< 3 Yohane 1 >

1 Ndine mkulu wampingo, kulembera: Gayo mnzanga wokondedwa, amene ndimamukonda mʼchoonadi.
L'aîné à Gaius, le bien-aimé, que j'aime en vérité.
2 Wokondedwa, ndimakupempherera kuti zako zonse zikuyendere bwino, ndikuti ukhale bwino mʼthupi mwako, monga momwe ulili moyo wako wauzimu.
Bien-aimés, je prie pour que vous prospériez en toutes choses et que vous soyez en bonne santé, comme votre âme prospère.
3 Ine ndinali ndi chimwemwe chachikulu pamene abale ena anafika nʼkundifotokozera za kukhulupirika kwako pa choonadi ndiponso mmene umayendera motsata choonadi.
Car j'ai éprouvé une grande joie lorsque des frères sont venus et ont témoigné de ta vérité, comme toi tu marches dans la vérité.
4 Palibe chondikondweretsa kwambiri kuposa kumva kuti ana anga akukhala mʼchoonadi.
Je n'ai pas de plus grande joie que celle-là: entendre parler de mes enfants qui marchent dans la vérité.
5 Wokondedwa, ndiwe wokhulupirika pa zimene ukuchitira abale, ngakhale kuti iwowo ndi alendo.
Bien-aimés, vous faites une œuvre fidèle dans tout ce que vous accomplissez pour ceux qui sont frères et étrangers.
6 Iwo anafotokozera mpingo za chikondi chako. Chonde uwathandize kupitiriza ulendo mʼnjira yokondweretsa Mulungu.
Ils ont témoigné de ton amour devant l'assemblée. Vous ferez bien de les envoyer en voyage d'une manière digne de Dieu,
7 Pakuti ananyamuka ulendo wawo chifukwa cha dzina la Ambuye, osalandira thandizo kwa osakhulupirira.
car c'est à cause du Nom qu'ils sont sortis, sans rien prendre des païens.
8 Ife tiyenera kumathandiza anthu oterewa, kuti tigwirizane nawo pa ntchito ya choonadi.
Nous devons donc les accueillir, afin d'être des compagnons de travail pour la vérité.
9 Ndinalembera mpingo, koma Diotrefe, amene amafuna kukhala wotsogolera, sanafune kutimvera.
J'ai écrit à l'assemblée, mais Diotrèphe, qui aime à être le premier parmi eux, n'accepte pas ce que nous disons.
10 Tsono ndikabwera ndidzakumbutsa zimene iye amachita. Iye amafalitsa nkhani zabodza zonena ife. Ndipo sakhutira ndi zimenezo, komanso iyeyo amakana kulandira abale. Komanso amaletsa amene akufuna kutero, ndipo amawachotsa mu mpingo.
C'est pourquoi, si je viens, j'appellerai l'attention sur les actes qu'il commet, en nous accusant injustement par des paroles méchantes. Non content de cela, il ne reçoit pas lui-même les frères, et ceux qui le veulent, il les interdit et les chasse de l'assemblée.
11 Wokondedwa, usatsatire zinthu zoyipa koma zinthu zabwino. Aliyense amene amachita zinthu zabwino ndi wochokera kwa Mulungu. Aliyense amene amachita zoyipa sanamuonepo Mulungu.
Bien-aimés, n'imitez pas ce qui est mauvais, mais ce qui est bon. Celui qui fait le bien est de Dieu. Celui qui fait le mal n'a pas vu Dieu.
12 Aliyense akumuchitira umboni wabwino wa Demetriyo. Ngakhale choona chomwe chimamuchitira umboni, ndipo iweyo ukudziwa kuti umboni wathu ndi woona.
Démétrius a le témoignage de tous, et de la vérité elle-même; oui, nous aussi nous témoignons, et vous savez que notre témoignage est vrai.
13 Ndili ndi zambiri zoti ndikulembereni, koma sindikufuna kuzilemba mʼkalata.
J'avais beaucoup de choses à vous écrire, mais je ne veux pas vous écrire avec de l'encre et une plume;
14 Ndiyembekezera kufika kwanuko posachedwapa, ndipo tidzakambirana pamaso ndi pamaso. Mtendere ukhale nawe. Abwenzi anu kuno akupereka moni. Upereke moni kwa abwenzi onse mmodzimmodzi.
mais j'espère vous voir bientôt. Nous nous parlerons alors face à face. Que la paix soit avec vous. Les amis vous saluent. Saluez les amis par leur nom.

< 3 Yohane 1 >