< Machitidwe a Atumwi 15 >

1 Anthu ena ochokera ku Yudeya anafika ku Antiokeya ndipo amaphunzitsa abale kuti, “Ngati simuchita mdulidwe potsata mwambo wa Mose, simungapulumuke.”
Some men came down from Judea and taught the brothers, "Unless you are circumcised after the custom of Moses, you cannot be saved."
2 Zimenezi zinachititsa Paulo ndi Barnaba kuti atsutsane nawo kwambiri. Kotero Paulo ndi Barnaba anasankhidwa pamodzi ndi abale ena kuti apite ku Yerusalemu kukaonana ndi atumwi ndi akulu ampingo kukakambirana za nkhaniyi.
Therefore when Paul and Barnabas had no small discord and discussion with them, they appointed Paul and Barnabas, and some others of them, to go up to Jerusalem to the apostles and elders about this question.
3 Mpingo unawaperekeza, ndipo pamene amadutsa ku Foinike ndi Samariya, iwo anafotokoza momwe a mitundu ina anatembenukira mtima. Nkhani imeneyi inakondweretsa kwambiri abale onse.
They, being sent on their way by the church, passed through both Phoenicia and Samaria, describing in detail the conversion of the non-Jewish people. They caused great joy to all the brothers.
4 Atafika ku Yerusalemu, iwo analandiridwa ndi mpingo, pamodzi ndi atumwi ndiponso akulu ampingo. Paulo ndi Barnaba anawafotokozera zonse zimene Mulungu anachita kudzera mwa iwo.
When they had come to Jerusalem, they were received by the church and the apostles and the elders, and they reported all things that God had done with them.
5 Kenaka, okhulupirira ena amene kale anali a gulu la Afarisi anayimirira ndipo anati, “Anthu a mitundu ina ayenera kuchita mdulidwe ndi kusunga malamulo a Mose.”
But some of the sect of the Pharisees who believed rose up, saying, "It is necessary to circumcise them, and to command them to keep the Law of Moses."
6 Atumwi ndi akulu ampingo anasonkhana kuti akambirane za nkhaniyi.
The apostles and the elders were gathered together to see about this matter.
7 Atakambirana kwambiri Petro anayimirira, ndipo anawayankhula nati: “Abale, mukudziwa kuti masiku oyambirira Mulungu anandisankha ine pakati panu kuti anthu a mitundu ina amve kuchokera pakamwa panga mawu a Uthenga Wabwino ndi kukhulupirira.
When there had been much discussion, Peter rose up and said to them, "Brothers, you know that a good while ago God made a choice among you, that by my mouth the nations should hear the word of the Good News, and believe.
8 Mulungu amene amadziwa mtima wa munthu, Iye anaonetsa kuti anawalandira powapatsa Mzimu Woyera, monga momwe anachita kwa ife.
God, who knows the heart, testified about them by giving the Holy Spirit, just like he did to us.
9 Iye sanasiyanitse pakati pa ife ndi iwo, pakuti anayeretsa mitima yawo mwachikhulupiriro.
He made no distinction between us and them, cleansing their hearts by faith.
10 Tsopano, chifukwa chiyani mukuyesa Mulungu poyika goli mʼkhosi la ophunzira, limene ngakhale ife kapena makolo athu sangathe kulisenza?
Now therefore why do you tempt God, that you should put a yoke on the neck of the disciples which neither our fathers nor we were able to bear?
11 Osatero! Ife tikukhulupirira kuti tinapulumutsidwa mwachisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu, monga iwonso anachitira.”
But we believe that we are saved through the grace of the Lord Jesus, just as they are."
12 Gulu lonse linakhala chete pamene amamvetsera Barnaba ndi Paulo akuwawuza za zizindikiro zodabwitsa zimene Mulungu anazichita pakati pa anthu a mitundu ina kudzera mwa iwo.
And all the people kept quiet, and they listened to Barnabas and Paul reporting what signs and wonders God had done among the nations through them.
13 Iwo atatha kuyankhula, Yakobo anayankhula nati: “Abale, tandimverani.
After they were silent, James answered, "Brothers, listen to me.
14 Simoni watifotokozera mmene Mulungu poyamba paja anaonetsa kukhudzidwa kwake pomwe anatenga anthu a mitundu ina kukhala ake.
Simeon has reported how God first visited the nations, to take out of them a people for his name.
15 Mawu a aneneri akuvomereza zimenezi, monga kwalembedwa kuti,
This agrees with the words of the prophets. As it is written,
16 “‘Zitatha izi Ine ndidzabwerera ndipo ndidzamanganso nyumba ya Davide imene inagwa. Ndidzakonzanso malo amene anagumuka, ndi kuyimanganso,
'After these things I will return; and I will rebuild the tabernacle of David that has fallen, and I will rebuild its ruins, and I will restore it,
17 kuti anthu otsalawo afunefune Ambuye, ndi anthu onse a mitundu ina amene atchedwa ndi dzina langa, akutero Ambuye, amene amachita zinthu zimenezi
that the rest of humanity may seek after the Lord, and all the nations who are called by my name, says the Lord, who makes these things
18 zinaululidwa kuyambira kalekale.’ (aiōn g165)
known from long ago.' (aiōn g165)
19 “Chifukwa chake, ine ndikuweruza kuti tisamavute anthu a mitundu ina amene atembenuka mtima kutsata Mulungu.
"Therefore my judgment is that we do not trouble those from among the non-Jewish people who turn to God,
20 Koma tiwalembere iwo, kuwawuza kuti asadye chakudya choperekedwa kwa mafano, apewenso dama, asadyenso nyama zochita kupotola kapena kudya magazi.
but that we write to them that they abstain from things defiled by idols, from sexual immorality, from what is strangled, and from blood.
21 Pakuti malamulo a Mose akhala akulalikidwa mu mzinda uliwonse, kuyambira kalekale ndipo amawerengedwa mʼMasunagoge tsiku la Sabata.”
For Moses from generations of old has in every city those who proclaim him, being read in the synagogues every Sabbath."
22 Pamenepo atumwi ndi akulu ampingo, pamodzi ndi mpingo onse, anagwirizana zosankha anthu ena pakati pawo kuti awatume ku Antiokeya pamodzi ndi Paulo ndi Bamaba. Iwo anasankha Yudasi, wotchedwa Barsaba ndi Sila, anthu awiri amene anali atsogoleri pakati pa abale,
Then it seemed good to the apostles and the elders, with the whole church, to choose men out of their company, and send them to Antioch with Paul and Barnabas: Judas called Barsabbas, and Silas, chief men among the brothers.
23 kuti akapereke kalata yonena kuti, Kuchokera kwa atumwi ndi akulu ampingo, abale anu, Kwa anthu a mitundu ina okhulupirira a ku Antiokeya, Siriya ndi Kilikiya: Tikupereka moni.
They wrote these things by their hand: "The apostles, the elders, and the brothers, to the non-Jewish brothers who are in Antioch, Syria, and Cilicia: greetings.
24 Ife tamva kuti anthu ena ochokera pakati pathu, amene sitinawatume anakusokonezani maganizo ndi kukuvutitsani ndi zimene amakuwuzani.
Because we have heard that some who went out from us have troubled you with words, unsettling your souls, to whom we gave no commandment;
25 Tsono ife tagwirizana kuti, tisankhe anthu ena ndi kuwatumiza kwa inu pamodzi ndi abale athu okondedwa Paulo ndi Barnaba,
it seemed good to us, having come to one accord, to choose out men and send them to you with our beloved Barnabas and Paul,
26 anthu amene anapereka moyo wawo chifukwa cha dzina la Ambuye athu Yesu Khristu.
who have risked their lives for the name of our Lord Jesus Christ.
27 Nʼchifukwa chake, tikutumiza Yudasi ndi Sila kuti adzachitire umboni ndi mawu a pakamwa pawo za zimene ife talemba.
We have sent therefore Judas and Silas, who themselves will also tell you the same things by word of mouth.
28 Pakuti zinakomera Mzimu Woyera ndiponso ife kuti tisakusenzetseni katundu wina, kupatula zoyenera zokhazi:
For it seemed good to the Holy Spirit, and to us, to lay no greater burden on you than these necessary things:
29 Mupewe kudya chakudya choperekedwa nsembe kwa mafano, musadye magazi, kapena nyama yopha mopotola ndiponso musachite dama. Mudzachita bwino mukapewa zimenezi. Tsalani bwino.
that you abstain from things sacrificed to idols, from blood, from things strangled, and from sexual immorality, from which if you keep yourselves, it will be well with you. Farewell."
30 Anthu aja anatumidwa ndipo anafika ku Antiokeya, kumene anasonkhanitsa mpingo pamodzi napereka kalatayo.
So, when they were sent off, they came to Antioch, and having gathered the congregation together, they delivered the letter.
31 Anthuwo anawerenga kalatayo ndipo abalewo anakondwa chifukwa cha mawu ake achirimbikitso.
When they had read it, they rejoiced over the encouragement.
32 Yudasi ndi Sila amene analinso aneneri, ananena zambiri zowalimbikitsa ndi kuwapatsa mphamvu abalewo.
Judas and Silas, also being prophets themselves, encouraged the brothers with many words, and strengthened them.
33 Atakhala kumeneko kwa kanthawi, abale aja anatsanzikana nawo mwamtendere kuti abwerere kwa amene anawatuma.
After they had spent some time there, they were sent back with greetings from the brothers to those that had sent them forth.
34 Koma Sila anasankha kuti akhale komweko.
However, Silas decided to remain there.
35 Koma Paulo ndi Barnaba anatsalira ku Antiokeya kumene iwo pamodzi ndi ena ambiri anaphunzitsa ndi kulalikira Mawu a Ambuye.
And Paul and Barnabas stayed in Antioch, teaching and proclaiming the word of the Lord, with many others also.
36 Patapita masiku ena Paulo anati kwa Barnaba, “Tiyeni tibwerere kuti tikaone abale ku mizinda yonse imene tinalalika Mawu a Ambuye ndipo tikaone mmene akuchitira.”
After some days Paul said to Barnabas, "Let us return now and visit our brothers in every city in which we proclaimed the word of the Lord, to see how they are doing."
37 Barnaba anafuna kutenga Yohane, wotchedwanso Marko, kuti apite nawo.
Barnabas planned to take John, who was called Mark, with them also.
38 Koma Paulo anaganiza kuti sichinali cha nzeru kumutenga Yohane chifukwa iye anawathawa ku Pamfiliya ndipo sanapitirire nawo pa ntchito.
But Paul did not think that it was a good idea to take with them someone who had withdrawn from them in Pamphylia, and did not go with them to do the work.
39 Iwo anatsutsana kwambiri kotero kuti anapatukana. Barnaba anatenga Marko ndipo anakwera sitima ya pamadzi kupita ku Kupro.
Then the contention grew so sharp that they separated from each other. Barnabas took Mark with him, and sailed away to Cyprus,
40 Paulo anasankha Sila. Abale atawapempherera kwa Ambuye kuti alandire chisomo, ananyamuka.
but Paul chose Silas, and went out, being commended by the brothers to the grace of the Lord.
41 Iye anadutsa ku Siriya ndi ku Kilikiya kupita akulimbikitsa mipingo.
He went through Syria and Cilicia, strengthening the churches.

< Machitidwe a Atumwi 15 >