< Machitidwe a Atumwi 25 >
1 Patapita masiku atatu Festo atafika mʼdera lake, anachoka ku Kaisareya ndi kupita ku Yerusalemu.
Třetí den po převzetí úřadu přijel Festus z Césareje do Jeruzaléma,
2 Kumeneko akulu a ansembe ndi atsogoleri a Chiyuda anabwera kwa iye ndi kumufotokozera mlandu wa Paulo.
kde přijal velekněze a další židovské představitele. Ti mu připomněli svou žalobu proti Pavlovi a snažili se pohnout Festa k tomu,
3 Iwo anamupempha Festo kuti awakomere mtima potumiza Paulo ku Yerusalemu, pakuti anali atakonzekera chiwembu kuti amuphe Pauloyo pa njira.
aby dal vězně dopravit zase zpět do Jeruzaléma; ve skutečnosti však zamýšleli Pavla na cestě přepadnout a zavraždit.
4 Festo anayankha kuti, “Paulo akusungidwa ku Kaisareya, ndipo ndipita kumeneko posachedwa.
Festus je však odbyl: „Vězeň je v Césareji a já se tam vrátím co nevidět.
5 Ena mwa atsogoleri anu apite nane kumeneko, kuti akafotokoze mlandu wa munthuyu, ngati anachita kanthu kalikonse kolakwika.”
Vyšlete se mnou své zplnomocněnce, a máte-li svou žalobu dobře podloženou, ať ji přednesou u řádného soudu.“
6 Festo atakhala nawo masiku asanu ndi atatu kapena khumi iye anapita ku Kaisareya, ndipo mmawa mwake anayitanitsa bwalo nalamula kuti abweretse Paulo pamaso pake.
V Jeruzalémě se zdržel ještě osm deset dní a pak se vrátil do Césareje.
7 Paulo atafika, Ayuda amene anafika kuchokera ku Yerusalemu anayima momuzungulira. Iwo anamunenera zinthu zoopsa zambiri zimene sakanatha kubweretsa umboni wake.
Hned následující den zahájil přelíčení a dal Pavla předvést. Jeruzalémští vyslanci vězně obžalovali z mnoha zločinů, ale neměli pro ně žádné důkazy.
8 Kenaka Paulo ananena mawu ake odziteteza kuti, “Ine sindinalakwirepo lamulo la Ayuda, kapena Nyumba ya Mulungu kapenanso Kaisara.”
Pavlova obhajoba zněla: „Neprovinil jsem se ani proti židovskému zákonu, ani proti chrámovým předpisům, a tím méně proti římskému právu.“
9 Festo, pofuna kuti Ayuda amukonde anafunsa Paulo kuti, “Kodi iwe ukufuna kupita ku Yerusalemu, kuti kumeneko ukafotokoze mlandu wako pamaso panga?”
Festus chtěl židům ukázat dobrou vůli, a tak Pavlovi navrhl: „Jsi ochoten postavit se v Jeruzalémě před soud, kterému bych předsedal?“
10 Paulo anayankha kuti, “Ine tsopano ndayima pamaso pa bwalo la milandu la Kaisara, ndiko kumene ayenera kundiweruza. Ine sindinalakwire Ayuda, monga inu mukudziwa bwino.
Pavel vytušil smrtelné nebezpečí, a tak odmítl: „Ne, trvám na tom, abych byl ponechán v pravomoci římského soudu. Sám jsi zjistil, že jsem se proti židům nijak neprovinil.
11 Koma ngati ndili wolakwa, ngati ndachita kanthu koyenera kuphedwa, ine sindikukana kufa. Koma ngati mlandu umene abweretsa Ayudawa siwoona, palibe munthu angathe kundipereka mʼmanja mwawo. Ndikupempha kuti ndikaweruzidwe ndi Kaisara!”
Kdyby mně byl prokázán nějaký zločin, byl bych ochoten podstoupit spravedlivý trest, třeba i popravu. Jejich žaloby jsou však smyšlené a ty nemáš právo vydat mě jim. Odvolám se k císařovu soudu!“
12 Festo atakambirana ndi akuluakulu abwalo lake, anati, “Popeza wapempha kupita kwa Kaisara, kwa Kaisara udzapitadi!”
Festus se odebral k poradě se svými rádci a vynesl rozsudek: „Odvoláváš se k císaři, tedy tam půjdeš.“
13 Patapita masiku ochepa mfumu Agripa pamodzi ndi Bernisi anabwera ku Kaisareya kudzalonjera Festo.
Po několika dnech navštívil Césareju král Herodes Agrippa se svojí sestrou Bereniké. Přijeli přivítat Festa a zdrželi se u něho delší dobu. Festus se jim při jedné příležitosti zmínil: „Podědil jsem tu po Felixovi zvláštního vězně.
14 Atakhala kumeneko masiku angapo, Festo anafotokozera mfumuyo za mlandu wa Paulo. Iye anati, “Kuli munthu wina kuno amene Felike anamusiya mʼndende.
15 Nditapita ku Yerusalemu akulu a ansembe ndi akuluakulu a Ayuda anandifotokozera mlandu wake ndipo anandipempha kuti ndigamule kuti ndi wolakwa.
V Jeruzalémě na něho žalovali velekněží a velerada a žádali na mně rozsudek smrti.
16 “Ine ndinawayankha kuti si mwambo wa Aroma kungomupereka munthu ayi. Munthu woyimbidwa mlanduyo amayenera kukumana nawo omunenezawo, kuti iye akhale ndi mwayi woyankhapo pa zimene akumuyimba mlanduzo.
Musel jsem jim dát lekci z římského práva a poučit je, že my Římané nikoho nesoudíme bez řádného slyšení obou stran a že každý musí dostat možnost obhajoby.
17 Atabwera kuno pamodzi ndi ine, sindinachedwetse mlanduwo, koma ndinayitanitsa bwalo mmawa mwake ndi kulamula kuti amubweretse munthuyo.
Hned po mém návratu do Césareje se dostavili žalobci, a tak jsem toho muže vyslechl.
18 Omuyimba mlandu aja atayimirira kuti ayankhule, iwo sananene cholakwa chilichonse chimene ndimayembekezera.
Očekával jsem kdovíjaké zločiny, ale nic takového mu nemohli dokázat.
19 Mʼmalo mwake, anatsutsana naye pa fundo zina za chipembedzo chawo ndi za munthu wakufa, dzina lake Yesu, amene Paulo akuti ali moyo.
Mají nějaké náboženské spory o jakéhosi Ježíše; byl popraven, ale ten Pavel tvrdí, že žije.
20 Ine ndinathedwa nzeru wosadziwa momwe ndikanafufuzira nkhaniyi; kotero ndinafunsa ngati akanafuna kupita ku Yerusalemu kuti akaweruzidwe kumeneko.
V tom se ovšem nevyznám. Když jsem mu navrhl, aby se obhajoval přímo v Jeruzalémě, trval na tom, aby byl ponechán v pravomoci římského soudu. Je to římský občan, a dokonce se odvolal k císaři. Tak ho tu mám ve vězení a s příštím transportem ho musím poslat do Říma.“
21 Koma Paulo anapempha kuti akaonekere pamaso pa mfumu ya Chiroma, ndipo ndinalamula kuti asungidwe mpaka pamene ndidzamutumize kwa Kaisara.”
22 Ndipo Agripa anati kwa Festo, “Ine ndikufuna ndimumve ndekha munthu ameneyu.” Iye anayankha kuti, “Mudzamumva mawa.”
Agrippa řekl Festovi: „Ten člověk mě zajímá, rád bych si ho poslechl.“Festus tedy navrhl, že uspořádá slyšení hned následujícího dne.
23 Mmawa mwake Agripa ndi Bernisi anabwera mwaulemu waukulu waufumu nalowa mʼbwalo la milandu pamodzi ndi akulu a asilikali ndiponso akuluakulu a mu mzindawo. Atalamula Festo kuti Paulo abwere, anabweradi.
Nazítří se dostavili Agrippa a Bereniké v celé královské pompě s dvorní suitou i hodnostáři města.
24 Festo anati, “Mfumu Agripa, ndi onse amene muli nafe pano, mukumuona munthu uyu! Ayuda onse anandipempha ine za uyu ku Yerusalemu ndiponso kuno ku Kaisareya, mofuwula kuti, ameneyu sayenera kukhala ndi moyo.
Festus dal předvést Pavla a představil ho slovy: „Králi Agrippo, dámy a pánové! To je člověk, jehož smrt tak neodbytně vymáhají židé v Jeruzalémě i zde.
25 Ine ndinapeza kuti iyeyu sanachite kanthu koyenera kufa, koma popeza anapempha kuti apite kwa mfumu ya Chiroma, ine ndinatsimikiza zomutumiza ku Roma.
Nedopustil se ničeho, za co by podle římského práva mohl být odsouzen k smrti. Sám se však odvolal k jeho císařskému veličenstvu, a tak jsem se rozhodl poslat ho do Říma. Jsem teď na rozpacích, co uvést v obžalovacím spisu, který musím vystavit. Snad mně v tom pomůžete vy, znalci židovských záležitostí, a zvláště ty, králi, až ho vyslechnete.“
26 Koma ndilibe kanthu kenikeni koti ndilembere Wolemekezekayo za iyeyu. Nʼchifukwa chake ndabwera naye pamaso pa nonsenu, makamaka kwa inuyo mfumu Agripa, kuti mwina mukamufunsitsa ndikhale ndi choti ndilembe.
27 Pakuti ine ndikuganiza kuti ndi chinthu chopanda nzeru kutumiza wamʼndende popanda kutchula zifukwa zenizeni za mlandu wake.”