< Machitidwe a Atumwi 21 >

1 Titalawirana nawo, tinachoka kumeneko mʼsitima ya pamadzi, ndipo tinayenda molunjika mpaka kufika ku Kosi. Mmawa mwake tinapita ku Rode, kuchokera kumeneko tinapita ku Patara.
tai rvisṛṣṭāḥ santo vayaṁ potaṁ bāhayitvā ṛjumārgeṇa koṣam upadvīpam āgatya pare'hani rodiyopadvīpam āgacchāma tatastasmāt pātārāyām upātiṣṭhāma|
2 Kumeneko tinapeza sitima yapamadzi yopita ku Foinike. Choncho tinalowamo nʼkunyamuka.
tatra phainīkiyādeśagāminam potamekaṁ prāpya tamāruhya gatavantaḥ|
3 Tinaona chilumba cha Kupro ndipo tinadutsa kummwera kwake nʼkupita ku Siriya. Tinakayima ku Turo chifukwa sitima yathuyo imayenera kusiya katundu kumeneko.
kupropadvīpaṁ dṛṣṭvā taṁ savyadiśi sthāpayitvā suriyādeśaṁ gatvā potasthadravyāṇyavarohayituṁ soranagare lāgitavantaḥ|
4 Tinafunafuna ophunzira kumeneko, ndipo titawapeza tinakhala nawo masiku asanu ndi awiri. Iwowa, mwa Mzimu Woyera anakakamiza Paulo kuti asapite ku Yerusalemu.
tatra śiṣyagaṇasya sākṣātkaraṇāya vayaṁ tatra saptadināni sthitavantaḥ paścātte pavitreṇātmanā paulaṁ vyāharan tvaṁ yirūśālamnagaraṁ mā gamaḥ|
5 Koma nthawi yathu itatha, tinachokako ndi kupitiriza ulendo wathu. Ophunzira onse pamodzi ndi akazi awo ndi ana anatiperekeza mpaka kunja kwa mzinda. Ndipo kumeneko tinagwada mʼmbali mwa nyanja ndi kupemphera.
tatasteṣu saptasu dineṣu yāpiteṣu satsu vayaṁ tasmāt sthānāt nijavartmanā gatavantaḥ, tasmāt te sabālavṛddhavanitā asmābhiḥ saha nagarasya parisaraparyyantam āgatāḥ paścādvayaṁ jaladhitaṭe jānupātaṁ prārthayāmahi|
6 Titatsanzikana, tinalowa mʼsitima ija, iwowo anabwerera ku nyumba zawo.
tataḥ parasparaṁ visṛṣṭāḥ santo vayaṁ potaṁ gatāste tu svasvagṛhaṁ pratyāgatavantaḥ|
7 Ife tinapitiriza ulendo wathu wochokera ku Turo mpaka tinafika ku Ptolemayi. Kumeneko tinalonjera abale ndi kukhala nawo tsiku limodzi.
vayaṁ soranagarāt nāvā prasthāya talimāyinagaram upātiṣṭhāma tatrāsmākaṁ samudrīyamārgasyānto'bhavat tatra bhrātṛgaṇaṁ namaskṛtya dinamekaṁ taiḥ sārddham uṣatavantaḥ|
8 Tinachoka mmawa mwake, mpaka tinakafika ku Kaisareya. Tinapita kukakhala mʼnyumba ya mlaliki Filipo, amene anali mmodzi mwa atumiki a mpingo asanu ndi awiri aja.
pare 'hani paulastasya saṅgino vayañca pratiṣṭhamānāḥ kaisariyānagaram āgatya susaṁvādapracārakānāṁ saptajanānāṁ philipanāmna ekasya gṛhaṁ praviśyāvatiṣṭhāma|
9 Iye anali ndi ana aakazi anayi osakwatiwa amene anali ndi mphatso ya uneneri.
tasya catasro duhitaro'nūḍhā bhaviṣyadvādinya āsan|
10 Titakhala kumeneko masiku ambiri, kunabwera mneneri wina wochokera ku Yudeya dzina lake Agabu.
tatrāsmāsu bahudināni proṣiteṣu yihūdīyadeśād āgatyāgābanāmā bhaviṣyadvādī samupasthitavān|
11 Atafika kwa ife, anatenga lamba wa Paulo, nadzimanga naye manja ake ndi mapazi ake ndipo anati, “Mzimu Woyera akuti, ‘Mwini lambayu, Ayuda adzamumanga chomwechi ku Yerusalemu, ndipo adzamupereka mʼmanja mwa anthu a mitundu ina.’”
sosmākaṁ samīpametya paulasya kaṭibandhanaṁ gṛhītvā nijahastāpādān baddhvā bhāṣitavān yasyedaṁ kaṭibandhanaṁ taṁ yihūdīyalokā yirūśālamanagara itthaṁ baddhvā bhinnadeśīyānāṁ kareṣu samarpayiṣyantīti vākyaṁ pavitra ātmā kathayati|
12 Titamva zimenezi, ife pamodzi ndi anthu kumeneko tinamudandaulira Paulo kuti asapite ku Yerusalemu.
etādṛśīṁ kathāṁ śrutvā vayaṁ tannagaravāsino bhrātaraśca yirūśālamaṁ na yātuṁ paulaṁ vyanayāmahi;
13 Koma Paulo anayankha kuti, “Chifukwa chiyani mukulira ndi kunditayitsa mtima? Ndine wokonzeka osati kumangidwa kokha ayi, komanso kufa ku Yerusalemu chifukwa cha dzina la Ambuye Yesu.”
kintu sa pratyāvādīt, yūyaṁ kiṁ kurutha? kiṁ krandanena mamāntaḥkaraṇaṁ vidīrṇaṁ kariṣyatha? prabho ryīśo rnāmno nimittaṁ yirūśālami baddho bhavituṁ kevala tanna prāṇān dātumapi sasajjosmi|
14 Titalephera kumuletsa tinamuleka ndipo tinati, “Chifuniro cha Ambuye chichitike.”
tenāsmākaṁ kathāyām agṛhītāyām īśvarasya yathecchā tathaiva bhavatvityuktvā vayaṁ nirasyāma|
15 Pambuyo pake, ife tinakonzeka ndi kunyamuka kumapita ku Yerusalemu.
pare'hani pātheyadravyāṇi gṛhītvā yirūśālamaṁ prati yātrām akurmma|
16 Ena mwa ophunzira a ku Kaisareya anatiperekeza mpaka kukatifikitsa ku nyumba ya Mnasoni, kumene tinakonza kuti tizikhalako. Iye anali wa ku Kupro ndiponso mmodzi wa ophunzira oyambirira.
tataḥ kaisariyānagaranivāsinaḥ katipayāḥ śiṣyā asmābhiḥ sārddham itvā kṛprīyena mnāsannāmnā yena prācīnaśiṣyena sārddham asmābhi rvastavyaṁ tasya samīpam asmān nītavantaḥ|
17 Titafika ku Yerusalemu, abale anatilandira mwachimwemwe.
asmāsu yirūśālamyupasthiteṣu tatrasthabhrātṛgaṇo'smān āhlādena gṛhītavān|
18 Mmawa mwake Paulo pamodzi ndi ife tonse tinapita kwa Yakobo, ndipo akulu onse a mpingo anali komweko.
parasmin divase paule'smābhiḥ saha yākūbo gṛhaṁ praviṣṭe lokaprācīnāḥ sarvve tatra pariṣadi saṁsthitāḥ|
19 Paulo anawalonjera ndi kuwafotokozera mwatsatanetsatane zimene Mulungu anachita pakati pa anthu a mitundu ina kudzera mu utumiki wake.
anantaraṁ sa tān natvā svīyapracāraṇena bhinnadeśīyān pratīśvaro yāni karmmāṇi sādhitavān tadīyāṁ kathām anukramāt kathitavān|
20 Atamva zimenezi, iwo anayamika Mulungu. Kenaka anawuza Paulo kuti, “Mʼbale, ukuona kuti pali Ayuda ambirimbiri amene anakhulupirira, ndipo ndi okhulupirika potsatira Malamulo a Mose.
iti śrutvā te prabhuṁ dhanyaṁ procya vākyamidam abhāṣanta, he bhrāta ryihūdīyānāṁ madhye bahusahasrāṇi lokā viśvāsina āsate kintu te sarvve vyavasthāmatācāriṇa etat pratyakṣaṁ paśyasi|
21 Iwo anawuzidwa kuti iwe umaphunzitsa Ayuda onse amene akukhala pakati pa anthu a mitundu ina kuti asiye kutsatira Mose, kuti asamachite mdulidwe kapena kutsatira miyambo.
śiśūnāṁ tvakchedanādyācaraṇaṁ pratiṣidhya tvaṁ bhinnadeśanivāsino yihūdīyalokān mūsāvākyam aśraddhātum upadiśasīti taiḥ śrutamasti|
22 Nanga pamenepa ife titani? Iwo adzamva ndithu kuti iwe wabwera,
tvamatrāgatosīti vārttāṁ samākarṇya jananivaho militvāvaśyamevāgamiṣyati; ataeva kiṁ karaṇīyam? atra vayaṁ mantrayitvā samupāyaṁ tvāṁ vadāmastaṁ tvamācara|
23 tsono iwe chita zimene ife tikuwuze. Tili nawo amuna anayi pano amene anachita lumbiro kwa Mulungu.
vrataṁ karttuṁ kṛtasaṅkalpā ye'smāṁka catvāro mānavāḥ santi
24 Muwatenge anthu amenewa, ndipo muchite nawo mwambo wowayeretsa ndipo muwalipirire zoti apereke kuti amete tsitsi lawo. Kotero aliyense adzadziwa kuti palibe choonadi pa zimene anamva za inu, koma kuti inu mwini mumakhala moyo womvera Malamulo.
tān gṛhītvā taiḥ sahitaḥ svaṁ śuciṁ kuru tathā teṣāṁ śiromuṇḍane yo vyayo bhavati taṁ tvaṁ dehi| tathā kṛte tvadīyācāre yā janaśruti rjāyate sālīkā kintu tvaṁ vidhiṁ pālayan vyavasthānusāreṇevācarasīti te bhotsante|
25 Koma kunena za anthu a mitundu ina amene asandulika okhulupirira, ife tinawalembera zimene tinavomerezana zakuti asadye chakudya choperekedwa ku mafano, asadye magazi, asadye nyama yopotola ndiponso asachite zadama.”
bhinnadeśīyānāṁ viśvāsilokānāṁ nikaṭe vayaṁ patraṁ likhitvetthaṁ sthirīkṛtavantaḥ, devaprasādabhojanaṁ raktaṁ galapīḍanamāritaprāṇibhojanaṁ vyabhicāraścaitebhyaḥ svarakṣaṇavyatirekeṇa teṣāmanyavidhipālanaṁ karaṇīyaṁ na|
26 Mmawa mwake Paulo anatenga amuna aja ndipo anachita mwambo wodziyeretsa. Kenaka anapita ku Nyumba ya Mulungu nakadziwitsa ansembe za tsiku limene adzatsiriza nthawi ya kudziyeretsa ndi kuperekera nsembe aliyense wa iwo.
tataḥ paulastān mānuṣānādāya parasmin divase taiḥ saha śuci rbhūtvā mandiraṁ gatvā śaucakarmmaṇo dineṣu sampūrṇeṣu teṣām ekaikārthaṁ naivedyādyutsargo bhaviṣyatīti jñāpitavān|
27 Ali pafupi kutsiriza masiku asanu ndi awiriwo, Ayuda ena ochokera ku Asiya anaona Paulo mʼNyumba ya Mulungu. Iwo anawutsa gulu lonse la anthu ndipo anamugwira Paulo,
teṣu saptasu dineṣu samāptakalpeṣu āśiyādeśanivāsino yihūdīyāstaṁ madhyemandiraṁ vilokya jananivahasya manaḥsu kupravṛttiṁ janayitvā taṁ dhṛtvā
28 akufuwula kuti, “Inu Aisraeli, tithandizeni! Ndi uyu munthu uja amaphunzitsa anthu onse ponseponse kuti azinyoza mtundu wathu ndiponso Malamulo athu ndi malo ano. Kuwonjezera pamenepo, walowetsa Agriki mʼbwalo la Nyumba ino ndipo wadetsa malo opatulika.”
proccaiḥ prāvocan, he isrāyellokāḥ sarvve sāhāyyaṁ kuruta| yo manuja eteṣāṁ lokānāṁ mūsāvyavasthāyā etasya sthānasyāpi viparītaṁ sarvvatra sarvvān śikṣayati sa eṣaḥ; viśeṣataḥ sa bhinnadeśīyalokān mandiram ānīya pavitrasthānametad apavitramakarot|
29 Iwo ananena izi chifukwa anali ataona Trofimo wa ku Efeso ali ndi Paulo mu mzindamo ndipo iwo ankaganiza kuti Paulo anamulowetsa mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu.
pūrvvaṁ te madhyenagaram iphiṣanagarīyaṁ traphimaṁ paulena sahitaṁ dṛṣṭavanta etasmāt paulastaṁ mandiramadhyam ānayad ityanvamimata|
30 Mzinda wonse unasokonezeka, ndipo anthu anabwera akuthamanga kuchokera kumbali zonse. Anamugwira Paulo, namukokera kunja kwa Nyumbayo, ndipo nthawi yomweyo anatseka zipata.
ataeva sarvvasmin nagare kalahotpannatvāt dhāvanto lokā āgatya paulaṁ dhṛtvā mandirasya bahirākṛṣyānayan tatkṣaṇād dvārāṇi sarvvāṇi ca ruddhāni|
31 Pamene anthuwo ankafuna kupha Paulo, nkhaniyi inamveka kwa mkulu wa magulu a asilikali a Aroma kuti mzinda wonse wa Yerusalemu wasokonezeka.
teṣu taṁ hantumudyateṣu yirūśālamnagare mahānupadravo jāta iti vārttāyāṁ sahasrasenāpateḥ karṇagocarībhūtāyāṁ satyāṁ sa tatkṣaṇāt sainyāni senāpatigaṇañca gṛhītvā javenāgatavān|
32 Nthawi yomweyo iye anatenga asilikali ndi atsogoleri a magulu a asilikali ndi kuthamangira kumene kunali anthuwo. Anthuwo ataona mkuluyo ndi asilikali ake analeka kumenya Paulo.
tato lokāḥ senāgaṇena saha sahasrasenāpatim āgacchantaṁ dṛṣṭvā paulatāḍanāto nyavarttanta|
33 Mkulu wa asilikaliyo anabwera nagwira Paulo, ndipo analamula kuti amangidwe ndi maunyolo awiri. Kenaka iye anafunsa kuti ndi ndani ndipo wachita chiyani.
sa sahasrasenāpatiḥ sannidhāvāgamya paulaṁ dhṛtvā śṛṅkhaladvayena baddham ādiśya tān pṛṣṭavān eṣa kaḥ? kiṁ karmma cāyaṁ kṛtavān?
34 Ena mʼgulumo anafuwula chinthu china ndi enanso chinanso. Tsono popeza mkulu wa asilikaliyo sanathe kudziwa choonadi chenicheni chifukwa cha phokoso, analamula kuti Paulo atengedwe kupita ku malo a asilikali.
tato janasamūhasya kaścid ekaprakāraṁ kaścid anyaprakāraṁ vākyam araut sa tatra satyaṁ jñātum kalahakāraṇād aśaktaḥ san taṁ durgaṁ netum ājñāpayat|
35 Paulo atafika pa makwerero olowera ku malo a asilikaliwo, ananyamulidwa ndi asilikali chifukwa cha ukali wa anthuwo.
teṣu sopānasyopari prāpteṣu lokānāṁ sāhasakāraṇāt senāgaṇaḥ paulamuttolya nītavān|
36 Gulu la anthu limene linamutsatira linapitiriza kufuwula kuti, “Ameneyo aphedwe basi!”
tataḥ sarvve lokāḥ paścādgāminaḥ santa enaṁ durīkuruteti vākyam uccairavadan|
37 Asilikali ali pafupi kulowa naye ku malo awo, iye anapempha mkulu wa asilikaliyo kuti, “Kodi mungandilole ndiyankhulepo?” Mkulu wa asilikaliyo anafunsa kuti, “Kodi umayankhula Chigriki?
paulasya durgānayanasamaye sa tasmai sahasrasenāpataye kathitavān, bhavataḥ purastāt kathāṁ kathayituṁ kim anumanyate? sa tamapṛcchat tvaṁ kiṁ yūnānīyāṁ bhāṣāṁ jānāsi?
38 Kodi sindiwe Mwigupto uja amene masiku apitawo unayambitsa kuwukira ndi kutsogolera anthu 4,000 owukira aja nʼkupita nawo ku chipululu?”
yo misarīyo janaḥ pūrvvaṁ virodhaṁ kṛtvā catvāri sahasrāṇi ghātakān saṅginaḥ kṛtvā vipinaṁ gatavān tvaṁ kiṁ saeva na bhavasi?
39 Paulo anayankha kuti, “Ine ndine Myuda, wa ku Tarisisi ku Kilikiya. Sindine nzika ya mzinda wamba. Chonde loleni ndiyankhule nawo anthuwa.”
tadā paulo'kathayat ahaṁ kilikiyādeśasya tārṣanagarīyo yihūdīyo, nāhaṁ sāmānyanagarīyo mānavaḥ; ataeva vinaye'haṁ lākānāṁ samakṣaṁ kathāṁ kathayituṁ māmanujānīṣva|
40 Ataloledwa ndi mkulu wa asilikaliyo, Paulo anayimirira pa makwereropo nakweza dzanja lake kwa gulu la anthuwo. Onse atakhala chete, iye anayankhula nawo mʼChihebri.
tenānujñātaḥ paulaḥ sopānopari tiṣṭhan hasteneṅgitaṁ kṛtavān, tasmāt sarvve susthirā abhavan| tadā paula ibrīyabhāṣayā kathayitum ārabhata,

< Machitidwe a Atumwi 21 >