< Machitidwe a Atumwi 24 >

1 Patapita masiku asanu mkulu wa ansembe Hananiya, pamodzi ndi akuluakulu ena ndi katswiri woyankhulira anthu pa milandu wotchedwa Tertuliyo anapita ku Kaisareya ndipo anafotokoza mlandu wa Paulo kwa Bwanamkubwayo.
Men fem Dage derefter drog Ypperstepræsten Ananias ned med nogle Ældste og en Taler, Tertullus, og disse førte Klage for Landshøvdingen imod Paulus.
2 Atamuyitana Paulo, ndipo Tertuliyo anafotokozera Felike nkhani yonse ya Paulo. Iye anati, “Wolemekezeka, ife takhala pamtendere nthawi yayitali chifukwa cha inu, ndipo utsogoleri wanu wanzeru wabweretsa kusintha mʼdziko lino.
Da han nu var kaldt ind, begyndte Tertullus at anklage ham og sagde:
3 Wolemekezeka Felike ife timazilandira zimenezi moyamika kwambiri ponseponse ndi mwa njira iliyonse.
„At vi ved dig nyde megen Fred, og at Forbedringer i alle Retninger og alle Vegne skaffes dette Folk ved din Omsorg, mægtigste Feliks! det erkende vi med al Taknemmelighed.
4 Koma kuti tisakuchedwetseni, ndikupempha kuti mwa kuleza mtima kwanu mutimvere ife.
Men for at jeg ikke skal opholde dig for længe, beder jeg, at du efter din Mildhed vil høre os kortelig.
5 “Ife tapeza kuti munthu uyu amayambitsa mavuto ndi kuwutsa mapokoso pakati pa Ayuda onse a dziko lonse lapansi. Iyeyu ndi mtsogoleri wa mpatuko wa Anazareti.
Vi have nemlig fundet, at denne Mand er en Pest og en Oprørsstifter iblandt alle Jøderne hele Verden over, samt er Fører for Nazaræernes Parti,
6 Anayesera ngakhale kudetsa Nyumba ya Mulungu wathu. Ndiye ife tinamugwira.
ja, han har endog forsøgt at vanhellige Helligdommen. Vi grebe ham da ogsaa [og vilde have dømt ham efter vor Lov.
7 Koma, mkulu wa asilikali Lusiya anafika mwamphamvu namuchotsa mʼmanja mwathu.
Men Krigsøversten Lysias kom til og borttog ham med megen Vold af vore Hænder
8 Ndipo Lusiya analamula kuti amene anali naye ndi mlandu abwere kwa inu. Mukamufunsa ameneyu kwa nokha mudzadziwa choonadi cha zimene ife tikumunenera.”
og bød hans Anklagere komme til dig]. Af ham kan du selv, naar du undersøger det, erfare alt det, hvorfor vi anklage ham.”
9 Ayuda anavomereza nanenetsa kuti zimenezi zinali zoona.
Men ogsaa Jøderne stemmede i med og paastode, at dette forholdt sig saaledes.
10 Bwanamkubwayo atakodola Paulo ndi kulola kuti ayankhule, Pauloyo anati, “Ine ndikudziwa kuti inu mwakhala mukuweruza dziko lino zaka zambiri, kotero ndikukondwera kuti ndikudziteteza ndekha pamaso panu.
Og Paulus svarede, da Landshøvdingen gav ham et Vink, at han skulde tale: „Efterdi jeg ved, at du i mange Aar har været Dommer for dette Folk, vil jeg frimodigt forsvare min Sag,
11 Inu mukhoza kupeza umboni wake. Sipanapite masiku khumi ndi awiri chipitireni changa ku Yerusalemu kukapembedza.
da du kan forvisse dig om, at det er ikke mere end tolv Dage, siden jeg kom op for at tilbede i Jerusalem.
12 Amene akundiyimba mlanduwa sanandipeze mʼNyumba ya Mulungu ndi kutsutsana ndi wina aliyense kapena kuyambitsa chisokonezo mʼsunagoge kapena pena paliponse mu mzindamo.
Og de have ikke fundet mig i Ordveksel med nogen eller i Færd med at vække Folkeopløb, hverken i Helligdommen eller i Synagogerne eller omkring i Staden.
13 Ndipo sangathe kupereka umboni wa mlandu umene akundiyimba inewu.
Og de kunne ej heller bevise dig det, som de nu anklage mig for.
14 Komatu ine ndikuvomera kuti ndimapembedza Mulungu wa makolo athu, monga wotsatira wa Njirayo, imene iwo akuyitchula mpatuko. Ine ndimakhulupirira chilichonse chimene chimagwirizana ndi malamulo ndiponso zimene zinalembedwa ndi Aneneri.
Men dette bekender jeg for dig, at jeg efter den Vej, som de kalde et Parti, tjener vor fædrene Gud saaledes, at jeg tror paa alt det, som staar i Loven, og det, som er skrevet hos Profeterne,
15 Ine ndili nacho chiyembekezo chomwecho chimene iwo ali nacho mwa Mulungu, kuti kudzakhala kuuka kwa akufa kwa olungama ndiponso kwa ochimwa.
og har det Haab til Gud, som ogsaa disse selv forvente, at der skal komme en Opstandelse baade af retfærdige og af uretfærdige.
16 Kotero ine ndimayesetsa kuti ndikhale ndi chikumbumtima chosanditsutsa pamaso pa Mulungu ndi anthu onse.
Derfor øver ogsaa jeg mig i altid at have en uskadt Samvittighed for Gud og Menneskene.
17 “Patapita zaka zambiri, ndinabwera ku Yerusalemu kudzapereka mphatso kwa anthu osauka a mtundu wanga komanso kudzapereka nsembe.
Men efter flere Aars Forløb er jeg kommen for at bringe Almisser til mit Folk og Ofre,
18 Pamene ndinkachita zimenezi, iwo anandipeza mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu nditachita mwambo wodziyeretsa. Panalibe gulu la anthu kapena kuti ndimachita za chisokonezo chilichonse.
hvad de fandt mig i Færd med, da jeg var bleven renset i Helligdommen, og ikke med Opløb og Larm; men det var nogle Jøder fra Asien,
19 Koma pali Ayuda ena ochokera ku Asiya, amene amayenera kukhala pano pamaso panu, kundiyimba mlandu ngati ali ndi kalikonse konditsutsa ine.
og de burde nu være til Stede hos dig og klage, om de have noget paa mig at sige.
20 Kapena awa amene ali panowa anene mlandu umene anapeza mwa ine, pamene ndinayima pamaso pa Bwalo lawo Lalikulu.
Eller lad disse her selv sige, hvad Uret de have fundet hos mig, da jeg stod for Raadet,
21 Koma cholakwa changa chingathe kukhala chokhachi chakuti, nditayima pamaso pawo ndinafuwula kuti, ‘Mukundiweruza ine lero chifukwa ndimakhulupirira kuti akufa adzauka.’”
uden det skulde være dette ene Ord, som jeg raabte, da jeg stod iblandt dem: Jeg dømmes i Dag af eder for dødes Opstandelse.”
22 Kenaka Felike, amene amadziwa bwino za Njirayo, anayamba wayimitsa mlanduwo, nati, “Ndidzagamula mlandu wako akabwera mkulu wa asilikali Lusiya.”
Nu udsatte Feliks Sagen, da han vidste ret god Besked om Vejen, og sagde: „Naar Krigsøversten Lysias kommer herned, vil jeg paakende eders Sag.”
23 Iye analamulira woyangʼanira asilikali 100 kuti alondere Paulo, koma azimupatsako ufulu ndiponso kulola abwenzi ake kuti adzimusamalira.
Og han befalede Høvedsmanden, at han skulde holdes bevogtet, men med Lempelse, og at han ikke maatte forbyde nogen af hans egne at gaa ham til Haande.
24 Patapita masiku angapo Felike anabwera pamodzi ndi mkazi wake Drusila, amene anali Myuda. Anayitana Paulo ndipo anamvetsera zimene amayankhula za chikhulupiriro mwa Khristu Yesu.
Men nogle Dage efter kom Feliks med sin Hustru Drusilla, som var en Jødinde, og lod Paulus hente og hørte ham om Troen paa Kristus Jesus.
25 Paulo atayankhula za chilungamo, za kudziretsa ndiponso za chiweruzo chimene chikubwera, Felike anachita mantha ndipo anati, “Basi tsopano! Pita. Tidzakuyitanitsa tikadzapeza mpata.”
Men da han talte med ham om Retfærdighed og Afholdenhed og den kommende Dom, blev Feliks forfærdet og svarede: „Gaa for denne Gang; men naar jeg faar Tid, vil jeg lade dig kalde til mig.”
26 Pa nthawi imeneyi amayembekeza kuti Paulo adzamupatsa ndalama, nʼchifukwa chake amamuyitanitsa kawirikawiri ndi kumayankhula naye.
Tillige haabede han ogsaa, at Paulus skulde give ham Penge; derfor lod han ham ogsaa oftere hente og samtalede med ham.
27 Patapita zaka ziwiri, Porkiyo Festo analowa mʼmalo mwa Felike, koma anamusiya Paulo mʼndende, chifukwa amafuna kuti Ayuda amukonde.
Men da to Aar vare forløbne, fik Feliks Porkius Festus til Efterfølger; og da Feliks vilde fortjene sig Tak af Jøderne, lod han Paulus blive tilbage i Lænker.

< Machitidwe a Atumwi 24 >