< Machitidwe a Atumwi 2 >
1 Litafika tsiku la chikondwerero cha Pentekosite, onse anali pamodzi.
Коли ж поча́вся день П'ятдесятниці, всі вони однодушно знахо́дилися вкупі.
2 Mwadzidzidzi kunamveka mkokomo kuchokera kumwamba ngati wa mphepo yamphamvu, ndipo inadzaza nyumba yonse imene amakhala.
І на́гло зчинився шум із не́ба, ніби буря рапто́ва зірва́лася, і перепо́внила ввесь той дім, де сиділи вони.
3 Iwo anaona zinthu zokhala ngati malilime amoto ogawikana ndipo anakhala pa aliyense wa iwo.
І з'явилися їм язи́ки поді́лені, немов би огне́нні, та й на кожному з них по одно́му осів.
4 Ndipo onse anadzazidwa ndi Mzimu Woyera, nayamba kuyankhula mu ziyankhulo zina, monga Mzimu Woyerayo anawayankhulitsa.
Усі ж вони спо́внились Духом Святим, і почали́ говорити іншими мо́вами, як їм Дух промовляти давав.
5 Ayuda woopa Mulungu ochokera ku mayiko onse a dziko lapansi ankakhala mu Yerusalemu nthawi imeneyi.
Перебува́ли ж в Єрусалимі юдеї, люди побожні, від усякого наро́ду під небом.
6 Utamveka mkokomo uja, gulu la anthu linasonkhana. Anthuwo anadabwa chifukwa aliyense anawamva atumwiwo akuyankhula ziyankhulo zosiyanasiyana.
А коли оцей го́мін зчинився, зібралася бе́зліч наро́ду, — та й диву далися, бо кожен із них тут почув, що вони розмовляли їхньою власною мовою!
7 Mothedwa nzeru anafunsana kuti, “Kodi anthu onse amene akuyankhulawa si Agalileya?
Усі ж побенте́жилися та дивувалися, та й казали один до одно́го: „Хіба ж не галіле́яни всі ці, що гово́рять?
8 Nanga bwanji aliyense wa ife akuwamva iwo mu chinenero cha kwawo?
Як же кожен із нас чує свою́ власну мову, що ми в ній народи́лись?
9 Apanti, Amedi ndi Aelami; okhala ku Mesopotamiya, ku Yudeya ndi ku Kapadokiya, ku Ponto ndi ku Asiya,
Парфя́ни та мі́дяни та еламі́ти, також ме́шканці Месопота́мії, Юдеї та Каппадокі́ї, Понту та Азії,
10 ku Frugiya ndi Pamfiliya, ku Igupto ndi ku madera a ku Libiya kufupi ndi ku Kurene; alendo ochokera ku Roma,
і Фрі́ґії та Памфі́лії, Єгипту й лівійських земель край Кіре́ни, і захожі римля́ни,
11 Ayuda ndi otsatira chipembedzo cha Chiyuda onse pamodzi; Akrete ndi Aarabu, ife tonse tikuwamva akuyankhula za ntchito zodabwitsa za Mulungu mu ziyankhulo zathu.”
юдеї й нововірці, крі́тяни й араби, — усі чуємо ми, що говорять вони про великі діла Божі мовами нашими!“
12 Modabwa ndi mothedwa nzeru anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Zimenezi zikutanthauzanji?”
І всі не вихо́дили з дива, і безрадні були, і говорили один до одно́го: „Що ж то статися має?“
13 Koma ena anawaseka nati, “Aledzera vinyo watsopano.”
А інші казали глузу́ючи: „Вони повпива́лись вином молодим!“
14 Koma Petro anayimirira pamodzi ndi atumwi khumi ndi mmodziwo ndipo anakweza mawu ake nayankhula kwa gulu la anthu nati: “Ayuda anzanga, ndi nonse amene muli mu Yerusalemu, mvetsetsani izi ndipo tcherani khutu ku zimene ndikunena.
Ставши ж Петро із Одинадцятьма́, свій голос підніс та й промовив до них: „Мужі юдейські та ме́шканці Єрусалиму! Нехай вам оце стане відо́ме, і послухайте слів моїх!
15 Kunena zoona, anthu awa sanaledzere ayi, monga momwe mukuganizira, pakuti ino ndi 9 koloko mmawa!
Бо не п'я́ні вони, як ви ду́маєте, — бо третя година дня,
16 Koma izi ndi zimene ananena Mneneri Yoweli kuti:
а це те, що пророк Йоі́л передрік:
17 “‘Mulungu akuti, mʼmasiku otsiriza ndidzakhuthulira Mzimu wanga pa anthu onse. Ana anu aamuna ndi aakazi adzanenera, anyamata anu adzaona masomphenya, nkhalamba zanu zidzalota maloto.
„І буде останніми днями, говорить Госпо́дь: Я виллю від Духа Свого на всяке тіло, — і будуть пророкува́ти сини ваші та ваші до́ньки, юнаки́ ж ваші бачити будуть виді́ння, а старим вашим сни будуть сни́тися.
18 Ngakhalenso pa antchito anga aamuna ndi aakazi, ndidzakhuthulira Mzimu wanga masiku amenewo, ndipo iwo adzanenera.
І на рабів Моїх і на рабинь Моїх за тих днів Я також виллю від Духа Свого, — і пророкувати вони бу́дуть!
19 Ndipo ndidzaonetsa zodabwitsa mlengalenga ndi zizindikiro pa dziko lapansi pano, ndizo magazi, moto ndi utsi watolotolo.
І дам чуда на небі вгорі, а внизу на землі ці знаме́на: кров, і огонь, і ку́ряву диму.
20 Dzuwa lidzadetsedwa ndipo mwezi udzaoneka ngati magazi lisanafike tsiku lalikulu ndi laulemerero la Ambuye.
Переміниться сонце на те́мряву, а місяць на кров, перше ніж день Господній настане, великий та славний!
21 Ndipo aliyense amene adzayitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka.’
І станеться, що кожен, хто покличе Господнє Ім'я́, той спасеться“.
22 “Inu Aisraeli mverani mawu awa; Yesu wa ku Nazareti anali munthu amene anaperekedwa kwa inu ndi Mulungu. Ndipo Mulungu anakutsimikizirani zimenezi ndi zamphamvu, zodabwitsa ndi zizindikiro zimene anachita mwa Iye pakati panu, monga inu mukudziwa.
Мужі ізраїльські, послухайте ви оцих слів: Ісуса Назаряни́на, Мужа, що Його Бог прославив вам силою, і чудами, і тими знаме́нами, що Бог через Нього вчинив серед вас, як самі ви те знаєте,
23 Yesu ameneyu anaperekedwa kwa inu mwa kufuna ndi kudziwiratu kwa Mulungu; ndipo inu mothandizidwa ndi anthu oyipa, munamupha Iye pomupachika pa mtanda.
Того, що був ви́даний певною волею та передба́ченням Божим, ви руками беззаконників розп'яли́ та забили.
24 Koma Mulungu anamuukitsa kwa akufa, kumumasula Iye ku zowawa za imfa, chifukwa kunali kosatheka kuti agwiridwe ndi imfa.
Та Бог воскресив Його, пута смерти усунувши, — вона бо тримати Його не могла.
25 Pakuti Davide ananena za Iye kuti, “‘Ndinaona Ambuye pamaso panga nthawi zonse. Chifukwa Iye ali kudzanja langa lamanja, Ine sindidzagwedezeka.
Бо каже про Нього Давид: „Мав я Господа за́всіди перед очима своїми, бо Він по правиці моїй, щоб я не захитався.
26 Chifukwa chake mtima wanga ndi wokondwa ndipo lilime langa likukondwera; thupi langanso lidzakhala ndi chiyembekezo.
Тому серце моє звеселилось, і зрадів мій язик, і тіло моє відпочи́не в надії.
27 Chifukwa simudzasiya moyo wanga kumalo a anthu akufa, ku manda, kapena kulekerera Woyerayo kuti awole. (Hadēs )
Бо не позоставши Ти в аду́ моєї душі, і не даси Ти Своєму Святому побачити тління! (Hadēs )
28 Inu munandidziwitsa ine njira zamoyo; Inu mudzandidzaza ndi chimwemwe pamaso panu.’
Ти дороги життя об'явив мені, Ти мене перепо́вниш утіхою перед обличчям Своїм“!
29 “Abale, ine ndikuwuzani motsimikiza kuti kholo lathu Davide anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda, ndipo manda ake alipo lero lino.
Мужі-браття! Нехай буде вільно мені сміло сказати вам про патріярха Давида, що помер і похований, і знахо́диться гріб його в нас аж до цього дня.
30 Koma iye anali mneneri ndipo anadziwa kuti Mulungu analonjeza ndi lumbiro kuti adzayika mmodzi wa zidzukulu zake pa mpando waufumu.
А бувши ж пророком, та відаючи, що „Бог клятвою клявся йому посади́ти на престолі його від плоду його сте́гон“,
31 Davide ataoneratu zimene zinali mʼtsogolo anayankhula za kuuka kwa Khristu, kuti Iye sanasiyidwe mʼmanda, ndipo thupi lake silinawole. (Hadēs )
у передба́ченні він говорив про Христове воскре́сення, що „не буде зоставлений в аду́“, ані тіло Його „не зазнає зотління“. (Hadēs )
32 Mulungu wamuukitsa Yesu ameneyu, ndipo ife ndife mboni za zimenezi.
Бог Ісуса Цього воскресив, чого свідки всі ми!
33 Khristu anakwezedwa kukhala kudzanja lamanja la Mulungu, nalandira Mzimu Woyera amene Atate anamulonjeza, ndipo watipatsa ife zimene mukuona ndi kumvazi.
А отож, як правицею Божою був Він возне́сений, і обі́тницю Духа Святого прийняв від Отця, то й злив Він оте, що ви бачите й чуєте.
34 Pakuti si Davide anakwera kumwamba koma iye akuti, “‘Ambuye anawuza Ambuye anga kuti: Khala kudzanja langa lamanja
Не зійшов бо на небо Давид, але сам він говорить: „Промовив Госпо́дь Господе́ві моєму: Сядь право́руч Мене,
35 mpaka nditasandutsa adani ako kukhala chopondapo mapazi ako.’
доки не покладу́ Я Твоїх ворогів підніжком ногам Твоїм!“
36 “Nʼchifukwa chake, Aisraeli onse adziwe ndithu kuti, Yesu amene inu munamupachika, Mulungu wamuyika kukhala Ambuye ndiponso Mpulumutsi.”
Ото ж, нехай ввесь Ізраїлів дім твердо знає, що і Господом, і Христом учинив Бог Його, Того Ісуса, що Його розп'яли́ ви!“
37 Anthu atamva zimenezi, anatsutsika kwambiri mu mtima ndipo anati kwa Petro ndi atumwi enawo, “Abale, kodi ife tichite chiyani?”
Як почули ж оце, вони серцем розжа́лобились, та й сказали Петрові та іншим апо́столам: „Що ж ми маємо робити, мужі-браття?“
38 Petro anawayankha kuti, “Lapani ndipo mubatizidwe aliyense wa inu, mʼdzina la Yesu Khristu kuti machimo anu akhululukidwe. Ndipo mudzalandira mphatso ya Mzimu Woyera.
А Петро до них каже: „Покайтеся, і нехай же охриститься кожен із вас у Ім'я́ Ісуса Христа на відпу́щення ваших гріхів, — і да́ра Духа Святого ви при́ймете!
39 Pakuti lonjezoli ndi lanu ndi ana anu ndiponso la onse amene ali kutali, ndi iwo onse amene Ambuye Mulungu wathu adzawayitane.”
Бо для вас ця обі́тниця, і для ваших дітей, і для всіх, що „дале́ко знаходяться, кого б тільки покликав Госпо́дь, Бог наш“.
40 Petro anawachenjeza ndi mawu ena ambiri, ndipo anawadandaulira iwo kuti, “Mudzipulumutse ku mʼbado owonongeka uno.”
І іншими багатьома́ словами він засвідчував та вмовляв їх, говорячи: „Рятуйтесь від цього лукавого роду!“
41 Iwo amene anawulandira uthenga wake anabatizidwa ndipo tsiku lomwelo miyoyo pafupifupi 3,000 inawonjezedwa ku gulu lawo.
Отож ті, хто прийняв його слово, охристилися. І пристало до них того дня душ тисяч зо три!
42 Iwo ankasonkhana pamodzi kuphunzitsidwa ndi atumwi, pachiyanjano, pachakudya ndi popemphera.
І вони перебува́ли в науці апо́стольській, та в спільно́ті брате́рській, і в лама́нні хліба, та в моли́твах.
43 Aliyense ankachita mantha chifukwa cha zodabwitsa ndi zizindikiro zambiri zimene atumwi ankachita.
І був о́страх у кожній душі, бо багато чинили апо́столи чуд та знаме́н.
44 Okhulupirira onse anali pamodzi ndipo aliyense ankapereka zinthu zake kuti zikhale za onse.
А всі віруючі були вкупі, і мали все спі́льним.
45 Ankagulitsa minda yawo ndi katundu wawo, ndi kugawira kwa aliyense molingana ndi zosowa zake.
І вони продавали маєтки та до́бра, і всім їх ділили, як кому чого треба було́.
46 Tsiku ndi tsiku ankasonkhana pamodzi pa bwalo la pa Nyumba ya Mulungu. Ankadya pamodzi mʼnyumba zawo mwasangala ndi mtima woona.
І кожного дня перебува́ли вони однодушно у храмі, і, ломлячи хліб по домах, поживу приймали із радістю та в сердечній просто́ті,
47 Ankayamika Mulungu ndipo anthu onse ankawakomera mtima. Ndipo tsiku ndi tsiku Ambuye ankawonjezera ena pa chiwerengero cha olandira chipulumutso.
вихваляючи Бога та маючи ласку в усього народу. І щоденно до Церкви Госпо́дь додава́в тих, що спасалися.