< Machitidwe a Atumwi 21 >

1 Titalawirana nawo, tinachoka kumeneko mʼsitima ya pamadzi, ndipo tinayenda molunjika mpaka kufika ku Kosi. Mmawa mwake tinapita ku Rode, kuchokera kumeneko tinapita ku Patara.
Kwasekusithi sisuka ngomkhumbi sesehlukene labo, sahamba ngendlela eqondileyo safika eKosi, langosuku olulandelayo eRodesi, sasuka lapho saya ePathara;
2 Kumeneko tinapeza sitima yapamadzi yopita ku Foinike. Choncho tinalowamo nʼkunyamuka.
sasesithola umkhumbi ochaphela eFenekiya, sangena sahamba ngomkhumbi.
3 Tinaona chilumba cha Kupro ndipo tinadutsa kummwera kwake nʼkupita ku Siriya. Tinakayima ku Turo chifukwa sitima yathuyo imayenera kusiya katundu kumeneko.
Kwathi sesiqhamuka eKuprosi, sasesiyitshiyela ngakwesokhohlo, saya ngomkhumbi eSiriya, sehlikela eTire; ngoba umkhumbi wawuzakwethulela khona impahla.
4 Tinafunafuna ophunzira kumeneko, ndipo titawapeza tinakhala nawo masiku asanu ndi awiri. Iwowa, mwa Mzimu Woyera anakakamiza Paulo kuti asapite ku Yerusalemu.
Sesibatholile abafundi, sahlala khona insuku eziyisikhombisa; bona bamtshela uPawuli ngoMoya, ukuthi angenyukeli eJerusalema.
5 Koma nthawi yathu itatha, tinachokako ndi kupitiriza ulendo wathu. Ophunzira onse pamodzi ndi akazi awo ndi ana anatiperekeza mpaka kunja kwa mzinda. Ndipo kumeneko tinagwada mʼmbali mwa nyanja ndi kupemphera.
Kwathi sekwenzakele ukuthi siqede insuku, sasuka sahamba, bonke basiphelekezela kanye labomkabo labantwana kwaze kwaba ngaphandle komuzi; njalo saguqa ngamadolo ekhunjini sakhuleka,
6 Titatsanzikana, tinalowa mʼsitima ija, iwowo anabwerera ku nyumba zawo.
sesivalelisene, sangena emkhunjini, kodwa bona babuyela kubo.
7 Ife tinapitiriza ulendo wathu wochokera ku Turo mpaka tinafika ku Ptolemayi. Kumeneko tinalonjera abale ndi kukhala nawo tsiku limodzi.
Kodwa thina, sesiqedile uhambo ngomkhumbi sisuka eTire, safika ePetolemayi, sesibingelele abazalwane sahlala labo usuku lwaba lunye.
8 Tinachoka mmawa mwake, mpaka tinakafika ku Kaisareya. Tinapita kukakhala mʼnyumba ya mlaliki Filipo, amene anali mmodzi mwa atumiki a mpingo asanu ndi awiri aja.
Kusisa thina esasiloPawuli sasuka safika eKesariya; sesingene endlini kaFiliphu umvangeli, owayengomunye wabayisikhombisa, sahlala laye.
9 Iye anali ndi ana aakazi anayi osakwatiwa amene anali ndi mphatso ya uneneri.
Yena-ke wayelamadodakazi amane, intombi, eziprofethayo.
10 Titakhala kumeneko masiku ambiri, kunabwera mneneri wina wochokera ku Yudeya dzina lake Agabu.
Kwathi sesihlezi insuku ezinengi, kwehla umprofethi othile uAgabusi ngebizo evela eJudiya,
11 Atafika kwa ife, anatenga lamba wa Paulo, nadzimanga naye manja ake ndi mapazi ake ndipo anati, “Mzimu Woyera akuti, ‘Mwini lambayu, Ayuda adzamumanga chomwechi ku Yerusalemu, ndipo adzamupereka mʼmanja mwa anthu a mitundu ina.’”
wasefika kithi, wathatha uzwezwe lukaPawuli, wazibopha izandla kanye lenyawo esithi: Utsho lokho uMoya oyiNgcwele: Indoda olungolwayo loluzwezwe, amaJuda eJerusalema azayibopha kanje, njalo ayinikele ezandleni zabezizwe.
12 Titamva zimenezi, ife pamodzi ndi anthu kumeneko tinamudandaulira Paulo kuti asapite ku Yerusalemu.
Sesizizwile lezizinto, samncenga thina kanye lalabo ababelapho, ukuthi angenyukeli eJerusalema.
13 Koma Paulo anayankha kuti, “Chifukwa chiyani mukulira ndi kunditayitsa mtima? Ndine wokonzeka osati kumangidwa kokha ayi, komanso kufa ku Yerusalemu chifukwa cha dzina la Ambuye Yesu.”
Kodwa uPawuli waphendula esithi: Lenzani likhala lidabula inhliziyo yami? Ngoba mina sengilungele, kungeyisikho ukubotshwa kuphela, kodwa lokufa eJerusalema ngenxa yebizo leNkosi uJesu.
14 Titalephera kumuletsa tinamuleka ndipo tinati, “Chifuniro cha Ambuye chichitike.”
Kwathi engancengeki, sathula sathi: Kayenziwe intando yeNkosi.
15 Pambuyo pake, ife tinakonzeka ndi kunyamuka kumapita ku Yerusalemu.
Emva kwalezinsuku sasesilungiselela, senyukela eJerusalema.
16 Ena mwa ophunzira a ku Kaisareya anatiperekeza mpaka kukatifikitsa ku nyumba ya Mnasoni, kumene tinakonza kuti tizikhalako. Iye anali wa ku Kupro ndiponso mmodzi wa ophunzira oyambirira.
Labathile babafundi beKesariya basebehamba lathi, babuya lothile uMnasoni umKuprosi, umfundi omdala, ebesizangenisa kuye.
17 Titafika ku Yerusalemu, abale anatilandira mwachimwemwe.
Njalo sesifikile eJerusalema, abazalwane basemukela ngokuthokoza.
18 Mmawa mwake Paulo pamodzi ndi ife tonse tinapita kwa Yakobo, ndipo akulu onse a mpingo anali komweko.
Kusisa uPawuli wangena lathi kuJakobe, labadala bonke babekhona.
19 Paulo anawalonjera ndi kuwafotokozera mwatsatanetsatane zimene Mulungu anachita pakati pa anthu a mitundu ina kudzera mu utumiki wake.
Kwathi esebabingelele, walandisa ngakunye ngakunye izinto uNkulunkulu azenzileyo phakathi kwabezizwe ngenkonzo yakhe.
20 Atamva zimenezi, iwo anayamika Mulungu. Kenaka anawuza Paulo kuti, “Mʼbale, ukuona kuti pali Ayuda ambirimbiri amene anakhulupirira, ndipo ndi okhulupirika potsatira Malamulo a Mose.
Kwathi sebekuzwile, bayidumisa iNkosi; bathi kuye: Uyabona, mzalwane, ukuthi zinengi kangakanani izigidi zamaJuda akholwayo; futhi bonke batshisekela umlayo;
21 Iwo anawuzidwa kuti iwe umaphunzitsa Ayuda onse amene akukhala pakati pa anthu a mitundu ina kuti asiye kutsatira Mose, kuti asamachite mdulidwe kapena kutsatira miyambo.
njalo sebetsheliwe ngawe, ukuthi ufundisa wonke amaJuda aphakathi kwabezizwe ukuthi adele uMozisi, usithi angasoki abantwana, lokuthi angahambi ngamasiko.
22 Nanga pamenepa ife titani? Iwo adzamva ndithu kuti iwe wabwera,
Pho-ke kuyini? Isibili kufanele ukuthi ixuku libuthane; ngoba bazakuzwa ukuthi usufikile.
23 tsono iwe chita zimene ife tikuwuze. Tili nawo amuna anayi pano amene anachita lumbiro kwa Mulungu.
Ngakho yenza lokhu esikutsho kuwe; silamadoda amane abalesifungo phezu kwawo;
24 Muwatenge anthu amenewa, ndipo muchite nawo mwambo wowayeretsa ndipo muwalipirire zoti apereke kuti amete tsitsi lawo. Kotero aliyense adzadziwa kuti palibe choonadi pa zimene anamva za inu, koma kuti inu mwini mumakhala moyo womvera Malamulo.
athathe kanye lawe, uzihlambulule kanye lawo, njalo uhlawule indleko zawo, ukuze aphuce amakhanda, njalo ukuze bakwazi bonke ukuthi kakulalutho kulokho abakutshelwe ngawe, kodwa ukuthi lawe uhamba ngokulondoloza umlayo.
25 Koma kunena za anthu a mitundu ina amene asandulika okhulupirira, ife tinawalembera zimene tinavomerezana zakuti asadye chakudya choperekedwa ku mafano, asadye magazi, asadye nyama yopotola ndiponso asachite zadama.”
Kodwa mayelana labezizwe abakholwayo thina sesibhalile, saquma sathi bangagcini lutho olunjalo, ngaphandle kokuthi kabazile okuhlatshelwe izithombe, legazi, lokukhanyiweyo, lokufeba.
26 Mmawa mwake Paulo anatenga amuna aja ndipo anachita mwambo wodziyeretsa. Kenaka anapita ku Nyumba ya Mulungu nakadziwitsa ansembe za tsiku limene adzatsiriza nthawi ya kudziyeretsa ndi kuperekera nsembe aliyense wa iwo.
UPawuli wasewathatha amadoda, kusisa wahlanjululwa kanye lawo wangena ethempelini, ukubika ukuphela kwensuku zokuhlanjululwa, kwaze kwalethwa umnikelo walowo lalowo wawo.
27 Ali pafupi kutsiriza masiku asanu ndi awiriwo, Ayuda ena ochokera ku Asiya anaona Paulo mʼNyumba ya Mulungu. Iwo anawutsa gulu lonse la anthu ndipo anamugwira Paulo,
Kwathi sezizaphela insuku eziyisikhombisa, amaJuda avela eAsiya ayembonile ethempelini, avusa ixuku lonke, amdumela ngezandla,
28 akufuwula kuti, “Inu Aisraeli, tithandizeni! Ndi uyu munthu uja amaphunzitsa anthu onse ponseponse kuti azinyoza mtundu wathu ndiponso Malamulo athu ndi malo ano. Kuwonjezera pamenepo, walowetsa Agriki mʼbwalo la Nyumba ino ndipo wadetsa malo opatulika.”
amemeza athi: Madoda maIsrayeli, sizani! Nguye lumuntu ofundisa bonke endaweni zonke okuphambene lesizwe, lomlayo, lalindawo; futhi ungenisile lamaGriki ethempelini, useyingcolisile lindawo engcwele.
29 Iwo ananena izi chifukwa anali ataona Trofimo wa ku Efeso ali ndi Paulo mu mzindamo ndipo iwo ankaganiza kuti Paulo anamulowetsa mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu.
Ngoba ayebonile ngaphambili uTrofimu umEfesu emzini elaye, amkhumbulela ukuthi uPawuli umngenisile ethempelini.
30 Mzinda wonse unasokonezeka, ndipo anthu anabwera akuthamanga kuchokera kumbali zonse. Anamugwira Paulo, namukokera kunja kwa Nyumbayo, ndipo nthawi yomweyo anatseka zipata.
Lomuzi wonke wanyakazela, labantu bagijimela ndawonye, bamdumela uPawuli bamhudulela ngaphandle kwethempeli; leminyango yahle yavalwa.
31 Pamene anthuwo ankafuna kupha Paulo, nkhaniyi inamveka kwa mkulu wa magulu a asilikali a Aroma kuti mzinda wonse wa Yerusalemu wasokonezeka.
Kuthe besafuna ukumbulala, ilizwi lafika enduneni enkulu yesigaba, ukuthi iJerusalema yonke iyaphithizela;
32 Nthawi yomweyo iye anatenga asilikali ndi atsogoleri a magulu a asilikali ndi kuthamangira kumene kunali anthuwo. Anthuwo ataona mkuluyo ndi asilikali ake analeka kumenya Paulo.
eyahle yathatha amabutho lezinduna zekhulu, yagijimela kubo; kwathi sebebona induna enkulu lamabutho, bayekela ukumtshaya uPawuli.
33 Mkulu wa asilikaliyo anabwera nagwira Paulo, ndipo analamula kuti amangidwe ndi maunyolo awiri. Kenaka iye anafunsa kuti ndi ndani ndipo wachita chiyani.
Induna enkulu yasisondela, yambamba, yalaya ukuthi kabotshwe ngamaketane amabili, yabuza ukuthi ungubani, lokuthi wenzeni.
34 Ena mʼgulumo anafuwula chinthu china ndi enanso chinanso. Tsono popeza mkulu wa asilikaliyo sanathe kudziwa choonadi chenicheni chifukwa cha phokoso, analamula kuti Paulo atengedwe kupita ku malo a asilikali.
Abanye exukwini bememeza okunye labanye okunye; kodwa ingelakulazi iqiniso ngenxa yomsindo, yalaya ukuthi asiwe enkambeni yamabutho.
35 Paulo atafika pa makwerero olowera ku malo a asilikaliwo, ananyamulidwa ndi asilikali chifukwa cha ukali wa anthuwo.
Kwathi esefikile ezikhwelweni, kwenzeka ukuthi athwalwe ngamabutho ngenxa yokufutheka kwexuku;
36 Gulu la anthu limene linamutsatira linapitiriza kufuwula kuti, “Ameneyo aphedwe basi!”
ngoba ixuku labantu lalandela limemeza lisithi: Msuseni!
37 Asilikali ali pafupi kulowa naye ku malo awo, iye anapempha mkulu wa asilikaliyo kuti, “Kodi mungandilole ndiyankhulepo?” Mkulu wa asilikaliyo anafunsa kuti, “Kodi umayankhula Chigriki?
Kwathi uPawuli esezangeniswa enkambeni yamabutho wathi enduneni enkulu: Kuvunyelwe yini ukuthi ngikhulume ulutho kuwe? Yona yasisithi: Uyasazi isiGriki yini?
38 Kodi sindiwe Mwigupto uja amene masiku apitawo unayambitsa kuwukira ndi kutsogolera anthu 4,000 owukira aja nʼkupita nawo ku chipululu?”
Kanti kawusuye yini lowomGibhithe okwathi kungakafiki lezinsuku wenza umvukela, wakhokhelela enkangala amadoda azinkulungwane ezine angababulali?
39 Paulo anayankha kuti, “Ine ndine Myuda, wa ku Tarisisi ku Kilikiya. Sindine nzika ya mzinda wamba. Chonde loleni ndiyankhule nawo anthuwa.”
Kodwa uPawuli wathi: Mina ngingumuntu ongumJuda, weTarsu yeKilikhiya, isakhamuzi somuzi ongadelelekanga; ngiyakuncenga, ngivumela ngikhulume ebantwini.
40 Ataloledwa ndi mkulu wa asilikaliyo, Paulo anayimirira pa makwereropo nakweza dzanja lake kwa gulu la anthuwo. Onse atakhala chete, iye anayankhula nawo mʼChihebri.
Kwathi esemvumele, uPawuli wema ezikhwelweni waqhweba abantu ngesandla; sekuthe cwaka, wasekhuluma labo ngolimi lwamaHebheru wathi:

< Machitidwe a Atumwi 21 >