< Machitidwe a Atumwi 24 >
1 Patapita masiku asanu mkulu wa ansembe Hananiya, pamodzi ndi akuluakulu ena ndi katswiri woyankhulira anthu pa milandu wotchedwa Tertuliyo anapita ku Kaisareya ndipo anafotokoza mlandu wa Paulo kwa Bwanamkubwayo.
pañcabhyō dinēbhyaḥ paraṁ hanānīyanāmā mahāyājakō'dhipatēḥ samakṣaṁ paulasya prātikūlyēna nivēdayituṁ tartullanāmānaṁ kañcana vaktāraṁ prācīnajanāṁśca saṅginaḥ kr̥tvā kaisariyānagaram āgacchat|
2 Atamuyitana Paulo, ndipo Tertuliyo anafotokozera Felike nkhani yonse ya Paulo. Iye anati, “Wolemekezeka, ife takhala pamtendere nthawi yayitali chifukwa cha inu, ndipo utsogoleri wanu wanzeru wabweretsa kusintha mʼdziko lino.
tataḥ paulē samānītē sati tartullastasyāpavādakathāṁ kathayitum ārabhata hē mahāmahimaphīlikṣa bhavatō vayam atinirvvighnaṁ kālaṁ yāpayāmō bhavataḥ pariṇāmadarśitayā ētaddēśīyānāṁ bahūni maṅgalāni ghaṭitāni,
3 Wolemekezeka Felike ife timazilandira zimenezi moyamika kwambiri ponseponse ndi mwa njira iliyonse.
iti hētō rvayamatikr̥tajñāḥ santaḥ sarvvatra sarvvadā bhavatō guṇān gāyamaḥ|
4 Koma kuti tisakuchedwetseni, ndikupempha kuti mwa kuleza mtima kwanu mutimvere ife.
kintu bahubhiḥ kathābhi rbhavantaṁ yēna na virañjayāmi tasmād vinayē bhavān banukampya madalpakathāṁ śr̥ṇōtu|
5 “Ife tapeza kuti munthu uyu amayambitsa mavuto ndi kuwutsa mapokoso pakati pa Ayuda onse a dziko lonse lapansi. Iyeyu ndi mtsogoleri wa mpatuko wa Anazareti.
ēṣa mahāmārīsvarūpō nāsaratīyamatagrāhisaṁghātasya mukhyō bhūtvā sarvvadēśēṣu sarvvēṣāṁ yihūdīyānāṁ rājadrōhācaraṇapravr̥ttiṁ janayatītyasmābhi rniścitaṁ|
6 Anayesera ngakhale kudetsa Nyumba ya Mulungu wathu. Ndiye ife tinamugwira.
sa mandiramapi aśuci karttuṁ cēṣṭitavān; iti kāraṇād vayam ēnaṁ dhr̥tvā svavyavasthānusārēṇa vicārayituṁ prāvarttāmahi;
7 Koma, mkulu wa asilikali Lusiya anafika mwamphamvu namuchotsa mʼmanja mwathu.
kintu luṣiyaḥ sahasrasēnāpatirāgatya balād asmākaṁ karēbhya ēnaṁ gr̥hītvā
8 Ndipo Lusiya analamula kuti amene anali naye ndi mlandu abwere kwa inu. Mukamufunsa ameneyu kwa nokha mudzadziwa choonadi cha zimene ife tikumunenera.”
ētasyāpavādakān bhavataḥ samīpam āgantum ājñāpayat| vayaṁ yasmin tamapavādāmō bhavatā padapavādakathāyāṁ vicāritāyāṁ satyāṁ sarvvaṁ vr̥ttāntaṁ vēdituṁ śakṣyatē|
9 Ayuda anavomereza nanenetsa kuti zimenezi zinali zoona.
tatō yihūdīyā api svīkr̥tya kathitavanta ēṣā kathā pramāṇam|
10 Bwanamkubwayo atakodola Paulo ndi kulola kuti ayankhule, Pauloyo anati, “Ine ndikudziwa kuti inu mwakhala mukuweruza dziko lino zaka zambiri, kotero ndikukondwera kuti ndikudziteteza ndekha pamaso panu.
adhipatau kathāṁ kathayituṁ paulaṁ pratīṅgitaṁ kr̥tavati sa kathitavān bhavān bahūn vatsarān yāvad ētaddēśasya śāsanaṁ karōtīti vijñāya pratyuttaraṁ dātum akṣōbhō'bhavam|
11 Inu mukhoza kupeza umboni wake. Sipanapite masiku khumi ndi awiri chipitireni changa ku Yerusalemu kukapembedza.
adya kēvalaṁ dvādaśa dināni yātāni, aham ārādhanāṁ karttuṁ yirūśālamanagaraṁ gatavān ēṣā kathā bhavatā jñātuṁ śakyatē;
12 Amene akundiyimba mlanduwa sanandipeze mʼNyumba ya Mulungu ndi kutsutsana ndi wina aliyense kapena kuyambitsa chisokonezo mʼsunagoge kapena pena paliponse mu mzindamo.
kintvibhē māṁ madhyēmandiraṁ kēnāpi saha vitaṇḍāṁ kurvvantaṁ kutrāpi bhajanabhavanē nagarē vā lōkān kupravr̥ttiṁ janayantuṁ na dr̥ṣṭavantaḥ|
13 Ndipo sangathe kupereka umboni wa mlandu umene akundiyimba inewu.
idānīṁ yasmin yasmin mām apavadantē tasya kimapi pramāṇaṁ dātuṁ na śaknuvanti|
14 Komatu ine ndikuvomera kuti ndimapembedza Mulungu wa makolo athu, monga wotsatira wa Njirayo, imene iwo akuyitchula mpatuko. Ine ndimakhulupirira chilichonse chimene chimagwirizana ndi malamulo ndiponso zimene zinalembedwa ndi Aneneri.
kintu bhaviṣyadvākyagranthē vyavasthāgranthē ca yā yā kathā likhitāstē tāsu sarvvāsu viśvasya yanmatam imē vidharmmaṁ jānanti tanmatānusārēṇāhaṁ nijapitr̥puruṣāṇām īśvaram ārādhayāmītyahaṁ bhavataḥ samakṣam aṅgīkarōmi|
15 Ine ndili nacho chiyembekezo chomwecho chimene iwo ali nacho mwa Mulungu, kuti kudzakhala kuuka kwa akufa kwa olungama ndiponso kwa ochimwa.
dhārmmikāṇām adhārmmikāṇāñca pramītalōkānāmēvōtthānaṁ bhaviṣyatīti kathāmimē svīkurvvanti tathāhamapi tasmin īśvarē pratyāśāṁ karōmi;
16 Kotero ine ndimayesetsa kuti ndikhale ndi chikumbumtima chosanditsutsa pamaso pa Mulungu ndi anthu onse.
īśvarasya mānavānāñca samīpē yathā nirdōṣō bhavāmi tadarthaṁ satataṁ yatnavān asmi|
17 “Patapita zaka zambiri, ndinabwera ku Yerusalemu kudzapereka mphatso kwa anthu osauka a mtundu wanga komanso kudzapereka nsembe.
bahuṣu vatsarēṣu gatēṣu svadēśīyalōkānāṁ nimittaṁ dānīyadravyāṇi naivēdyāni ca samādāya punarāgamanaṁ kr̥tavān|
18 Pamene ndinkachita zimenezi, iwo anandipeza mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu nditachita mwambo wodziyeretsa. Panalibe gulu la anthu kapena kuti ndimachita za chisokonezo chilichonse.
tatōhaṁ śuci rbhūtvā lōkānāṁ samāgamaṁ kalahaṁ vā na kāritavān tathāpyāśiyādēśīyāḥ kiyantō yihudīyalōkā madhyēmandiraṁ māṁ dhr̥tavantaḥ|
19 Koma pali Ayuda ena ochokera ku Asiya, amene amayenera kukhala pano pamaso panu, kundiyimba mlandu ngati ali ndi kalikonse konditsutsa ine.
mamōpari yadi kācidapavādakathāsti tarhi bhavataḥ samīpam upasthāya tēṣāmēva sākṣyadānam ucitam|
20 Kapena awa amene ali panowa anene mlandu umene anapeza mwa ine, pamene ndinayima pamaso pa Bwalo lawo Lalikulu.
nōcēt pūrvvē mahāsabhāsthānāṁ lōkānāṁ sannidhau mama daṇḍāyamānatvasamayē, ahamadya mr̥tānāmutthānē yuṣmābhi rvicāritōsmi,
21 Koma cholakwa changa chingathe kukhala chokhachi chakuti, nditayima pamaso pawo ndinafuwula kuti, ‘Mukundiweruza ine lero chifukwa ndimakhulupirira kuti akufa adzauka.’”
tēṣāṁ madhyē tiṣṭhannahaṁ yāmimāṁ kathāmuccaiḥ svarēṇa kathitavān tadanyō mama kōpi dōṣō'labhyata na vēti varam ētē samupasthitalōkā vadantu|
22 Kenaka Felike, amene amadziwa bwino za Njirayo, anayamba wayimitsa mlanduwo, nati, “Ndidzagamula mlandu wako akabwera mkulu wa asilikali Lusiya.”
tadā phīlikṣa ētāṁ kathāṁ śrutvā tanmatasya viśēṣavr̥ttāntaṁ vijñātuṁ vicāraṁ sthagitaṁ kr̥tvā kathitavān luṣiyē sahasrasēnāpatau samāyātē sati yuṣmākaṁ vicāram ahaṁ niṣpādayiṣyāmi|
23 Iye analamulira woyangʼanira asilikali 100 kuti alondere Paulo, koma azimupatsako ufulu ndiponso kulola abwenzi ake kuti adzimusamalira.
anantaraṁ bandhanaṁ vinā paulaṁ rakṣituṁ tasya sēvanāya sākṣātkaraṇāya vā tadīyātmīyabandhujanān na vārayituñca śamasēnāpatim ādiṣṭavān|
24 Patapita masiku angapo Felike anabwera pamodzi ndi mkazi wake Drusila, amene anali Myuda. Anayitana Paulo ndipo anamvetsera zimene amayankhula za chikhulupiriro mwa Khristu Yesu.
alpadināt paraṁ phīlikṣō'dhipati rdruṣillānāmnā yihūdīyayā svabhāryyayā sahāgatya paulamāhūya tasya mukhāt khrīṣṭadharmmasya vr̥ttāntam aśrauṣīt|
25 Paulo atayankhula za chilungamo, za kudziretsa ndiponso za chiweruzo chimene chikubwera, Felike anachita mantha ndipo anati, “Basi tsopano! Pita. Tidzakuyitanitsa tikadzapeza mpata.”
paulēna nyāyasya parimitabhōgasya caramavicārasya ca kathāyāṁ kathitāyāṁ satyāṁ phīlikṣaḥ kampamānaḥ san vyāharad idānīṁ yāhi, aham avakāśaṁ prāpya tvām āhūsyāmi|
26 Pa nthawi imeneyi amayembekeza kuti Paulo adzamupatsa ndalama, nʼchifukwa chake amamuyitanitsa kawirikawiri ndi kumayankhula naye.
muktipraptyarthaṁ paulēna mahyaṁ mudrādāsyantē iti patyāśāṁ kr̥tvā sa punaḥ punastamāhūya tēna sākaṁ kathōpakathanaṁ kr̥tavān|
27 Patapita zaka ziwiri, Porkiyo Festo analowa mʼmalo mwa Felike, koma anamusiya Paulo mʼndende, chifukwa amafuna kuti Ayuda amukonde.
kintu vatsaradvayāt paraṁ parkiyaphīṣṭa phālikṣasya padaṁ prāptē sati phīlikṣō yihūdīyān santuṣṭān cikīrṣan paulaṁ baddhaṁ saṁsthāpya gatavān|