< Machitidwe a Atumwi 25 >
1 Patapita masiku atatu Festo atafika mʼdera lake, anachoka ku Kaisareya ndi kupita ku Yerusalemu.
Festus, having entered on his duties as governor of the province, two days later went up from Caesarea to Jerusalem.
2 Kumeneko akulu a ansembe ndi atsogoleri a Chiyuda anabwera kwa iye ndi kumufotokozera mlandu wa Paulo.
The High Priests and the leading men among the Jews immediately made representations to him against Paul, and begged him--
3 Iwo anamupempha Festo kuti awakomere mtima potumiza Paulo ku Yerusalemu, pakuti anali atakonzekera chiwembu kuti amuphe Pauloyo pa njira.
asking it as a favour, to Paul's prejudice--to have him brought to Jerusalem. They were planning an ambush to kill him on the way.
4 Festo anayankha kuti, “Paulo akusungidwa ku Kaisareya, ndipo ndipita kumeneko posachedwa.
Festus, however, replied that Paul was in custody in Caesarea, and that he was himself going there very soon.
5 Ena mwa atsogoleri anu apite nane kumeneko, kuti akafotokoze mlandu wa munthuyu, ngati anachita kanthu kalikonse kolakwika.”
"Therefore let those of you," he said, "who can come, go down with me, and impeach the man, if there is anything amiss in him."
6 Festo atakhala nawo masiku asanu ndi atatu kapena khumi iye anapita ku Kaisareya, ndipo mmawa mwake anayitanitsa bwalo nalamula kuti abweretse Paulo pamaso pake.
After a stay of eight or ten days in Jerusalem--not more--he went down to Caesarea; and the next day, taking his seat on the tribunal, he ordered Paul to be brought in.
7 Paulo atafika, Ayuda amene anafika kuchokera ku Yerusalemu anayima momuzungulira. Iwo anamunenera zinthu zoopsa zambiri zimene sakanatha kubweretsa umboni wake.
Upon Paul's arrival, the Jews who had come down from Jerusalem stood round him, and brought many grave charges against him which they were unable to substantiate.
8 Kenaka Paulo ananena mawu ake odziteteza kuti, “Ine sindinalakwirepo lamulo la Ayuda, kapena Nyumba ya Mulungu kapenanso Kaisara.”
But, in reply, Paul said, "Neither against the Jewish Law, nor against the Temple, nor against Caesar, have I committed any offence whatever."
9 Festo, pofuna kuti Ayuda amukonde anafunsa Paulo kuti, “Kodi iwe ukufuna kupita ku Yerusalemu, kuti kumeneko ukafotokoze mlandu wako pamaso panga?”
Then Festus, being anxious to gratify the Jews, asked Paul, "Are you willing to go up to Jerusalem, and there stand your trial before me on these charges?"
10 Paulo anayankha kuti, “Ine tsopano ndayima pamaso pa bwalo la milandu la Kaisara, ndiko kumene ayenera kundiweruza. Ine sindinalakwire Ayuda, monga inu mukudziwa bwino.
"I am standing before Caesar's tribunal," replied Paul, "where alone I ought to be tried. The Jews have no real ground of complaint against me, as in fact you yourself are beginning to see more clearly.
11 Koma ngati ndili wolakwa, ngati ndachita kanthu koyenera kuphedwa, ine sindikukana kufa. Koma ngati mlandu umene abweretsa Ayudawa siwoona, palibe munthu angathe kundipereka mʼmanja mwawo. Ndikupempha kuti ndikaweruzidwe ndi Kaisara!”
If, however, I have done wrong and have committed any offence for which I deserve to die, I do not ask to be excused that penalty. But if there is no truth in what these men allege against me, no one has the right to give me up to them as a favour. I appeal to Caesar."
12 Festo atakambirana ndi akuluakulu abwalo lake, anati, “Popeza wapempha kupita kwa Kaisara, kwa Kaisara udzapitadi!”
Then, after conferring with the Council, Festus replied, "To Caesar you have appealed: to Caesar you shall go."
13 Patapita masiku ochepa mfumu Agripa pamodzi ndi Bernisi anabwera ku Kaisareya kudzalonjera Festo.
A short time after this, Agrippa the king and Bernice came to Caesarea to pay a complimentary visit to Festus;
14 Atakhala kumeneko masiku angapo, Festo anafotokozera mfumuyo za mlandu wa Paulo. Iye anati, “Kuli munthu wina kuno amene Felike anamusiya mʼndende.
and, during their rather long stay, Festus laid Paul's case before the king. "There is a man here," he said, "whom Felix left a prisoner,
15 Nditapita ku Yerusalemu akulu a ansembe ndi akuluakulu a Ayuda anandifotokozera mlandu wake ndipo anandipempha kuti ndigamule kuti ndi wolakwa.
about whom, when I went to Jerusalem, the High Priests and the Elders of the Jews made representations to me, begging that sentence might be pronounced against him.
16 “Ine ndinawayankha kuti si mwambo wa Aroma kungomupereka munthu ayi. Munthu woyimbidwa mlanduyo amayenera kukumana nawo omunenezawo, kuti iye akhale ndi mwayi woyankhapo pa zimene akumuyimba mlanduzo.
My reply was that it is not the custom among the Romans to give up any one for punishment before the accused has had his accusers face to face, and has had an opportunity of defending himself against the charge which has been brought against him.
17 Atabwera kuno pamodzi ndi ine, sindinachedwetse mlanduwo, koma ndinayitanitsa bwalo mmawa mwake ndi kulamula kuti amubweretse munthuyo.
"When, therefore, a number of them came here, the next day I took my seat on the tribunal, without any loss of time, and ordered the man to be brought in.
18 Omuyimba mlandu aja atayimirira kuti ayankhule, iwo sananene cholakwa chilichonse chimene ndimayembekezera.
But, when his accusers stood up, they did not charge him with the misdemeanours of which I had been suspecting him.
19 Mʼmalo mwake, anatsutsana naye pa fundo zina za chipembedzo chawo ndi za munthu wakufa, dzina lake Yesu, amene Paulo akuti ali moyo.
But they quarrelled with him about certain matters connected with their own religion, and about one Jesus who had died, but--so Paul persistently maintained--is now alive.
20 Ine ndinathedwa nzeru wosadziwa momwe ndikanafufuzira nkhaniyi; kotero ndinafunsa ngati akanafuna kupita ku Yerusalemu kuti akaweruzidwe kumeneko.
I was at a loss how to investigate such questions, and asked Paul whether he would care to go to Jerusalem and there stand his trial on these matters.
21 Koma Paulo anapempha kuti akaonekere pamaso pa mfumu ya Chiroma, ndipo ndinalamula kuti asungidwe mpaka pamene ndidzamutumize kwa Kaisara.”
But when Paul appealed to have his case kept for the Emperor's decision, I ordered him to be kept in prison until I could send him up to Caesar."
22 Ndipo Agripa anati kwa Festo, “Ine ndikufuna ndimumve ndekha munthu ameneyu.” Iye anayankha kuti, “Mudzamumva mawa.”
"I should like to hear the man myself," said Agrippa. "to-morrow," replied Festus, "you shall." Accordingly, the next day, Agrippa and Bernice came in state
23 Mmawa mwake Agripa ndi Bernisi anabwera mwaulemu waukulu waufumu nalowa mʼbwalo la milandu pamodzi ndi akulu a asilikali ndiponso akuluakulu a mu mzindawo. Atalamula Festo kuti Paulo abwere, anabweradi.
and took their seats in the Judgement Hall, attended by the Tribunes and the men of high rank in the city; and, at the command of Festus, Paul was brought in.
24 Festo anati, “Mfumu Agripa, ndi onse amene muli nafe pano, mukumuona munthu uyu! Ayuda onse anandipempha ine za uyu ku Yerusalemu ndiponso kuno ku Kaisareya, mofuwula kuti, ameneyu sayenera kukhala ndi moyo.
Then Festus said, "King Agrippa and all who are present with us, you see here the man about whom the whole nation of the Jews made suit to me, both in Jerusalem and here, crying out that he ought not to live any longer.
25 Ine ndinapeza kuti iyeyu sanachite kanthu koyenera kufa, koma popeza anapempha kuti apite kwa mfumu ya Chiroma, ine ndinatsimikiza zomutumiza ku Roma.
I could not discover that he had done anything for which he deserved to die; but as he has himself appealed to the Emperor, I have decided to send him to Rome.
26 Koma ndilibe kanthu kenikeni koti ndilembere Wolemekezekayo za iyeyu. Nʼchifukwa chake ndabwera naye pamaso pa nonsenu, makamaka kwa inuyo mfumu Agripa, kuti mwina mukamufunsitsa ndikhale ndi choti ndilembe.
I have nothing very definite, however, to tell our Sovereign about him. So I have brought the man before you all--and especially before you, King Agrippa--that after he has been examined I may find something which I can put into writing.
27 Pakuti ine ndikuganiza kuti ndi chinthu chopanda nzeru kutumiza wamʼndende popanda kutchula zifukwa zenizeni za mlandu wake.”
For, when sending a prisoner to Rome, it seems to me to be absurd not to state the charges against him."