< Machitidwe a Atumwi 11 >
1 Atumwi ndi abale a ku Yudeya konse anamva kuti anthu a mitundu ina analandiranso Mawu a Mulungu.
Now the Apostles and the brethren who were throughout Judaea heard that, the nations also, had welcomed the word of God.
2 Tsono Petro atafika ku Yerusalemu, abale amene anali a mdulidwe anamutsutsa iye,
And, when Peter came up unto Jerusalem, they of the circumcision began to find fault with him,
3 ndipo anati, “Iwe unalowa mʼnyumba ya anthu osachita mdulidwe ndi kudya nawo.”
Saying—he went in unto men uncircumcised, and did eat with them.
4 Koma Petro anayamba kuwafotokozera zonse mwatsatanetsatane momwe zinachitikira kuti,
But Peter, making a beginning, went on to set forth the matter unto them in order, saying—
5 “Ine ndimapemphera mu mzinda wa Yopa ndipo ndili ngati wokomoka ndinaona masomphenya. Ndinaona chinthu chokhala ngati chinsalu chachikulu chikutsika kuchokera kumwamba chogwiridwa msonga zake zinayi, ndipo chinatsikira pa ine.
I was in the city of Joppa praying, and saw in a trance, a vision: —coming down a sort of vessel, like a large sheet, by four corners, being let down out of heaven, and it came even unto me:
6 Ine ndinayangʼana mʼkati mwake ndipo ndinaona nyama za miyendo inayi za mʼdziko lapansi, zirombo, zokwawa, ndi mbalame zamlengalenga.
Into which steadfastly looking, began to observe, and saw the quadrupeds of the earth, and the wild beasts, and the creeping things, and the birds of heaven.
7 Kenaka ine ndinamva mawu akuti, ‘Petro, Imirira. Ipha, nudye.’
Moreover heard a voice also, saying unto me—Rise, Peter! slay and eat.
8 “Ine ndinayankha kuti, ‘Ayi, Ambuye! Pakuti chinthu chodetsedwa ndi chonyansa sindinadyepo pakamwa pangapa.’
But I said—By no means, Lord, because, a common or unclean thing, hath at no time entered into my mouth.
9 “Mawu ochokera kumwamba ananenanso kachiwiri kuti, ‘Chimene Mulungu wachiyeretsa usanene kuti ndi chodetsedwa.’
And a voice answered, a second time, out of heaven—What things, God, hath cleansed, be not, thou, making common.
10 Zimenezi zinachitika katatu ndipo kenaka zonse zinatengedwa kupita kumwamba.
And, this, took place thrice, —and the whole was drawn up again into heaven;
11 “Nthawi yomweyo anthu atatu amene anatumidwa kuchokera ku Kaisareya anayima pa nyumba yomwe ndimakhalayo.
And lo! immediately, three men halted at the house wherein we were, sent from Caesarea unto me.
12 Mzimu anandiwuza kuti ndisakayike, koma ndipite nawo. Abale asanu ndi mmodzi awa anapitanso nane ndipo tinalowa mʼnyumba ya munthuyo.
And the Spirit bade me go with them, nothing doubting. And there went with me these six brethren also; and we entered into the house of the man,
13 Iye anatiwuza mmene anaonera mngelo atayimirira mʼnyumba mwake ndi kumuwuza kuti, ‘Tumiza anthu ku Yopa kuti akayitane Simoni wotchedwa Petro.
And he related to us how he had seen the messenger in his house, standing, and saying—Send away unto Joppa, and fetch Simon, who is surnamed Peter;
14 Iye adzakuwuza uthenga umene udzapulumutsa iwe ndi a pa banja ako.’
Who shall speak words unto thee, whereby thou shall be saved, thou, and all thy house.
15 “Nditangoyamba kuyankhula, Mzimu Woyera anafika pa iwo monga momwe anafikira pa ife poyamba paja.
And, as I began to be speaking, the Holy Spirit fell upon them, just as upon us also at the beginning.
16 Kenaka ndinakumbukira zimene Ambuye ananena kuti, ‘Yohane anabatiza ndi madzi, koma inu mudzabatizidwa ndi Mzimu Woyera.’
And I was put in mind of the word of the Lord, how he used to say—John, indeed, immersed with water; but, ye, shall be immersed in Holy Spirit.
17 Tsono ngati Mulungu anawapatsa iwo mphatso yomweyo imene anatipatsa ife, amene tinakhulupirira Ambuye Yesu Khristu, ndine yani kuti nditsutsane ndi Mulungu?”
If therefore the like free-gift God gave unto them, as even unto us, when we had believed upon the Lord Jesus Christ, who was, I, that could withstand God?
18 Iwo atamva zimenezi analibenso chonena ndipo anayamika Mulungu nati, “Potero Mulungu wapatsa anthu a mitundu ina mwayi wotembenuka mtima ndi kulandira moyo.”
And, having heard these things, they held their peace, and glorified God, saying—Hence, even unto the nations, God hath granted repentance unto life.
19 Tsopano amene anabalalika chifukwa cha mazunzo amene anayamba ataphedwa Stefano, anapita mpaka ku Foinike, ku Kupro ndi ku Antiokeya, ndipo ankalalikira kwa Ayuda okha.
They, therefore, who had been scattered abroad by reason of the tribulation that took place on account of Stephen, passed through as far as Phoenice and Cyprus and Antioch, unto no one speaking the word, save alone unto Jews.
20 Komabe, ena pakati pawo ochokera ku Kupro ndi ku Kurene anapita ku Antiokeya ndipo iwo anayamba kuyankhulanso kwa Agriki, nawawuza za Uthenga Wabwino wa Ambuye Yesu.
And there were some from among them, Cyprians and Cyrenians, who, indeed, coming unto Antioch, began speaking, even unto the Grecian Jews, announcing the glad tidings as to the Lord Jesus;
21 Mphamvu ya Ambuye inali nawo ndipo anthu ambiri anakhulupirira natembenukira kwa Ambuye.
And the hand of the Lord was with them, and a great number—they who believed—turned unto the Lord.
22 Mbiri imeneyi inamveka ku mpingo wa ku Yerusalemu ndipo iwo anatumiza Barnaba ku Antiokeya.
And the matter was reported in the hearing of the assembly that was in Jerusalem, concerning them; and they sent forth Barnabas, as far as Antioch;
23 Atafika ndi kuona chisomo cha Mulungu pa iwo, anakondwa ndi kuwalimbikitsa anthu onsewo kuti apitirire kukhala woona mu mtima mwa Ambuye.
Who, arriving, and seeing the favour which was of God, rejoiced, and went on to beseech all, with the purpose of their heart, to abide [in] the Lord;
24 Barnabayo anali munthu wabwino, wodzazidwa ndi Mzimu Woyera ndi chikhulupiriro ndipo gulu lalikulu la anthu linabwera kwa Ambuye.
Because he was a good man, and full of Holy Spirit and faith; and a considerable multitude were added unto the Lord.
25 Kenaka Barnaba anapita ku Tarisisi kukafuna Saulo,
He went away, however, unto Tarsus, to seek up Saul;
26 ndipo pamene anamupeza anabwera naye ku Antiokeya. Barnaba ndi Saulo anasonkhana ndi mpingo kwa chaka chimodzi naphunzitsa anthu ambirimbiri. Okhulupirirawo anayamba kutchedwa Akhristu ku Antiokeya.
And, finding him, he brought him unto Antioch. And so it was with them, that, for a whole year, they were brought together in the assembly, and taught a considerable multitude; also that the disciples, first in Antioch, were called, Christians.
27 Masiku amenewo ku Antiokeya kunafika aneneri ena ochokera ku Yerusalemu.
Now, in these days, there came down from Jerusalem, prophets, unto Antioch.
28 Mmodzi wa iwo dzina lake Agabu, anayimirira ndipo Mzimu anamutsogolera kunenera zamʼtsogolo kuti padzakhala njala yayikulu pa dziko lonse lapansi. (Izi zinachitikadi nthawi ya ulamuliro wa Klaudiyo).
And one from among them, by name Agabus, rising up, gave a sign, through means of the Spirit, that, a great famine, was coming over all the inhabited earth; which, indeed, came to pass under Claudius.
29 Ophunzirawo, aliyense monga mwakupata kwake, anatsimikiza kuthandiza abale okhala ku Yudeya.
And, according as any one of the disciples was being prospered, they each one of them set apart [something] for ministering, to send unto the brethren, who dwelt in Jerusalem; —
30 Izi anazichitadi ndipo anatuma Barnaba ndi Saulo kukapereka mphatsozo kwa akulu a mpingo.
Which thing they also did, sending it unto the Elders, through the hand of Barnabas and Saul.