< Machitidwe a Atumwi 1 >

1 Mʼbuku langa loyamba, ndinakulembera iwe Teofilo zonse zimene Yesu anayamba kuchita ndi kuphunzitsa,
The former treatise, O Theophilus, I made concerning all that Jesus undertook both to do and to teach;
2 mpaka tsiku limene anatengedwa kupita kumwamba, mwamphamvu ya Mzimu Woyera, atawalangiza atumwi amene anawasankha.
till the day in which He was taken up, after He had by the holy Spirit given instructions to the apostles whom He had chosen:
3 Zitatha zowawa zake Yesu anadzionetsa kwa ophunzira ake, ndi kuonetsanso maumboni ambiri kuti anali wamoyo. Iye anadzionetsera kwa iwo ndi kuwaphunzitsa za ufumu wa Mulungu pa masiku makumi anayi.
to whom also He presented Himself alive, after He had suffered, by many certain proofs; being seen among them for forty days, and speaking of the things relating to the kingdom of God.
4 Nthawi ina atasonkhana nawo pamodzi, Yesu analamulira ophunzira ake kuti, “Musachoke mu Yerusalemu, koma mudikire mphatso imene Atate anga analonjeza yomwe ndinakuwuzani.
And meeting them together He commanded them not to depart from Jerusalem, but to wait for the promise of the Father, which, said He, ye have heard from me;
5 Pakuti Yohane anakubatizani ndi madzi, koma posachedwapa inu mudzabatizidwa ndi Mzimu Woyera.”
for John indeed baptized with water, but ye shall within a few days be baptized with the holy Spirit.
6 Atumwi atasonkhana pamodzi, iwo anamufunsa Iye kuti, “Ambuye, kodi nthawi ino mubwezeretsa ufumu kwa Israeli?”
Being therefore come together they asked Him, saying, Lord, wilt thou at this time restore the kingdom to Israel?
7 Yesu anawawuza kuti, “Sikofunika kuti mudziwe za nthawi kapena masiku amene Atate ayika mwa ulamuliro wawo.
And He said unto them, It is not for you to know the times or seasons, which the Father hath reserved in his own power.
8 Koma mudzalandira mphamvu Mzimu Woyera akadzafika pa inu; ndipo mudzakhala mboni zanga mu Yerusalemu, ku Yudeya konse ndi ku Samariya, mpaka ku malekezero a dziko lapansi.”
But ye shall receive power from the holy Spirit coming upon you: and ye shall be my witnesses both in Jerusalem, and in all Judea, and Samaria, and to the uttermost part of the earth.
9 Atatha kuyankhula zimenezi, Yesu anatengedwa kupita kumwamba ophunzira ake akuona, ndipo anabisika mʼmitambo.
And having said these things, as they were looking upon Him, He was lifted up, and a cloud received Him out of their sight.
10 Yesu akukwera kumwamba, ophunzira ake anayangʼanitsitsa ndi chidwi mʼmitambo. Mwadzidzidzi anaona anthu awiri ovala zoyera atayimirira pambali pawo.
And while they were looking stedfastly toward heaven, as He went up, behold two men in white stood by them;
11 Iwo anati, “Inu, anthu a ku Galileya, chifukwa chiyani mukuyima ndi kumayangʼana mʼmitambo? Yesu amene wachotsedwa pakati panu ndi kupita kumwamba, adzabweranso mʼnjira yomweyi mwamuona akupita kumwamba.”
who said, Ye men of Galilee, why do ye stand gazing up to heaven? This Jesus who is taken up from you into heaven, shall so come in the manner ye have seen Him going into heaven.
12 Pamenepo atumwi anabwerera ku Yerusalemu kuchokera ku phiri la Olivi, mtunda wosakwana kilomita kuchokera mu mzindamo.
Then they returned to Jerusalem from the mountain called Olivet, which is from Jerusalem a sabbath-day's journey.
13 Atafika mu mzindamo, analowa mʼchipinda chammwamba kumene amakhala. Amene analipo anali awa: Petro, Yohane, Yakobo ndi Andreya; Filipo ndi Tomasi, Bartumeyu ndi Mateyu; Yakobo mwana wa Alifeyo ndi Simoni Zelote ndi Yuda mwana wa Yakobo.
And when they were come in to the city, they went up into an upper room, where Peter, and James, and John, and Andrew, Philip and Thomas, Bartholomew, and Matthew, James the son of Alpheus, and Simon the zealot, and Jude the brother of James, usually abode.
14 Onsewa ndi mtima umodzi anapitiriza kupemphera pamodzi ndi amayi, ndi Mariya amayi ake a Yesu, ndiponso abale ake a Yesu.
These all persevered with one accord in prayer and supplication with the women, and Mary the mother of Jesus, and his brethren.
15 Pa nthawi imeneyo Petro anayimirira pakati pa okhulupirira (gulu la anthu pafupifupi 120).
And in these days Peter stood up in the midst of the disciples, (now the number of the persons that were together was about an hundred and twenty, )
16 Iye anati, “Abale anga, Malemba anayenera kukwaniritsidwa omwe Mzimu Woyera anayankhula kalekale kudzera mwa Davide za Yudasi, amene anatsogolera amene anamugwira Yesu.
and said, Men and brethren, it was necessary that this scripture should be fulfilled, which the holy Ghost spake by the mouth of David, concerning Judas, who was guide to them that apprehended Jesus:
17 Iye anali mmodzi wa gulu lathu ndipo anatumikira pamodzi ndi ife.”
for he was numbered with us, and had obtained a part of this ministry.
18 (Yudasi anagula munda ndi ndalama zimene anazipeza pochita zoyipa zija; kumeneko, iye anagwa chamutu, naphulika pakati ndipo matumbo ake wonse anakhuthuka.
(Now this man purchased a field with the reward of iniquity; and falling down on his face, burst asunder in the middle, and all his bowels gushed out:
19 Aliyense mu Yerusalemu anamva zimenezi, kotero anatcha mundawo mʼchiyankhulo chawo kuti Akeledama, kutanthauza, Munda wa Magazi).
(and it was known to all the inhabitants of Jerusalem, so that the field is called in their own dialect, Aceldama, that is, the field of blood: )
20 Petro anati, “Pakuti kwalembedwa mʼbuku la Masalimo kuti, “Nyumba yake isanduke bwinja, ndipo pasakhale wogonamo. Ndiponso, “Wina atenge ntchito yake yautsogoleri.
for it is written in the book of Psalms, Let his habitation be desolate, and let none dwell in it; and again, Let another take his office.)
21 Chifukwa chake ndi kofunika kusankha mmodzi wa anthu amene akhala nafe nthawi yonse imene Ambuye Yesu ankayenda nafe,
Wherefore it is necessary that one of these men, who have been conversant with us all the time that the Lord Jesus came in and out among us,
22 kuyambira pa nthawi ya ubatizo wa Yohane mpaka nthawi imene Yesu anatengedwa pakati pathu. Pakuti mmodzi wa anthu awa ayenera kukhala mboni pamodzi ndi ife zakuuka kwake.”
from the baptism of John, till the day that He was taken up from us, should be joined with us as a witness of his resurrection.
23 Pamenepo anasankha anthu awiri, Yosefe wotchedwa Barsaba (wodziwikanso kuti Yusto) ndi Matiyasi.
And they proposed two, Joseph called Barsabas, who was surnamed Justus, and Matthias.
24 Kenaka iwo anapemphera nati, “Ambuye mukudziwa mtima wa aliyense. Tionetseni amene mwamusankha mwa awiri awa
And they prayed and said, Thou, Lord, who knowest the hearts of all, shew us, which of these two Thou hast chosen,
25 kuti atenge ntchito iyi ya utumwi, imene Yudasi anasiya napita kumalo womuyenera.”
to take part of this ministry and apostleship, from which Judas is fallen by his transgression, that he might go to his own place.
26 Tsono anachita maere, ndipo maerewo anagwera Matiyasi. Tsono iye anawonjezedwa pa gulu la atumwi khumi ndi mmodziwo.
And they gave out their lots, and the lot fell upon Matthias, and he was numbered with the apostles.

< Machitidwe a Atumwi 1 >