< Machitidwe a Atumwi 15 >

1 Anthu ena ochokera ku Yudeya anafika ku Antiokeya ndipo amaphunzitsa abale kuti, “Ngati simuchita mdulidwe potsata mwambo wa Mose, simungapulumuke.”
Kwasekusehla abathile bevela eJudiya, bafundisa abazalwane ukuthi: Nxa lingasokwanga ngokwesiko likaMozisi, lingesindiswe.
2 Zimenezi zinachititsa Paulo ndi Barnaba kuti atsutsane nawo kwambiri. Kotero Paulo ndi Barnaba anasankhidwa pamodzi ndi abale ena kuti apite ku Yerusalemu kukaonana ndi atumwi ndi akulu ampingo kukakambirana za nkhaniyi.
Ngakho kwathi sekulokuphambana lokuphikisana okungekuncinyane ngoPawuli loBarnabasi bemelane labo, bamisa ukuthi uPawuli loBarnabasi labanye abathile kubo benyukele kubaphostoli labadala eJerusalema, ngaloludaba.
3 Mpingo unawaperekeza, ndipo pamene amadutsa ku Foinike ndi Samariya, iwo anafotokoza momwe a mitundu ina anatembenukira mtima. Nkhani imeneyi inakondweretsa kwambiri abale onse.
Ngakho, kwathi sebephelekezelwe libandla, badabula iFenekiya leSamariya, balandisa ngokuphenduka kwabezizwe; benzela bonke abazalwane intokozo enkulu.
4 Atafika ku Yerusalemu, iwo analandiridwa ndi mpingo, pamodzi ndi atumwi ndiponso akulu ampingo. Paulo ndi Barnaba anawafotokozera zonse zimene Mulungu anachita kudzera mwa iwo.
Kwathi sebefikile eJerusalema, bemukelwa libandla labaphostoli labadala, njalo balandisa ukuthi zingakanani izinto uNkulunkulu ayezenze labo.
5 Kenaka, okhulupirira ena amene kale anali a gulu la Afarisi anayimirira ndipo anati, “Anthu a mitundu ina ayenera kuchita mdulidwe ndi kusunga malamulo a Mose.”
Kodwa kwasukuma abanye abakholwayo abangabehlelo labaFarisi, besithi: Kufanele ukubasoka, lokubalaya bagcine umlayo kaMozisi.
6 Atumwi ndi akulu ampingo anasonkhana kuti akambirane za nkhaniyi.
Kwasekubuthana abaphostoli labadala ndawonye ukuze baluhlole loludaba.
7 Atakambirana kwambiri Petro anayimirira, ndipo anawayankhula nati: “Abale, mukudziwa kuti masiku oyambirira Mulungu anandisankha ine pakati panu kuti anthu a mitundu ina amve kuchokera pakamwa panga mawu a Uthenga Wabwino ndi kukhulupirira.
Kwathi sebephikisene kakhulu, uPetro wasukuma wathi kubo: Madoda bazalwane, lina liyazi ukuthi ensukwini zakuqala uNkulunkulu wakhetha phakathi kwethu, ukuthi ngomlomo wami abezizwe balizwe ilizwi levangeli, bakholwe.
8 Mulungu amene amadziwa mtima wa munthu, Iye anaonetsa kuti anawalandira powapatsa Mzimu Woyera, monga momwe anachita kwa ife.
Njalo uNkulunkulu umazi wenhliziyo wabafakazela, ebanika uMoya oyiNgcwele, lanjengathi;
9 Iye sanasiyanitse pakati pa ife ndi iwo, pakuti anayeretsa mitima yawo mwachikhulupiriro.
futhi kehlukanisanga phakathi kwethu labo, ehlambulula inhliziyo zabo ngokholo.
10 Tsopano, chifukwa chiyani mukuyesa Mulungu poyika goli mʼkhosi la ophunzira, limene ngakhale ife kapena makolo athu sangathe kulisenza?
Pho-ke limlingelani uNkulunkulu, ngokubeka ijogwe entanyeni yabafundi, obaba bethu kanye lathi esingabanga lamandla okulithwala?
11 Osatero! Ife tikukhulupirira kuti tinapulumutsidwa mwachisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu, monga iwonso anachitira.”
Kodwa sikholwa ukuthi sisindiswa ngomusa weNkosi uJesu Kristu, ngandlelanye labo.
12 Gulu lonse linakhala chete pamene amamvetsera Barnaba ndi Paulo akuwawuza za zizindikiro zodabwitsa zimene Mulungu anazichita pakati pa anthu a mitundu ina kudzera mwa iwo.
Ixuku lonke laselithula; laselisizwa uBarnabasi loPawuli belandisa ukuthi zingakanani izibonakaliso lezimangaliso uNkulunkulu ayezenze ngabo phakathi kwabezizwe.
13 Iwo atatha kuyankhula, Yakobo anayankhula nati: “Abale, tandimverani.
Kwathi bona sebeqedile ukukhuluma, uJakobe waphendula wathi: Madoda bazalwane, ngilalelani:
14 Simoni watifotokozera mmene Mulungu poyamba paja anaonetsa kukhudzidwa kwake pomwe anatenga anthu a mitundu ina kukhala ake.
USimeyoni uselandisile ukuthi uNkulunkulu wahambela njani abezizwe ekuqaleni ukuze azuzele ibizo lakhe abantu kubo.
15 Mawu a aneneri akuvomereza zimenezi, monga kwalembedwa kuti,
Njalo amazwi abaprofethi ayavumelana lalokhu, njengoba kulotshiwe ukuthi:
16 “‘Zitatha izi Ine ndidzabwerera ndipo ndidzamanganso nyumba ya Davide imene inagwa. Ndidzakonzanso malo amene anagumuka, ndi kuyimanganso,
Emva kwalezizinto ngizabuya, ngilakhe futhi ithabhanekele likaDavida eliwileyo; njalo ngizakwakha okudilikileyo kwalo, njalo ngilimise;
17 kuti anthu otsalawo afunefune Ambuye, ndi anthu onse a mitundu ina amene atchedwa ndi dzina langa, akutero Ambuye, amene amachita zinthu zimenezi
ukuze abaseleyo babantu bayidinge iNkosi, labezizwe bonke ibizo lami elibizwa phezu kwabo, itsho iNkosi eyenza lezizinto zonke.
18 zinaululidwa kuyambira kalekale.’ (aiōn g165)
Kwaziwa kuNkulunkulu imisebenzi yonke yakhe kusukela ephakadeni. (aiōn g165)
19 “Chifukwa chake, ine ndikuweruza kuti tisamavute anthu a mitundu ina amene atembenuka mtima kutsata Mulungu.
Ngakho mina ngiquma ukuthi singabakhathazi labo kwabezizwe abaphendukela kuNkulunkulu;
20 Koma tiwalembere iwo, kuwawuza kuti asadye chakudya choperekedwa kwa mafano, apewenso dama, asadyenso nyama zochita kupotola kapena kudya magazi.
kodwa sibabhalele ukuthi bazile amanyala ezithombe, lokufeba, lokukhanyiweyo, legazi.
21 Pakuti malamulo a Mose akhala akulalikidwa mu mzinda uliwonse, kuyambira kalekale ndipo amawerengedwa mʼMasunagoge tsiku la Sabata.”
Ngoba uMozisi ulabo kusukela ezizukulwaneni zendulo abamtshumayelayo umuzi ngomuzi, efundwa emasinagogeni isabatha ngesabatha.
22 Pamenepo atumwi ndi akulu ampingo, pamodzi ndi mpingo onse, anagwirizana zosankha anthu ena pakati pawo kuti awatume ku Antiokeya pamodzi ndi Paulo ndi Bamaba. Iwo anasankha Yudasi, wotchedwa Barsaba ndi Sila, anthu awiri amene anali atsogoleri pakati pa abale,
Kwasekubonakala kukuhle kubaphostoli lakubadala kanye lebandla lonke, ukuthuma amadoda akhethiweyo phakathi kwabo eAntiyoki loPawuli loBarnabasi; babe ngoJudasi othiwa futhi nguBarsaba, loSilasi, amadoda angabakhokheli phakathi kwabazalwane,
23 kuti akapereke kalata yonena kuti, Kuchokera kwa atumwi ndi akulu ampingo, abale anu, Kwa anthu a mitundu ina okhulupirira a ku Antiokeya, Siriya ndi Kilikiya: Tikupereka moni.
basebebhala lokhu ngesandla sabo ukuthi: Abaphostoli labadala labazalwane kubazalwane abangabezizwe eAntiyoki leSiriya leKilikhiya, bayabingelela;
24 Ife tamva kuti anthu ena ochokera pakati pathu, amene sitinawatume anakusokonezani maganizo ndi kukuvutitsani ndi zimene amakuwuzani.
njengoba sizwile ukuthi abathile abaphume kithi balikhathazile ngamazwi, bedunga imiphefumulo yenu, besithi lisokwe lilonde umthetho, bona esingabalayanga;
25 Tsono ife tagwirizana kuti, tisankhe anthu ena ndi kuwatumiza kwa inu pamodzi ndi abale athu okondedwa Paulo ndi Barnaba,
kwabonakala kukuhle kithi singqondonye, ukuthi siwakhethe amadoda siwathume kini, kanye labathandekayo bethu uBarnabasi loPawuli,
26 anthu amene anapereka moyo wawo chifukwa cha dzina la Ambuye athu Yesu Khristu.
abantu abanikele impilo yabo ngenxa yebizo leNkosi yethu uJesu Kristu.
27 Nʼchifukwa chake, tikutumiza Yudasi ndi Sila kuti adzachitire umboni ndi mawu a pakamwa pawo za zimene ife talemba.
Ngakho sithumile uJudasi loSilasi, abazakuthi labo ngelizwi lomlomo balitshele izinto ezifananayo.
28 Pakuti zinakomera Mzimu Woyera ndiponso ife kuti tisakusenzetseni katundu wina, kupatula zoyenera zokhazi:
Ngoba kwabonakala kukuhle kuMoya oNgcwele, lakithi, ukuthi singalethesi umthwalo omkhulu, ngaphandle kwalezizinto ezifunekayo:
29 Mupewe kudya chakudya choperekedwa nsembe kwa mafano, musadye magazi, kapena nyama yopha mopotola ndiponso musachite dama. Mudzachita bwino mukapewa zimenezi. Tsalani bwino.
Ukuthi lizile okuhlatshelwe izithombe, legazi, lokukhanyiweyo, lokufeba; lezizinto nxa lizazizila, lizabe lenze kuhle. Salani kuhle.
30 Anthu aja anatumidwa ndipo anafika ku Antiokeya, kumene anasonkhanitsa mpingo pamodzi napereka kalatayo.
Ngakho sebebakhululile beza eAntiyoki; futhi sebelihlanganisile ixuku, balinika incwadi.
31 Anthuwo anawerenga kalatayo ndipo abalewo anakondwa chifukwa cha mawu ake achirimbikitso.
Kwathi sebefundile, bathokoza ngenduduzo.
32 Yudasi ndi Sila amene analinso aneneri, ananena zambiri zowalimbikitsa ndi kuwapatsa mphamvu abalewo.
UJudasi kanye loSilasi, njengoba labo babengabaprofethi, balaya abazalwane ngamazwi amanengi, babaqinisa.
33 Atakhala kumeneko kwa kanthawi, abale aja anatsanzikana nawo mwamtendere kuti abwerere kwa amene anawatuma.
Sebehlale isikhathi, bayekelwa basuka ngokuthula kubazalwane baya kubaphostoli,
34 Koma Sila anasankha kuti akhale komweko.
kodwa kwabonakala kukuhle kuSilasi ukuthi asale khona.
35 Koma Paulo ndi Barnaba anatsalira ku Antiokeya kumene iwo pamodzi ndi ena ambiri anaphunzitsa ndi kulalikira Mawu a Ambuye.
UPawuli loBarnabasi basebesala eAntiyoki, befundisa betshumayela indaba ezinhle zelizwi leNkosi, kanye labanye abanengi.
36 Patapita masiku ena Paulo anati kwa Barnaba, “Tiyeni tibwerere kuti tikaone abale ku mizinda yonse imene tinalalika Mawu a Ambuye ndipo tikaone mmene akuchitira.”
Emva kwensuku ezithile uPawuli wasesithi kuBarnabasi: Ake sibuye sihambele abazalwane bethu emizini yonke, lapho esatshumayela khona ilizwi leNkosi, sibone ukuthi bahlezi njani.
37 Barnaba anafuna kutenga Yohane, wotchedwanso Marko, kuti apite nawo.
UBarnabasi wasehlosa ukuthatha uJohane, othiwa nguMarko, ahambe labo.
38 Koma Paulo anaganiza kuti sichinali cha nzeru kumutenga Yohane chifukwa iye anawathawa ku Pamfiliya ndipo sanapitirire nawo pa ntchito.
Kodwa uPawuli wacabanga ukuthi kufanele ukuthi bangamthathi ahambe labo lowo owabatshiya ePamfiliya, kaze aya labo emsebenzini.
39 Iwo anatsutsana kwambiri kotero kuti anapatukana. Barnaba anatenga Marko ndipo anakwera sitima ya pamadzi kupita ku Kupro.
Kwasekuvela ukuphikisana okukhulu, baze behlukana phakathi; uBarnabasi wasethatha uMarko wahamba laye ngomkhumbi, baya eKuprosi.
40 Paulo anasankha Sila. Abale atawapempherera kwa Ambuye kuti alandire chisomo, ananyamuka.
Kodwa uPawuli wakhetha uSilasi wasuka wahamba, esenikelwe emuseni kaNkulunkulu ngabazalwane.
41 Iye anadutsa ku Siriya ndi ku Kilikiya kupita akulimbikitsa mipingo.
Wasedabula iSiriya leKilikhiya, eqinisa amabandla.

< Machitidwe a Atumwi 15 >