< Machitidwe a Atumwi 10 >
1 Ku Kaisareya kunali munthu wina dzina lake Korneliyo, mkulu wa asilikali 100 wa gulu la Italiya.
Now a Captain of the Italian Regiment, named Cornelius, was quartered at Caesarea.
2 Iye ndi banja lake lonse amapembedza ndi kuopa Mulungu. Iye amathandiza osowa mowolowamanja ndipo amapemphera kwa Mulungu nthawi zonse.
He was religious and God-fearing--and so was every member of his household. He was also liberal in his charities to the people, and continually offered prayer to God.
3 Tsiku lina, nthawi ili ngati 3 koloko masana, anaona masomphenya. Anaona bwino ndithu mngelo wa Mulungu, amene anabwera kwa iye ndi kuti, “Korneliyo.”
About three o'clock one afternoon he had a vision, and distinctly saw an angel of God enter his house, who called him by name, saying, "Cornelius!"
4 Korneliyo anamuyangʼanitsitsa mngeloyo mwa mantha. Iye anafunsa kuti, “Nʼchiyani kodi Ambuye?” Mngelo anayankha kuti, “Mapemphero ako ndi zachifundo zako zafika pamaso pa Mulungu ngati chikumbutso.
Looking steadily at him, and being much alarmed, he said, "What do you want, Sir?" "Your prayers and charities," he replied, "have gone up and have been recorded before God.
5 Tsopano tuma anthu apite ku Yopa kuti akayitane munthu dzina lake Simoni Petro.
And now send to Jaffa and fetch Simon, surnamed Peter.
6 Iye akukhala ndi Simoni mmisiri wa zikopa, amene nyumba yake ili mʼmbali mwa nyanja.”
He is staying as a guest with Simon, a tanner, who has a house close to the sea."
7 Mngeloyo anayankhula naye anachoka, Korneliyo anayitana antchito ake awiri ndiponso msilikali mmodzi wa iwo amene ankamutumikira yemwe ankapembedza Mulungu.
So when the angel who had been speaking to him was gone, Cornelius called two of his servants and a God-fearing soldier who was in constant attendance on him,
8 Iye anawafotokozera zonse zimene zinachitika ndipo anawatuma kuti apite ku Yopa.
and, after telling them everything, he sent them to Jaffa.
9 Mmawa mwake, nthawi ili ngati 12 koloko anthuwo atayandikira mzindawo, Petro anakwera pa denga kukapemphera.
The next day, while they were still on their journey and were getting near the town, about noon Peter went up on the house-top to pray.
10 Iye anamva njala ndipo anafuna chakudya, ndipo akukonza chakudyacho, iye anachita ngati wakomoka.
He had become unusually hungry and wished for food; but, while they were preparing it, he fell into a trance.
11 Iye anaona kuthambo kutatsekuka, ndi chinthu china chikutsitsidwa pansi chooneka ngati chinsalu chachikulu chomangidwa pa msonga zake zinayi.
The sky had opened to his view, and what seemed to be an enormous sail was descending, being let down to the earth by ropes at the four corners.
12 Mʼmenemo munali nyama zonse zamiyendo inayi pamodzinso ndi zokwawa za dziko lapansi ndiponso mbalame zamlengalenga.
In it were all kinds of quadrupeds, reptiles and birds,
13 Petro anamva mawu akuti, “Petro, dzuka, ipha nudye.”
and a voice came to him which said, "Rise, Peter, kill and eat."
14 Petro anayankha kuti, “Ayi, Ambuye! Ine sindinadyepo kanthu kosayeretsedwa kapena konyansa.”
"On no account, Lord," he replied; "for I have never yet eaten anything unholy and impure."
15 Petro anamvanso kachiwiri mawu akuti, “Usachiyese chonyansa chimene Mulungu wachiyeretsa.”
Again a second time a voice was heard which said, "What God has purified, you must not regard as unholy."
16 Zimenezi zinachitika katatu ndipo nthawi yomweyo chinsalu chija chinatengedwanso kupita kumwamba.
This was said three times, and immediately the sail was drawn up out of sight.
17 Petro akuganizira za tanthauzo la masomphenyawo, anthu amene Korneliyo anawatuma anapeza kumene kunali nyumba ya Simoni ndipo anayima pa chipata.
While Peter was greatly perplexed as to the meaning of the vision which he had seen, just then the men sent by Cornelius, having by inquiry found out Simon's house,
18 Iwo anayitana nafunsa ngati Simoni amene amadziwika ndi dzina loti Petro amakhala kumeneko.
had come to the door and had called the servant, and were asking, "Is Simon, surnamed Peter, staying here?"
19 Petro akuganizirabe za masomphenyawo, Mzimu Woyera anati kwa iye, “Simoni, anthu atatu akukufunafuna.
And Peter was still earnestly thinking over the vision, when the Spirit said to him, "Three men are now inquiring for you.
20 Dzuka, tsika. Usakayike upite nawo pakuti ndawatuma ndine.”
Rise, go down, and go with them without any misgivings; for it is I who have sent them to you."
21 Petro anatsika ndipo anati kwa anthuwo, “Amene mukufunayo ndine. Mwabwera kuno chifukwa chiyani?”
So Peter went down and said to the men, "I am the Simon you are inquiring for. What is the reason of your coming?"
22 Anthuwo anayankha kuti, “Ife tachokera kwa Korneliyo, mkulu woyangʼanira asilikali 100. Iye ndi munthu wolungama ndiponso woopa Mulungu, amene amalemekezedwa ndi Ayuda onse. Mngelo woyera anamuwuza kuti mupite ku nyumba yake kuti akamve mawu amene inu mukanene.”
Their reply was, "Cornelius, a Captain, an upright and God-fearing man, of whom the whole Jewish nation speaks well, has been divinely instructed by a holy angel to send for you to come to his house and listen to what you have to say."
23 Pamenepo Petro anawalowetsa mʼnyumba ndipo anawasamala ngati alendo ake. Mmawa mwake Petro ananyamuka napita nawo ndipo abale ena a ku Yopa anapita naye pamodzi.
Upon hearing this, Peter invited them in, and gave them a lodging. The next day he set out with them, some of the brethren from Jaffa going with him,
24 Tsiku linalo Petro anafika ku Kaisareya. Korneliyo anawadikirira ndipo anali atawasonkhanitsa pamodzi abale ake ndi abwenzi ake a pamtima.
and the day after that they reached Caesarea. There Cornelius was awaiting their arrival, and had invited all his relatives and intimate friends to be present.
25 Petro akulowa mʼnyumba, Korneliyo anakumana naye ndipo anadzigwetsa pa mapazi ake namulambira.
When Peter entered the house, Cornelius met him, and threw himself at his feet to do him homage.
26 Koma Petro anamuyimiritsa nati, “Imirira, inenso ndine munthu ngati iwe.”
But Peter lifted him up. "Stand up," he said; "I myself also am but a man."
27 Akuyankhula naye, Petro analowa mʼnyumba ndipo anapeza gulu lalikulu la anthu litasonkhana.
So Peter went in and conversed with him, and found a large company assembled.
28 Iye anawawuza kuti, “Inu mukudziwa bwino kuti ndi kutsutsana ndi lamulo ngati Myuda ayanjana ndi Mkunja kapena kuyendera wina aliyense wa mtundu wina. Koma Mulungu wandionetsa ine kuti ndisatchule munthu aliyense kuti ndi wosayenera kapena wonyansa.
He said to them, "You know better than most that a Jew is strictly forbidden to associate with a Gentile or visit him; but God has taught me to call no one unholy or unclean.
29 Nʼchifukwa chake ndabwera mosawiringula pamene munandiyitana. Tsopano ndikufunseni,” Mwandiyitanira chiyani?
So for this reason, when sent for, I came without raising any objection. I therefore ask why you sent for me."
30 Komeliyo anayankha kuti, “Masiku anayi apitawo, nthawi yonga yomwe ino, 3 koloko masana ndimapemphera mʼnyumba mwanga. Mwadzidzidzi patsogolo panga panayimirira munthu wovala zovala zonyezimira.
"Just at this hour, three days ago," replied Cornelius, "I was offering afternoon prayer in my house, when suddenly a man in shining raiment stood in front of me,
31 Ndipo anati, ‘Korneliyo, Mulungu wamva mapemphero ako ndipo wakumbukira mphatso zako kwa osauka.
who said, "'Cornelius, your prayer has been heard, and your charities have been put on record before God.
32 Tuma anthu ku Yopa akayitane Simoni wotchedwa Petro. Iye akukhala mʼnyumba ya Simoni mmisiri wazikopa amene amakhala mʼmbali mwa nyanja.’
Send therefore to Jaffa, and invite Simon, surnamed Peter, to come here. He is staying as a guest in the house of Simon, a tanner, close to the sea.'
33 Nʼchifukwa chake ndinatumiza anthu nthawi yomweyo ndipo mwachita bwino kuti mwabwera. Tsopano ife tonse tili pano pamaso pa Mulungu kuti timve zonse zimene Ambuye akukulamulani kuti mutiwuze ife.”
"Immediately, therefore, I sent to you, and I thank you heartily for having come. That is why all of us are now assembled here in God's presence, to listen to what the Lord has commanded you to say."
34 Ndipo Petro anayamba kuyankhula nati, “Zoonadi, tsopano ndazindikira kuti Mulungu sakondera.
Then Peter began to speak. "I clearly see," he said, "that God makes no distinctions between one man and another;
35 Koma amalandira anthu a mtundu uli wonse amene amaopa Iye ndiponso kuchita chilungamo.
but that in every nation those who fear Him and live good lives are acceptable to Him.
36 Uwu ndi uthenga umene Mulungu anatumiza kwa Aisraeli, kulalikira Uthenga Wabwino wamtendere mwa Yesu Khristu amene ndi Ambuye wa onse.
The Message which He sent to the descendants of Israel, when He announced the Good News of peace through Jesus Christ--He is Lord of all--that Message you cannot but know;
37 Inu mukudziwa zimene zinachitika ku Yudeya konse, kuyambira ku Galileya pambuyo pa ubatizo umene Yohane analalikira,
the story, I mean, which has spread through the length and breadth of Judaea, beginning in Galilee after the baptism which John proclaimed.
38 kuti Mulungu, anamudzoza Yesu, wa ku Nazareti ndi Mzimu Woyera ndi mphamvu ndiponso mmene Iye anapita nachita zabwino ndi kuchiritsa onse amene anali pansi pa mphamvu ya mdierekezi, popeza kuti Mulungu anali naye.
It tells how God anointed Jesus of Nazareth with the Holy Spirit and with power, so that He went about everywhere doing acts of kindness, and curing all who were being continually oppressed by the Devil--for God was with Jesus.
39 “Ife ndife mboni za zonse zimene anachita mʼdziko la Ayuda ndiponso ku Yerusalemu. Anamupha Iye pakumupachika pa mtengo,
"And we are witnesses as to all that He did both in the country of the Jews and in Jerusalem. But they even put Him to death, by crucifixion.
40 koma Mulungu anamuukitsa kwa akufa pa tsiku lachitatu, ndipo analola kuti aonekere poyera.
That same Jesus God raised to life on the third day, and permitted Him to appear unmistakably,
41 Iye sanaonekere kwa anthu onse koma kwa mboni zimene Mulungu anazisankhiratu, kwa ife amene timadya ndi kumwa naye atauka kwa akufa.
not to all the people, but to witnesses--men previously chosen by God--namely, to us, who ate and drank with Him after He rose from the dead.
42 Iye anatilamulira ife kuti tilalikire kwa anthu ndi kuchitira umboni kuti Iye ndiye amene Mulungu anamusankha kukhala woweruza wa amoyo ndi akufa.
And He has commanded us to preach to the people and solemnly declare that this is He who has been appointed by God to be the Judge of the living and the dead.
43 Aneneri onse achitira Iye umboni kuti aliyense amene akhulupirira Iye amakhululukidwa machimo chifukwa cha dzina lake.”
To Him all the Prophets bear witness, and testify that through His name all who believe in Him receive the forgiveness of their sins."
44 Petro akuyankhulabe mawu amenewa, Mzimu Woyera unatsikira pa onse amene amamva uthengawo.
While Peter was speaking these words, the Holy Spirit fell on all who were listening to the Message.
45 Abale a mdulidwe omwe anabwera ndi Petro anadabwa kuona kuti mphatso ya Mzimu Woyera yapatsidwanso kwa anthu a mitundu ina.
And all the Jewish believers who had come with Peter were astonished that on the Gentiles also the gift of the Holy Spirit was poured out.
46 Pakuti anamva iwo akuyankhula mʼmalilime ndi kuyamika Mulungu. Ndipo Petro anati,
For they heard them speaking in tongues and extolling the majesty of God. Then Peter said,
47 “Kodi alipo amene angawaletse anthu awa kubatizidwa mʼmadzi? Iwotu alandira Mzimu Woyera monga ifenso.”
"Can any one forbid the use of water, and object to these persons being baptized--men who have received the Holy Spirit just as we did?"
48 Tsono iye analamula kuti abatizidwe mʼdzina la Yesu Khristu. Ndipo anthu aja anamupempha Petro kuti akhale nawo masiku angapo.
And he directed that they should be baptized in the name of Jesus Christ. Then they begged him to remain with them for a time.