< Machitidwe a Atumwi 1 >
1 Mʼbuku langa loyamba, ndinakulembera iwe Teofilo zonse zimene Yesu anayamba kuchita ndi kuphunzitsa,
Theophilus, ka lekhabu masa-a kahin sei chu, Yeshua thilbolle thuhil kipattil thudol jouse le
2 mpaka tsiku limene anatengedwa kupita kumwamba, mwamphamvu ya Mzimu Woyera, atawalangiza atumwi amene anawasankha.
Lhagao thenga kona alhendoh solchah ho thu apeh jouva pat ama van'a lahtouva aum ni gei thu ahi.
3 Zitatha zowawa zake Yesu anadzionetsa kwa ophunzira ake, ndi kuonetsanso maumboni ambiri kuti anali wamoyo. Iye anadzionetsera kwa iwo ndi kuwaphunzitsa za ufumu wa Mulungu pa masiku makumi anayi.
Chuche thingpel chunga athia athodoh jou ni somli sung chun, ama solchah ho henga akilah jin, chule ama ahing monge ti chu photchetna tamtah avetsah jin, chuleh Pathen lenggam thudol aseiyin ahi.
4 Nthawi ina atasonkhana nawo pamodzi, Yesu analamulira ophunzira ake kuti, “Musachoke mu Yerusalemu, koma mudikire mphatso imene Atate anga analonjeza yomwe ndinakuwuzani.
Chuin solchah ho toh anehkhom laiyin, aman amaho chu thu apen, “Kana seipeh bangun Pan akitepna thilpeh ahinsol masangsen nanghon Jerusalem dalhah hih un.
5 Pakuti Yohane anakubatizani ndi madzi, koma posachedwapa inu mudzabatizidwa ndi Mzimu Woyera.”
John in twiya baptize nachansah'u ahin, ahin tuapat nikho phabep joule nangho Lhagao Thenga baptize nachan ding'u ahi.” ati.
6 Atumwi atasonkhana pamodzi, iwo anamufunsa Iye kuti, “Ambuye, kodi nthawi ino mubwezeretsa ufumu kwa Israeli?”
Hichun solchah ho chu Yeshua toh aumkhom pet un, amahon adongun, “Pakai, Israelte chamlhat nading leh a lenggam nakiledohsah kit nading phat chu hitam?” atiuvin ahi.
7 Yesu anawawuza kuti, “Sikofunika kuti mudziwe za nthawi kapena masiku amene Atate ayika mwa ulamuliro wawo.
Aman adonbut in, “Anikho leh aphat chu Pa changseh thaneina-a um ahin, nangho hetding dol ahipoi.
8 Koma mudzalandira mphamvu Mzimu Woyera akadzafika pa inu; ndipo mudzakhala mboni zanga mu Yerusalemu, ku Yudeya konse ndi ku Samariya, mpaka ku malekezero a dziko lapansi.”
Ahinlah Lhagao Theng nachung uva ahung chuh teng leh nanghon thahatna nanei ding'u ahi. Chutengleh nangho Jerusalema, Judea gam'a, Samaria gam, leh leiset chung pumpia kathu hettoh sah'a napan ding'u ahi,” ati.
9 Atatha kuyankhula zimenezi, Yesu anatengedwa kupita kumwamba ophunzira ake akuona, ndipo anabisika mʼmitambo.
Thu hicheng chu asei jouvin, amahon avet jinglaiyun ama chu meiloma lahtouvin aumin ahileh amahon amupha tapouvin ahi.
10 Yesu akukwera kumwamba, ophunzira ake anayangʼanitsitsa ndi chidwi mʼmitambo. Mwadzidzidzi anaona anthu awiri ovala zoyera atayimirira pambali pawo.
Chutia amahon van lam'a lahtouva aumpet avet jinglaiyun pon-banga kivon mi ni alah'uvah ahung ding lhonin,
11 Iwo anati, “Inu, anthu a ku Galileya, chifukwa chiyani mukuyima ndi kumayangʼana mʼmitambo? Yesu amene wachotsedwa pakati panu ndi kupita kumwamba, adzabweranso mʼnjira yomweyi mwamuona akupita kumwamba.”
“Galilee mite, ibola nadinuva vanlam navet jingu ham? Yeshua nangho koma kona vana lahtouva aum banga hi nikhatle vanna kona hung kile kitding ahi!” atilhone.
12 Pamenepo atumwi anabwerera ku Yerusalemu kuchokera ku phiri la Olivi, mtunda wosakwana kilomita kuchokera mu mzindamo.
Chuin solchah hochu Jerusalema kona mile keh'a gamla Olive mola kon chun Jerusalem'ah ahung kile tauvin ahi.
13 Atafika mu mzindamo, analowa mʼchipinda chammwamba kumene amakhala. Amene analipo anali awa: Petro, Yohane, Yakobo ndi Andreya; Filipo ndi Tomasi, Bartumeyu ndi Mateyu; Yakobo mwana wa Alifeyo ndi Simoni Zelote ndi Yuda mwana wa Yakobo.
Jerusalem ahung lhunun aumnau inchung langah akaltouvun ahi. Amaho chu: Peter, John, Jacob, Andrew, Philip, Thomas, Bartholomew, Matthew, Jacob (Alphaeus chapa), Simon (Zealot), chule Judas (Jacob chapa), ahiuve.
14 Onsewa ndi mtima umodzi anapitiriza kupemphera pamodzi ndi amayi, ndi Mariya amayi ake a Yesu, ndiponso abale ake a Yesu.
Amaho chengse hi Yeshua nu Mary leh numei dang phabeptoh, Yeshua sopite phabeptoh akipunkhomun gunchu leh lungkhat tahin atao jom jing tauve.
15 Pa nthawi imeneyo Petro anayimirira pakati pa okhulupirira (gulu la anthu pafupifupi 120).
Yeshua tahsan mipi jakhat le somni akikhop khom laitah uvin Peter adingdoh in,
16 Iye anati, “Abale anga, Malemba anayenera kukwaniritsidwa omwe Mzimu Woyera anayankhula kalekale kudzera mwa Davide za Yudasi, amene anatsogolera amene anamugwira Yesu.
“Sopite ho, Yeshua manho lamkaiya pang Judas thudol hi, kumsottah masanga Lhagao Thengin Leng David kam'a anaphondohsa Pathen lekhabua thu chu guilhungah ahi.
17 Iye anali mmodzi wa gulu lathu ndipo anatumikira pamodzi ndi ife.”
Ijeh-inem itileh Judas chu eiho lah'a khat ahin, hiche lhacha hina jonghi changah ahi,” ati.
18 (Yudasi anagula munda ndi ndalama zimene anazipeza pochita zoyipa zija; kumeneko, iye anagwa chamutu, naphulika pakati ndipo matumbo ake wonse anakhuthuka.
(Aman khan gitlou man sumin gambeh khat achon, akhupboh in achun atumpi apohkeh-in agil jouse ahung dohtan ahi.
19 Aliyense mu Yerusalemu anamva zimenezi, kotero anatcha mundawo mʼchiyankhulo chawo kuti Akeledama, kutanthauza, Munda wa Magazi).
Judas thi thuhi Jerusalem mite jouse koma ahung kithangsoh tan ahileh amahon hiche gambeh chu Aramaic paovin Akeldama asah tauvin, hichu Thisan gambeh tina ahi.)
20 Petro anati, “Pakuti kwalembedwa mʼbuku la Masalimo kuti, “Nyumba yake isanduke bwinja, ndipo pasakhale wogonamo. Ndiponso, “Wina atenge ntchito yake yautsogoleri.
Peter in asei jom kit in, “Psalm lekhabua kimu bang in ‘Ama In chu onghen, koima cheng hihhen, chuleh ama panmun chu midangkhat changhen,’ ati.
21 Chifukwa chake ndi kofunika kusankha mmodzi wa anthu amene akhala nafe nthawi yonse imene Ambuye Yesu ankayenda nafe,
Hijeh a chu Judas panmun khel ding mikhat ilhen ding'u ahin amachu Pakai Yeshua toh iumkhomlai uva pat'a eiholah a umjing khat hiding.
22 kuyambira pa nthawi ya ubatizo wa Yohane mpaka nthawi imene Yesu anatengedwa pakati pathu. Pakuti mmodzi wa anthu awa ayenera kukhala mboni pamodzi ndi ife zakuuka kwake.”
John'in baptize achansah jouva pat eiholah'a kona Yeshua lahtouva aumni geiya eiholah a lhajing hiding, amachu Yeshua thodoh thudol hettohsah dinga eiholah'a pang ding ahi,” ati.
23 Pamenepo anasankha anthu awiri, Yosefe wotchedwa Barsaba (wodziwikanso kuti Yusto) ndi Matiyasi.
Chuin mi ni: Barsabbas kiti Joseph (Justus tiajong kihe) le Matthias chu alhengdoh-un,
24 Kenaka iwo anapemphera nati, “Ambuye mukudziwa mtima wa aliyense. Tionetseni amene mwamusankha mwa awiri awa
Amaho ataovun, “Vo Pakai, nangma mijouse lungthim hesoh nahi,
25 kuti atenge ntchito iyi ya utumwi, imene Yudasi anasiya napita kumalo womuyenera.”
Hiche teni hi koijoh in Judas khel'a solchah na atoh dingham neihetsah uvin, ajeh chu Judas chun hiche solchah natoh hi alhatan ahi.”
26 Tsono anachita maere, ndipo maerewo anagwera Matiyasi. Tsono iye anawonjezedwa pa gulu la atumwi khumi ndi mmodziwo.
Chuin amahon vang asangun ahileh Matthias chu solchah somlekhat holah a akisimtha tan ahi.