< Machitidwe a Atumwi 20 >
1 Litatha phokoso, Paulo anayitanitsa ophunzira ndipo atawalimbikitsa anawatsanzika ndipo ananyamuka kupita ku Makedoniya.
MAHOPE iho o ka pau ana ae o keia haunaele, hoakoakoa iho la o Paulo i na hanmana, a honi ae la, a puka aku la iwaho, e hele i Makedonia.
2 Iye anayendera madera a kumeneko, nalimbitsa mtima anthu, ndipo pomaliza pake anapita ku Grisi.
Kaahele ae la ia ma ia mau aina, a hooikaika aku la ia lakou me ka olelo nui, hele aku la i Helene;
3 Kumeneko anakhala miyezi itatu. Popeza kuti Ayuda anakonza zomuchita chiwembu pamene amati azinyamuka kupita ku Siriya pa sitima ya pamadzi, iye anaganiza zobwereranso kudzera ku Makedoniya.
Noho iho la malaila ekolu malama: a i kona kokoko ana o holo i Suria, hoohalua aku la na Iudaio ia ia, nolaila, manao iho la ia e hoi ma Makedonia aku.
4 Iye anapita pamodzi ndi Sopatro mwana wa Puro wa ku Bereya, Aristariko ndi Sekundo a ku Tesalonika, Gayo wa ku Derbe ndi Timoteyo, ndipo a ku Asiya anali Tukiko ndi Trofimo.
Hele pu aku la me ia a hiki i Asia o Sopatero, no Beroia, a me Arisetareko laua o Sekunedo no Tesalonike, a me Gaio laua o Timoteo no Derebe, a me Tukiko laua o Teropima no Asia.
5 Anthu amenewa anatsogola ndipo anakatidikira ku Trowa.
Hele mua aku la lakou nei, a kakali iho la ma Teroa no makou.
6 Koma ife tinayenda pa sitima ya pamadzi kuchokera ku Filipi chitatha Chikondwerero cha Buledi wopanda Yisiti. Patapita masiku asanu tinakumana nawo enawo ku Trowa, ndipo tinakhala kumeneko masiku asanu ndi awiri.
A mahope iho o na la o ka berena hu ole, holo aku la makou mai Pilipi aku, po alima hiki aku makou io lakou la ma Teroa; malaila makou i noho ai i na la ehiku.
7 Pa tsiku loyamba la Sabata, tinasonkhana kuti tidye mgonero. Paulo analalikira kwa anthu chifukwa anaganiza zoti achoke tsiku linalo, ndipo analalika mpaka pakati pa usiku.
A i ka la mua o ka hebedoma, i ko na haumana akoakoa ana o wawahi i ka berena, kamailio mai la o Paulo ia lakou, ua makaukau hoi e holo ia kakahiaka ae. Hooloihi hoi i ka olelo ana a hiki i ke aumoe.
8 Munali nyale zambiri mʼchipinda chammwamba mʼmene tinasonkhanamo.
Ua nui no hoi na kukui ma ke keena maluna, i kahi a makou i akoakoa ai.
9 Pa chipinda chachitatu chammwamba cha nyumbayo, pa zenera, panakhala mnyamata wina dzina lake Utiko, amene ankasinza pomwe Paulo amayankhulabe. Atagona tulo, iye anagwa pansi kuchokera pa chipinda chammwamba ndipo anamutola atafa.
Noho iho la kekahi kanaka opiopio ma ka pukamakani, o Eutuko kona inoa, ua kaumaha i ka hiamoe nui; a i ka Paulo kamailio loihi ana, pauhia iho la ia i ka hiamoe, a haule iho la ia ilalo, mai ke kolu o ka papa mai, a hapaiia ae la ia, ua make.
10 Paulo anatsika, nadziponya pa mnyamatayo, namukumbatira. Paulo anati, “Musadandaule, ali moyo!”
Iho mai la o Paulo ilalo, moe iho la maluna ona, puliki aku la ia ia, i mai la, Mai makau oukou; no ka mea, eia no kona ola maloko ona.
11 Kenaka Paulo anakweranso, mʼchipinda muja nanyema buledi nadya. Atayankhula mpaka kucha, anachoka.
Pii hou aku la ia, wawahi ae la i ka berena, ai iho la, kamailio loihi mai la, a wanaao ae, alaila, hele aku la ia.
12 Anthu anatenga mnyamatayo kupita kwawo ali moyo ndipo anatonthozedwa mtima kwambiri.
Lawe mai la lakou i ua kanaka opiopio la, ua ola, aole okana mai ko lakou olioli.
13 Ife tinatsogola kukakwera sitima ya pa madzi kupita ku Aso, kumene tinayembekeza kukatenga Paulo. Iye anakonza motero chifukwa amayenda wapansi.
Holo mua aku la makou ma ka moku, a holo aku la i Aso: manao iho la malaila e hoee ia Paulo maloko, no ka mea, pela ia i kauoha mai ai, no kona makemake a hele wawae ilaila.
14 Pamene anakumana nafe ku Aso tinamutenga ndipo tinapita ku Mitilene.
A halawai mai la ia me makou ma Aso, hoee mai la makou ia ia, a holo ma Mitulene.
15 Mmawa mwake tinachoka kumeneko pa sitima ya pamadzi ndipo tinafika pafupi ndi Kiyo. Tsiku linalo tinawolokera ku Samo, ndipo tsiku linanso tinafika ku Mileto.
Holo aku la makou mailaila aku, a ao ae hiki ma Kio, a ia la ae, hiki makou i Samo, a noho ma Terogulio; a ia la ae, hele mai makou a Mileto.
16 Paulo anali atatsimikiza kuti alambalale Efeso kuopa kutaya nthawi ku Asiya, pakuti ankafulumira kuti akafike ku Yerusalemu kuti ngati nʼkotheka kuti tsiku la Pentekosite akakhale ali ku Yerusalemu.
Ua paa no ko Paulo manao, e holo ma Epeso ae, aole hoi e kali ma Asia; no ka mea, ua wikiwiki no ia, ina pono ia ia ke hiki i Ierusalema ma ka la Penetekota.
17 Paulo ali ku Mileto, anatumiza mawu ku Efeso kuyitana akulu ampingo.
Hoouna ae la ia, mai Mileto aku a Epeso, e kii i na lunakahiko o ka ekalesia.
18 Iwo atafika, Paulo anati, “Inu mukudziwa mmene ndinakhalira nanu nthawi yonse imene ndinali nanu kuyambira tsiku loyamba limene ndinafika ku Asiya.
A hiki lakou io na la, i mai la oia ia lakou, Ua ike no oukou, mai ka la makamua a'u i hiki mai ai i Asia nei, i ke ano o ko'u noho ana me oukou i na manawa a pau,
19 Ndinatumikira Ambuye modzichepetsa kwambiri ndiponso ndi misozi, ngakhale ndinayesedwa kwambiri ndi ziwembu za Ayuda.
E hookauwa ana'ku na ka Haku me ka manao hoohaahaa a pau, a me na waimaka, a me na pilikia i loaa ia'u, no ka hoohalua ana o na Iudaio;
20 Inu mukudziwa kuti, sindinakubisireni kanthu kalikonse kopindulitsa koma ndinakuphunzitsani poyera komanso nyumba ndi nyumba.
Aole hoi au i huna i kekahi mea pono, aka, ua hoike au ia oukou, ua ao aku hoi ia oukou ma ke akea, a ma kela hale a ia hale aku,
21 Ine ndinawuza Ayuda komanso Agriki kuti ayenera kutembenukira kwa Mulungu polapa ndikuti akhulupirire Ambuye athu Yesu.
E hoike ana'ku i na Iudaio, a i na Helene, i ka mihi aku i ke Akua, a me ka manaoio aku i ka Haku, ia Iesu Kristo.
22 “Ndipo tsopano, mokakamizidwa ndi Mzimu, ndikupita ku Yerusalemu, sindikudziwa zimene zikandichitikire kumeneko.”
Eia hoi au, ke hele paa aku nei ma ka uhane i Ierusalema; aole nae au i ike i na mea e loohia ai ia'u ilaila:
23 Chimene ndikudziwa ndi chakuti Mzimu Woyera wandichenjeza mu mzinda uliwonse kuti ndende ndi mavuto zikundidikira.
Aka, ke hoike pono mai nei ka Uhane Hemolele ma na kulanakauhale a pau, i mai, Ua makaukau na kaula paa a me ka pilikia no'u.
24 Koma sindilabadira konse za moyo wanga ngati kuti ndi wa mtengo wapatali kwa ine, malingana ndikatsirize ntchito yanga ndi utumiki umene Ambuye Yesu anandipatsa, ntchito yochitira umboni Uthenga Wabwino wachisomo cha Mulungu.
Aole hoi au e manao i keia mau mea, aole no hoi e manao wau he mea makemake no'u kuu ola nei, i hoopau wau i ko'u hele ana me ka olioli, a me ka oihana i loaa mai ia'u na ka Haku mai, na Iesu; i hoike aku no hoi au i ka euanelio o ka lokomaikai o ke Akua.
25 “Tsopano ndikudziwa kuti inu nonse amene ndinakuyenderani ndi kumakulalikirani ufumu wa Mulungu simudzaonanso nkhope yanga.
Aia hoi, ano la, ua ike no wau, aole e ike hou ia ko'u maka e oukou a pau, ka poe au i hoike aku ai i ke aupuni o ke Akua, i ko'u hele ana mawaena o oukou.
26 Chifukwa chake, ine ndikukuwuzani lero kuti ndilibe mlandu ndi munthu aliyense.
No ia mea, ke hoike aku nei au ia oukou i keia la, ua maemae au i ke koko o na mea a pau.
27 Pakuti sindinakubisireni pokulalikirani chifuniro chonse cha Mulungu.
No ka mea, aole au i molowa i ko'u hai ana aku ia oukou i ka makemake a pau a ke Akua.
28 Mudziyangʼanire nokha ndiponso muyangʼanire gulu lankhosa limene Mzimu Woyera anakuyikani kuti mukhale oyangʼanira ake. Khalani abusa a mpingo wa Mulungu umene Iye anawugula ndi magazi ake.
Nolaila e ao oukou ia oukou iho, a me ka ohana a pau, maluna ona i hooliloia'i oukou e ka Uhane Hemolele i poe kahu. E hanai i ka ekalesia o ke Akua, i ka mea ana i kuai ai i kona koko iho.
29 Ndikudziwa kuti ndikachoka ine, padzafika mimbulu yolusa pakati panu imene sidzalekerera gulu lankhosalo.
No ka mea, ua ike no au i keia, a hala au, alaila e komo mai na iliohae ino loa iwaena o oukou, aole loa lakou e minamina i ka ohana.
30 Ngakhale pakati pa inu nokha padzapezeka anthu oyankhula zonama ndi cholinga chofuna kukhala ndi ophunzira kuti awatsate.
E ku mai no hoi kekahi poe kanaka no oukou iho, e olelo no i na mea hoopunipuni e hoohuli i haumana mamuli o lakou.
31 Tsono inu, samalani! Kumbukirani kuti kwa zaka zitatu, usana ndi usiku ndiponso ndi misozi sindinaleke kuchenjeza aliyense wa inu.
No ia mea, e makaala oukou, e hoomanao hoi i na makahiki ekolu a'u i hoomaha ole ai ke ao aku ia oukou a pau i ka po, a me ke ao, me na waimaka.
32 “Tsopano ine ndikukuperekani kwa Mulungu ndiponso kwa mawu a chisomo chake, amene ali ndi mphamvu zokulitsa inu ndi kukupatsani chuma pakati pa onse amene anayeretsedwa.
E na hoahanau, ano la, ke haawi aku nei au ia oukou i ke Akua, a i ka olelo o kona lokomaikai, i ka mea hiki ke hookupaa ia oukou, a me ka haawi ia oukou i hooilina mawaena o ka poe a pau i hoomaemaeia.
33 Ine sindinasirire siliva kapena golide kapena zovala za munthu aliyense.
Aole loa au i kuko aku i ke kala, a me ke gula, a me ka aahu o kekahi.
34 Inu nomwe mukudziwa kuti manja angawa ananditumikira kuti tipeze zimene ine ndi anzanga tinkazifuna.
Oiaio, ua ike no oukou, ua hookauwa mai keia mau lima no ko'u hemahema, a no ka poe me a'u.
35 Pa zonse zimene ndinachita, ndinakuonetsani kuti pogwira ntchito molimbika motere tiyenera kuthandiza ofowoka, pokumbukira mawu a Ambuye Yesu akuti, ‘Kupereka kumadalitsa kuposa kulandira.’”
Ua hoike aku no au ia oukou, i na mea a pau, a pela hoi e pono ai ke hana oukou, a e kokua aku no hoi i ka poe palupalu; e manao no hoi i ka olelo a ka Haku, a Iesu, i kana i ana mai, Ua oi aku ka pomaikai o ka haawi ana aku mamua o ka loaa ana mai.
36 Atanena zimenezi, anagwada pansi pamodzi ndi ena onse, napemphera.
Olelo mai la ia i keia mau mea, kukuli iho la ia, a pule aku la me lakou a pau.
37 Onse analira pamene amamukumbatira ndi kupsompsona.
Uwe nui iho la lakou a pau, a hina lakou ma ka ai o Paulo, honi mai la ia ia;
38 Chimene chinamvetsa chisoni kwambiri ndi mawu ake akuti sadzaonanso nkhope yake. Kenaka iwo anamuperekeza ku sitima yapamadzi.
No kela olelo ana i i mai ai, aole lakou e ike hou i kona maka, nolaila ko lakou kaumaha nui. Ukali aku la lakou ia ia ma ka moku.