< Machitidwe a Atumwi 23 >

1 Paulo anayangʼanitsitsa anthu a Bwalo Lalikulu nati, “Abale anga, ndakhala ndi chikumbumtima chabwino pamaso pa Mulungu mpaka lero lino.”
sabhāsadlokān prati paulo'nanyadṛṣṭyā paśyan akathayat, he bhrātṛgaṇā adya yāvat saralena sarvvāntaḥkaraṇeneśvarasya sākṣād ācarāmi|
2 Chifukwa cha mawu amenewa, mkulu wa ansembe Ananiya analamulira amene anali pafupi ndi Paulo kuti amumenye pakamwa.
anena hanānīyanāmā mahāyājakastaṁ kapole capeṭenāhantuṁ samīpasthalokān ādiṣṭavān|
3 Pamenepo Paulo anamuwuza kuti, “Mulungu adzakukantha, iwe munthu wachiphamaso! Wakhala pamenepo kuti undiweruze ine monga mwalamulo, koma iweyo ukuphwanya lamulolo polamulira kuti andimenye!”
tadā paulastamavadat, he bahiṣpariṣkṛta, īśvarastvāṁ praharttum udyatosti, yato vyavasthānusāreṇa vicārayitum upaviśya vyavasthāṁ laṅghitvā māṁ praharttum ājñāpayasi|
4 Anthu amene anayimirira pafupi ndi Paulo anati, “Bwanji ukunyoza mkulu wa ansembe wa Mulungu?”
tato nikaṭasthā lokā akathayan, tvaṁ kim īśvarasya mahāyājakaṁ nindasi?
5 Paulo anayankha nati, “Abale, ine sindinazindikire kuti ndi mkulu wa ansembe; pakuti kunalembedwa kuti, ‘Usayankhule zoyipa kwa mtsogoleri wa anthu ako.’”
tataḥ paulaḥ pratibhāṣitavān he bhrātṛgaṇa mahāyājaka eṣa iti na buddhaṁ mayā tadanyacca svalokānām adhipatiṁ prati durvvākyaṁ mā kathaya, etādṛśī lipirasti|
6 Paulo atazindikira kuti ena mwa iwo anali Asaduki ndiponso ena anali Afarisi, anafuwula mʼbwalo muja kuti, “Abale anga, ine ndine Mfarisi, mwana wa Mfarisi. Ndikuweruzidwa chifukwa cha chiyembekezo cha kuuka kwa akufa.”
anantaraṁ paulasteṣām arddhaṁ sidūkilokā arddhaṁ phirūśilokā iti dṛṣṭvā proccaiḥ sabhāsthalokān avadat he bhrātṛgaṇa ahaṁ phirūśimatāvalambī phirūśinaḥ satnānaśca, mṛtalokānām utthāne pratyāśākaraṇād ahamapavāditosmi|
7 Iye atanena zimenezi, mkangano unabuka pakati pa Afarisi ndi Asaduki mpaka anthu kugawikana.
iti kathāyāṁ kathitāyāṁ phirūśisidūkinoḥ parasparaṁ bhinnavākyatvāt sabhāyā madhye dvau saṁghau jātau|
8 Asaduki amati kulibe kuuka kwa akufa, kulibenso ngakhale angelo kapena mizimu, koma Afarisi amakhulupirira zonsezi.
yataḥ sidūkilokā utthānaṁ svargīyadūtā ātmānaśca sarvveṣām eteṣāṁ kamapi na manyante, kintu phirūśinaḥ sarvvam aṅgīkurvvanti|
9 Panali phokoso lalikulu, ndipo aphunzitsi ena amalamulo amene anali a gulu la Afarisi anayimirira natsutsa kwambiri. Iwo anati, “Ife sitikupeza cholakwa ndi munthu uyu, chifukwa mwina ndi mzimu kapena mngelo amene wayankhula naye.”
tataḥ parasparam atiśayakolāhale samupasthite phirūśināṁ pakṣīyāḥ sabhāsthā adhyāpakāḥ pratipakṣā uttiṣṭhanto 'kathayan, etasya mānavasya kamapi doṣaṁ na paśyāmaḥ; yadi kaścid ātmā vā kaścid dūta enaṁ pratyādiśat tarhi vayam īśvarasya prātikūlyena na yotsyāmaḥ|
10 Mkangano unakula kwambiri kotero kuti mkulu wa asilikali anachita mantha kuti mwina anthu angakhadzule Paulo. Iye analamulira asilikali ake apite kukamuchotsa pakati pawo mwamphamvu ndi kubwera naye ku malo a asilikaliwo.
tasmād atīva bhinnavākyatve sati te paulaṁ khaṇḍaṁ khaṇḍaṁ kariṣyantītyāśaṅkayā sahasrasenāpatiḥ senāgaṇaṁ tatsthānaṁ yātuṁ sabhāto balāt paulaṁ dhṛtvā durgaṁ netañcājñāpayat|
11 Usiku omwewo Ambuye anayimirira pambali pa Paulo nati, “Limba mtima! Monga wandichitira Ine umboni mu Yerusalemu, moteronso uyenera kundichitira umboni ku Roma.”
rātro prabhustasya samīpe tiṣṭhan kathitavān he paula nirbhayo bhava yathā yirūśālamnagare mayi sākṣyaṁ dattavān tathā romānagarepi tvayā dātavyam|
12 Kutacha Ayuda ena anakonza chiwembu ndipo analumbira kuti sadya kapena kumwa mpaka atapha Paulo.
dine samupasthite sati kiyanto yihūdīyalokā ekamantraṇāḥ santaḥ paulaṁ na hatvā bhojanapāne kariṣyāma iti śapathena svān abadhnan|
13 Anthu amene anakonza chiwembuchi analipo makumi anayi.
catvāriṁśajjanebhyo'dhikā lokā iti paṇam akurvvan|
14 Iwo anapita kwa akulu a ansembe ndi akuluakulu a Ayuda nakawawuza kuti, “Ife talumbira kolimba kuti sitidya kalikonse mpaka titapha Paulo.
te mahāyājakānāṁ prācīnalokānāñca samīpaṁ gatvā kathayan, vayaṁ paulaṁ na hatvā kimapi na bhokṣyāmahe dṛḍhenānena śapathena baddhvā abhavāma|
15 Tsopano inu pamodzi ndi akuluakulu a Bwalo Lalikulu mupemphe mkulu wa asilikali kuti akubweretsereni Paulo ngati kuti mukufuna kudziwa bwino za mlandu wake. Ife takonzeka kudzamupha asanafike kumeneko.”
ataeva sāmprataṁ sabhāsadlokaiḥ saha vayaṁ tasmin kañcid viśeṣavicāraṁ kariṣyāmastadarthaṁ bhavān śvo 'smākaṁ samīpaṁ tam ānayatviti sahasrasenāpataye nivedanaṁ kuruta tena yuṣmākaṁ samīpaṁ upasthiteḥ pūrvvaṁ vayaṁ taṁ hantu sajjiṣyāma|
16 Koma mwana wa mlongo wake wa Paulo atamva za chiwembuchi, anapita ku malo a asilikali aja namufotokozera Paulo.
tadā paulasya bhāgineyasteṣāmiti mantraṇāṁ vijñāya durgaṁ gatvā tāṁ vārttāṁ paulam uktavān|
17 Paulo anayitana mmodzi wa wolamulira asilikali 100 aja, namuwuza kuti, “Pita naye mnyamatayu kwa mkulu wa asilikali. Iyeyu ali ndi mawu oti akamuwuze.”
tasmāt paula ekaṁ śatasenāpatim āhūya vākyamidam bhāṣitavān sahasrasenāpateḥ samīpe'sya yuvamanuṣyasya kiñcinnivedanam āste, tasmāt tatsavidham enaṁ naya|
18 Anamutengadi mnyamatayo napita naye kwa mkulu wa asilikali uja, nati, “Wamʼndende uja Paulo anandiyitana, nandipempha kuti ndibweretse mnyamatayu kwa inu chifukwa ali ndi kanthu koti akuwuzeni.”
tataḥ sa tamādāya sahasrasenāpateḥ samīpam upasthāya kathitavān, bhavataḥ samīpe'sya kimapi nivedanamāste tasmāt bandiḥ paulo māmāhūya bhavataḥ samīpam enam ānetuṁ prārthitavān|
19 Mkulu wa asilikali uja anagwira dzanja mnyamatayo napita naye paseli ndipo anamufunsa kuti, “Kodi ukufuna kuti undiwuze chiyani?”
tadā sahasrasenāpatistasya hastaṁ dhṛtvā nirjanasthānaṁ nītvā pṛṣṭhavān tava kiṁ nivedanaṁ? tat kathaya|
20 Mnyamatayo anati, “Ayuda agwirizana zoti akupempheni kuti mawa mubwere ndi Paulo ku Bwalo Lalikulu, ngati kuti akufuna kudziwa bwino za iye.
tataḥ sokathayat, yihūdīyalākāḥ paule kamapi viśeṣavicāraṁ chalaṁ kṛtvā taṁ sabhāṁ netuṁ bhavataḥ samīpe nivedayituṁ amantrayan|
21 Inu musawamvere, chifukwa pali anthu opitirira makumi anayi amene akumudikirira pa njira. Iwo alumbira kuti sadya kapena kumwa mpaka atapha Paulo. Panopa ndi okonzeka kale, akungodikira kuti muwavomere pempho lawo.”
kintu mavatā tanna svīkarttavyaṁ yatasteṣāṁ madhyevarttinaścatvāriṁśajjanebhyo 'dhikalokā ekamantraṇā bhūtvā paulaṁ na hatvā bhojanaṁ pānañca na kariṣyāma iti śapathena baddhāḥ santo ghātakā iva sajjitā idānīṁ kevalaṁ bhavato 'numatim apekṣante|
22 Mkulu wa asilikaliyo anawuza mnyamatayo kuti apite koma anamuchenjeza kuti, “Usawuze munthu aliyense kuti wandifotokozera zimenezi.”
yāmimāṁ kathāṁ tvaṁ niveditavān tāṁ kasmaicidapi mā kathayetyuktvā sahasrasenāpatistaṁ yuvānaṁ visṛṣṭavān|
23 Kenaka mkulu wa asilikaliyo anayitana awiri a asilikali olamulira asilikali 100 nawalamula kuti, “Uzani asilikali 200, asilikali 70 okwera pa akavalo ndi 200 onyamula mikondo kuti akonzeke kupita ku Kaisareya usiku omwe uno nthawi ya 9 koloko.
anantaraṁ sahasrasenāpati rdvau śatasenāpatī āhūyedam ādiśat, yuvāṁ rātrau praharaikāvaśiṣṭāyāṁ satyāṁ kaisariyānagaraṁ yātuṁ padātisainyānāṁ dve śate ghoṭakārohisainyānāṁ saptatiṁ śaktidhārisainyānāṁ dve śate ca janān sajjitān kurutaṁ|
24 Mumukonzerenso Paulo akavalo woti akwerepo kuti akafike bwino kwa bwanamkubwa Felike.”
paulam ārohayituṁ phīlikṣādhipateḥ samīpaṁ nirvvighnaṁ netuñca vāhanāni samupasthāpayataṁ|
25 Iye analemba kalata iyi:
aparaṁ sa patraṁ likhitvā dattavān tallikhitametat,
26 Ine Klaudiyo Lusiya, Kwa wolemekezeka, bwanamkubwa Felike: Ndikupereka moni.
mahāmahimaśrīyuktaphīlikṣādhipataye klaudiyaluṣiyasya namaskāraḥ|
27 Munthuyo Ayuda anamugwira ndipo anali pafupi kumupha, koma ine ndinapita ndi asilikali nʼkukamulanditsa pakuti ndinamva kuti ndi nzika ya Chiroma.
yihūdīyalokāḥ pūrvvam enaṁ mānavaṁ dhṛtvā svahastai rhantum udyatā etasminnantare sasainyohaṁ tatropasthāya eṣa jano romīya iti vijñāya taṁ rakṣitavān|
28 Ndinkafuna kudziwa mlandu umene anapalamula, choncho ndinapita naye ku Bwalo lawo Lalikulu.
kinnimittaṁ te tamapavadante tajjñātuṁ teṣā sabhāṁ tamānāyitavān|
29 Ine ndinapeza kuti amamuyimba mlandu wa nkhani ya malamulo awo, koma panalibe mlandu woyenera kumuphera kapena kumuyika mʼndende.
tatasteṣāṁ vyavasthāyā viruddhayā kayācana kathayā so'pavādito'bhavat, kintu sa śṛṅkhalabandhanārho vā prāṇanāśārho bhavatīdṛśaḥ kopyaparādho mayāsya na dṛṣṭaḥ|
30 Nditawuzidwa kuti amukonzera chiwembu munthuyu, ine ndamutumiza kwa inu msanga. Ine ndalamulanso amene akumuyimba mlanduwo kuti abwere kwa inu kudzafotokoza nkhaniyo.
tathāpi manuṣyasyāsya vadhārthaṁ yihūdīyā ghātakāiva sajjitā etāṁ vārttāṁ śrutvā tatkṣaṇāt tava samīpamenaṁ preṣitavān asyāpavādakāṁśca tava samīpaṁ gatvāpavaditum ājñāpayam| bhavataḥ kuśalaṁ bhūyāt|
31 Pamenepo asilikali aja anatenga Paulo monga anawalamulira napita naye ku Antipatri usiku.
sainyagaṇa ājñānusāreṇa paulaṁ gṛhītvā tasyāṁ rajanyām āntipātrinagaram ānayat|
32 Mmawa mwake iwo anabwerera ku malo a asilikali nasiya okwera pa akavalo kuti apitirire ndi Paulo.
pare'hani tena saha yātuṁ ghoṭakārūḍhasainyagaṇaṁ sthāpayitvā parāvṛtya durgaṁ gatavān|
33 Asilikali okwera pa akavalowo atafika ku Kaisareya anapereka kalatayo kwa bwanamkubwa, namuperekanso Paulo.
tataḥ pare ghoṭakārohisainyagaṇaḥ kaisariyānagaram upasthāya tatpatram adhipateḥ kare samarpya tasya samīpe paulam upasthāpitavān|
34 Bwanamkubwayo anawerenga kalatayo ndipo anamufunsa Paulo za dera limene amachokera. Atazindikira kuti amachokera ku Kilikiya,
tadādhipatistatpatraṁ paṭhitvā pṛṣṭhavān eṣa kimpradeśīyo janaḥ? sa kilikiyāpradeśīya eko jana iti jñātvā kathitavān,
35 iye anati, “Ndidzamva mlandu wako okuyimba mlandu akabwera kuno.” Ndipo analamulira kuti asilikali adzimulondera Paulo ku nyumba ya mfumu Herode.
tavāpavādakagaṇa āgate tava kathāṁ śroṣyāmi| herodrājagṛhe taṁ sthāpayitum ādiṣṭavān|

< Machitidwe a Atumwi 23 >