< Machitidwe a Atumwi 22 >

1 Iye anati, “Inu abale anga ndi makolo anga, tamvani mawu akudziteteza kwanga.”
Možjé bratje in očetje! čujte sedaj moj odgovor k vam.
2 Atamva iye akuyankhula Chihebri, anakhala chete. Kenaka Paulo anati,
(Ko so pa slišali, da jim v Hebrejskem jeziku govorí, bili so še bolj tiho.) In reče:
3 “Ine ndine Myuda, wobadwira ku Tarisisi wa ku Kilikiya, koma ndinaleredwa mu mzinda muno, ndinaphunzitsidwa mwatsatanetsatane kusunga malamulo a makolo athu ndi Gamalieli ndipo ndinali wodzipereka pa za Mulungu monga mmene inu mulili lero.
Jaz sem mož Jud, rojen v Tarsu Cilicijskem, odgojen pa v tem mestu pri nogah Gamalijelovih, podučen na tanko v očetovskej postavi, vnet za Boga, kakor ste vsi vi danes.
4 Ine ndinkazunza anthu otsatira Njirayi mpaka kuwapha. Ndinkagwira amuna ndi amayi ndi kuwayika mʼndende.
Jaz sem preganjal ta pot noter do smrti, vežoč in izdajoč v ječe možé in žene,
5 Mkulu wa ansembe ndiponso akuluakulu a Ayuda angathe kundichitira umboni. Iwowa anandipatsa makalata opita nawo kwa abale awo ku Damasiko. Ndipo ndinapita kumeneko kuti ndikawagwire anthu amenewa ndi kubwera nawo ku Yerusalemu kuti adzalangidwe.
Kakor mi tudi véliki duhoven priča, in vse starešinstvo; od kterih sem tudi pisem prejel do bratov in sem šel v Damask, da bi pripeljal tudi tiste, kteri so tam bili, zvezane v Jeruzalem, da bi se mučili.
6 “Nthawi ya masana, nditayandikira ku Damasiko, mwadzidzidzi kuwala kwakukulu kochokera kumwamba kunandizungulira.
Zgodí pa se, ko sem šel in sem se bližál Damasku, okoli poldneva, da me nagloma obsije velika svetloba z neba;
7 Ndinagwa pansi ndipo ndinamva mawu akuti, ‘Saulo! Saulo! Ukundizunziranji?’”
In padel sem na tla, in slišal sem glas, da mi pravi: Savel, Savel! kaj me preganjaš?
8 Ine ndinafunsa kuti, “Ndinu ndani Ambuye?” Iye anayankha kuti, “Ndine Yesu wa ku Nazareti, amene iwe ukumuzunza.”
Jaz sem pa odgovoril: Kdo si, Gospod? In reče mi: Jaz sem Jezus Nazarečan, kterega ti preganjaš.
9 Anzanga a paulendo anaona kuwalako, koma sanamve mawuwo, a Iye amene amayankhula nane.
Tisti pa, kteri so bili z menoj, videli so sicer svetlobo, in uplašili so se; ali glasú niso slišali, kteri mi je govoril.
10 Ine ndinafunsa kuti, “Kodi ndichite chiyani Ambuye?” Ambuye anati, “Imirira ndipo pita ku Damasiko. Kumeneko adzakuwuza zonse zimene ukuyenera kuchita.”
In rekel sem: Kaj naj storim, Gospod? A Gospod mi reče: Vstani in pojdi v Damask; in tam ti se bo povedalo vse, kar ti je odločeno, da storiš.
11 Anzanga anandigwira dzanja kupita nane ku Damasiko, popeza kuwala kunja kunandichititsa khungu.
Ko pa nisem videl od bliščeče te svetlobe, peljali so me za roko, kteri so bili z menoj, in prišel sem v Damask.
12 “Munthu wina dzina lake Hananiya anabwera kudzandiona. Iyeyu anali munthu woopa Mulungu ndi wosunga Malamulo. Ayuda onse okhala kumeneko amamupatsa ulemu waukulu.
Neki Ananija pa, človek pobožen po postavi, kteri ima pričevanje od vseh Judov, kteri tam prebivajo,
13 Iye anayimirira pafupi nane nati, ‘Mʼbale Saulo, penyanso!’ Ndipo nthawi yomweyo ndinapenya ndikumuona iyeyo.
Pride k meni, in vstopivši se, reče mi: Savel brat, spreglej! In jaz sem še tisti čas pogledal na-nj.
14 “Ndipo iye anati, ‘Mulungu wa makolo athu wakusankha iwe kuti udziwe chifuniro chake ndi kuona Wolungamayo ndi kumva mawu ochokera pakamwa pake.
On pa reče: Bog očetov naših te je izvolil, da spoznaj voljo njegovo, in vidiš pravičnega, in slišiš glas iz ust njegovih;
15 Iwe udzakhala mboni yake kwa anthu onse pa zimene waziona ndi kuzimva.
Kajti boš mu priča pri vseh ljudéh tega, kar si videl in slišal.
16 Ndipo tsopano ukudikira chiyani? Dzuka ndi kutama dzina la Ambuye mopemba, ubatizidwe ndi kuchotsa machimo ako.’
In sedaj, kaj se obotavljaš? Vstani, in krsti se, in operi grehe svoje, poklicavši ime Gospodovo.
17 “Nditabwerera ku Yerusalemu, ndikupemphera mʼNyumba ya Mulungu, ndinachita ngati ndakomoka.
Zgodí se pa, ko sem se bil vrnil v Jeruzalem, in sem v tempeljnu molil, da sem se zamaknil,
18 Ndinaona Ambuye akundiwuza kuti, ‘Fulumira! Tuluka mu Yerusalemu msangamsanga, chifukwa anthuwa sadzavomereza umboni wako wonena za Ine.’”
In videl sem ga, in rekel mi je: Pohiti in izidi naglo iz Jeruzalema, ker ne bodo sprejeli pričevanja tvojega za-me.
19 Ine ndinayankha Ambuye kuti, “Anthu awa akudziwa kuti ine ndinkapita ku sunagoge iliyonse ndipo ndinkawaponya mʼndende ndi kuwakwapula amene ankakhulupirira inu.
In jaz sem rekel: Gospod! sami vedó, da sem jaz zapiral in bíl po shajališčih té, kteri so verovali v tebe;
20 Ndipo pamene ankapha Stefano, ine ndinali pomwepo kuvomereza ndi kusunga zovala za amene amamupha.”
In ko se je prelivala kri Štefana pričevalca tvojega, tudi jaz sem stal zraven, in privolil sem na smrt njegovo, in varoval sem oblačila tistih, kteri so ga pobijali.
21 Pamenepo Ambuye anandiwuza kuti, “Nyamuka; Ine ndidzakutuma kutali kwa anthu a mitundu ina.”
In reče mi: Pojdi; kajti jaz te bom daleč poslal med pogane.
22 Gulu la anthu linamvetsera mawu a Paulo mpaka pamene ananena izi, kenaka anakweza mawu awo nafuwula kuti, “Ameneyo aphedwe basi! Ngosayenera kukhala moyo!”
In poslušali so ga do te besede, ter povzdignejo glas svoj, govoreč: Vzemi z zemlje takošnega; ker ni prav, da živí.
23 Akufuwula ndi kuponya zovala zawo ndi kuwaza fumbi kumwamba,
Ko so pa kričali, in metali oblačila, in prah lučali k višku,
24 mkulu wa asilikali analamulira kuti amutenge Paulo kupita naye ku malo a asilikali. Iye analamula kuti Paulo akwapulidwe kwambiri ndi kumufunsa kuti apeze chimene anthu ankafuwulira chotere.
Ukaže ga jezernik v grad odpeljati, rekši, naj ga z biči iztezajo, da bi zvedel, za kakošno krivico tako vpijejo nad njim.
25 Atamumanga kuti amukwapule, Paulo anati kwa msilikali wolamulira asilikali 100 amene anayima pamenepo, “Kodi malamulo amalola kukwapula nzika ya Chiroma imene sinapezedwe yolakwa?”
Ko so ga pa z jermeni pritegnili, reče Pavel stotniku, kteri je tam stal: Smete li človeka Rimljana, in neobsojenega bičati?
26 Wolamulira asilikali 100 uja atamva zimenezi, anapita kwa mkulu wa asilikali ndi kumufotokozera. Iye anafunsa kuti, “Kodi mukuchita chiyani ndi munthuyu amene ndi nzika ya Chiroma?”
Slišavši pa to stotnik, pristopi in sporočí jezerniku, govoreč: Glej, kaj boš storil; kajti ta človek je Rimljan.
27 Mkulu wa asilikali uja anapita kwa Paulo ndipo anamufunsa kuti, “Tandiwuze, kodi ndiwe nzika ya Chiroma?” Paulo anayankha kuti, “Inde.”
Pristopivši pa jezernik, reče mu: Povej mi, če si ti Rimljan? On pa reče: Dà.
28 Kenaka mkulu wa asilikaliyo anati, “Ine ndinapereka ndalama zambiri kuti ndikhale nzika.” Paulo anayankha kuti, “Koma ine ndinabadwa nzika.”
In jezernik odgovorí: Jaz sem za veliko denarja to državljanstvo pridobil. A Pavel reče: Jaz sem se pa tudi rodil.
29 Iwo amene anati amufunse analeka nthawi yomweyo. Mkulu wa asilikali uja anachita mantha atazindikira kuti wamanga Paulo amene ndi nzika ya Chiroma.
Tedaj so precej odstopili od njega, kteri so ga imeli tezati; pa tudi jezernik se je bal, ko je zvedel, da je Rimljan, in da ga je bil zvezal.
30 Mmawa mwake, mkulu wa asilikali pofuna kupeza chifukwa chenicheni chimene Ayuda amamunenera Paulo, anamumasula ndipo analamula kuti akulu a ansembe ndi onse akuluakulu a Bwalo Lalikulu asonkhane. Ndipo iye anabweretsa Paulo namuyimiritsa patsogolo pawo.
Drugi dan pa, ker je hotel za gotovo zvedeti, za kaj ga Judje tožijo, razveže ga od vezî, in ukaže priti velikemu duhovnu in vsemu zboru njihovemu; in pripeljavši Pavla dol, postavi ga pred-nje.

< Machitidwe a Atumwi 22 >