< Machitidwe a Atumwi 21 >
1 Titalawirana nawo, tinachoka kumeneko mʼsitima ya pamadzi, ndipo tinayenda molunjika mpaka kufika ku Kosi. Mmawa mwake tinapita ku Rode, kuchokera kumeneko tinapita ku Patara.
When, at last, we had torn ourselves away and had set sail, we ran in a straight course to Cos; the next day to Rhodes, and from there to Patara.
2 Kumeneko tinapeza sitima yapamadzi yopita ku Foinike. Choncho tinalowamo nʼkunyamuka.
Finding a ship bound for Phoenicia, we went on board and put to sea.
3 Tinaona chilumba cha Kupro ndipo tinadutsa kummwera kwake nʼkupita ku Siriya. Tinakayima ku Turo chifukwa sitima yathuyo imayenera kusiya katundu kumeneko.
After sighting Cyprus and leaving that island on our left, we continued our voyage to Syria and put in at Tyre; for there the ship was to unload her cargo.
4 Tinafunafuna ophunzira kumeneko, ndipo titawapeza tinakhala nawo masiku asanu ndi awiri. Iwowa, mwa Mzimu Woyera anakakamiza Paulo kuti asapite ku Yerusalemu.
Having searched for the disciples and found them, we stayed at Tyre for seven days; and, taught by the Spirit, they repeatedly urged Paul not to proceed to Jerusalem.
5 Koma nthawi yathu itatha, tinachokako ndi kupitiriza ulendo wathu. Ophunzira onse pamodzi ndi akazi awo ndi ana anatiperekeza mpaka kunja kwa mzinda. Ndipo kumeneko tinagwada mʼmbali mwa nyanja ndi kupemphera.
When, however, our time was up, we left and went on our way, all the disciples and their wives and children coming to see us off. Then, after kneeling down on the beach and praying,
6 Titatsanzikana, tinalowa mʼsitima ija, iwowo anabwerera ku nyumba zawo.
we took leave of one another; and we went on board, while they returned home.
7 Ife tinapitiriza ulendo wathu wochokera ku Turo mpaka tinafika ku Ptolemayi. Kumeneko tinalonjera abale ndi kukhala nawo tsiku limodzi.
As for us, our voyage was over when having sailed from Tyre we reached Ptolemais. here we inquired after the welfare of the brethren, and remained a day with them.
8 Tinachoka mmawa mwake, mpaka tinakafika ku Kaisareya. Tinapita kukakhala mʼnyumba ya mlaliki Filipo, amene anali mmodzi mwa atumiki a mpingo asanu ndi awiri aja.
On the morrow we left Ptolemais and went on to Caesarea, where we came to the house of Philip the Evangelist, who was one of the seven, and stayed with him.
9 Iye anali ndi ana aakazi anayi osakwatiwa amene anali ndi mphatso ya uneneri.
Now Philip had four unmarried daughters who were prophetesses;
10 Titakhala kumeneko masiku ambiri, kunabwera mneneri wina wochokera ku Yudeya dzina lake Agabu.
and during our somewhat lengthy stay a Prophet of the name of Agabus came down from Judaea.
11 Atafika kwa ife, anatenga lamba wa Paulo, nadzimanga naye manja ake ndi mapazi ake ndipo anati, “Mzimu Woyera akuti, ‘Mwini lambayu, Ayuda adzamumanga chomwechi ku Yerusalemu, ndipo adzamupereka mʼmanja mwa anthu a mitundu ina.’”
When he arrived he took Paul's loincloth, and bound his own feet and arms with it, and said, "Thus says the Holy Spirit, 'So will the Jews in Jerusalem bind the owner of this loincloth, and will hand him over to the Gentiles.'"
12 Titamva zimenezi, ife pamodzi ndi anthu kumeneko tinamudandaulira Paulo kuti asapite ku Yerusalemu.
As soon as we heard these words, both we and the brethren at Caesarea entreated Paul not to go up to Jerusalem.
13 Koma Paulo anayankha kuti, “Chifukwa chiyani mukulira ndi kunditayitsa mtima? Ndine wokonzeka osati kumangidwa kokha ayi, komanso kufa ku Yerusalemu chifukwa cha dzina la Ambuye Yesu.”
His reply was, "What can you mean by thus breaking my heart with your grief? Why, as for me, I am ready not only to go to Jerusalem and be put in chains, but even to die there for the sake of the Lord Jesus."
14 Titalephera kumuletsa tinamuleka ndipo tinati, “Chifuniro cha Ambuye chichitike.”
So when he was not to be dissuaded, we ceased remonstrating with him and said, "The Lord's will be done!"
15 Pambuyo pake, ife tinakonzeka ndi kunyamuka kumapita ku Yerusalemu.
A few days afterwards we loaded our baggage-cattle and continued our journey to Jerusalem.
16 Ena mwa ophunzira a ku Kaisareya anatiperekeza mpaka kukatifikitsa ku nyumba ya Mnasoni, kumene tinakonza kuti tizikhalako. Iye anali wa ku Kupro ndiponso mmodzi wa ophunzira oyambirira.
Some of the disciples from Caesarea also joined our party, and brought with them Mnason, a Cyprian, one of the early disciples, at whose house we were to lodge.
17 Titafika ku Yerusalemu, abale anatilandira mwachimwemwe.
At length we reached Jerusalem, and there the brethren gave us a hearty welcome.
18 Mmawa mwake Paulo pamodzi ndi ife tonse tinapita kwa Yakobo, ndipo akulu onse a mpingo anali komweko.
On the following day we went with Paul to call on James, and all the Elders of the Church came also.
19 Paulo anawalonjera ndi kuwafotokozera mwatsatanetsatane zimene Mulungu anachita pakati pa anthu a mitundu ina kudzera mu utumiki wake.
After exchanging friendly greetings, Paul told in detail all that God had done among the Gentiles through his instrumentality.
20 Atamva zimenezi, iwo anayamika Mulungu. Kenaka anawuza Paulo kuti, “Mʼbale, ukuona kuti pali Ayuda ambirimbiri amene anakhulupirira, ndipo ndi okhulupirika potsatira Malamulo a Mose.
And they, when they had heard his statement, gave the glory to God. Then they said, "You see, brother, how many tens of thousands of Jews there are among those who have accepted the faith, and they are all zealous upholders of the Law.
21 Iwo anawuzidwa kuti iwe umaphunzitsa Ayuda onse amene akukhala pakati pa anthu a mitundu ina kuti asiye kutsatira Mose, kuti asamachite mdulidwe kapena kutsatira miyambo.
Now what they have been repeatedly told about you is that you teach all the Jews among the Gentiles to abandon Moses, and that you forbid them to circumcise their children or observe old-established customs.
22 Nanga pamenepa ife titani? Iwo adzamva ndithu kuti iwe wabwera,
What then ought you to do? They are sure to hear that you have come to Jerusalem;
23 tsono iwe chita zimene ife tikuwuze. Tili nawo amuna anayi pano amene anachita lumbiro kwa Mulungu.
so do this which we now tell you. We have four men here who have a vow resting on them.
24 Muwatenge anthu amenewa, ndipo muchite nawo mwambo wowayeretsa ndipo muwalipirire zoti apereke kuti amete tsitsi lawo. Kotero aliyense adzadziwa kuti palibe choonadi pa zimene anamva za inu, koma kuti inu mwini mumakhala moyo womvera Malamulo.
Associate with these men and purify yourself with them, and pay their expenses so that they can shave their heads. Then everybody will know that there is no truth in these stories about you, but that in your own actions you yourself scrupulously obey the Law.
25 Koma kunena za anthu a mitundu ina amene asandulika okhulupirira, ife tinawalembera zimene tinavomerezana zakuti asadye chakudya choperekedwa ku mafano, asadye magazi, asadye nyama yopotola ndiponso asachite zadama.”
But as for the Gentiles who have accepted the faith, we have communicated to them our decision that they are carefully to abstain from anything sacrificed to an idol, from blood, from what is strangled, and from fornication."
26 Mmawa mwake Paulo anatenga amuna aja ndipo anachita mwambo wodziyeretsa. Kenaka anapita ku Nyumba ya Mulungu nakadziwitsa ansembe za tsiku limene adzatsiriza nthawi ya kudziyeretsa ndi kuperekera nsembe aliyense wa iwo.
So Paul associated with the men; and the next day, having purified himself with them, he went into the Temple, giving every one to understand that the days of their purification were finished, and there he remained until the sacrifice for each of them was offered.
27 Ali pafupi kutsiriza masiku asanu ndi awiriwo, Ayuda ena ochokera ku Asiya anaona Paulo mʼNyumba ya Mulungu. Iwo anawutsa gulu lonse la anthu ndipo anamugwira Paulo,
But, when the seven days were nearly over, the Jews from the province of Asia, having seen Paul in the Temple, set about rousing the fury of all the people against him.
28 akufuwula kuti, “Inu Aisraeli, tithandizeni! Ndi uyu munthu uja amaphunzitsa anthu onse ponseponse kuti azinyoza mtundu wathu ndiponso Malamulo athu ndi malo ano. Kuwonjezera pamenepo, walowetsa Agriki mʼbwalo la Nyumba ino ndipo wadetsa malo opatulika.”
They laid hands on him, crying out, "Men of Israel, help! help! This is the man who goes everywhere preaching to everybody against the Jewish people and the Law and this place. And besides, he has even brought Gentiles into the Temple and has desecrated this holy place."
29 Iwo ananena izi chifukwa anali ataona Trofimo wa ku Efeso ali ndi Paulo mu mzindamo ndipo iwo ankaganiza kuti Paulo anamulowetsa mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu.
(For they had previously seen Trophimus the Ephesian with him in the city, and imagined that Paul had brought him into the Temple.)
30 Mzinda wonse unasokonezeka, ndipo anthu anabwera akuthamanga kuchokera kumbali zonse. Anamugwira Paulo, namukokera kunja kwa Nyumbayo, ndipo nthawi yomweyo anatseka zipata.
The excitement spread through the whole city, and the people rushed in crowds to the Temple, and there laid hold of Paul and began to drag him out; and the Temple gates were immediately closed.
31 Pamene anthuwo ankafuna kupha Paulo, nkhaniyi inamveka kwa mkulu wa magulu a asilikali a Aroma kuti mzinda wonse wa Yerusalemu wasokonezeka.
But while they were trying to kill Paul, word was taken up to the Tribune in command of the battalion, that all Jerusalem was in a ferment.
32 Nthawi yomweyo iye anatenga asilikali ndi atsogoleri a magulu a asilikali ndi kuthamangira kumene kunali anthuwo. Anthuwo ataona mkuluyo ndi asilikali ake analeka kumenya Paulo.
He instantly sent for a few soldiers and their officers, and came down among the people with all speed. At the sight of the Tribune and the troops they ceased beating Paul.
33 Mkulu wa asilikaliyo anabwera nagwira Paulo, ndipo analamula kuti amangidwe ndi maunyolo awiri. Kenaka iye anafunsa kuti ndi ndani ndipo wachita chiyani.
Then the Tribune, making his way to him, arrested him, and, having ordered him to be secured with two chains, proceeded to ask who he was and what he had been doing.
34 Ena mʼgulumo anafuwula chinthu china ndi enanso chinanso. Tsono popeza mkulu wa asilikaliyo sanathe kudziwa choonadi chenicheni chifukwa cha phokoso, analamula kuti Paulo atengedwe kupita ku malo a asilikali.
Some of the crowd shouted one accusation against Paul and some another, until, as the uproar made it impossible for the truth to be ascertained with certainty, the Tribune ordered him to be brought into the barracks.
35 Paulo atafika pa makwerero olowera ku malo a asilikaliwo, ananyamulidwa ndi asilikali chifukwa cha ukali wa anthuwo.
When Paul was going up the steps, he had to be carried by the soldiers because of the violence of the mob;
36 Gulu la anthu limene linamutsatira linapitiriza kufuwula kuti, “Ameneyo aphedwe basi!”
for the whole mass of the people pressed on in the rear, shouting, "Away with him!"
37 Asilikali ali pafupi kulowa naye ku malo awo, iye anapempha mkulu wa asilikaliyo kuti, “Kodi mungandilole ndiyankhulepo?” Mkulu wa asilikaliyo anafunsa kuti, “Kodi umayankhula Chigriki?
When he was about to be taken into the barracks, Paul said to the Tribune, "May I speak to you?" "Do you know Greek?" the Tribune asked.
38 Kodi sindiwe Mwigupto uja amene masiku apitawo unayambitsa kuwukira ndi kutsogolera anthu 4,000 owukira aja nʼkupita nawo ku chipululu?”
"Are you not the Egyptian who some years ago excited the riot of the 4,000 cut-throats, and led them out into the Desert?"
39 Paulo anayankha kuti, “Ine ndine Myuda, wa ku Tarisisi ku Kilikiya. Sindine nzika ya mzinda wamba. Chonde loleni ndiyankhule nawo anthuwa.”
"I am a Jew," replied Paul, "belonging to Tarsus in Cilicia, and am a citizen of no unimportant city. Give me leave, I pray you, to speak to the people."
40 Ataloledwa ndi mkulu wa asilikaliyo, Paulo anayimirira pa makwereropo nakweza dzanja lake kwa gulu la anthuwo. Onse atakhala chete, iye anayankhula nawo mʼChihebri.
So with his permission Paul stood on the steps and motioned with his hand to the people to be quiet; and when there was perfect silence he addressed them in Hebrew.