< Machitidwe a Atumwi 14 >
1 Ku Ikoniya, Paulo ndi Barnaba analowanso mʼsunagoge ya Ayuda. Kumeneko iwo anaphunzitsa momveka bwino kotero kuti anthu ambiri Achiyuda ndi anthu a mitundu ina anakhulupirira.
At Iconium Paul and Barnabas went as usual into the Jewish meeting place and spoke very convincingly [about the Lord Jesus]. As a result, many Jews and also non-Jews believed [in Jesus].
2 Koma Ayuda amene anakana kukhulupirira anawutsa anthu a mitundu ina nawononga maganizo awo kutsutsana ndi abale.
But [some of] the Jews refused to believe [that message, and] told the non-Jews not to believe it. They told the non-Jewish people that the message [about Jesus] was not true. As a result, [some of] the non-Jews became angry towards the believers [there].
3 Ndipo Paulo ndi Barnaba anakhala kumeneko nthawi yayitali, nalalikira molimba mtima za Ambuye amene anawapatsa mphamvu yochitira zozizwitsa ndi zizindikiro zodabwitsa pochitira umboni mawu a chisomo.
So Paul and Barnabas spent considerable time there speaking boldly for the Lord, and the Lord Jesus enabled them to do many miracles. In this way he showed [people] that the message about how the Lord saves us in a way that we do not deserve is true.
4 Anthu a mu mzindamo anagawikana; ena anali mbali ya Ayuda, ena mbali ya atumwi.
The people [who lived] in [Iconium] city strongly disagreed with each other [concerning the message about Jesus]. Some of them agreed with the Jews [SYN] [who did not believe that message]. Others agreed with Paul and Barnabas.
5 Pamenepo anthu a mitundu ina ndi Ayuda, pamodzi ndi atsogoleri awo anakonza chiwembu choti azunze atumwiwo ndi kuwagenda ndi miyala.
Then the non-Jewish people and the Jewish [leaders] [SYN] [who opposed those two] talked among themselves about how they could mistreat them. Some of the important men in that city agreed to help them. Together, they decided that they would [kill Paul and Barnabas by] throwing stones at them.
6 Koma atazindikira zimenezi, anathawira ku Lusitra ndi Derbe, mizinda ya ku Lukaoniya, ndiponso ku dziko lozungulira mizindayo,
But Paul and Barnabas heard about that, so they quickly went away to Lycaonia [district. They went] to Lystra and Derbe [cities in that district] and to the area surrounding [those cities].
7 kumene anapitiriza kulalikira Uthenga Wabwino.
[While they were] in that area, they continually told people the message [about the Lord Jesus].
8 Ku Lusitra kunali munthu wolumala miyendo, amene sanayendepo chibadwire chake.
[Once while Paul was preaching to people] in Lystra, a man was sitting there who was crippled in his legs. When [his mother] bore him he had crippled legs, so he was never able to walk.
9 Iyeyu, amamvetsera pamene Paulo amayankhula. Paulo anamuyangʼanitsitsa ndipo anaona kuti anali ndi chikhulupiriro choti achiritsidwe nacho.
He listened as Paul was speaking [about the Lord Jesus]. Paul looked directly at him and could see [in the man’s face] that he believed that [the Lord Jesus] could make him well.
10 Ndipo Paulo anamuyitana mofuwula nati, “Imirira!” Atamva zimenezi, munthuyo anayimirira, nayamba kuyenda.
So Paul called out [to him], “Stand up!” [When the man heard that], he [immediately] jumped up and began to walk [normally].
11 Gulu la anthu litaona zimene Paulo anachitazi, linafuwula mʼChilukaoniya kuti, “Milungu yatitsikira yooneka ngati anthu!”
When the crowd saw what Paul had done, [they thought that Paul and Barnabas] [were/must be]) [the gods that they worshipped]. So they shouted [excitedly] in their [own] Lycaonia language, “[Look! These people are] the gods [that we(inc) worship! They] made themselves look like people and have come down [from the sky/heaven to help us]!”
12 Barnaba anamutcha Zeusi ndipo Paulo anamutcha Herimesi chifukwa ndiye amatsogolera kuyankhula.
They began to say that Barnabas was [probably the chief god, whose name was]. And [they began to say that] Paul was Hermes, [the messenger/spokesman for the other gods. They mistakenly thought that] because Paul was the one who had been speaking.
13 Wansembe wa Zeusi amene nyumba yopembedzera Zeusiyo inali kunja pafupi ndi mzindawo, anabweretsa ngʼombe yayimuna yovekedwa nkhata za maluwa pa chipata cha mzindawo chifukwa iyeyo pamodzi ndi anthu ena onse aja amafuna kudzipereka nsembe kwa Paulo ndi Barnaba.
Just outside [the gates of] the city there was a temple [where the people worshipped Zeus. The priest who was there heard what Paul and Barnabas had done, so he came] to the city gate, where many people had already gathered. He brought [two] bulls with wreaths [of flowers around their necks]. The priest and the other people wanted to kill the bulls [as part of a ceremony] to worship Paul and Barnabas.
14 Koma Barnaba ndi Paulo atamva zimenezi, anangʼamba zovala zawo, nathamangira pakati pa gulu la anthuwo, akufuwula kuti,
But when the apostles, Barnabas and Paul, heard about that, [and understood that the people thought that they were gods and wanted to sacrifice the bulls to worship them], they [were very distressed], so they tore their own clothes. They rushed among the people, shouting,
15 “Anthu inu, bwanji mukuchita zimenezi? Ifenso ndife anthu monga inu nomwe. Ife takubweretserani Uthenga Wabwino, kuti musiye zinthu zachabezi ndi kutsata Mulungu wamoyo, amene analenga kumwamba ndi dziko lapansi, nyanja ndi zonse zimene zili mʼmenemo.
“Men, (you must not kill those bulls [to worship us(dl)!]/why are you doing this?) [RHQ] [We are not gods]! We are just human beings like you! We have come to tell you some good news! [We have come to tell you about] God who is all-powerful. He wants you to stop worshipping other gods, because they cannot help you. This true God made the heaven/sky and the earth and the oceans and everything in it.
16 Kale Iye analola anthu a mitundu ina yonse kutsata njira zawozawo.
In the past, all of you non-Jewish people [worshipped whatever gods that you wanted to]. God let you worship them, [because you did not know him].
17 Komabe wakhala akudzichitira yekha umboni: Iye amaonetsa kukoma mtima kwake pogwetsa mvula kuchokera kumwamba ndi zipatso pa nyengo yake. Amakupatsani chakudya chambiri ndipo amadzaza mitima yanu ndi chimwemwe.”
But he has shown us [LIT] [that] he acts kindly [toward us(inc)]. He is the one who causes it to rain and causes crops to grow. He is the one who gives you plenty of food, and makes you very happy.”
18 Ngakhale ndi mawu awa, anavutika kuletsa gulu la anthu kuti asapereke nsembe kwa iwo.
The people heard what [Paul] said, but they still thought that they should sacrifice those bulls to worship Paul and Barnabas. [But finally, the people decided not to do it].
19 Kenaka kunabwera Ayuda ena kuchokera ku Antiokeya ndi Ikoniya nakopa gulu la anthu lija. Iwo anamugenda miyala Paulo namukokera kunja kwa mzindawo, kuganiza kuti wafa.
[However], after that, some Jews came from Antioch and Iconium and persuaded many of the people of Lystra [that the message Paul had been telling them] was not true. The people [who believed what those Jews said became angry with Paul. They let the Jews] throw stones at him [until he fell down, unconscious]. They [all] thought that he was dead, so they dragged him outside the city [and left him lying there]. But some of the believers [in Lystra had followed them outside the city].
20 Koma ophunzira atamuzungulira, Pauloyo anayimirira nalowanso mu mzindawo. Mmawa mwake iye ndi Barnaba anachoka ndi kupita ku Derbe.
They came and stood around Paul, [where he was lying on the ground]. And Paul [became conscious! He] stood up and went back into the city [with the believers]. Acts 14:20b-23 The next day, Paul and Barnabas [left Lystra and] traveled to Derbe.
21 Iwo analalikira Uthenga Wabwino mu mzindawo ndipo anthu ambiri anatembenuka mtima ndi kukhala ophunzira. Kenaka anabwerera ku Lusitra, ku Ikoniya ndi ku Antiokeya.
They [stayed there several days and they kept telling] the people the good message [about Jesus]. Many people became believers. After that, Paul and Barnabas [started on their way back. They] went again to Lystra. [Then they went from there] to Iconium, and [then they went] to Antioch [in Pisidia province].
22 Kumeneko analimbikitsa mitima ya ophunzira ndi kuwapatsa mphamvu kuti akhalebe woona mʼchikhulupiriro. Iwo anati, “Ife tiyenera kudutsa mʼmasautso ambiri kuti tikalowe mu ufumu wa Mulungu.”
[In each city], they helped the believers [SYN] to become strong [spiritually], and they urged them to keep on trusting in [the Lord Jesus]. They told [the believers], “It is necessary that [we endure] people often persecuting us [(inc)] before we enter the place where God will rule [over us forever].”
23 Paulo ndi Barnaba anasankha akulu ampingo pa mpingo uliwonse, ndipo atapemphera ndi kusala kudya anawapereka kwa Ambuye amene anamukhulupirira.
Paul and Barnabas appointed leaders for each congregation. [And before Paul and Barnabas left each town, they gathered the believers together and spent some time] praying and (fasting/not eating any food). Then Paul and Barnabas entrusted the [leaders and other believers] to the Lord [Jesus], in whom they had believed, [in order that he would care for them].
24 Atadutsa Pisidiya, anafika ku Pamfiliya.
After Paul and Barnabas had traveled through Pisidia [district], they went [south] to Pamphylia [district].
25 Atalalikira Mawu ku Perga, anapita ku Ataliya.
[In that district], they [arrived] at Perga and preached God’s message [about the Lord Jesus to the people there. Then] they went down [to the seacoast] at Attalia.
26 Ku Ataliyako, anakwera sitima ya pamadzi kubwerera ku Antiokeya kumene anayitanidwa mwachisomo cha Mulungu kuti agwire ntchito imene tsopano anali atayitsiriza.
There they got on a ship and went back to Antioch [in Syria province]. That was the place where Paul and Barnabas had been appointed {where [believers] had sent Paul and Barnabas} to go [to other places] and preach. [Antioch was the place where the believers] had asked God to kindly help Paul and Barnabas in the work that they had now completed.
27 Atangofika ku Antiokeya, anasonkhanitsa pamodzi mpingo ndipo anafotokoza zonse zimene Mulungu anachita kudzera mwa iwo ndiponso mmene Iye anatsekulira a mitundu ina njira ya chikhulupiriro.
When they arrived in Antioch, they called the believers together. Then Paul and Barnabas told them all that God had helped them to do. [Specifically, they told them how God] had enabled [IDM] [many] non-Jewish people to believe [in Jesus].
28 Ndipo anakhala kumeneko ndi ophunzira nthawi yayitali.
Then Paul and Barnabas stayed in Antioch with the [other] believers for several months.