< Machitidwe a Atumwi 12 >
1 Inali nthawi yomweyi imene mfumu Herode anamanga ena a mu mpingo ndi cholinga chakuti awazunze.
А Цар І́род тоді підні́с руки, щоб декого з Церкви гноби́ти.
2 Iye analamula kuti Yakobo mʼbale wa Yohane, aphedwe ndi lupanga.
І мечем він стяв Якова, брата Іванового.
3 Ataona kuti zimenezi zinakondweretsa Ayuda, anawonjeza ndi kugwiranso Petro. Izi zinachitika pa nthawi ya Chikondwerero cha Buledi wopanda Yisiti.
А бачивши, що подо́балося це юдеям, він задумав схопи́ти й Петра. Були ж дні Опрі́сноків.
4 Atamugwira Petro, namutsekera mʼndende, anamupereka kwa magulu anayi a asilikali kuti amuyangʼanire, gulu lililonse linali ndi asilikali anayi. Herode anafuna kumuzenga mlandu pamaso pa anthu onse chikondwerero cha Paska chitapita.
І, схопи́вши його, посадив до в'язниці, і передав чотирьом чвіркам воякі́в, щоб його стерегли, бажаючи вивести людям його по Па́сці.
5 Kotero Petro anasungidwa mʼndende, koma mpingo unamupempherera kolimba kwa Mulungu.
Отож, у в'язниці Петра стерегли, а Церква ре́вно молилася Богові за нього.
6 Usiku woti mmawa mwake Herode amuzenga mlandu, Petro amagona pakati pa asilikali awiri, atamangidwa maunyolo awiri, ndiponso alonda atayima pa khomo.
А як Ірод хотів його ви́вести, Петро спав тієї ночі між двома́ вояка́ми, закутий у два ланцюги́, і сторо́жа пильнувала в'язницю при две́рях.
7 Mwadzidzidzi mngelo wa Ambuye anaonekera ndipo kuwala kunawunika mʼchipindamo. Mngeloyo anamugwedeza Petro mʼnthiti ndi kumudzutsa. Iye anati, “Fulumira, imirira!” Ndipo maunyolo anagwa kuchoka mʼmanja a Petro.
І ось ангол Господній з'явився, і в в'язниці засяяло світло. І, доторкнувшись до боку Петрового, він збудив його, кажучи: „Мерщі́й встава́й!“І ланцюги́ йому з рук поспада́ли.
8 Kenaka mngelo anati kwa iye, “Vala zovala ndi nsapato.” Ndipo Petro atachita izi mngeloyo anamuwuzanso kuti, “Funda chovala chako ndipo unditsate.”
А ангол до нього промовив: „Підпережи́ся, і взуй санда́лі свої“. І він так учинив. І каже йому: „Зодягнися в плаща свого, та й за мною йди“.
9 Petro anatsatira natuluka mʼndende, koma sanazindikire kuti zimene mngeloyo amachita zimachitikadi; iye amaganiza kuti amaona masomphenya.
І, вийшовши, він ішов услід за ним, і не знав, чи то правда, що робилось від ангола, бо ду́мав, що видіння він бачить.
10 Iwo anadutsa gulu loyamba ndi lachiwiri la asilikali ndipo anafika pa chitseko chachitsulo cholowera mu mzinda. Chitsekocho chinatsekuka chokha ndipo anadutsa. Pamene anayenda kutalika kwa msewu umodzi, mwadzidzidzi mngelo uja anachoka.
Як сторо́жу минули вони першу й другу, то прийшли до залізної брами, що до міста веде, — і вона відчинилась сама ім. І, вийшовши, пройшли одну вулицю, — і відступив ангол зараз від нього.
11 Pamenepo Petro anazindikira nati, “Tsopano ndikudziwa mosakayika kuti Ambuye anatuma mngelo wake kudzandipulumutsa mʼmanja mwa Herode, ndi ku zoyipa zonse zimene Ayuda amafuna kundichitira.”
Сказав же Петро, оприто́мнівши: „Тепер знаю правдиво, що Господь послав Свого ангола, і видер мене із рук Іродових та від усього чека́ння народу юдейського“.
12 Atazindikira zimenezi anapita ku nyumba ya Mariya amayi ake a Yohane, wotchedwanso Marko, kumene kunasonkhana anthu ambiri ndipo amapemphera.
А зміркувавши, він прийшов до сади́би Марії, матері Івана, званого Ма́рком, де багато зібралося й молилося.
13 Petro anagogoda pa chitseko cha panja, ndipo mtsikana wantchito dzina lake Roda anabwera kuti adzatsekule chitseko.
І як Петро в фіртку брами постукав, то вийшла послухати служни́ця, що звалася Ро́да,
14 Atazindikira mawu a Petro anakondwa kwambiri ndipo anabwerera osatsekula ndipo anafuwula kuti, “Petro ali pa khomopa!”
та голос Петрів розпізнавши, вона з радощів не відчинила воріт, а прибігши, сказала, що Петро при воро́тях стоїть!
15 Anthuwo anati kwa iye, “Wopenga iwe!” Atalimbikira kunena kuti zinali zoona, iwo anati, “Ameneyo ndi mngelo wake.”
А вони їй сказали: „Чи ти навісна́?“Та вона запевняла своє́, що є так. Вони ж говорили: „То ангол його!“
16 Koma Petro anapitiriza kugogoda ndipo atatsekula chitseko ndi kumuona, anthuwo anadabwa kwambiri.
А Петро й далі стукав. Коли ж відчинили, вони його вгледіли та й дивувалися.
17 Petro anakweza dzanja ndi kuwawuza kuti akhale chete ndipo anawafotokozera mmene Ambuye anamutulutsira mʼndende. Iye anati, “Uzani Yakobo ndi abale ena za zimenezi.” Kenaka anachoka napita kumalo ena.
Махнувши ж рукою до них, щоб мовчали, він їм розповів, як Господь його вивів із в'язниці. І сказав: „Сповістіть про це Якова й браттю“. І, вийшовши, він до іншого місця пішов.
18 Pamene kunacha kunali phokoso lalikulu pakati pa asilikali, iwo anafunsa kuti, “Kodi chamuchitikira Petro ndi chiyani?”
Коли ж настав день, поміж вояка́ми зчинилась велика тривога, що́ то сталось з Петром.
19 Herode atamufunafuna ndipo wosamupeza, anawafunsa asilikali ndipo analamulira kuti asilikaliwo aphedwe. Kenaka Herode anachoka ku Yudeya ndi kupita ku Kaisareya ndipo anakhala kumeneko kwa kanthawi
А Ірод, пошукавши його й не знайшовши, віддав варту під суд, і звелів їх стра́тити. А сам із Юдеї відбув в Кесарі́ю, і там перебува́в.
20 Herode anakwiyira anthu a ku Turo ndi Sidoni; anthuwo anagwirizana zoti akambirane naye. Atapeza thandizo kuchokera kwa Blasito, wantchito wokhulupirika wa mfumu, anapempha kuti pakhale mtendere, chifukwa dziko lawo limadalira dziko la mfumuyo pa chakudya chawo.
А І́род розгніваний був на тиря́н та сидо́нян. І вони однодушно до нього прийшли, і вблагали царсько́го постельника Вла́ста, та й миру просили, бо їхня земля годувалась з царсько́ї.
21 Pa tsiku limene anasankha Herode, atavala zovala zake zaufumu, anakhala pa mpando wake ndipo anayankhula kwa anthuwo.
Дня ж призначеного І́род убрався в одежу царську́, і на підвищенні сів та й до ни́х говорив.
22 Anthuwo anafuwula nati, “Amenewa ndi mawu a mulungu osati a munthu ayi.”
А на́товп кричав: „Голос Божий, а не лю́дський!“
23 Nthawi yomweyo mngelo wa Mulungu anamukantha chifukwa sanapereke ulemu kwa Mulungu ndipo anadyedwa ndi mphutsi nafa.
І ангол Господній ура́зив знена́цька його, бо він не віддав слави Богові. І черва́ його з'їла, і він умер.
24 Koma Mawu a Mulungu anapitirirabe kufalikirafalikira.
Слово ж Боже росло та помно́жувалось.
25 Barnaba ndi Saulo atamaliza ntchito yawo anachoka ku Yerusalemu, atatenga Yohane wotchedwanso Marko.
А Варнава та Савл, службу виконавши, повернулись із Єрусалиму, узявши з собою Івана, що про́званий Ма́рком.