< Machitidwe a Atumwi 15 >

1 Anthu ena ochokera ku Yudeya anafika ku Antiokeya ndipo amaphunzitsa abale kuti, “Ngati simuchita mdulidwe potsata mwambo wa Mose, simungapulumuke.”
Then some men came down from Judea and were teaching the brothers: “If you are not circumcised according to the custom of Moses, you cannot be saved.”
2 Zimenezi zinachititsa Paulo ndi Barnaba kuti atsutsane nawo kwambiri. Kotero Paulo ndi Barnaba anasankhidwa pamodzi ndi abale ena kuti apite ku Yerusalemu kukaonana ndi atumwi ndi akulu ampingo kukakambirana za nkhaniyi.
Therefore, when Paul and Barnabas had a great dissension and debate with them, the brothers appointed Paul and Barnabas and some others from among the believers to go up to the apostles and elders in Jerusalem to discuss this issue.
3 Mpingo unawaperekeza, ndipo pamene amadutsa ku Foinike ndi Samariya, iwo anafotokoza momwe a mitundu ina anatembenukira mtima. Nkhani imeneyi inakondweretsa kwambiri abale onse.
After being sent on their way by the church, they passed through Phoenicia and Samaria and brought great joy to all the brothers when they described in detail the conversion of the Gentiles.
4 Atafika ku Yerusalemu, iwo analandiridwa ndi mpingo, pamodzi ndi atumwi ndiponso akulu ampingo. Paulo ndi Barnaba anawafotokozera zonse zimene Mulungu anachita kudzera mwa iwo.
When they arrived in Jerusalem, they were welcomed by the church, the apostles, and the elders, and they reported all that God had done through them.
5 Kenaka, okhulupirira ena amene kale anali a gulu la Afarisi anayimirira ndipo anati, “Anthu a mitundu ina ayenera kuchita mdulidwe ndi kusunga malamulo a Mose.”
But some of the believers who belonged to the sect of the Pharisees stood up, saying, “It is necessary to circumcise the Gentiles and command them to keep the law of Moses.”
6 Atumwi ndi akulu ampingo anasonkhana kuti akambirane za nkhaniyi.
So the apostles and the elders gathered together to consider this matter.
7 Atakambirana kwambiri Petro anayimirira, ndipo anawayankhula nati: “Abale, mukudziwa kuti masiku oyambirira Mulungu anandisankha ine pakati panu kuti anthu a mitundu ina amve kuchokera pakamwa panga mawu a Uthenga Wabwino ndi kukhulupirira.
After there had been much debate, Peter stood up and said to them, “Brothers, you know that in the early days God made a choice among us, that by the words of my mouth the Gentiles would hear the message of the gospel and believe.
8 Mulungu amene amadziwa mtima wa munthu, Iye anaonetsa kuti anawalandira powapatsa Mzimu Woyera, monga momwe anachita kwa ife.
And God, who knows the heart, testified to them by giving them the Holy Spirit, just as he did to us.
9 Iye sanasiyanitse pakati pa ife ndi iwo, pakuti anayeretsa mitima yawo mwachikhulupiriro.
He made no distinction between us and them, purifying their hearts by faith.
10 Tsopano, chifukwa chiyani mukuyesa Mulungu poyika goli mʼkhosi la ophunzira, limene ngakhale ife kapena makolo athu sangathe kulisenza?
Now then, why are you putting God to the test by placing a yoke on the neck of the disciples that neither our fathers nor we have been able to bear?
11 Osatero! Ife tikukhulupirira kuti tinapulumutsidwa mwachisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu, monga iwonso anachitira.”
On the contrary, we believe that we are saved by the grace of the Lord Jesus in the same way they are.”
12 Gulu lonse linakhala chete pamene amamvetsera Barnaba ndi Paulo akuwawuza za zizindikiro zodabwitsa zimene Mulungu anazichita pakati pa anthu a mitundu ina kudzera mwa iwo.
Then the entire assembly fell silent as they listened to Barnabas and Paul tell of all the signs and wonders God had performed through them among the Gentiles.
13 Iwo atatha kuyankhula, Yakobo anayankhula nati: “Abale, tandimverani.
When they had finished speaking, James replied, “Brothers, listen to me.
14 Simoni watifotokozera mmene Mulungu poyamba paja anaonetsa kukhudzidwa kwake pomwe anatenga anthu a mitundu ina kukhala ake.
Simeon has related how God first visited the Gentiles, to take from among them a people for his name.
15 Mawu a aneneri akuvomereza zimenezi, monga kwalembedwa kuti,
The words of the prophets are in agreement with this, just as it is written:
16 “‘Zitatha izi Ine ndidzabwerera ndipo ndidzamanganso nyumba ya Davide imene inagwa. Ndidzakonzanso malo amene anagumuka, ndi kuyimanganso,
‘After this I will return and rebuild the tabernacle of David that has fallen; I will rebuild its ruins and erect it again,
17 kuti anthu otsalawo afunefune Ambuye, ndi anthu onse a mitundu ina amene atchedwa ndi dzina langa, akutero Ambuye, amene amachita zinthu zimenezi
so that the rest of mankind may seek the Lord, even all the Gentiles who are called by my name, says the Lord, who does all these things.’
18 zinaululidwa kuyambira kalekale.’ (aiōn g165)
All God's works are known to him from long ago. (aiōn g165)
19 “Chifukwa chake, ine ndikuweruza kuti tisamavute anthu a mitundu ina amene atembenuka mtima kutsata Mulungu.
Therefore my judgment is that we not create difficulties for those among the Gentiles who turn to God,
20 Koma tiwalembere iwo, kuwawuza kuti asadye chakudya choperekedwa kwa mafano, apewenso dama, asadyenso nyama zochita kupotola kapena kudya magazi.
but that we write to them, telling them to abstain from things defiled by idols, from fornication, from what has been strangled, and from blood.
21 Pakuti malamulo a Mose akhala akulalikidwa mu mzinda uliwonse, kuyambira kalekale ndipo amawerengedwa mʼMasunagoge tsiku la Sabata.”
For from generations of old, Moses has had those who preach him in every city, because he is read in the synagogues every Sabbath.”
22 Pamenepo atumwi ndi akulu ampingo, pamodzi ndi mpingo onse, anagwirizana zosankha anthu ena pakati pawo kuti awatume ku Antiokeya pamodzi ndi Paulo ndi Bamaba. Iwo anasankha Yudasi, wotchedwa Barsaba ndi Sila, anthu awiri amene anali atsogoleri pakati pa abale,
Then it seemed good to the apostles and to the elders, together with the whole church, to send men chosen from among them to Antioch with Paul and Barnabas, namely, Judas (called Barsabbas) and Silas, leading men among the brothers,
23 kuti akapereke kalata yonena kuti, Kuchokera kwa atumwi ndi akulu ampingo, abale anu, Kwa anthu a mitundu ina okhulupirira a ku Antiokeya, Siriya ndi Kilikiya: Tikupereka moni.
and to send with them this letter they had written: “The apostles, elders, and brothers, to the Gentile brothers in Antioch, Syria, and Cilicia: Greetings.
24 Ife tamva kuti anthu ena ochokera pakati pathu, amene sitinawatume anakusokonezani maganizo ndi kukuvutitsani ndi zimene amakuwuzani.
Since we have heard that certain men, whom we did not authorize, have gone out from us and troubled you with their words, unsettling your minds by saying that you must be circumcised and keep the law,
25 Tsono ife tagwirizana kuti, tisankhe anthu ena ndi kuwatumiza kwa inu pamodzi ndi abale athu okondedwa Paulo ndi Barnaba,
it seemed good to us, having come to one accord, to send you men chosen from among us, along with our beloved Barnabas and Paul,
26 anthu amene anapereka moyo wawo chifukwa cha dzina la Ambuye athu Yesu Khristu.
who have risked their lives for the name of our Lord Jesus Christ.
27 Nʼchifukwa chake, tikutumiza Yudasi ndi Sila kuti adzachitire umboni ndi mawu a pakamwa pawo za zimene ife talemba.
Therefore we have sent Judas and Silas, who will tell you the same things in their own words.
28 Pakuti zinakomera Mzimu Woyera ndiponso ife kuti tisakusenzetseni katundu wina, kupatula zoyenera zokhazi:
For it seemed good to the Holy Spirit and to us to lay upon you no further burden than these essentials:
29 Mupewe kudya chakudya choperekedwa nsembe kwa mafano, musadye magazi, kapena nyama yopha mopotola ndiponso musachite dama. Mudzachita bwino mukapewa zimenezi. Tsalani bwino.
You must abstain from what has been sacrificed to idols, from blood, from what has been strangled, and from fornication. If you keep yourselves from these things, you will do well. Farewell.”
30 Anthu aja anatumidwa ndipo anafika ku Antiokeya, kumene anasonkhanitsa mpingo pamodzi napereka kalatayo.
So when these men had been sent off, they went to Antioch, and after gathering the congregation together, they delivered the letter.
31 Anthuwo anawerenga kalatayo ndipo abalewo anakondwa chifukwa cha mawu ake achirimbikitso.
When the people read it, they rejoiced over its encouragement.
32 Yudasi ndi Sila amene analinso aneneri, ananena zambiri zowalimbikitsa ndi kuwapatsa mphamvu abalewo.
Then Judas and Silas, who were themselves prophets, encouraged and strengthened the brothers with many words.
33 Atakhala kumeneko kwa kanthawi, abale aja anatsanzikana nawo mwamtendere kuti abwerere kwa amene anawatuma.
After spending some time there, they were sent off to the apostles in peace by the brothers.
34 Koma Sila anasankha kuti akhale komweko.
35 Koma Paulo ndi Barnaba anatsalira ku Antiokeya kumene iwo pamodzi ndi ena ambiri anaphunzitsa ndi kulalikira Mawu a Ambuye.
But Paul and Barnabas stayed in Antioch, teaching and preaching, along with many others, the good news of the word of the Lord.
36 Patapita masiku ena Paulo anati kwa Barnaba, “Tiyeni tibwerere kuti tikaone abale ku mizinda yonse imene tinalalika Mawu a Ambuye ndipo tikaone mmene akuchitira.”
After some days had gone by, Paul said to Barnabas, “Let us return and visit our brothers in every city where we proclaimed the word of the Lord, to see how they are doing.”
37 Barnaba anafuna kutenga Yohane, wotchedwanso Marko, kuti apite nawo.
Now Barnabas wanted to bring John, who was called Mark.
38 Koma Paulo anaganiza kuti sichinali cha nzeru kumutenga Yohane chifukwa iye anawathawa ku Pamfiliya ndipo sanapitirire nawo pa ntchito.
But Paul thought it best not to bring this man who had deserted them in Pamphylia and had not gone on with them in their work.
39 Iwo anatsutsana kwambiri kotero kuti anapatukana. Barnaba anatenga Marko ndipo anakwera sitima ya pamadzi kupita ku Kupro.
So there arose a sharp disagreement, with the result that they parted from one another. Barnabas took Mark and sailed off to Cyprus,
40 Paulo anasankha Sila. Abale atawapempherera kwa Ambuye kuti alandire chisomo, ananyamuka.
but Paul chose Silas and departed, once he had been committed by the brothers to the grace of God.
41 Iye anadutsa ku Siriya ndi ku Kilikiya kupita akulimbikitsa mipingo.
And he went through Syria and Cilicia, strengthening the churches.

< Machitidwe a Atumwi 15 >