< Machitidwe a Atumwi 1 >
1 Mʼbuku langa loyamba, ndinakulembera iwe Teofilo zonse zimene Yesu anayamba kuchita ndi kuphunzitsa,
U A hoonoho aku au, e Teopilo, i ka mooolelo mua, no namea a pau a Iesu i hoomaka'i e hana a e ao mai no hoi,
2 mpaka tsiku limene anatengedwa kupita kumwamba, mwamphamvu ya Mzimu Woyera, atawalangiza atumwi amene anawasankha.
A hiki i ka la i laweia'ku ai ia iluna, mahope o kana kauoha ana mai ma ka Uhane Hemolele i na lunaolelo ana i wae mai ai.
3 Zitatha zowawa zake Yesu anadzionetsa kwa ophunzira ake, ndi kuonetsanso maumboni ambiri kuti anali wamoyo. Iye anadzionetsera kwa iwo ndi kuwaphunzitsa za ufumu wa Mulungu pa masiku makumi anayi.
Hoike ola mai no oia ia ia iho ia lakou mahope o kona make ana, ma na hoailona hoike he nui loa, me ka ikeia e lakou i na la ho kanaha, a olelo mai no ia i na mea o ke aupuni o ke Akua:
4 Nthawi ina atasonkhana nawo pamodzi, Yesu analamulira ophunzira ake kuti, “Musachoke mu Yerusalemu, koma mudikire mphatso imene Atate anga analonjeza yomwe ndinakuwuzani.
A i kona halawai ana me lakou, kauoha mai la oia ia lakou, aole e haalele ia Ierusalema, aka, e kali i ka ka Makua olelo hoopomaikai, a oukou i lohe ai ia'u.
5 Pakuti Yohane anakubatizani ndi madzi, koma posachedwapa inu mudzabatizidwa ndi Mzimu Woyera.”
No ka mea, ua bapetizo io no o Ioane me ka wai; aka, e bapetizoia no hoi oukou i ka Uhane Hemolele, mahope iho o na la aohe nui.
6 Atumwi atasonkhana pamodzi, iwo anamufunsa Iye kuti, “Ambuye, kodi nthawi ino mubwezeretsa ufumu kwa Israeli?”
No ia mea, i ko lakou akoakoa ana, ninau aku la lakou ia ia, i aku la, E ka Haku, e hoihoi mai anei oe i ke aupuni no ka Iseraela i keia wa?
7 Yesu anawawuza kuti, “Sikofunika kuti mudziwe za nthawi kapena masiku amene Atate ayika mwa ulamuliro wawo.
I mai la oia ia lakou, Aole ia oukou ka ike i na wa, a me na kau a ka Makua i waiho ai i kona mana iho.
8 Koma mudzalandira mphamvu Mzimu Woyera akadzafika pa inu; ndipo mudzakhala mboni zanga mu Yerusalemu, ku Yudeya konse ndi ku Samariya, mpaka ku malekezero a dziko lapansi.”
Aka, e loaa no ia oukou ka mana, ke hiki mai ka Uhane Hemolele maluna iho o oukou; a e lilo auanei oukou i poe hoike no'u ma Ierusalema, a ma Iudea a pau, a ma Samaria, a hiki wale aku i ke kihi o ka honua.
9 Atatha kuyankhula zimenezi, Yesu anatengedwa kupita kumwamba ophunzira ake akuona, ndipo anabisika mʼmitambo.
A oki ae la kana olelo ana ia mau mea, e nana aku ana lakou, a laweia'ku la ia iluna; a na ke ao no ia i apo mai, mai ko lakou mau maka aku.
10 Yesu akukwera kumwamba, ophunzira ake anayangʼanitsitsa ndi chidwi mʼmitambo. Mwadzidzidzi anaona anthu awiri ovala zoyera atayimirira pambali pawo.
A i ko lakou haka pono ana aku i ka lani, i kona pii ana, aia hoi, ku kokoke mai la me lakou na kanaka elua, me ka aahu keokeo;
11 Iwo anati, “Inu, anthu a ku Galileya, chifukwa chiyani mukuyima ndi kumayangʼana mʼmitambo? Yesu amene wachotsedwa pakati panu ndi kupita kumwamba, adzabweranso mʼnjira yomweyi mwamuona akupita kumwamba.”
I mai la hoi laua, E na kanaka o Galilaia, no ke aha la oukou e ku nei e nana aku ana i ka lani? O Iesu nei, ka mea i laweia'ku nei i ka lani, mai o oukou aku nei, pela no ia e hoi hou mai ai e like me ka oukou ike ana aku ia ia e pii ana i ka lani.
12 Pamenepo atumwi anabwerera ku Yerusalemu kuchokera ku phiri la Olivi, mtunda wosakwana kilomita kuchokera mu mzindamo.
Alaila, hoi aku la lakou i Ierusalema, mai ka mauna aku i kapaia o Oliveta, ua kokoke no ia i Ierusalema, o ko ka la Sabati hele ana.
13 Atafika mu mzindamo, analowa mʼchipinda chammwamba kumene amakhala. Amene analipo anali awa: Petro, Yohane, Yakobo ndi Andreya; Filipo ndi Tomasi, Bartumeyu ndi Mateyu; Yakobo mwana wa Alifeyo ndi Simoni Zelote ndi Yuda mwana wa Yakobo.
A komo lakou iloko, pii aku la, a iloko o kekahi keena maluna, malaila lakou i noho ai, o Petero, a me Iakobo, a me Ioane, a me Anederea, a me Pilipo, a me Toma, a me Baretolomaio, a me Mataio, a me Iakobo a Alepaio, a me Simona Zelote, a me Inda ka hoahanau no Iakobo.
14 Onsewa ndi mtima umodzi anapitiriza kupemphera pamodzi ndi amayi, ndi Mariya amayi ake a Yesu, ndiponso abale ake a Yesu.
Hoomau iho la lakou nei a pau i ka pule ana, a me ka nonoi aku, me ka lokahi o ka manao, o na wahine hoi kekahi, a me Maria, ka makuwahine o Iesu, a me kona poe hoahanau.
15 Pa nthawi imeneyo Petro anayimirira pakati pa okhulupirira (gulu la anthu pafupifupi 120).
I ua mau la la, ku ae la o Petero iwaenakonu o na haumana, i mai la, (o ka nui o ko lakou inoa, hookahi haneri me ka iwakalua, )
16 Iye anati, “Abale anga, Malemba anayenera kukwaniritsidwa omwe Mzimu Woyera anayankhula kalekale kudzera mwa Davide za Yudasi, amene anatsogolera amene anamugwira Yesu.
E na kanaka, na hoahanau, he mea pono e hookoia keia palapala a ka Uhane Hemolele i hai mai ai ma ka waha o Davida no Iuda, ka mea nana i alakai i ka poe i hopu ia Iesu.
17 Iye anali mmodzi wa gulu lathu ndipo anatumikira pamodzi ndi ife.”
No ka mea, ua helu pu ia oia me kakou, a loaa no hoi ia ia kekahi o neia oihana.
18 (Yudasi anagula munda ndi ndalama zimene anazipeza pochita zoyipa zija; kumeneko, iye anagwa chamutu, naphulika pakati ndipo matumbo ake wonse anakhuthuka.
A kuai iho la ia i aina me ka uku no ka hewa; a haule iho la ia ilalo kona poo, nahae iho la iwaenakonu ona, a pahu aku la kona naau a pau iwaho.
19 Aliyense mu Yerusalemu anamva zimenezi, kotero anatcha mundawo mʼchiyankhulo chawo kuti Akeledama, kutanthauza, Munda wa Magazi).
A ikea iho la ia mea e ka poe a pau e noho ana ma Ierusalema; nolaila ua kapaia'ku la ia aina, ma ka lakou olelo, Akeledama, o ke ano keia, O ka aina koko.
20 Petro anati, “Pakuti kwalembedwa mʼbuku la Masalimo kuti, “Nyumba yake isanduke bwinja, ndipo pasakhale wogonamo. Ndiponso, “Wina atenge ntchito yake yautsogoleri.
No ka mea, ua palanalaia ma ka buke Halelu, E lilo kona hale i neoneo, aole loa kekahi e noho ilaila; a, E lawe hoi kekahi i kana oihana.
21 Chifukwa chake ndi kofunika kusankha mmodzi wa anthu amene akhala nafe nthawi yonse imene Ambuye Yesu ankayenda nafe,
Nolaila, o na kanaka i hele pu ai me kakou i na wa a pau loa a ka Haku, a Iesu i hele mai ai, a i hele aku ai iwaena o kakou,
22 kuyambira pa nthawi ya ubatizo wa Yohane mpaka nthawi imene Yesu anatengedwa pakati pathu. Pakuti mmodzi wa anthu awa ayenera kukhala mboni pamodzi ndi ife zakuuka kwake.”
Mai ka hoomaka ana o Ioane e bapetizo ai, a hiki mai i ka la i laweia'ku ai ia mai o kakou aku, he mea pono e lilo kekahi o lakou i mea hoike pu me kakou i kona alahou ana mai.
23 Pamenepo anasankha anthu awiri, Yosefe wotchedwa Barsaba (wodziwikanso kuti Yusto) ndi Matiyasi.
Wae aku la lakou i elua, o Iosepa i kapaia o Baresaba, o Iouseto kekahi inoa ona, a me Matia hoi.
24 Kenaka iwo anapemphera nati, “Ambuye mukudziwa mtima wa aliyense. Tionetseni amene mwamusankha mwa awiri awa
Pule aku la lakou, i aku la, E ka Haku, ka mea ike i ka naau o na mea a pau loa, e hoike mai oe i ka mea o laua nei au e koho mai ai,
25 kuti atenge ntchito iyi ya utumwi, imene Yudasi anasiya napita kumalo womuyenera.”
I lawe pu ia i kekahi o keia oihana, a me ko ka lunaolelo, mai ia wahi mai ko Iuda haule ana, i hele aku ia i kona wahi iho.
26 Tsono anachita maere, ndipo maerewo anagwera Matiyasi. Tsono iye anawonjezedwa pa gulu la atumwi khumi ndi mmodziwo.
Hailona iho la lakou, a lilo ka hailona ia Matia; a helu pu ia iho la ia me na lunaolelo he umikumamakahi.