< Machitidwe a Atumwi 20 >
1 Litatha phokoso, Paulo anayitanitsa ophunzira ndipo atawalimbikitsa anawatsanzika ndipo ananyamuka kupita ku Makedoniya.
Men efter at dette Røre var stillet, lod Paulus Disciplene hente og formanede dem, tog Afsked og begav sig derfra for at rejse til Makedonien.
2 Iye anayendera madera a kumeneko, nalimbitsa mtima anthu, ndipo pomaliza pake anapita ku Grisi.
Og da han var dragen igennem disse Egne og havde formanet dem med megen Tale, kom han til Grækenland.
3 Kumeneko anakhala miyezi itatu. Popeza kuti Ayuda anakonza zomuchita chiwembu pamene amati azinyamuka kupita ku Siriya pa sitima ya pamadzi, iye anaganiza zobwereranso kudzera ku Makedoniya.
Der tilbragte han tre Måneder, og da Jøderne havde Anslag for imod ham, just som han skulde til at sejle til Syrien, blev han til Sinds at vende tilbage igennem Makedonien.
4 Iye anapita pamodzi ndi Sopatro mwana wa Puro wa ku Bereya, Aristariko ndi Sekundo a ku Tesalonika, Gayo wa ku Derbe ndi Timoteyo, ndipo a ku Asiya anali Tukiko ndi Trofimo.
Men Pyrrus's Søn Sopater fra Berøa og af Thessalonikerne Aristarkus og Sekundus og Kajus fra Derbe og Timotheus og af Asiaterne Tykikus og Trofimus fulgte med ham til Asien.
5 Anthu amenewa anatsogola ndipo anakatidikira ku Trowa.
Disse droge forud og biede på os i Troas;
6 Koma ife tinayenda pa sitima ya pamadzi kuchokera ku Filipi chitatha Chikondwerero cha Buledi wopanda Yisiti. Patapita masiku asanu tinakumana nawo enawo ku Trowa, ndipo tinakhala kumeneko masiku asanu ndi awiri.
men vi sejlede efter de usyrede Brøds Dage ud fra Filippi og kom fem Dage efter til dem i Troas, hvor vi tilbragte syv Dage.
7 Pa tsiku loyamba la Sabata, tinasonkhana kuti tidye mgonero. Paulo analalikira kwa anthu chifukwa anaganiza zoti achoke tsiku linalo, ndipo analalika mpaka pakati pa usiku.
Men på den første Dag i Ugen, da vi vare forsamlede for at bryde Brødet, samtalede Paulus med dem, da han den næste Dag vilde rejse derfra, og han blev ved med at tale indtil Midnat.
8 Munali nyale zambiri mʼchipinda chammwamba mʼmene tinasonkhanamo.
Men der var mange Lamper i Salen ovenpå, hvor vi vare samlede.
9 Pa chipinda chachitatu chammwamba cha nyumbayo, pa zenera, panakhala mnyamata wina dzina lake Utiko, amene ankasinza pomwe Paulo amayankhulabe. Atagona tulo, iye anagwa pansi kuchokera pa chipinda chammwamba ndipo anamutola atafa.
Og der sad i Vinduet en ung Mand ved Navn Eutykus; han faldt i en dyb Søvn, da Paulus fortsatte Samtalen så længe, og overvældet af Søvnen styrtede han ned fra det tredje Stokværk og blev tagen død op.
10 Paulo anatsika, nadziponya pa mnyamatayo, namukumbatira. Paulo anati, “Musadandaule, ali moyo!”
Men Paulus gik ned og kastede sig over ham og omfavnede ham og sagde: "Larmer ikke; thi hans Sjæl er i ham."
11 Kenaka Paulo anakweranso, mʼchipinda muja nanyema buledi nadya. Atayankhula mpaka kucha, anachoka.
Men han gik op igen og brød Brødet og nød deraf og talte endnu længe med dem indtil Dagningen, og dermed drog han bort.
12 Anthu anatenga mnyamatayo kupita kwawo ali moyo ndipo anatonthozedwa mtima kwambiri.
Men de bragte det unge Menneske levende op og vare ikke lidet trøstede.
13 Ife tinatsogola kukakwera sitima ya pa madzi kupita ku Aso, kumene tinayembekeza kukatenga Paulo. Iye anakonza motero chifukwa amayenda wapansi.
Men vi gik forud til Skibet og sejlede til Assus og skulde derfra tage Paulus med; thi således havde han bestemt det, da han selv vilde gå til Fods.
14 Pamene anakumana nafe ku Aso tinamutenga ndipo tinapita ku Mitilene.
Da han nu stødte til os i Assus, toge vi ham om Bord og kom til Mitylene.
15 Mmawa mwake tinachoka kumeneko pa sitima ya pamadzi ndipo tinafika pafupi ndi Kiyo. Tsiku linalo tinawolokera ku Samo, ndipo tsiku linanso tinafika ku Mileto.
Og vi sejlede derfra og kom den næste Dag lige udfor Kios; Dagen derpå lagde vi til ved Samos og kom næste Dag til Milet.
16 Paulo anali atatsimikiza kuti alambalale Efeso kuopa kutaya nthawi ku Asiya, pakuti ankafulumira kuti akafike ku Yerusalemu kuti ngati nʼkotheka kuti tsiku la Pentekosite akakhale ali ku Yerusalemu.
Thi Paulus havde besluttet at sejle Efesus forbi, for at det ikke skulde hændes, at han blev opholdt i Asien; thi han hastede for at komme til Jerusalem på Pinsedagen, om det var ham muligt.
17 Paulo ali ku Mileto, anatumiza mawu ku Efeso kuyitana akulu ampingo.
Men fra Milet sendte han Bud til Efesus og lod Menighedens Ældste kalde til sig.
18 Iwo atafika, Paulo anati, “Inu mukudziwa mmene ndinakhalira nanu nthawi yonse imene ndinali nanu kuyambira tsiku loyamba limene ndinafika ku Asiya.
Og da de kom til ham, sagde han til dem: "I vide, hvorledes jeg færdedes iblandt eder den hele Tid igennem fra den første Dag, jeg kom til Asien,
19 Ndinatumikira Ambuye modzichepetsa kwambiri ndiponso ndi misozi, ngakhale ndinayesedwa kwambiri ndi ziwembu za Ayuda.
idet jeg tjente Herren i al Ydmyghed og under Tårer og Prøvelser, som timedes mig ved Jødernes Efterstræbelser;
20 Inu mukudziwa kuti, sindinakubisireni kanthu kalikonse kopindulitsa koma ndinakuphunzitsani poyera komanso nyumba ndi nyumba.
hvorledes jeg ikke har unddraget mig fra at forkynde eder noget som helst af det, som kunde være til Gavn, og at lære eder offentligt og i Husene,
21 Ine ndinawuza Ayuda komanso Agriki kuti ayenera kutembenukira kwa Mulungu polapa ndikuti akhulupirire Ambuye athu Yesu.
idet jeg vidnede både for Jøder og Grækere om Omvendelsen til Gud og Troen på vor Herre Jesus Kristus.
22 “Ndipo tsopano, mokakamizidwa ndi Mzimu, ndikupita ku Yerusalemu, sindikudziwa zimene zikandichitikire kumeneko.”
Og nu se, bunden af Ånden drager jeg til Jerusalem uden at vide, hvad der skal møde mig,
23 Chimene ndikudziwa ndi chakuti Mzimu Woyera wandichenjeza mu mzinda uliwonse kuti ndende ndi mavuto zikundidikira.
kun, at den Helligånd i hver By vidner for mig og siger, at Lænker og Trængsler vente mig.
24 Koma sindilabadira konse za moyo wanga ngati kuti ndi wa mtengo wapatali kwa ine, malingana ndikatsirize ntchito yanga ndi utumiki umene Ambuye Yesu anandipatsa, ntchito yochitira umboni Uthenga Wabwino wachisomo cha Mulungu.
Men jeg agter ikke mit Liv noget værd for mig selv, for at jeg kan fuldende mit Løb og den Tjeneste, som jeg har fået af den Herre Jesus, at vidne om Guds Nådes Evangelium.
25 “Tsopano ndikudziwa kuti inu nonse amene ndinakuyenderani ndi kumakulalikirani ufumu wa Mulungu simudzaonanso nkhope yanga.
Og nu se, jeg ved, at I ikke mere skulle se mit Ansigt, alle I, iblandt hvem jeg gik om og prædikede Riget.
26 Chifukwa chake, ine ndikukuwuzani lero kuti ndilibe mlandu ndi munthu aliyense.
Derfor vidner jeg for eder på denne Dag, at jeg er ren for alles Blod;
27 Pakuti sindinakubisireni pokulalikirani chifuniro chonse cha Mulungu.
thi jeg unddrog mig ikke fra at forkynde eder hele Guds Råd.
28 Mudziyangʼanire nokha ndiponso muyangʼanire gulu lankhosa limene Mzimu Woyera anakuyikani kuti mukhale oyangʼanira ake. Khalani abusa a mpingo wa Mulungu umene Iye anawugula ndi magazi ake.
Så giver Agt på eder selv og den hele Hjord, i hvilken den Helligånd satte eder som Tilsynsmænd, til at vogte Guds Menighed, som han erhvervede sig med sit eget Blod.
29 Ndikudziwa kuti ndikachoka ine, padzafika mimbulu yolusa pakati panu imene sidzalekerera gulu lankhosalo.
Jeg ved, at der efter min Bortgang skal komme svare Ulve ind iblandt eder, som ikke ville spare Hjorden.
30 Ngakhale pakati pa inu nokha padzapezeka anthu oyankhula zonama ndi cholinga chofuna kukhala ndi ophunzira kuti awatsate.
Og af eders egen Midte skal der opstå Mænd, som skulle tale forvendte Ting for at drage Disciplene efter sig.
31 Tsono inu, samalani! Kumbukirani kuti kwa zaka zitatu, usana ndi usiku ndiponso ndi misozi sindinaleke kuchenjeza aliyense wa inu.
Derfor våger og kommer i Hu, at jeg har ikke ophørt i tre År, Nat og Dag, at påminde hver enkelt med Tårer.
32 “Tsopano ine ndikukuperekani kwa Mulungu ndiponso kwa mawu a chisomo chake, amene ali ndi mphamvu zokulitsa inu ndi kukupatsani chuma pakati pa onse amene anayeretsedwa.
Og nu overgiver jeg eder til Gud og hans Nådes Ord, som formår at opbygge eder og at give eder Arven iblandt alle de helligede.
33 Ine sindinasirire siliva kapena golide kapena zovala za munthu aliyense.
Jeg har ikke begæret nogens Sølv eller Guld eller Klædebon.
34 Inu nomwe mukudziwa kuti manja angawa ananditumikira kuti tipeze zimene ine ndi anzanga tinkazifuna.
I vide selv, at disse Hænder have tjent for mine Fornødenheder og for dem, som vare med mig.
35 Pa zonse zimene ndinachita, ndinakuonetsani kuti pogwira ntchito molimbika motere tiyenera kuthandiza ofowoka, pokumbukira mawu a Ambuye Yesu akuti, ‘Kupereka kumadalitsa kuposa kulandira.’”
Jeg viste eder i alle Ting, at således bør vi arbejde og tage os af de skrøbelige og ihukomme den Herres Jesu Ord, at han selv har sagt: "Det er saligere at give end at tage."
36 Atanena zimenezi, anagwada pansi pamodzi ndi ena onse, napemphera.
Og da han havde sagt dette, faldt han på sine Knæ og bad med dem alle.
37 Onse analira pamene amamukumbatira ndi kupsompsona.
Og de brast alle i heftig Gråd, og de faldt Paulus om Halsen og kyssede ham.
38 Chimene chinamvetsa chisoni kwambiri ndi mawu ake akuti sadzaonanso nkhope yake. Kenaka iwo anamuperekeza ku sitima yapamadzi.
Og mest smertede dem det Ord, han havde sagt, at de ikke mere skulde se hans Ansigt. Så ledsagede de ham til Skibet.