< 3 Yohane 1 >

1 Ndine mkulu wampingo, kulembera: Gayo mnzanga wokondedwa, amene ndimamukonda mʼchoonadi.
Umdala, kuye uGayusi othandekayo, mina engimthanda ngeqiniso.
2 Wokondedwa, ndimakupempherera kuti zako zonse zikuyendere bwino, ndikuti ukhale bwino mʼthupi mwako, monga momwe ulili moyo wako wauzimu.
Sithandwa, kuzo zonke izinto ngifisa ukuthi uphumelele njalo uphile, njengalokhu umphefumulo wakho uphumelela.
3 Ine ndinali ndi chimwemwe chachikulu pamene abale ena anafika nʼkundifotokozera za kukhulupirika kwako pa choonadi ndiponso mmene umayendera motsata choonadi.
Ngoba ngathokoza kakhulukazi, lapho kufika abazalwane, befakazela iqiniso lakho, njengoba wena uhamba eqinisweni.
4 Palibe chondikondweretsa kwambiri kuposa kumva kuti ana anga akukhala mʼchoonadi.
Kangilantokozo enkulu edlula lezizinto, ukuthi ngizwe ukuthi abantwana bami bahamba eqinisweni.
5 Wokondedwa, ndiwe wokhulupirika pa zimene ukuchitira abale, ngakhale kuti iwowo ndi alendo.
Sithandwa, wenza ngokuthembeka loba yikuphi okwenza kubazalwane lakwabemzini,
6 Iwo anafotokozera mpingo za chikondi chako. Chonde uwathandize kupitiriza ulendo mʼnjira yokondweretsa Mulungu.
abafakazele uthando lwakho phambi kwebandla; uzakwenza kuhle uba ubaphelekezela ngokufanele uNkulunkulu.
7 Pakuti ananyamuka ulendo wawo chifukwa cha dzina la Ambuye, osalandira thandizo kwa osakhulupirira.
Ngoba ngenxa yebizo lakhe baphumile bengemukeli lutho kwabezizwe.
8 Ife tiyenera kumathandiza anthu oterewa, kuti tigwirizane nawo pa ntchito ya choonadi.
Ngakho thina sifanele ukubemukela abanjalo, ukuze sibe yizisebenzi kanye leqiniso.
9 Ndinalembera mpingo, koma Diotrefe, amene amafuna kukhala wotsogolera, sanafune kutimvera.
Ngabhalela ibandla; kodwa uDiyotrefe othanda ukuba ngowokuqala kubo kasemukeli.
10 Tsono ndikabwera ndidzakumbutsa zimene iye amachita. Iye amafalitsa nkhani zabodza zonena ife. Ndipo sakhutira ndi zimenezo, komanso iyeyo amakana kulandira abale. Komanso amaletsa amene akufuna kutero, ndipo amawachotsa mu mpingo.
Ngakho, uba ngifika, ngizakhumbuza imisebenzi yakhe ayenzayo, uyasihleba ngamazwi amabi; futhi kakholiswa yilezizinto, yena uqobo kemukeli abazalwane, uyabalela lalabo abathanda ukukwenza, njalo uyabaxotsha ebandleni.
11 Wokondedwa, usatsatire zinthu zoyipa koma zinthu zabwino. Aliyense amene amachita zinthu zabwino ndi wochokera kwa Mulungu. Aliyense amene amachita zoyipa sanamuonepo Mulungu.
Sithandwa, ungakulingiseli okubi, kodwa okuhle. Owenza okuhle ungokaNkulunkulu; kodwa owenza okubi kambonanga uNkulunkulu.
12 Aliyense akumuchitira umboni wabwino wa Demetriyo. Ngakhale choona chomwe chimamuchitira umboni, ndipo iweyo ukudziwa kuti umboni wathu ndi woona.
NgoDemetriyu kufakazwe yibo bonke, langeqiniso uqobo; lathi futhi siyafakaza, lani liyazi ukuthi ubufakazi bethu buqinisile.
13 Ndili ndi zambiri zoti ndikulembereni, koma sindikufuna kuzilemba mʼkalata.
Bengilezinto ezinengi zokubhala, kodwa kangithandi ukukubhalela ngeyinki losiba;
14 Ndiyembekezera kufika kwanuko posachedwapa, ndipo tidzakambirana pamaso ndi pamaso. Mtendere ukhale nawe. Abwenzi anu kuno akupereka moni. Upereke moni kwa abwenzi onse mmodzimmodzi.
kodwa ngithemba ukukubona masinyane, sibe sesikhuluma umlomo ngomlomo. Ukuthula kakube kuwe. Abangane bayakubingelela. Bingelela abangane ngamabizo.

< 3 Yohane 1 >