< Machitidwe a Atumwi 22 >

1 Iye anati, “Inu abale anga ndi makolo anga, tamvani mawu akudziteteza kwanga.”
„Bratři a otcové, rád bych se před vámi obhájil.“
2 Atamva iye akuyankhula Chihebri, anakhala chete. Kenaka Paulo anati,
Lidé byli překvapeni, že mluví jejich rodným jazykem, a tak tiše poslouchali. Pavel pokračoval:
3 “Ine ndine Myuda, wobadwira ku Tarisisi wa ku Kilikiya, koma ndinaleredwa mu mzinda muno, ndinaphunzitsidwa mwatsatanetsatane kusunga malamulo a makolo athu ndi Gamalieli ndipo ndinali wodzipereka pa za Mulungu monga mmene inu mulili lero.
„Jsem žid, narozený sice v Tarsu v Kilikii, ale vychován jsem byl zde v Jeruzalémě. Vám dobře známý učenec Gamaliel mě vyškolil přesně podle zákona našich otců a horlil jsem pro Boha, právě tak jako vy dnes.
4 Ine ndinkazunza anthu otsatira Njirayi mpaka kuwapha. Ndinkagwira amuna ndi amayi ndi kuwayika mʼndende.
Víru v Ježíše Krista jsem nenáviděl k smrti. Dokonce jsem jeho vyznavače, muže i ženy, dával zatýkat a věznit.
5 Mkulu wa ansembe ndiponso akuluakulu a Ayuda angathe kundichitira umboni. Iwowa anandipatsa makalata opita nawo kwa abale awo ku Damasiko. Ndipo ndinapita kumeneko kuti ndikawagwire anthu amenewa ndi kubwera nawo ku Yerusalemu kuti adzalangidwe.
To mi může dosvědčit velekněz a celá velerada. Jednou mi také vydali pověřující listiny pro židovskou obec v Damašku a já jsem se tam vypravil, abych mezi nimi pozatýkal křesťany a dopravil je do Jeruzaléma k potrestání.
6 “Nthawi ya masana, nditayandikira ku Damasiko, mwadzidzidzi kuwala kwakukulu kochokera kumwamba kunandizungulira.
A poslyšte, co se stalo. Bylo kolem poledne a my jsme byli na dohled od damašských hradeb. Náhle se okolo mne rozzářilo oslnivé světlo, mnohem jasnější než polední slunce.
7 Ndinagwa pansi ndipo ndinamva mawu akuti, ‘Saulo! Saulo! Ukundizunziranji?’”
Padl jsem na zem, když jsem uslyšel hlas: ‚Saule, Saule, proč mne pronásleduješ?‘
8 Ine ndinafunsa kuti, “Ndinu ndani Ambuye?” Iye anayankha kuti, “Ndine Yesu wa ku Nazareti, amene iwe ukumuzunza.”
Ozval jsem se: ‚Kdo jsi, Pane?‘Slyšel jsem odpověď: ‚Já jsem Ježíš z Nazaretu a ty bojuješ proti mně.‘
9 Anzanga a paulendo anaona kuwalako, koma sanamve mawuwo, a Iye amene amayankhula nane.
Moji průvodci byli tím světlem také oslněni, ale neslyšeli, že by ke mně někdo mluvil.
10 Ine ndinafunsa kuti, “Kodi ndichite chiyani Ambuye?” Ambuye anati, “Imirira ndipo pita ku Damasiko. Kumeneko adzakuwuza zonse zimene ukuyenera kuchita.”
Zeptal jsem se: ‚Pane, co mám dělat?‘Ježíš mi odpověděl: ‚Teď vstaň a jdi do Damašku. Tam ti řeknou, jaký mám pro tebe úkol.‘
11 Anzanga anandigwira dzanja kupita nane ku Damasiko, popeza kuwala kunja kunandichititsa khungu.
Jas toho světla mne docela oslepil a tak jsem klopýtal do Damašku, veden za ruce svými průvodci.
12 “Munthu wina dzina lake Hananiya anabwera kudzandiona. Iyeyu anali munthu woopa Mulungu ndi wosunga Malamulo. Ayuda onse okhala kumeneko amamupatsa ulemu waukulu.
Tam mne navštívil Ananiáš, zbožný ctitel zákona, kterého si židé v Damašku velice vážili.
13 Iye anayimirira pafupi nane nati, ‘Mʼbale Saulo, penyanso!’ Ndipo nthawi yomweyo ndinapenya ndikumuona iyeyo.
Přišel a řekl mi: ‚Bratře Saule, otevři oči!‘Tu se mi vrátil zrak a já ho uviděl.
14 “Ndipo iye anati, ‘Mulungu wa makolo athu wakusankha iwe kuti udziwe chifuniro chake ndi kuona Wolungamayo ndi kumva mawu ochokera pakamwa pake.
Řekl ještě: ‚Tak to chtěl Bůh, abys konečně poznal jeho vůli, abys uviděl Božího Spravedlivého a uslyšel jeho vlastní hlas.
15 Iwe udzakhala mboni yake kwa anthu onse pa zimene waziona ndi kuzimva.
Staneš se Ježíšovým svědkem celému světu a budeš všude vyprávět, co jsi viděl a slyšel.
16 Ndipo tsopano ukudikira chiyani? Dzuka ndi kutama dzina la Ambuye mopemba, ubatizidwe ndi kuchotsa machimo ako.’
Neváhej, vyznej, že je tvým Pánem, dej se pokřtít na znamení, že jsi očištěn od hříchů.‘
17 “Nditabwerera ku Yerusalemu, ndikupemphera mʼNyumba ya Mulungu, ndinachita ngati ndakomoka.
Později, když jsem se vrátil do Jeruzaléma a modlil se v chrámu, měl jsem ještě jedno vidění.
18 Ndinaona Ambuye akundiwuza kuti, ‘Fulumira! Tuluka mu Yerusalemu msangamsanga, chifukwa anthuwa sadzavomereza umboni wako wonena za Ine.’”
Viděl jsem Pána a slyšel jeho slova: ‚Nezdržuj se a rychle odejdi z Jeruzaléma. Tady nepřijmou tvoje svědectví o mně.‘
19 Ine ndinayankha Ambuye kuti, “Anthu awa akudziwa kuti ine ndinkapita ku sunagoge iliyonse ndipo ndinkawaponya mʼndende ndi kuwakwapula amene ankakhulupirira inu.
Ale já jsem odporoval: ‚Pane, tady jsem dával tvoje věrné věznit a bičovat v synagogách.
20 Ndipo pamene ankapha Stefano, ine ndinali pomwepo kuvomereza ndi kusunga zovala za amene amamupha.”
Tady byla prolita první krev, krev tvého svědka Štěpána. Já byl při tom, souhlasil jsem s tím a hlídal jsem pláště těm, kdo ho kamenovali. Všichni to tu o mně vědí.‘
21 Pamenepo Ambuye anandiwuza kuti, “Nyamuka; Ine ndidzakutuma kutali kwa anthu a mitundu ina.”
Pán mi však řekl: ‚Jen jdi, protože tě pošlu k pohanům.‘“
22 Gulu la anthu linamvetsera mawu a Paulo mpaka pamene ananena izi, kenaka anakweza mawu awo nafuwula kuti, “Ameneyo aphedwe basi! Ngosayenera kukhala moyo!”
Až potud dav Pavla pozorně poslouchal, ale zmínka o pohanech je znovu pobouřila. Začali mávat plášti, házeli na něho hrsti prachu a křičeli: „Pryč s tím zrádcem! Na smrt! Nemá tu co dělat!“
23 Akufuwula ndi kuponya zovala zawo ndi kuwaza fumbi kumwamba,
24 mkulu wa asilikali analamulira kuti amutenge Paulo kupita naye ku malo a asilikali. Iye analamula kuti Paulo akwapulidwe kwambiri ndi kumufunsa kuti apeze chimene anthu ankafuwulira chotere.
Velitel dal Pavla rychle odvést do pevnosti a nařídil, aby ho zbičovali a vyslechli; chtěl vědět, čím vzbudil tolik nenávisti.
25 Atamumanga kuti amukwapule, Paulo anati kwa msilikali wolamulira asilikali 100 amene anayima pamenepo, “Kodi malamulo amalola kukwapula nzika ya Chiroma imene sinapezedwe yolakwa?”
Už ho připoutali k bičovací lavici, když se Pavel obrátil k velícímu setníkovi: „Nemáte přece právo bičovat římského občana. Musím být postaven před řádný soud.“
26 Wolamulira asilikali 100 uja atamva zimenezi, anapita kwa mkulu wa asilikali ndi kumufotokozera. Iye anafunsa kuti, “Kodi mukuchita chiyani ndi munthuyu amene ndi nzika ya Chiroma?”
Důstojník dal přerušit přípravy, šel k veliteli a hlásil mu: „Stal se nějaký omyl, ten člověk prohlašuje, že je občanem Říma.“
27 Mkulu wa asilikali uja anapita kwa Paulo ndipo anamufunsa kuti, “Tandiwuze, kodi ndiwe nzika ya Chiroma?” Paulo anayankha kuti, “Inde.”
Velitel s ním šel k Pavlovi a zeptal se: „Je pravda, že jsi římský občan?“„Ano, jsem, “odpověděl vězeň.
28 Kenaka mkulu wa asilikaliyo anati, “Ine ndinapereka ndalama zambiri kuti ndikhale nzika.” Paulo anayankha kuti, “Koma ine ndinabadwa nzika.”
Velitel zapochyboval: „Vím z vlastní zkušenosti, že je to pěkně drahé. Kdepak bys na to vzal?“Pavel řekl: „Já jsem nic nekupoval, jsem občanem od narození.“
29 Iwo amene anati amufunse analeka nthawi yomweyo. Mkulu wa asilikali uja anachita mantha atazindikira kuti wamanga Paulo amene ndi nzika ya Chiroma.
Po tomto prohlášení vojáci odhodili důtky a spěšně jej odvazovali. Velitel měl obavy, protože se dopustil takového přehmatu vůči rodilému římskému občanu. Rozhodl se, že vyšetří, z čeho židé Pavla vlastně obviňují.
30 Mmawa mwake, mkulu wa asilikali pofuna kupeza chifukwa chenicheni chimene Ayuda amamunenera Paulo, anamumasula ndipo analamula kuti akulu a ansembe ndi onse akuluakulu a Bwalo Lalikulu asonkhane. Ndipo iye anabweretsa Paulo namuyimiritsa patsogolo pawo.
Na velitelovu žádost se nazítří sešla židovská velerada za předsednictví úřadujícího i minulého velekněze.

< Machitidwe a Atumwi 22 >