< Machitidwe a Atumwi 17 >

1 Atadutsa ku Amfipoli ndi Apoloniya, anafika ku Tesalonika, kumene kunali sunagoge ya Ayuda.
Kwathi sebedabule iAmfipholi leApoloniya, bafika eThesalonika, lapho okwakukhona isinagoge lamaJuda;
2 Paulo, monga mwachizolowezi chake, analowa mʼsunagoge, ndipo anakambirana nawo Mawu a Mulungu kwa masabata atatu,
njalo njengomkhuba kaPawuli wangena kuwo, wakhulumisana lawo ngokuvela emibhalweni okwamasabatha amathathu,
3 kuwafotokozera ndi kuwatsimikizira kuti Khristu anayenera kufa ndi kuuka. Iye anati, “Yesu amene ndikukulalikirani ndiye Khristu.”
evula etshengisa ukuthi kwakufanele uKristu ahlupheke avuke kwabafileyo, lokuthi: UJesu lo, mina engimtshumayela kini, unguKristu.
4 Ena mwa Ayuda anakopeka mtima ndipo anatsatira Paulo ndi Sila, monganso linachitira gulu lalikulu la Agriki woopa Mulungu, pamodzi ndi amayi odziwika ambiri.
Labanye babo bakholwa, bazihlanganisa loPawuli loSilasi, njalo ixuku elikhulu lamaGriki akhonzayo, lakwabesifazana abadumileyo abangabalutshwana.
5 Koma Ayuda ena anachita nsanje; kotero anasonkhanitsa anthu akhalidwe loyipa ochokera pa msika ndipo napanga gulu nayambitsa chipolowe mu mzindawo. Anathamangira ku nyumba ya Yasoni kukafuna Paulo ndi Sila kuti awabweretse pa gulu la anthu.
Kodwa amaJuda angakholwayo aba lomona, athatha amanye amadoda amabi angamavila emdangeni, enza ixuku, adunga umuzi; ahlasela indlu kaJasoni, edinga ukubakhuphela ebantwini;
6 Koma atalephera kuwapeza, anakokera Yasoniyo ndi abale ena ku bwalo la akulu a mzindawo akufuwula kuti, “Anthu awa, Paulo ndi Sila, amene akhala akusokoneza dziko lonse lapansi, tsopano afikanso kuno.
kwathi engabatholi, adonsela uJasoni labazalwane abathile kubaphathi bomuzi, ememeza esithi: Laba abayaluzelisa umhlaba, bona sebefikile lalapha,
7 Yasoni ndiye anawalandira mʼnyumba mwake. Onsewa akuchita zotsutsana ndi malamulo a Kaisara pomanena kuti palinso mfumu ina, yotchedwa Yesu.”
uJasoni abemukeleyo; lalaba bonke benza okuphambene lemithetho kaKesari, besithi kukhona enye inkosi, enguJesu.
8 Atamva zimenezi, gulu la anthu ndi akulu a mzinda anavutika mu mtima.
Asedunga ixuku labaphathi bomuzi besizwa lezizinto.
9 Iwo analipiritsa Yasoni ndi anzakewo ndipo anawamasula.
Kwathi sebethethe isibambiso kuJasoni lakwabanye, abakhulula.
10 Mdima utagwa, abale anatumiza Paulo ndi Sila ku Bereya. Atafika kumeneko anapita ku sunagoge ya Ayuda.
Njalo abazalwane bahle basusa uPawuli loSilasi babathuma eBeriya ebusuku; okwathi sebefikile khona basuka baya esinagogeni lamaJuda.
11 Tsopano anthu a ku Bereya anali akhalidwe labwino kusiyana ndi Atesalonika, pakuti iwo analandira mawu ndi chidwi chachikulu ndipo ankasanthula Malemba tsiku ndi tsiku kuti aone ngati zimene ankanena Paulozo zinali zoona.
Lawo ayelungile kulalawo aweThesalonika, emukela ilizwi ngokuvuma konke, ehlolisisa imibhalo insuku ngensuku, ukuthi zinjalo yini lezizinto.
12 Ayuda ambiri anakhulupirira, monga anachitiranso amayi ndi amuna ambiri odziwika a Chigriki.
Ngakho amanengi kuwo akholwa, lakwabesifazana abahloniphekayo abangamaGriki lakwabesilisa abangabalutshwana.
13 Ayuda a ku Tesalonika atadziwa kuti Paulo akulalikira Mawu a Mulungu ku Bereya, anapitanso kumeneko, ndi kuwutsa mitima ya anthu nayambitsa chisokonezo.
Kodwa kwathi amaJuda eThesalonika esekwazi ukuthi ilizwi likaNkulunkulu liyatshunyayelwa nguPawuli leBeriya, eza lakhona enyakazelisa amaxuku.
14 Nthawi yomweyo abale anatumiza Paulo ku nyanja koma Sila ndi Timoteyo anatsalira ku Bereya.
Njalo ngalesosikhathi abazalwane bahle bamthuma uPawuli kungathi uya elwandle; kodwa uSilasi loTimothi basala khona.
15 Anthu amene anamuperekeza Paulo nafika naye ku Atene, ndipo anabwerera ku Bereya atawuzidwa kuti Sila ndi Timoteyo amutsatire msanga.
Lalabo ababephelekezela uPawuli, bamfikisa eAtene; sebemukele umlayezelo oya kuSilasi loTimothi, ukuthi beze kuye ngokuphangisa okukhulu, basuka bahamba.
16 Paulo akudikira Timoteyo ndi Sila ku Atene, anavutika mu mtima kwambiri poona kuti mzindawo unali odzaza ndi mafano.
Kwathi uPawuli esabalindele eAtene, umoya wakhe wakhathazeka phakathi kwakhe, ebona umuzi ugcwele izithombe.
17 Tsono anakambirana ndi Ayuda ndi Agriki amene amaopa Mulungu mʼsunagoge, komanso anthu amene amapezeka pa msika tsiku ndi tsiku ndi ena amene amakumana nawo.
Ngakho waphikisana lamaJuda esinagogeni labanye abakhonzayo, lasemdangeni insuku zonke lalabo ahlangana labo.
18 Gulu la Aepikureya ndi Astoiki, anthu anzeru, anayamba kutsutsana naye. Ena a iwo anafunsa kuti, “Kodi wolongololayu akufuna kunena chiyani?” Enanso anati, “Akuoneka ngati akulalikira milungu yachilendo.” Iwo ananena zimenezi chifukwa Paulo amalalikira Uthenga Wabwino wa Yesu ndi kuuka kwa akufa.
Labathile kuzo izazi zamaEpikuri lamaStoyiki baphikisana laye. Labanye bathi: Uwumane lolu lufuna ukuthini? Kodwa abanye bathi: Kungathi ungotshumayela onkulunkulu bezizweni; ngoba ngevangeli watshumayela kubo uJesu lokuvuka kwabafileyo.
19 Kenaka iwo anamutenga nafika naye ku bwalo la Areopagi kumene anamufunsa kuti, “Kodi tingadziweko chiphunzitso chatsopano chimene ukuchifotokozachi?
Basebemthatha, bamusa eAreyopagu besithi: Singazi yini ukuthi iyini limfundiso entsha oyifundisayo?
20 Iwe ukubweretsa zinthu zina zachilendo mʼmakutu mwathu, ndipo ife tikufuna tidziwe tanthauzo lake.”
Ngoba uletha indaba ezimangalisayo ezithile endlebeni zethu; ngakho sifisa ukwazi ukuthi lezizinto ziyini.
21 Atene onse ndi alendo amene amakhala kumeneko samachita kanthu kena koma kufotokoza ndi kumvera fundo zatsopano.
Ngoba bonke abeAtene lezethekeli ezihlala khona babechitha isikhathi kungeyisikho ngolutho olunye, ngaphandle kokutshela lokuzwa into entsha.
22 Paulo anayimirira mʼbwalo la Areopagi nati: “Inu anthu a ku Atene! Ine ndikuona kuti mʼnjira zonse ndinu opembedza kwambiri.
Kwathi uPawuli esima phakathi kweAreyopagu, wathi: Madoda maAtene, ngiyabona ukuthi ezintweni zonke kungathi lilenkolelo enkulu.
23 Pakuti pamene ndimayenda ndi kuona zinthu zimene mumazipembedza, ndapezanso guwa lansembe lolembedwapo kuti, kwa mulungu wosadziwika. Tsopano chimene mumachipembedza osachidziwa ndi chimene ndikuchilalikira.
Ngoba ngithe ngidabula ngikhangela izinto zenu elizikhonzayo, ngasengifica ilathi elilotshwe ukuthi: KUNKULUNKULU ONGAZIWAYO. Lowo-ke elimkhonza lingamazi, nguye mina engimtshumayela kini.
24 “Mulungu amene analenga dziko lapansi ndiponso zonse zili mʼmenemo ndiye Ambuye wakumwamba ndi dziko lapansi ndipo sakhala mʼnyumba zachipembedzo zomangidwa ndi manja.
UNkulunkulu owenza umhlaba lakho konke okukuwo, yena, oyiNkosi yezulu lomhlaba, kahlali emathempelini enziwe ngezandla,
25 Ndipo satumikiridwa ndi manja a anthu ngati kuti Iye amasowa kanthu, chifukwa Iye ndiye amapereka moyo ndi mpweya kwa anthu onse ndi zina zonse.
futhi kakhonzwa ngezandla zabantu, njengoswela ulutho, ngoba yena uqobo lwakhe uyabapha bonke impilo lokuphefumula lazo zonke izinto;
26 Kuchoka kwa munthu mmodzi Iye analenga mtundu uliwonse wa anthu, kuti akakhale pa dziko lonse lapansi; ndipo Iye anakonzeratu nthawi yawo ndiponso malo enieni kumene adzakhale.
njalo wazenza zonke izizwe zabantu zivela egazini linye, ukuthi zihlale ebusweni bonke bomhlaba, wazimisela izikhathi eziqunyiweyo ngaphambili lemingcele yokuhlala kwazo;
27 Mulungu anachita izi kuti anthu amufunefune, ndikuti pomufunafunapo amupeze ngakhale kuti Iye sali kutali ndi aliyense wa ife.
ukuze zidinge iNkosi, ukuthi mhlawumbe sibili zimuzwe zimthole, njalo kanti kakhatshana kulowo lalowo wethu.
28 ‘Pakuti timakhala mwa Iye, kuyenda mwa Iye ndi kukhala moyo mwa Iye.’ Monga olemba ndakatulo anu ena akuti, ‘Ife ndi zidzukulu zake.’
Ngoba kuye siphila njalo sihamba futhi sikhona; njengoba lembongi ezithile zakini zithe: Ngoba futhi siyinzalo yakhe.
29 “Tsono popeza ndife ana a Mulungu, tisaganize kuti umulungu wake ndi wofanana ndi ndalama zagolide, zasiliva, mwala, kapenanso fanizo lopangidwa mwaluso la nzeru za anthu.
Ngakho lokhu siyinzalo kaNkulunkulu, kakufanele ukuthi sinakane ukuthi ubuNkulunkulu bunjengegolide kumbe isiliva loba ilitshe, okubazwe ngeminwe langokunakana kwabantu.
30 Nthawi imene anthu sankadziwa, Mulungu anawalekerera koma tsopano akulamulira kuti anthu onse, kulikonse atembenuke mtima.
Ngakho izikhathi zokungazi uNkulunkulu kazinanzanga, kodwa khathesi uyalaya bonke abantu endaweni zonke ukuthi baphenduke;
31 Pakuti Iye wayika tsiku limene adzaweruze dziko lapansi mwa chilungamo kudzera mwa Munthu amene anamusankha. Iye watsimikizira anthu onse zimenezi pomuukitsa.”
ngoba umisile usuku, azakwahlulela ngalo umhlaba ngokulunga, ngendoda ayimisileyo, waqinisa kubo bonke, ngokuyivusa kwabafileyo.
32 Atamva za kuuka kwa akufa, ena a iwo anaseka, koma enanso anati, “Ife tikufuna tidzamvenso zimenezi tsiku lina.”
Kwathi besizwa ngokuvuka kwabafileyo, abanye bahleka usulu; kodwa abanye bathi: Sizaphinda sikuzwe ngalokhu.
33 Ndipo Paulo anatuluka mʼBwalolo.
Langokunjalo uPawuli waphuma phakathi kwabo.
34 Anthu ena ochepa anamutsatira Paulo ndipo anakhulupirira. Pakati pawo panali Dionisiyo mmodzi wa bwalo la Areopagi ndi mayi wina wotchedwa Damalisi ndi enanso.
Kodwa amadoda athile anamathela kuye, akholwa; phakathi kwawo kwakukhona loDiyonisiyu umAreyopagu, lowesifazana obizo lakhe nguDamari, labanye kanye labo.

< Machitidwe a Atumwi 17 >