< Machitidwe a Atumwi 12 >
1 Inali nthawi yomweyi imene mfumu Herode anamanga ena a mu mpingo ndi cholinga chakuti awazunze.
In that tyme Herode the kynge stretched forthe his handes to vexe certayne of the congregacion.
2 Iye analamula kuti Yakobo mʼbale wa Yohane, aphedwe ndi lupanga.
And he kylled Iames the brother of Iohn with the swerde:
3 Ataona kuti zimenezi zinakondweretsa Ayuda, anawonjeza ndi kugwiranso Petro. Izi zinachitika pa nthawi ya Chikondwerero cha Buledi wopanda Yisiti.
and because he sawe that it pleased ye Iewes he proceded forther and toke Peter also. Then were the dayes of swete breed.
4 Atamugwira Petro, namutsekera mʼndende, anamupereka kwa magulu anayi a asilikali kuti amuyangʼanire, gulu lililonse linali ndi asilikali anayi. Herode anafuna kumuzenga mlandu pamaso pa anthu onse chikondwerero cha Paska chitapita.
And when he had caught him he put him in preson and delyvered him to. iiii. quaternios of soudiers to be kepte entendynge after ester to brynge him forth to the people.
5 Kotero Petro anasungidwa mʼndende, koma mpingo unamupempherera kolimba kwa Mulungu.
Then was Peter kepte in preson. But prayer was made with out ceasynge of the congregacion vnto God for him.
6 Usiku woti mmawa mwake Herode amuzenga mlandu, Petro amagona pakati pa asilikali awiri, atamangidwa maunyolo awiri, ndiponso alonda atayima pa khomo.
And when Herode wolde have brought him oute vnto the people the same nyght slepte Peter bitwene two soudiers bounde with two chaynes and the kepers before the dore kepte the preson.
7 Mwadzidzidzi mngelo wa Ambuye anaonekera ndipo kuwala kunawunika mʼchipindamo. Mngeloyo anamugwedeza Petro mʼnthiti ndi kumudzutsa. Iye anati, “Fulumira, imirira!” Ndipo maunyolo anagwa kuchoka mʼmanja a Petro.
And beholde the angell of ye Lorde was there present and a lyght shyned in the lodge. And smote Peter on the syde and steryd him vp sayinge: aryse vp quyckly. And his cheynes fell of fro his hondes.
8 Kenaka mngelo anati kwa iye, “Vala zovala ndi nsapato.” Ndipo Petro atachita izi mngeloyo anamuwuzanso kuti, “Funda chovala chako ndipo unditsate.”
And the angell sayd vnto him: gyrde thy selfe and bynde on thy sandales. And so he dyd. And he sayde vnto him: cast thy mantle aboute the and folowe me.
9 Petro anatsatira natuluka mʼndende, koma sanazindikire kuti zimene mngeloyo amachita zimachitikadi; iye amaganiza kuti amaona masomphenya.
And he came oute and folowed him and wist not that it was truthe which was done by the angell but thought he had sene a vision.
10 Iwo anadutsa gulu loyamba ndi lachiwiri la asilikali ndipo anafika pa chitseko chachitsulo cholowera mu mzinda. Chitsekocho chinatsekuka chokha ndipo anadutsa. Pamene anayenda kutalika kwa msewu umodzi, mwadzidzidzi mngelo uja anachoka.
When they were past ye fyrst and ye seconde watche they came vnto yt yron gate yt ledeth vnto the cyte which opened to them by his awne accorde. And they went out and passed thorowe one strete and by and by the angell departed fro him.
11 Pamenepo Petro anazindikira nati, “Tsopano ndikudziwa mosakayika kuti Ambuye anatuma mngelo wake kudzandipulumutsa mʼmanja mwa Herode, ndi ku zoyipa zonse zimene Ayuda amafuna kundichitira.”
And when Peter was come to him selfe he sayde: now I knowe of a surety that the Lorde hath sent his angell and hath delyvered me out of the honde of Herode and from all the waytynge for of the people of ye Iewes.
12 Atazindikira zimenezi anapita ku nyumba ya Mariya amayi ake a Yohane, wotchedwanso Marko, kumene kunasonkhana anthu ambiri ndipo amapemphera.
And as he consydred the thinge he cam to ye housse of Mary the mother of one Iohn which was called Marke also where many were gaddered to gedder in prayer.
13 Petro anagogoda pa chitseko cha panja, ndipo mtsikana wantchito dzina lake Roda anabwera kuti adzatsekule chitseko.
As Peter knocked at the entry dore a damsell cam forth to herken named Rhoda.
14 Atazindikira mawu a Petro anakondwa kwambiri ndipo anabwerera osatsekula ndipo anafuwula kuti, “Petro ali pa khomopa!”
And when she knew Peters voyce she opened not the entrey for gladnes but ran in and told how Peter stode before the entrey.
15 Anthuwo anati kwa iye, “Wopenga iwe!” Atalimbikira kunena kuti zinali zoona, iwo anati, “Ameneyo ndi mngelo wake.”
And they sayde vnto her: thou arte mad. And she bare them doune yt it was even so. Then sayde they: it is his angell.
16 Koma Petro anapitiriza kugogoda ndipo atatsekula chitseko ndi kumuona, anthuwo anadabwa kwambiri.
Peter cotynued knockinge. When they had opened the dore and sawe him they were astonyed.
17 Petro anakweza dzanja ndi kuwawuza kuti akhale chete ndipo anawafotokozera mmene Ambuye anamutulutsira mʼndende. Iye anati, “Uzani Yakobo ndi abale ena za zimenezi.” Kenaka anachoka napita kumalo ena.
And he beckened vnto them with ye honde to holde their peace and tolde them by what meanes ye Lorde had brought him oute of the preson. And sayde: goo shew these thinges vnto Iames and to the brethren. And he departed and went into a nother place.
18 Pamene kunacha kunali phokoso lalikulu pakati pa asilikali, iwo anafunsa kuti, “Kodi chamuchitikira Petro ndi chiyani?”
Assone as it was daye ther was no lyttell a doo amoge the soudyers what was becum of Peter.
19 Herode atamufunafuna ndipo wosamupeza, anawafunsa asilikali ndipo analamulira kuti asilikaliwo aphedwe. Kenaka Herode anachoka ku Yudeya ndi kupita ku Kaisareya ndipo anakhala kumeneko kwa kanthawi
When Herode had called for him and founde him not he examined the kepers and comaunded to departe. And he descended from Iewry to Cesarea and ther abode.
20 Herode anakwiyira anthu a ku Turo ndi Sidoni; anthuwo anagwirizana zoti akambirane naye. Atapeza thandizo kuchokera kwa Blasito, wantchito wokhulupirika wa mfumu, anapempha kuti pakhale mtendere, chifukwa dziko lawo limadalira dziko la mfumuyo pa chakudya chawo.
Herode was displeased with them of Tyre and Sydon. And they came all at once and made intercession vnto Blastus the kynges chamberlen and desyred peace because their countrey was norysshed by the kynges londe.
21 Pa tsiku limene anasankha Herode, atavala zovala zake zaufumu, anakhala pa mpando wake ndipo anayankhula kwa anthuwo.
And upon a daye appoynted Herode arayed him in royall apparell and set him in his seate and made an oraycon vnto them.
22 Anthuwo anafuwula nati, “Amenewa ndi mawu a mulungu osati a munthu ayi.”
And the people gave a shoute sayinge: it is ye voyce of a God and not of a man.
23 Nthawi yomweyo mngelo wa Mulungu anamukantha chifukwa sanapereke ulemu kwa Mulungu ndipo anadyedwa ndi mphutsi nafa.
And immediatly the angell of ye Lorde smote him because he gave not God the honoure and he was eatyn of wormes and gave vp the goost.
24 Koma Mawu a Mulungu anapitirirabe kufalikirafalikira.
And ye worde of God grewe and multiplied.
25 Barnaba ndi Saulo atamaliza ntchito yawo anachoka ku Yerusalemu, atatenga Yohane wotchedwanso Marko.
And Barnabas and Paul returned to Ierusalem when they had fulfilled their office and toke with them Iohn which was also called Marcus.