< Machitidwe a Atumwi 20 >
1 Litatha phokoso, Paulo anayitanitsa ophunzira ndipo atawalimbikitsa anawatsanzika ndipo ananyamuka kupita ku Makedoniya.
When the uproar had ceased, Paul sent for the disciples; and, after speaking words of encouragement to them, he took his leave, and started for Macedonia.
2 Iye anayendera madera a kumeneko, nalimbitsa mtima anthu, ndipo pomaliza pake anapita ku Grisi.
Passing through those districts he encouraged the disciples in frequent addresses, and then came into Greece, and spent three months there.
3 Kumeneko anakhala miyezi itatu. Popeza kuti Ayuda anakonza zomuchita chiwembu pamene amati azinyamuka kupita ku Siriya pa sitima ya pamadzi, iye anaganiza zobwereranso kudzera ku Makedoniya.
The Jews having planned to waylay him whenever he might be on the point of taking ship for Syria, he decided to travel back by way of Macedonia.
4 Iye anapita pamodzi ndi Sopatro mwana wa Puro wa ku Bereya, Aristariko ndi Sekundo a ku Tesalonika, Gayo wa ku Derbe ndi Timoteyo, ndipo a ku Asiya anali Tukiko ndi Trofimo.
He was accompanied as far as the province of Asia by Sopater the Beroean, the son of Pyrrhus; by the Thessalonians, Aristarchus and Secundus; by Gaius of Derbe, and Timothy; and by the Asians, Tychicus and Trophimus.
5 Anthu amenewa anatsogola ndipo anakatidikira ku Trowa.
These brethren had gone on and were waiting for us in the Troad.
6 Koma ife tinayenda pa sitima ya pamadzi kuchokera ku Filipi chitatha Chikondwerero cha Buledi wopanda Yisiti. Patapita masiku asanu tinakumana nawo enawo ku Trowa, ndipo tinakhala kumeneko masiku asanu ndi awiri.
But we ourselves sailed from Philippi after the days of Unleavened Bread, and five days later joined them in the Troad, where we remained for a week.
7 Pa tsiku loyamba la Sabata, tinasonkhana kuti tidye mgonero. Paulo analalikira kwa anthu chifukwa anaganiza zoti achoke tsiku linalo, ndipo analalika mpaka pakati pa usiku.
On the first day of the week, when we had met to break bread, Paul, who was going away the next morning, was preaching to them, and prolonged his discourse till midnight.
8 Munali nyale zambiri mʼchipinda chammwamba mʼmene tinasonkhanamo.
Now there were a good many lamps in the room upstairs where we all were,
9 Pa chipinda chachitatu chammwamba cha nyumbayo, pa zenera, panakhala mnyamata wina dzina lake Utiko, amene ankasinza pomwe Paulo amayankhulabe. Atagona tulo, iye anagwa pansi kuchokera pa chipinda chammwamba ndipo anamutola atafa.
and a youth of the name of Eutychus was sitting at the window. This lad, gradually sinking into deep sleep while Paul preached at unusual length, overcome at last by sleep, fell from the second floor and was taken up dead.
10 Paulo anatsika, nadziponya pa mnyamatayo, namukumbatira. Paulo anati, “Musadandaule, ali moyo!”
Paul, however, went down, threw himself upon him, and folding him in his arms said, "Do not be alarmed; his life is still in him."
11 Kenaka Paulo anakweranso, mʼchipinda muja nanyema buledi nadya. Atayankhula mpaka kucha, anachoka.
Then he went upstairs again, broke bread, and took some food; and after a long conversation which was continued till daybreak, at last he parted from them.
12 Anthu anatenga mnyamatayo kupita kwawo ali moyo ndipo anatonthozedwa mtima kwambiri.
They had taken the lad home alive, and were greatly comforted.
13 Ife tinatsogola kukakwera sitima ya pa madzi kupita ku Aso, kumene tinayembekeza kukatenga Paulo. Iye anakonza motero chifukwa amayenda wapansi.
The rest of us had already gone on board a ship, and now we set sail for Assos, intending to take Paul on board there; for so he had arranged, he himself intending to go by land.
14 Pamene anakumana nafe ku Aso tinamutenga ndipo tinapita ku Mitilene.
Accordingly, when he met us at Assos, we took him on board and came to Mitylene.
15 Mmawa mwake tinachoka kumeneko pa sitima ya pamadzi ndipo tinafika pafupi ndi Kiyo. Tsiku linalo tinawolokera ku Samo, ndipo tsiku linanso tinafika ku Mileto.
Sailing from there, we arrived the next day off Chios. On the next we touched at Samos; and on the day following reached Miletus.
16 Paulo anali atatsimikiza kuti alambalale Efeso kuopa kutaya nthawi ku Asiya, pakuti ankafulumira kuti akafike ku Yerusalemu kuti ngati nʼkotheka kuti tsiku la Pentekosite akakhale ali ku Yerusalemu.
For Paul's plan was to sail past Ephesus, so as not to spend much time in the province of Asia; since he was very desirous of being in Jerusalem, if possible, on the day of the Harvest Festival.
17 Paulo ali ku Mileto, anatumiza mawu ku Efeso kuyitana akulu ampingo.
From Miletus he sent to Ephesus for the Elders of the Church to come to him.
18 Iwo atafika, Paulo anati, “Inu mukudziwa mmene ndinakhalira nanu nthawi yonse imene ndinali nanu kuyambira tsiku loyamba limene ndinafika ku Asiya.
Upon their arrival he said to them, "You Elders well know, from the first day of my setting foot in the province of Asia, the kind of life I lived among you the whole time,
19 Ndinatumikira Ambuye modzichepetsa kwambiri ndiponso ndi misozi, ngakhale ndinayesedwa kwambiri ndi ziwembu za Ayuda.
serving the Lord in all humility, and with tears, and amid trials which came upon me through the plotting of the Jews--
20 Inu mukudziwa kuti, sindinakubisireni kanthu kalikonse kopindulitsa koma ndinakuphunzitsani poyera komanso nyumba ndi nyumba.
and that I never shrank from declaring to you anything that was profitable, or from teaching you in public and in your homes,
21 Ine ndinawuza Ayuda komanso Agriki kuti ayenera kutembenukira kwa Mulungu polapa ndikuti akhulupirire Ambuye athu Yesu.
and urging upon both Jews and Greeks the necessity of turning to God and of believing in Jesus our Lord.
22 “Ndipo tsopano, mokakamizidwa ndi Mzimu, ndikupita ku Yerusalemu, sindikudziwa zimene zikandichitikire kumeneko.”
"And now, impelled by a sense of duty, I am on my way to Jerusalem, not knowing what will happen to me there,
23 Chimene ndikudziwa ndi chakuti Mzimu Woyera wandichenjeza mu mzinda uliwonse kuti ndende ndi mavuto zikundidikira.
except that the Holy Spirit, at town after town, testifies to me that imprisonment and suffering are awaiting me.
24 Koma sindilabadira konse za moyo wanga ngati kuti ndi wa mtengo wapatali kwa ine, malingana ndikatsirize ntchito yanga ndi utumiki umene Ambuye Yesu anandipatsa, ntchito yochitira umboni Uthenga Wabwino wachisomo cha Mulungu.
But even the sacrifice of my life I count as nothing, if only I may perfect my earthly course, and be faithful to the duty which the Lord Jesus has entrusted to me of proclaiming, as of supreme importance, the Good News of God's grace.
25 “Tsopano ndikudziwa kuti inu nonse amene ndinakuyenderani ndi kumakulalikirani ufumu wa Mulungu simudzaonanso nkhope yanga.
"And now, I know that none of you among whom I have gone in and out proclaiming the coming of the Kingdom will any longer see my face.
26 Chifukwa chake, ine ndikukuwuzani lero kuti ndilibe mlandu ndi munthu aliyense.
Therefore I protest to you to-day that I am not responsible for the ruin of any one of you.
27 Pakuti sindinakubisireni pokulalikirani chifuniro chonse cha Mulungu.
For I have not shrunk from declaring to you God's whole truth.
28 Mudziyangʼanire nokha ndiponso muyangʼanire gulu lankhosa limene Mzimu Woyera anakuyikani kuti mukhale oyangʼanira ake. Khalani abusa a mpingo wa Mulungu umene Iye anawugula ndi magazi ake.
"Take heed to yourselves and to all the flock among which the Holy Spirit has placed you to take the oversight for Him and act as shepherds to the Church of God, which He has bought with His own blood.
29 Ndikudziwa kuti ndikachoka ine, padzafika mimbulu yolusa pakati panu imene sidzalekerera gulu lankhosalo.
I know that, when I am gone, cruel wolves will come among you and will not spare the flock;
30 Ngakhale pakati pa inu nokha padzapezeka anthu oyankhula zonama ndi cholinga chofuna kukhala ndi ophunzira kuti awatsate.
and that from among your own selves men will rise up who will seek with their perverse talk to draw away the disciples after them.
31 Tsono inu, samalani! Kumbukirani kuti kwa zaka zitatu, usana ndi usiku ndiponso ndi misozi sindinaleke kuchenjeza aliyense wa inu.
Therefore be on the alert; and remember that, night and day, for three years, I never ceased admonishing every one, even with tears.
32 “Tsopano ine ndikukuperekani kwa Mulungu ndiponso kwa mawu a chisomo chake, amene ali ndi mphamvu zokulitsa inu ndi kukupatsani chuma pakati pa onse amene anayeretsedwa.
"And now I commend you to God and to the word of His grace. He is able to build you up and to give you your inheritance among His people.
33 Ine sindinasirire siliva kapena golide kapena zovala za munthu aliyense.
No one's silver or gold or clothing have I coveted.
34 Inu nomwe mukudziwa kuti manja angawa ananditumikira kuti tipeze zimene ine ndi anzanga tinkazifuna.
You yourselves know that these hands of mine have provided for my own necessities and for the people with me.
35 Pa zonse zimene ndinachita, ndinakuonetsani kuti pogwira ntchito molimbika motere tiyenera kuthandiza ofowoka, pokumbukira mawu a Ambuye Yesu akuti, ‘Kupereka kumadalitsa kuposa kulandira.’”
In all things I have set you an example, showing you that, by working as I do, you ought to help the weak, and to bear in mind the words of the Lord Jesus, how He Himself said, "'It is more blessed to give than to receive.'"
36 Atanena zimenezi, anagwada pansi pamodzi ndi ena onse, napemphera.
Having spoken thus, Paul knelt down and prayed with them all;
37 Onse analira pamene amamukumbatira ndi kupsompsona.
and with loud lamentation they all threw their arms round his neck, and kissed him lovingly,
38 Chimene chinamvetsa chisoni kwambiri ndi mawu ake akuti sadzaonanso nkhope yake. Kenaka iwo anamuperekeza ku sitima yapamadzi.
grieved above all things at his having told them that after that day they were no longer to see his face. And they went with him to the ship.