwa anthu a mtundu wako ndiponso mwa anthu a mitundu ina. Ine ndikukutuma kwa iwo,
idet jeg udfrier dig fra Folket og fra Hedningerne, til hvilke jeg udsender dig
18 kuti ukatsekule maso awo kuti atembenuke mtima kuchoka ku mdima ndi kulowa mʼkuwala, kuchoka ku mphamvu za Satana ndi kupita kwa Mulungu, kuti alandire chikhululukiro cha machimo awo ndi kukhala mʼgulu la amene akuyeretsedwa chifukwa chokhulupirira Ine.
for at oplade deres Øjne, så de må omvende sig fra Mørke til Lys og fra Satans Magt til Gud, for at de kunne få Syndernes Forladelse og Lod iblandt dem, som ere helligede ved Troen på mig.
19 “Nʼchifukwa chake Mfumu Agripa, sindinakane kumvera masomphenya wochokera kumwamba.
Derfor, Kong Agrippa! blev jeg ikke ulydig imod det himmelske Syn;
20 Kuyambira kwa anthu a ku Damasiko, a ku Yerusalemu, a ku Yudeya konse ndi kwa anthu a mitundu inanso, ndinalalikira kuti akuyenera kulapa ndi kutembenukira kwa Mulungu ndikuti aonetse kulapa kwawo mwa ntchito zawo.
men jeg forkyndte både først for dem i Damaskus og så i Jerusalem og over hele Judæas Land og for Hedningerne, at de skulde fatte et andet Sind og omvende sig til Gud og gøre Gerninger, Omvendelsen værdige.
21 Ichi nʼchifukwa chake Ayuda anandigwira mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu nafuna kundipha.
For denne Sags Skyld grebe nogle Jøder mig i Helligdommen og forsøgte at slå mig ihjel.
22 Koma Mulungu wakhala akundithandiza mpaka lero lino. Ine ndayima pano kuti ndichitire umboni kwa anthu onse otchuka ndi anthu wamba. Ine sindikunena zina zowonjezera koma zimene Aneneri ndi Mose ananena kuti zidzachitika.
Det er altså ved den Hjælp, jeg har fået fra Gud, at jeg har stået indtil denne Dag og vidnet både for små og store, idet jeg intet siger ud over det, som både Profeterne og Moses have sagt skulde ske,
23 Iwo ananena kuti Khristu adzamva zowawa ndipo popeza Iye adzakhala woyamba kuuka kwa akufa, adzalalikira za kuwunika kwa anthu a mtundu wake ndiponso kwa anthu a mitundu ina.”
at Kristus skulde lide, at han som den første af de dødes Opstandelse skulde forkynde Lys både for Folket og for Hedningerne."
24 Paulo akudziteteza, Festo anakweza mawu nati, “Wazungulira mutu Paulo! Kuphunzira kwako kwakuchititsa misala.”
Men da han forsvarede sig således, sagde Festus med høj Røst: "Du raser, Paulus! den megen Lærdom gør dig rasende."
25 Paulo anayankha nati, “Wolemekezeka Festo, sindine wozungulira mutu. Zimene ndikunena ndi zoona ndiponso za nzeru.
Men Paulus sagde: "Jeg raser ikke, mægtigste Festus! men jeg taler sande og betænksomme Ord.
26 Mfumu ikuzidziwa bwino zinthu izi, ndipo ndikuyankhula momasuka kwa iyo. Ine ndikukhulupirira kuti palibe kanthu nʼkamodzi komwe kamene sukukadziwa, chifukwa izi sizinachike mseri.
Thi Kongen ved Besked om dette, og til ham taler jeg frimodigt, efterdi jeg er vis på, at slet intet af dette er skjult for ham; thi dette er ikke sket i en Vrå.
27 Mfumu Agripa, kodi mumakhulupirira mawu a aneneri? Ine ndikudziwa kuti mumakhulupirira.”
Tror du, Kong Agrippa, Profeterne? Jeg ved, at du tror dem."
28 Kenaka Agripa anati kwa Paulo, “Kodi ukuganiza kuti mʼkanthawi kochepa kotere ungandikope kuti ndikhale Mkhristu?”
Men Agrippa sagde til Paulus: "Der fattes lidet i, at du overtaler mig til at blive en Kristen."
29 Paulo anayankha kuti, “Ngakhale kanthawi kochepa kapena nthawi yayitali, ine ndikupempha kwa Mulungu kuti osati inu nokha koma aliyense amene akundimva lero lino akhale monga ine, kupatulapo maunyolo okhawa.”
Men Paulus sagde: "Jeg vilde ønske til Gud, enten der fattes lidet eller meget, at ikke alene du, men også alle, som høre mig i Dag, måtte blive sådan, som jeg selv er, på disse Lænker nær."
30 Mfumu inayimirira pamodzi ndi bwanamkubwa ndi Bernisi ndiponso anthu onse amene anakhala nawo pamodzi.
Da stod Kongen op og Landshøvdingen og Berenike og de, som sade hos dem.
31 Inatuluka mʼchipindamo, ndipo pamene imayankhula inati, “Munthu uyu sanachite kanthu koyenera kuphedwa kapena kumangidwa.”
Og da de gik bort, talte de med hverandre og sagde: "Denne Mand gør intet, som fortjener Død eller Lænker."
32 Agripa anati kwa Festo, “Munthu uyu akanamasulidwa akanakhala kuti sanapemphe zokaonekera kwa Kaisara.”
Men Agrippa sagde til Festus: "Denne Mand kunde være løsladt, dersom han ikke havde skudt sig ind under Kejseren."

< Machitidwe a Atumwi 26 >