< Machitidwe a Atumwi 15 >

1 Anthu ena ochokera ku Yudeya anafika ku Antiokeya ndipo amaphunzitsa abale kuti, “Ngati simuchita mdulidwe potsata mwambo wa Mose, simungapulumuke.”
Abhantu bhamo hahishile afume hu Uyahudi bhabhamanyizyaga aje nkasiga mutahiriwa sigamubhajie ahwokoshe esheria ya Musa heyanjile.”
2 Zimenezi zinachititsa Paulo ndi Barnaba kuti atsutsane nawo kwambiri. Kotero Paulo ndi Barnaba anasankhidwa pamodzi ndi abale ena kuti apite ku Yerusalemu kukaonana ndi atumwi ndi akulu ampingo kukakambirana za nkhaniyi.
U Paulo nu Barnaba pabhali adalisanye na bhantu ebho bhalabhabhabhuulwaga ezyo bhabhatuma aPaulo, nu Barnaba, nabhanje bhamo aje bhabhale hu Yerusalemu bhabhuuzye hwa mitume nazee bheshibhanza.
3 Mpingo unawaperekeza, ndipo pamene amadutsa ku Foinike ndi Samariya, iwo anafotokoza momwe a mitundu ina anatembenukira mtima. Nkhani imeneyi inakondweretsa kwambiri abale onse.
Bhaala bhabhatumwilwe bhashiliye hu Foinike na Samaria alumbilile huje amataifa bhagalushiye Ungulubhi. Bhaletile uluseshelo lugosi hwa bhantu,
4 Atafika ku Yerusalemu, iwo analandiridwa ndi mpingo, pamodzi ndi atumwi ndiponso akulu ampingo. Paulo ndi Barnaba anawafotokozera zonse zimene Mulungu anachita kudzera mwa iwo.
Nabhafiha hu Yerusalemu atume nazee bhabhakalibizya bhope bhabhabuula zyontu zya bhombile Ungulubhi humakhono gabho.
5 Kenaka, okhulupirira ena amene kale anali a gulu la Afarisi anayimirira ndipo anati, “Anthu a mitundu ina ayenera kuchita mdulidwe ndi kusunga malamulo a Mose.”
Bhabhabhula na huje akristo bhabhafumile ohu bhabhamanyizya aKristo, abhamataifa huje nkasigamutahiriwa, nazikhate esheria zya Musa semubhajiye ahwokoshe.”
6 Atumwi ndi akulu ampingo anasonkhana kuti akambirane za nkhaniyi.
Atume wazee bhakhala nalise bhelele ijambo eli.
7 Atakambirana kwambiri Petro anayimirira, ndipo anawayankhula nati: “Abale, mukudziwa kuti masiku oyambirira Mulungu anandisankha ine pakati panu kuti anthu a mitundu ina amve kuchokera pakamwa panga mawu a Uthenga Wabwino ndi kukhulupirira.
Ijambo eli bhakhiiye tee walyo pamande uPetro wimilila wayanga, “Awe bhayaa muhwizuha huje utagalila sheshi Ungulubhi antumile aje hilomu lyane Amataifa bhuumvwe izu lya Ngulubhi nalyeteshe.
8 Mulungu amene amadziwa mtima wa munthu, Iye anaonetsa kuti anawalandira powapatsa Mzimu Woyera, monga momwe anachita kwa ife.
Ungulubhi, yahwenya amoyo ayanga nabho nabhapele Umpepo Ufinjile, neshi atipiye ate;
9 Iye sanasiyanitse pakati pa ife ndi iwo, pakuti anayeretsa mitima yawo mwachikhulupiriro.
siga alelegenye ate na bheene abhalintinye amoyo aje gabe minza, nu lweteho.
10 Tsopano, chifukwa chiyani mukuyesa Mulungu poyika goli mʼkhosi la ophunzira, limene ngakhale ife kapena makolo athu sangathe kulisenza?
Yeenu tihulenga Ungulubhi nabhatwinshe ijoko lyabhapotilwe aise bhetu natibhayotipotilwe nayo?
11 Osatero! Ife tikukhulupirira kuti tinapulumutsidwa mwachisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu, monga iwonso anachitira.”
Lelo tihwitiha aje tihwokoha hu Neema ya Yesu neshi shashili.”
12 Gulu lonse linakhala chete pamene amamvetsera Barnaba ndi Paulo akuwawuza za zizindikiro zodabwitsa zimene Mulungu anazichita pakati pa anthu a mitundu ina kudzera mwa iwo.
Ubhungano gwonti gwapumile kati, aPaulo nu Barnaba pabhayangaga ezyabhombile Ungulubhi ingosi ne zyaswijezye hwa mataifa.
13 Iwo atatha kuyankhula, Yakobo anayankhula nati: “Abale, tandimverani.
Nabhaleha ayanje, uYakobo wope wimilila wayanga, “Wagabhamwitu ntejelezi.
14 Simoni watifotokozera mmene Mulungu poyamba paja anaonetsa kukhudzidwa kwake pomwe anatenga anthu a mitundu ina kukhala ake.
U Simoni ayanjile Ungulubhi shatumile nezyabhombile Ungulubhi hwa bhantu ebha hwitawa lya Yesu.
15 Mawu a aneneri akuvomereza zimenezi, monga kwalembedwa kuti,
Enongwa zya akue zihwitihana nezi shazisimbilwe.
16 “‘Zitatha izi Ine ndidzabwerera ndipo ndidzamanganso nyumba ya Davide imene inagwa. Ndidzakonzanso malo amene anagumuka, ndi kuyimanganso,
'Ihaiwela naizenje nantele enyumba ya Daudi, yehagwiye pansi ihaipalinganya papananjishe,
17 kuti anthu otsalawo afunefune Ambuye, ndi anthu onse a mitundu ina amene atchedwa ndi dzina langa, akutero Ambuye, amene amachita zinthu zimenezi
aje abhantu bhabhasagiye bhamwanze Ungulubhi na bhaMataifa bhabhasalulwe nu Ngulubhi.'
18 zinaululidwa kuyambira kalekale.’ (aiōn g165)
Eshi shayanga Ugosi yabhombize ezi zyazimanyishe ahwande hali (aiōn g165)
19 “Chifukwa chake, ine ndikuweruza kuti tisamavute anthu a mitundu ina amene atembenuka mtima kutsata Mulungu.
Ane enjiga tisabhatamansye abhantu bha Mataifa bhabhagalushile Ungulubhi;
20 Koma tiwalembere iwo, kuwawuza kuti asadye chakudya choperekedwa kwa mafano, apewenso dama, asadyenso nyama zochita kupotola kapena kudya magazi.
lelo tibhasimbile huje bhasegushe(bhapehane) nevifwani nenfwa nyewe, ni danda nu umalaya.
21 Pakuti malamulo a Mose akhala akulalikidwa mu mzinda uliwonse, kuyambira kalekale ndipo amawerengedwa mʼMasunagoge tsiku la Sabata.”
Afume empapo eya kuulu bhahweli abhantu shila muji bhabhalumbilila nahubhaazye uMusa mumasinagogi shila Lutuyo.”
22 Pamenepo atumwi ndi akulu ampingo, pamodzi ndi mpingo onse, anagwirizana zosankha anthu ena pakati pawo kuti awatume ku Antiokeya pamodzi ndi Paulo ndi Bamaba. Iwo anasankha Yudasi, wotchedwa Barsaba ndi Sila, anthu awiri amene anali atsogoleri pakati pa abale,
Eshi ezyo enongwa zyabhoneha nyinza hwa bhantu bhonti bhabhasalula, u Yuda yahetwaga Barsaba, nu Silas, bhabhabhalongozi bhi kanisa bhabhatuma hu Antiokia nu Paulo nu Barnaba.
23 kuti akapereke kalata yonena kuti, Kuchokera kwa atumwi ndi akulu ampingo, abale anu, Kwa anthu a mitundu ina okhulupirira a ku Antiokeya, Siriya ndi Kilikiya: Tikupereka moni.
Bhasimbile eshi, “Atume, nazee naholo, hwa holo betu akristo Amataifa bhabhali hu Antiokia, hu Shamu nahu Kilikia, tibhalamuha.
24 Ife tamva kuti anthu ena ochokera pakati pathu, amene sitinawatume anakusokonezani maganizo ndi kukuvutitsani ndi zimene amakuwuzani.
Tumvwizyu huje bhenzele abhantu bhafumile ohu bhasigatibhatumile ate bhabhaleteye emanyizyo, zyazibhayanzizye, mumoyo genyu.
25 Tsono ife tagwirizana kuti, tisankhe anthu ena ndi kuwatumiza kwa inu pamodzi ndi abale athu okondedwa Paulo ndi Barnaba,
Ate tilolile shinza aje tibhatume abhamwetu pandwemo na Paulo nu Barnaba,
26 anthu amene anapereka moyo wawo chifukwa cha dzina la Ambuye athu Yesu Khristu.
abhantu bhabhahwisuulile amoyo gabho hunongwa yitawa lya Yesu Kilisti.
27 Nʼchifukwa chake, tikutumiza Yudasi ndi Sila kuti adzachitire umboni ndi mawu a pakamwa pawo za zimene ife talemba.
Tabhatumile aYuda nu Sila, bhabhabhuule zyonti ezyo zyatisimbile.
28 Pakuti zinakomera Mzimu Woyera ndiponso ife kuti tisakusenzetseni katundu wina, kupatula zoyenera zokhazi:
Esho shizungwizye Umpepo Ufinjile, huje tisabhatwinshe izigo imwamu ashile gaalaga singwa Ungulubhi:
29 Mupewe kudya chakudya choperekedwa nsembe kwa mafano, musadye magazi, kapena nyama yopha mopotola ndiponso musachite dama. Mudzachita bwino mukapewa zimenezi. Tsalani bwino.
aje mugalushe afume huvifwani, ni danda, ne vyaviniongwile nu umalaya. Nkamubhasegushe nevii shabhabhe shinza hulimwe. Kwa helini.”
30 Anthu aja anatumidwa ndipo anafika ku Antiokeya, kumene anasonkhanitsa mpingo pamodzi napereka kalatayo.
Esho bhaabhalile hu Antiokia; bhatwala ekalata, bhabhabhuunganya bhonti.
31 Anthuwo anawerenga kalatayo ndipo abalewo anakondwa chifukwa cha mawu ake achirimbikitso.
Nabhabhaazizya ekalata ila bhasungwilwe tee, amoyo gabho gashiiye.
32 Yudasi ndi Sila amene analinso aneneri, ananena zambiri zowalimbikitsa ndi kuwapatsa mphamvu abalewo.
U Yuda nu Sila, na kuwe bhabhagwizizye umwoyo.
33 Atakhala kumeneko kwa kanthawi, abale aja anatsanzikana nawo mwamtendere kuti abwerere kwa amene anawatuma.
Nabhakhala uhwo pamante bhahasogola humwoyo ugwinza afume hwabhatumwilwe.
34 Koma Sila anasankha kuti akhale komweko.
[Lelo shabhoneha shinza uSila huje asagale uhwo]
35 Koma Paulo ndi Barnaba anatsalira ku Antiokeya kumene iwo pamodzi ndi ena ambiri anaphunzitsa ndi kulalikira Mawu a Ambuye.
U Paulo na bhanji bhakhiiye hu Antiokia bhalumbililaga na manyizye izu lya Ngulubhi.
36 Patapita masiku ena Paulo anati kwa Barnaba, “Tiyeni tibwerere kuti tikaone abale ku mizinda yonse imene tinalalika Mawu a Ambuye ndipo tikaone mmene akuchitira.”
Nabhakhala ensiku zyenyinji uPaulo wabhuula uBarnaba, “Huje salii tibhajendele mwonti mwatalumbililaga tibhenye shabhahwendelela.
37 Barnaba anafuna kutenga Yohane, wotchedwanso Marko, kuti apite nawo.
U Barnaba ahanza humweje u Yohana(Marko).
38 Koma Paulo anaganiza kuti sichinali cha nzeru kumutenga Yohane chifukwa iye anawathawa ku Pamfiliya ndipo sanapitirire nawo pa ntchito.
U Paulo siga asungwilwe humwe uMarko, yabhaleshile siga alongozenye nabho abhaleshile hu Pamfilia na hukuendelea nao katika kazi.
39 Iwo anatsutsana kwambiri kotero kuti anapatukana. Barnaba anatenga Marko ndipo anakwera sitima ya pamadzi kupita ku Kupro.
Bhahadalisanya tee pamande bhalehana, u Barnaba wamwega uMarko na shuule nawo, bhinjila mumeli bhabhala hu Kipro,
40 Paulo anasankha Sila. Abale atawapempherera kwa Ambuye kuti alandire chisomo, ananyamuka.
U Paulo wamwega, u Sila nasogole nawo.
41 Iye anadutsa ku Siriya ndi ku Kilikiya kupita akulimbikitsa mipingo.
Bhabhalile hu Shamu nahu Kilikia azeenje amoyo gabhaala bhabhalyeteshe izu lya Ngulubhi.

< Machitidwe a Atumwi 15 >