< Machitidwe a Atumwi 16 >

1 Paulo anafika ku Derbe ndi Lusitra, kumene kumakhala ophunzira wina dzina lake Timoteyo. Amayi ake anali Myuda wokhulupirira, koma abambo ake anali Mgriki.
ပေါ်လော ဒရ္ဗ္ဗီလုသ္တြာနဂရယောရုပသ္ထိတောဘဝတ် တတြ တီမထိယနာမာ ၑိၐျ ဧက အာသီတ်; သ ဝိၑွာသိနျာ ယိဟူဒီယာယာ ယောၐိတော ဂရ္ဗ္ဘဇာတး ကိန္တု တသျ ပိတာနျဒေၑီယလောကး၊
2 Abale a ku Lusitra ndi Ikoniya anamuchitira iye umboni wabwino.
သ ဇနော လုသ္တြာ-ဣကနိယနဂရသ္ထာနာံ ဘြာတၖဏာံ သမီပေပိ သုချာတိမာန် အာသီတ်၊
3 Paulo anafuna kumutenga pa ulendo, kotero anachita mdulidwe chifukwa cha Ayuda amene amakhala mʼderalo pakuti onse amadziwa kuti abambo ake anali Mgriki.
ပေါ်လသ္တံ သွသင်္ဂိနံ ကရ္တ္တုံ မတိံ ကၖတွာ တံ ဂၖဟီတွာ တဒ္ဒေၑနိဝါသိနာံ ယိဟူဒီယာနာမ် အနုရောဓာတ် တသျ တွက္ဆေဒံ ကၖတဝါန် ယတသ္တသျ ပိတာ ဘိန္နဒေၑီယလောက ဣတိ သရွွဲရဇ္ဉာယတ၊
4 Pamene amayenda mzinda ndi mzinda, amafotokoza zimene atumwi ndi akulu ampingo ku Yerusalemu anagwirizana kuti anthu azitsatire.
တတး ပရံ တေ နဂရေ နဂရေ ဘြမိတွာ ယိရူၑာလမသ္ထဲး ပြေရိတဲ ရ္လောကပြာစီနဲၑ္စ နိရူပိတံ ယဒ် ဝျဝသ္ထာပတြံ တဒနုသာရေဏာစရိတုံ လောကေဘျသ္တဒ် ဒတ္တဝန္တး၊
5 Kotero mipingo inalimbikitsidwa mʼchikhulupiriro ndipo anthu amachulukirachulukirabe tsiku ndi tsiku.
တေနဲဝ သရွွေ ဓရ္မ္မသမာဇား ခြီၐ္ဋဓရ္မ္မေ သုသ္ထိရား သန္တး ပြတိဒိနံ ဝရ္ဒ္ဓိတာ အဘဝန်၊
6 Paulo ndi anzake anadutsa mayiko a Frugiya ndi Galatiya, Mzimu Woyera atawaletsa kulalikira Mawu a Mulungu ku Asiya.
တေၐု ဖြုဂိယာဂါလာတိယာဒေၑမဓျေန ဂတေၐု သတ္သု ပဝိတြ အာတ္မာ တာန် အာၑိယာဒေၑေ ကထာံ ပြကာၑယိတုံ ပြတိၐိဒ္ဓဝါန်၊
7 Atafika ku malire a Musiya, anayesa kulowa ku Bituniya, koma Mzimu wa Yesu sunawalole kutero.
တထာ မုသိယာဒေၑ ဥပသ္ထာယ ဗိထုနိယာံ ဂန္တုံ တဲရုဒျောဂေ ကၖတေ အာတ္မာ တာန် နာနွမနျတ၊
8 Ndipo iwo anadutsa Musiya ndipo anapita ku Trowa.
တသ္မာတ် တေ မုသိယာဒေၑံ ပရိတျဇျ တြောယာနဂရံ ဂတွာ သမုပသ္ထိတား၊
9 Nthawi ya usiku Paulo anaona masomphenya, munthu wa ku Makedoniya atayimirira ndi kumupempha kuti, “Bwerani ku Makedoniya, mudzatithandize.”
ရာတြော် ပေါ်လး သွပ္နေ ဒၖၐ္ဋဝါန် ဧကော မာကိဒနိယလောကသ္တိၐ္ဌန် ဝိနယံ ကၖတွာ တသ္မဲ ကထယတိ, မာကိဒနိယာဒေၑမ် အာဂတျာသ္မာန် ဥပကုရွွိတိ၊
10 Paulo ataona masomphenyawa, tinakonzeka kupita ku Makedoniya, kutsimikiza kuti Mulungu anatiyitana kuti tikalalikire Uthenga Wabwino.
တသျေတ္ထံ သွပ္နဒရ္ၑနာတ် ပြဘုသ္တဒ္ဒေၑီယလောကာန် ပြတိ သုသံဝါဒံ ပြစာရယိတုမ် အသ္မာန် အာဟူယတီတိ နိၑ္စိတံ ဗုဒ္ဓွာ ဝယံ တူရ္ဏံ မာကိဒနိယာဒေၑံ ဂန္တုမ် ဥဒျောဂမ် အကုရ္မ္မ၊
11 Kuchokera ku Trowa tinakwera sitima ya pamadzi kupita ku Samotrake ndipo mmawa mwake tinapitirira mpaka ku Neapoli.
တတး ပရံ ဝယံ တြောယာနဂရာဒ် ပြသ္ထာယ ၒဇုမာရ္ဂေဏ သာမထြာကိယောပဒွီပေန ဂတွာ ပရေ'ဟနိ နိယာပလိနဂရ ဥပသ္ထိတား၊
12 Kuchokera kumeneko tinapita ku Filipi, boma la Aroma ndiponso mzinda waukulu wa dera la Makedoniya. Tinakhala kumeneko masiku owerengeka.
တသ္မာဒ် ဂတွာ မာကိဒနိယာန္တရွွရ္တ္တိ ရောမီယဝသတိသ္ထာနံ ယတ် ဖိလိပီနာမပြဓာနနဂရံ တတြောပသ္ထာယ ကတိပယဒိနာနိ တတြ သ္ထိတဝန္တး၊
13 Pa tsiku la Sabata tinatuluka mu mzindawo kupita ku mtsinje kumene timayembekezera kukapeza malo opempherera. Tinakhala pansi ndipo tinayamba kuyankhula ndi amayi amene anasonkhana pamenepo.
ဝိၑြာမဝါရေ နဂရာဒ် ဗဟိ ရ္ဂတွာ နဒီတဋေ ယတြ ပြာရ္ထနာစာရ အာသီတ် တတြောပဝိၑျ သမာဂတာ နာရီး ပြတိ ကထာံ ပြာစာရယာမ၊
14 Mmodzi wa amayi amene amamvetserawo ndi Lidiya amene amagulitsa nsalu zofiira, wochokera ku mzinda wa Tiyatira, ndipo amapembedza Mulungu. Ambuye anatsekula mtima wake kuti amve mawu a Paulo.
တတး ထုယာတီရာနဂရီယာ ဓူၐရာမ္ဗရဝိကြာယိဏီ လုဒိယာနာမိကာ ယာ ဤၑွရသေဝိကာ ယောၐိတ် ၑြောတြီဏာံ မဓျ အာသီတ် တယာ ပေါ်လောက္တဝါကျာနိ ယဒ် ဂၖဟျန္တေ တဒရ္ထံ ပြဘုသ္တသျာ မနောဒွါရံ မုက္တဝါန်၊
15 Iye ndi a mʼbanja lake atabatizidwa, anatiyitana kuti tipite ku nyumba yake. Iye anati, “Ngati mwanditenga ine kukhala wokhulupirira mwa Ambuye, bwerani mudzakhale mʼnyumba mwanga.” Ndipo anatiwumiriza ife kwambiri.
အတး သာ ယောၐိတ် သပရိဝါရာ မဇ္ဇိတာ သတီ ဝိနယံ ကၖတွာ ကထိတဝတီ, ယုၐ္မာကံ ဝိစာရာဒ် ယဒိ ပြဘော် ဝိၑွာသိနီ ဇာတာဟံ တရှိ မမ ဂၖဟမ် အာဂတျ တိၐ္ဌတ၊ ဣတ္ထံ သာ ယတ္နေနာသ္မာန် အသ္ထာပယတ်၊
16 Tsiku lina pamene timapita kumalo wopempherera, tinakumana ndi mtsikana wina amene anali ndi mzimu woyipa umene umanena zamʼtsogolo. Iye amapezera ndalama zambiri ambuye ake pa ulosi wake.
ယသျာ ဂဏနယာ တဒဓိပတီနာံ ဗဟုဓနောပါရ္ဇနံ ဇာတံ တာဒၖၑီ ဂဏကဘူတဂြသ္တာ ကာစန ဒါသီ ပြာရ္ထနာသ္ထာနဂမနကာလ အာဂတျာသ္မာန် သာက္ၐာတ် ကၖတဝတီ၊
17 Mtsikanayu anatsatira Paulo ndi ife, akufuwula kuti, “Anthu awa ndi atumiki a Mulungu Wammwambamwamba, amene akukuwuzani inu njira yachipulumutso.”
သာသ္မာကံ ပေါ်လသျ စ ပၑ္စာဒ် ဧတျ ပြောစ္စဲး ကထာမိမာံ ကထိတဝတီ, မနုၐျာ ဧတေ သရွွောပရိသ္ထသျေၑွရသျ သေဝကား သန္တော'သ္မာန် ပြတိ ပရိတြာဏသျ မာရ္ဂံ ပြကာၑယန္တိ၊
18 Iye anachita izi masiku ambiri. Kenaka Paulo anavutika mu mtima, natembenuka ndipo anati kwa mzimuwo, “Ndikukulamula iwe mʼdzina la Yesu Khristu kuti utuluke mwa iye!” Nthawi yomweyo mzimuwo unatuluka.
သာ ကနျာ ဗဟုဒိနာနိ တာဒၖၑမ် အကရောတ် တသ္မာတ် ပေါ်လော ဒုးခိတး သန် မုခံ ပရာဝရ္တျ တံ ဘူတမဝဒဒ်, အဟံ ယီၑုခြီၐ္ဋသျ နာမ္နာ တွာမာဇ္ဉာပယာမိ တွမသျာ ဗဟိရ္ဂစ္ဆ; တေနဲဝ တတ္က္ၐဏာတ် သ ဘူတသ္တသျာ ဗဟိရ္ဂတး၊
19 Pamene ambuye a mtsikana uja anazindikira kuti chiyembekezo chawo chopezera ndalama chatha, anagwira Paulo ndi Sila nawakokera ku bwalo la akulu.
တတး သွေၐာံ လာဘသျ ပြတျာၑာ ဝိဖလာ ဇာတေတိ ဝိလောကျ တသျား ပြဘဝး ပေါ်လံ သီလဉ္စ ဓၖတွာကၖၐျ ဝိစာရသ္ထာနေ'ဓိပတီနာံ သမီပမ် အာနယန်၊
20 Anawabweretsa iwo kwa oweruza milandu ndipo anati, “Anthu awa ndi Ayuda, iwo akuvutitsa mu mzinda wathu.
တတး ၑာသကာနာံ နိကဋံ နီတွာ ရောမိလောကာ ဝယမ် အသ္မာကံ ယဒ် ဝျဝဟရဏံ ဂြဟီတုမ် အာစရိတုဉ္စ နိၐိဒ္ဓံ,
21 Ndipo akuphunzitsa miyambo imene ife Aroma sitiloledwa kuyilandira kapena kuyichita.”
ဣမေ ယိဟူဒီယလောကား သန္တောပိ တဒေဝ ၑိက္ၐယိတွာ နဂရေ'သ္မာကမ် အတီဝ ကလဟံ ကုရွွန္တိ,
22 Gulu la anthu linatsutsana ndi Paulo ndi Sila, ndipo woweruza milandu analamula kuti avulidwe ndi kumenyedwa.
ဣတိ ကထိတေ သတိ လောကနိဝဟသ္တယေား ပြာတိကူလျေနောဒတိၐ္ဌတ် တထာ ၑာသကာသ္တယော ရွသ္တြာဏိ ဆိတွာ ဝေတြာဃာတံ ကရ္တ္တုမ် အာဇ္ဉာပယန်၊
23 Atawakwapula kwambiri anawaponya mʼndende, nalamula woyangʼanira kuti awasunge mosamalitsa.
အပရံ တေ တော် ဗဟု ပြဟာရျျ တွမေတော် ကာရာံ နီတွာ သာဝဓာနံ ရက္ၐယေတိ ကာရာရက္ၐကမ် အာဒိၑန်၊
24 Chifukwa cha mawu amenewa woyangʼanira ndende anakawayika mʼchipinda chamʼkati mwa ndende, nawamangirira miyendo yawo mʼzigologolo.
ဣတ္ထမ် အာဇ္ဉာံ ပြာပျ သ တာဝဘျန္တရသ္ထကာရာံ နီတွာ ပါဒေၐု ပါဒပါၑီဘိ ရ္ဗဒ္ဓွာ သ္ထာပိတာဝါန်၊
25 Koma pakati pa usiku Paulo ndi Sila ankapemphera ndi kuyimba nyimbo zolemekeza Mulungu, ndipo akayidi ena ankamvetsera.
အထ နိၑီထသမယေ ပေါ်လသီလာဝီၑွရမုဒ္ဒိၑျ ပြာထနာံ ဂါနဉ္စ ကၖတဝန္တော်, ကာရာသ္ထိတာ လောကာၑ္စ တဒၑၖဏွန္
26 Mwadzidzidzi kunachitika chivomerezi champhamvu kotero kuti maziko a ndende anagwedezeka. Nthawi yomweyo zitseko zonse za ndende zinatsekuka, ndipo maunyolo a aliyense anamasuka.
တဒါကသ္မာတ် မဟာန် ဘူမိကမ္ပော'ဘဝတ် တေန ဘိတ္တိမူလေန သဟ ကာရာ ကမ္ပိတာဘူတ် တတ္က္ၐဏာတ် သရွွာဏိ ဒွါရာဏိ မုက္တာနိ ဇာတာနိ သရွွေၐာံ ဗန္ဓနာနိ စ မုက္တာနိ၊
27 Woyangʼanira ndende uja atadzuka ku tulo, anaona kuti zitseko za ndende zinali zotsekula, ndipo anasolola lupanga lake nafuna kudzipha chifukwa ankaganiza kuti amʼndende athawa.
အတဧဝ ကာရာရက္ၐကော နိဒြာတော ဇာဂရိတွာ ကာရာယာ ဒွါရာဏိ မုက္တာနိ ဒၖၐ္ဋွာ ဗန္ဒိလောကား ပလာယိတာ ဣတျနုမာယ ကောၐာတ် ခင်္ဂံ ဗဟိး ကၖတွာတ္မဃာတံ ကရ္တ္တုမ် ဥဒျတး၊
28 Koma Paulo anafuwula kuti, “Usadzipweteke! Tonse tilipo!”
ကိန္တု ပေါ်လး ပြောစ္စဲသ္တမာဟူယ ကထိတဝါန် ပၑျ ဝယံ သရွွေ'တြာသ္မဟေ, တွံ နိဇပြာဏဟိံသာံ မာကာရ္ၐီး၊
29 Woyangʼanira ndendeyo anayitanitsa nyale, nathamangira mʼkati ndipo anadzigwetsa pa mapazi a Paulo ndi Sila akunjenjemera.
တဒါ ပြဒီပမ် အာနေတုမ် ဥက္တွာ သ ကမ္ပမာနး သန် ဥလ္လမ္ပျာဘျန္တရမ် အာဂတျ ပေါ်လသီလယေား ပါဒေၐု ပတိတဝါန်၊
30 Iye anawatulutsa kunja ndipo anawafunsa kuti, “Amuna inu, ndichite chiyani kuti ndipulumuke?”
ပၑ္စာတ် သ တော် ဗဟိရာနီယ ပၖၐ္ဋဝါန် ဟေ မဟေစ္ဆော် ပရိတြာဏံ ပြာပ္တုံ မယာ ကိံ ကရ္တ္တဝျံ?
31 Iwo anayankha kuti, “Khulupirira Ambuye Yesu ndipo udzapulumuka, iwe ndi a mʼbanja lako.”
ပၑ္စာတ် တော် သွဂၖဟမာနီယ တယေား သမ္မုခေ ခါဒျဒြဝျာဏိ သ္ထာပိတဝါန် တထာ သ သွယံ တဒီယား သရွွေ ပရိဝါရာၑ္စေၑွရေ ဝိၑွသန္တး သာနန္ဒိတာ အဘဝန်၊
32 Kenaka analalikira mawu a Ambuye kwa iyeyo ndi onse amene anali mʼnyumba mwake.
တသ္မဲ တသျ ဂၖဟသ္ထိတသရွွလောကေဘျၑ္စ ပြဘေား ကထာံ ကထိတဝန္တော်၊
33 Usiku womwewo woyangʼanira ndendeyo anawatenga nakawatsuka mabala awo; ndipo pomwepo iye ndi a mʼbanja lake anabatizidwa.
တထာ ရာတြေသ္တသ္မိန္နေဝ ဒဏ္ဍေ သ တော် ဂၖဟီတွာ တယေား ပြဟာရာဏာံ က္ၐတာနိ ပြက္ၐာလိတဝါန် တတး သ သွယံ တသျ သရွွေ ပရိဇနာၑ္စ မဇ္ဇိတာ အဘဝန်၊
34 Woyangʼanira ndendeyo anapita nawo ku nyumba yake, nakawapatsa chakudya, ndipo banja lonse linadzazidwa ndi chimwemwe chifukwa anakhulupirira Mulungu.
ပၑ္စာတ် တော် သွဂၖဟမာနီယ တယေား သမ္မုခေ ခါဒျဒြဝျာဏိ သ္ထာပိတဝါန် တထာ သ သွယံ တဒီယား သရွွေ ပရိဝါရာၑ္စေၑွရေ ဝိၑွသန္တး သာနန္ဒိတာ အဘဝန်၊
35 Kutacha, woweruza milandu uja anatuma asilikali kwa woyangʼanira ndendeyo kukanena kuti, “Amasuleni anthu aja.”
ဒိန ဥပသ္ထိတေ တော် လောကော် မောစယေတိ ကထာံ ကထယိတုံ ၑာသကား ပဒါတိဂဏံ ပြေၐိတဝန္တး၊
36 Woyangʼanira ndendeyo anawuza Paulo kuti, “Woweruza milandu walamula kuti iwe ndi Sila mumasulidwe. Tsopano muzipita. Pitani mumtendere.”
တတး ကာရာရက္ၐကး ပေါ်လာယ တာံ ဝါရ္တ္တာံ ကထိတဝါန် ယုဝါံ တျာဇယိတုံ ၑာသကာ လောကာန ပြေၐိတဝန္တ ဣဒါနီံ ယုဝါံ ဗဟိ ရ္ဘူတွာ ကုၑလေန ပြတိၐ္ဌေတာံ၊
37 Koma Paulo anati kwa asilikaliwo: “Iwo anatikwapula pa gulu la anthu asanatiweruze, ngakhale kuti ndife nzika za Chiroma natiponya mʼndende. Kodi tsopano akufuna kutitulutsa mwamseri? Ayi! Asiyeni abwere okha kuti adzatitulutse.”
ကိန္တု ပေါ်လသ္တာန် အဝဒတ် ရောမိလောကယောရာဝယေား ကမပိ ဒေါၐမ် န နိၑ္စိတျ သရွွေၐာံ သမက္ၐမ် အာဝါံ ကၑယာ တာဍယိတွာ ကာရာယာံ ဗဒ္ဓဝန္တ ဣဒါနီံ ကိမာဝါံ ဂုပ္တံ ဝိသ္တြက္ၐျန္တိ? တန္န ဘဝိၐျတိ, သွယမာဂတျာဝါံ ဗဟိး ကၖတွာ နယန္တု၊
38 Asilikali aja anakafotokozera woweruza milandu ndipo pamene anamva kuti Paulo ndi Sila anali nzika za Chiroma, anachita mantha.
တဒါ ပဒါတိဘိး ၑာသကေဘျ ဧတဒွါရ္တ္တာယာံ ကထိတာယာံ တော် ရောမိလောကာဝိတိ ကထာံ ၑြုတွာ တေ ဘီတား
39 Iye anabwera kudzawapepesa ndipo anawatulutsa mʼndende, nawapempha kuti achoke mu mzindawo.
သန္တသ္တယေား သန္နိဓိမာဂတျ ဝိနယမ် အကုရွွန် အပရံ ဗဟိး ကၖတွာ နဂရာတ် ပြသ္ထာတုံ ပြာရ္ထိတဝန္တး၊
40 Paulo ndi Sila atatuluka mʼndende, anapita ku nyumba ya Lidiya, kumene anakumana ndi abale nawalimbikitsa. Kenaka anachoka.
တတသ္တော် ကာရာယာ နိရ္ဂတျ လုဒိယာယာ ဂၖဟံ ဂတဝန္တော် တတြ ဘြာတၖဂဏံ သာက္ၐာတ္ကၖတျ တာန် သာန္တွယိတွာ တသ္မာတ် သ္ထာနာတ် ပြသ္ထိတော်၊

< Machitidwe a Atumwi 16 >