< Machitidwe a Atumwi 22 >
1 Iye anati, “Inu abale anga ndi makolo anga, tamvani mawu akudziteteza kwanga.”
“Ka champui Isrealngei ki dikna thurchi nin kôm ki ril hih rangâi roi!” a tia.
2 Atamva iye akuyankhula Chihebri, anakhala chete. Kenaka Paulo anati,
Hebrew chongin a chong ti an riet lechu an dâirek uol zoia Paul'n a ti banga.
3 “Ine ndine Myuda, wobadwira ku Tarisisi wa ku Kilikiya, koma ndinaleredwa mu mzinda muno, ndinaphunzitsidwa mwatsatanetsatane kusunga malamulo a makolo athu ndi Gamalieli ndipo ndinali wodzipereka pa za Mulungu monga mmene inu mulili lero.
Hanchu Paul'n, “Juda ki ni, Cilicia rama Tarsus khuoa suok ki ni, hannirese Jerusalema Gamaliel minchuna hong seilien ki nia, ei richibulngei anga balam inngartaka lei inchu ki ni. Aviensûn hin nangni ngei angtaka Pathien tienga theidôra inpêk ke lei ni.
4 Ine ndinkazunza anthu otsatira Njirayi mpaka kuwapha. Ndinkagwira amuna ndi amayi ndi kuwayika mʼndende.
Hi Lampui lei jûingei hih that rang dôra lei pûta ku nuom lei lo ngâi ki ni, pasal nupang ku sûra intâng ina lei khum ngâi ki ni.
5 Mkulu wa ansembe ndiponso akuluakulu a Ayuda angathe kundichitira umboni. Iwowa anandipatsa makalata opita nawo kwa abale awo ku Damasiko. Ndipo ndinapita kumeneko kuti ndikawagwire anthu amenewa ndi kubwera nawo ku Yerusalemu kuti adzalangidwe.
Ochai Inlalngei le Roijêkpungei murdi'n ko chong hih adik ti nangni ril thei an tih, an kôm renga Damascus taka Juda champuingei sûrna rang lekha ka mana, masikin ma khuo mingei hah sûra dûkmintonga zingjirûi leh khita Jerusalema hong tuong ranga se ki nia.
6 “Nthawi ya masana, nditayandikira ku Damasiko, mwadzidzidzi kuwala kwakukulu kochokera kumwamba kunandizungulira.
“Hanchu ke sea, Damascus khuo kôl kin phâk le sûnchimripa inningloi rengin invân renga vârin mi juong êla.
7 Ndinagwa pansi ndipo ndinamva mawu akuti, ‘Saulo! Saulo! Ukundizunziranji?’”
Hanchu nuoia kên leta, chong ki rieta, ‘Sual, Sual ithomo dûk mi ni mintonga?’ a tia.
8 Ine ndinafunsa kuti, “Ndinu ndani Ambuye?” Iye anayankha kuti, “Ndine Yesu wa ku Nazareti, amene iwe ukumuzunza.”
Keiman, ‘Pumapa Tumo ni ni?’ tiin ke rekela, ama han ko kôm, ‘Keima Nazareth Jisua, dûk ni mintong ngâipu hah ki ni,’ a tia.
9 Anzanga a paulendo anaona kuwalako, koma sanamve mawuwo, a Iye amene amayankhula nane.
Ko kôla miriemngei han vâr chu an mua, hannirese ko kôma chong juong tung hah chu riet mak ngei.
10 Ine ndinafunsa kuti, “Kodi ndichite chiyani Ambuye?” Ambuye anati, “Imirira ndipo pita ku Damasiko. Kumeneko adzakuwuza zonse zimene ukuyenera kuchita.”
Keiman ‘Pumapa imo ko tho rang?’ ki tia, Pumapa han ko kôm ‘Inthoi inla Damascus khuo lût roh, mahan Pathien'n no tho rang ngei murdi nang lei ril atih’ a tia.
11 Anzanga anandigwira dzanja kupita nane ku Damasiko, popeza kuwala kunja kunandichititsa khungu.
Avâr hah avâr rai sikin ki mitngei khom ajînga, masikin ka champuingei han ku kutin min keiruoia Damascus khuoa kin lût zoi.
12 “Munthu wina dzina lake Hananiya anabwera kudzandiona. Iyeyu anali munthu woopa Mulungu ndi wosunga Malamulo. Ayuda onse okhala kumeneko amamupatsa ulemu waukulu.
“Ma khopuilien han mi inkhat a riming Ananias, Pathien biek mi le balam lei jûi ngâi a oma, mataka Juda omngei murdi'n an mirit sabaka.
13 Iye anayimirira pafupi nane nati, ‘Mʼbale Saulo, penyanso!’ Ndipo nthawi yomweyo ndinapenya ndikumuona iyeyo.
Ama hah ko kôm a honga, ko kôla ândinga, Lâibung Saul hong mu thei ta roh, mi tia. Ma zora tak han ko hong muthei nôk zoia, ama hah ko hong ena.
14 “Ndipo iye anati, ‘Mulungu wa makolo athu wakusankha iwe kuti udziwe chifuniro chake ndi kuona Wolungamayo ndi kumva mawu ochokera pakamwa pake.
Ama han, ei richibulngei Pathien lungdo ngei riet rang le mi diktak tîrlâm hah mua, a chongbâingei riet rangin nang a thang ani.
15 Iwe udzakhala mboni yake kwa anthu onse pa zimene waziona ndi kuzimva.
Nu mu le ni riet ngei angtak han mi murdi chunga rietpuipu na la ni rang sikin.
16 Ndipo tsopano ukudikira chiyani? Dzuka ndi kutama dzina la Ambuye mopemba, ubatizidwe ndi kuchotsa machimo ako.’
Atûn reng, hi hin khoi mo na la ôt bang? Inthoi inla, baptisma chang inla ni sietnangei rusûk minsâina rangin a kôm chubaitho ta roh, a tia.
17 “Nditabwerera ku Yerusalemu, ndikupemphera mʼNyumba ya Mulungu, ndinachita ngati ndakomoka.
“Jerusalem tieng ki kîr nôka, Biekina Pathien kôm chubai ko tho lâiin inlârnân,
18 Ndinaona Ambuye akundiwuza kuti, ‘Fulumira! Tuluka mu Yerusalemu msangamsanga, chifukwa anthuwa sadzavomereza umboni wako wonena za Ine.’”
Mahan Pumapa ku mua, ko kôm, ‘Inrangin Jerusalem mâk roh, ku thurchi ni misîr rang, hi muna mingeiin an modôm loi rang sikin’ a tia.
19 Ine ndinayankha Ambuye kuti, “Anthu awa akudziwa kuti ine ndinkapita ku sunagoge iliyonse ndipo ndinkawaponya mʼndende ndi kuwakwapula amene ankakhulupirira inu.
Hanchu keiman, ‘Pumapa, synagog murdi ngei lûta nang iempungei lei sûra lei jêm ngâipu hah ki ni tiin min riet let kêng alei ni.
20 Ndipo pamene ankapha Stefano, ine ndinali pomwepo kuvomereza ndi kusunga zovala za amene amamupha.”
Male no chong rietpuipu Stephan an that zora han khom ko oma, an that rang hah asa lei ti puipu le ama that ngei an puonngei lei dar pepu hah ki ni,’ ki tia.
21 Pamenepo Ambuye anandiwuza kuti, “Nyamuka; Ine ndidzakutuma kutali kwa anthu a mitundu ina.”
Pumapa'n, ‘Se roh, alataka Jentailngei kôm nang tîr ki tih,’” a tia.
22 Gulu la anthu linamvetsera mawu a Paulo mpaka pamene ananena izi, kenaka anakweza mawu awo nafuwula kuti, “Ameneyo aphedwe basi! Ngosayenera kukhala moyo!”
Hanchu, ha thurchi ten hah an rangâia, masuole chu rôl inringtakin an inieka minboi pai roi! That roi! a ring rangin chuk mak an tia.
23 Akufuwula ndi kuponya zovala zawo ndi kuwaza fumbi kumwamba,
Anrêngin an inieka an puonngei an vôka, pildi invân tieng an vôra.
24 mkulu wa asilikali analamulira kuti amutenge Paulo kupita naye ku malo a asilikali. Iye analamula kuti Paulo akwapulidwe kwambiri ndi kumufunsa kuti apeze chimene anthu ankafuwulira chotere.
Hanchu Rom râlmi ulientakpu han Paul hah rukulpui sûng tieng ruoi rangin chong a pêka, a chunga ma angdôra an hêtsana abi riet theina rangin jêm pumin rekel tit rangin a ti pe ngeia.
25 Atamumanga kuti amukwapule, Paulo anati kwa msilikali wolamulira asilikali 100 amene anayima pamenepo, “Kodi malamulo amalola kukwapula nzika ya Chiroma imene sinapezedwe yolakwa?”
Hannirese jêm ranga an khit suole chu, Paul'n a kôma inding râlmi razakhat ruoipu kôm han, “Rom mi adik loina khoite boi hih jêm rangin balam ani mo?” a tipea.
26 Wolamulira asilikali 100 uja atamva zimenezi, anapita kwa mkulu wa asilikali ndi kumufotokozera. Iye anafunsa kuti, “Kodi mukuchita chiyani ndi munthuyu amene ndi nzika ya Chiroma?”
Râlmi razakhat ruoipu han ha chong hah a rietin chu, râlmi ulientak kôm a sea. “Khoimo tho rang nin ti hi? Ma miriem hih Rom mi ke ani” a tipea.
27 Mkulu wa asilikali uja anapita kwa Paulo ndipo anamufunsa kuti, “Tandiwuze, kodi ndiwe nzika ya Chiroma?” Paulo anayankha kuti, “Inde.”
Masuole chu, râlmi ulientakpu hah Paul kôm a sea, “Rom mi ni ni mo, mi ril roh!” tiin a rekela, Paul'n “Ki ni,” a tiin a thuona.
28 Kenaka mkulu wa asilikaliyo anati, “Ine ndinapereka ndalama zambiri kuti ndikhale nzika.” Paulo anayankha kuti, “Koma ine ndinabadwa nzika.”
Râlmi ulientakpu han “Kei chu Rom mi changna rang hin sum tamtak ka thâm ok,” a tia, Aniatachu Paul'n kei chu “Rom mi nisai piela juonzir ki ni,” tiin athuona.
29 Iwo amene anati amufunse analeka nthawi yomweyo. Mkulu wa asilikali uja anachita mantha atazindikira kuti wamanga Paulo amene ndi nzika ya Chiroma.
Voikhat rengin, Paul kôma chong rekel rang dônpu ngei murdi khom an rot let zoia. Râlmi ulientak ha khom Paul hah Rom mi ani ti a riet lechu asân a chi zoi, moton han Paul ha zingjirûi leh a lei thung zoi sikin.
30 Mmawa mwake, mkulu wa asilikali pofuna kupeza chifukwa chenicheni chimene Ayuda amamunenera Paulo, anamumasula ndipo analamula kuti akulu a ansembe ndi onse akuluakulu a Bwalo Lalikulu asonkhane. Ndipo iye anabweretsa Paulo namuyimiritsa patsogolo pawo.
Hanchu, anangtûka chu râlmi ulien han, Judangei itho sikin mo Paul an nônna riet rang a nuom sikin, a zingjirûi khitna an sût pea, ochaisingei le roijêkpungei murdi lei intûp rangin chong a pêka, masuole chu Paul ha a tuonga an makunga a minding zoi.