< 3 Yohane 1 >

1 Ndine mkulu wampingo, kulembera: Gayo mnzanga wokondedwa, amene ndimamukonda mʼchoonadi.
Den Ældste til Kajus, den elskede, hvem jeg elsker i Sandhed.
2 Wokondedwa, ndimakupempherera kuti zako zonse zikuyendere bwino, ndikuti ukhale bwino mʼthupi mwako, monga momwe ulili moyo wako wauzimu.
Du elskede! jeg ønsker, at det i alle Ting må gå dig vel, og du må være karsk, ligesom det går din Sjæl vel.
3 Ine ndinali ndi chimwemwe chachikulu pamene abale ena anafika nʼkundifotokozera za kukhulupirika kwako pa choonadi ndiponso mmene umayendera motsata choonadi.
Thi jeg blev meget glad, da der kom Brødre og vidnede om Sandheden i dig, hvorledes du vandrer i Sandheden.
4 Palibe chondikondweretsa kwambiri kuposa kumva kuti ana anga akukhala mʼchoonadi.
Jeg har ingen større Glæde end denne, at jeg hører, at mine Børn vandre i Sandheden.
5 Wokondedwa, ndiwe wokhulupirika pa zimene ukuchitira abale, ngakhale kuti iwowo ndi alendo.
Du elskede! en trofast Gerning gør du i alt, hvad du virker for Brødrene, og det for femmede,
6 Iwo anafotokozera mpingo za chikondi chako. Chonde uwathandize kupitiriza ulendo mʼnjira yokondweretsa Mulungu.
hvilke have vidnet for Menigheden om din Kærlighed; og du vil gøre vel i at fremme deres Rejse således, som det er Gud værdigt.
7 Pakuti ananyamuka ulendo wawo chifukwa cha dzina la Ambuye, osalandira thandizo kwa osakhulupirira.
Thi for Navnets Skyld ere de dragne ud, uden at tage noget at Hedningerne.
8 Ife tiyenera kumathandiza anthu oterewa, kuti tigwirizane nawo pa ntchito ya choonadi.
Derfor ere vi skyldige at tage os af sådanne, for at vi kunne blive Medarbejdere for Sandheden.
9 Ndinalembera mpingo, koma Diotrefe, amene amafuna kukhala wotsogolera, sanafune kutimvera.
Jeg har skrevet noget til Menigheden; men Diotrefes, som gerne vil være den ypperste iblandt dem, anerkender os ikke.
10 Tsono ndikabwera ndidzakumbutsa zimene iye amachita. Iye amafalitsa nkhani zabodza zonena ife. Ndipo sakhutira ndi zimenezo, komanso iyeyo amakana kulandira abale. Komanso amaletsa amene akufuna kutero, ndipo amawachotsa mu mpingo.
Derfor vil jeg, når jeg kommer erindre om de Gerninger, han gør, idet han bagvasker os med onde Ord; og ikke tilfreds dermed, tager han både selv ikke Brødrene for gode, og dem, som ville det, forhindrer han deri og udstøder dem af Menigheden.
11 Wokondedwa, usatsatire zinthu zoyipa koma zinthu zabwino. Aliyense amene amachita zinthu zabwino ndi wochokera kwa Mulungu. Aliyense amene amachita zoyipa sanamuonepo Mulungu.
Du elskede! efterfølg ikke det onde, men det gode. Den, som gør godt, er af Gud; den, som gør ondt, har ikke set Gud.
12 Aliyense akumuchitira umboni wabwino wa Demetriyo. Ngakhale choona chomwe chimamuchitira umboni, ndipo iweyo ukudziwa kuti umboni wathu ndi woona.
Demetrius har et godt Vidnesbyrd af alle og af Sandheden selv; også vi vidne, og du ved, at vort Vidnesbyrd er sandt.
13 Ndili ndi zambiri zoti ndikulembereni, koma sindikufuna kuzilemba mʼkalata.
Jeg havde meget at skrive til dig, men jeg vil ikke skrive til dig med Blæk og Pen.
14 Ndiyembekezera kufika kwanuko posachedwapa, ndipo tidzakambirana pamaso ndi pamaso. Mtendere ukhale nawe. Abwenzi anu kuno akupereka moni. Upereke moni kwa abwenzi onse mmodzimmodzi.
Men jeg håber snart at se dig, og da skulle vi mundtligt tale sammen. Fred være med dig! Vennerne hilse dig. Hils Vennerne, hver især!

< 3 Yohane 1 >