< 2 Timoteyo 1 >
1 Paulo mtumwi wa Khristu Yesu mwa chifuniro cha Mulungu. Anandituma kuti ndilalike za lonjezo la moyo umene uli mwa Khristu Yesu.
παυλοσ αποστολοσ ιησου χριστου δια θεληματοσ θεου κατ επαγγελιαν ζωησ τησ εν χριστω ιησου
2 Kwa Timoteyo, mwana wanga wokondedwa: Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi Ambuye athu Yesu Khristu.
τιμοθεω αγαπητω τεκνω χαρισ ελεοσ ειρηνη απο θεου πατροσ και χριστου ιησου του κυριου ημων
3 Ndikuyamika Mulungu amene ndimamutumikira ndi chikumbumtima chosatsutsika, monga momwe ankachitira makolo anga. Usiku ndi usana ndimakukumbukira mosalekeza mʼmapemphero anga.
χαριν εχω τω θεω ω λατρευω απο προγονων εν καθαρα συνειδησει ωσ αδιαλειπτον εχω την περι σου μνειαν εν ταισ δεησεσιν μου νυκτοσ και ημερασ
4 Ndikamakumbukira misozi yako, ndimalakalaka nditakuona kuti ndidzazidwe ndi chimwemwe.
επιποθων σε ιδειν μεμνημενοσ σου των δακρυων ινα χαρασ πληρωθω
5 Ndakumbukira za chikhulupiriro chako choona chimene chinayamba mwa agogo ako a Loisi ndi mwa amayi ako Yunike ndipo ndikutsimikiza mtima kuti chilinso mwa iwe.
υπομνησιν λαμβανων τησ εν σοι ανυποκριτου πιστεωσ ητισ ενωκησεν πρωτον εν τη μαμμη σου λωιδι και τη μητρι σου ευνικη πεπεισμαι δε οτι και εν σοι
6 Nʼchifukwa chake ndikukukumbutsa kuti upemerere monga amachitira moto, mphatso imene Mulungu anakupatsa nditakusanjika manja.
δι ην αιτιαν αναμιμνησκω σε αναζωπυρειν το χαρισμα του θεου ο εστιν εν σοι δια τησ επιθεσεωσ των χειρων μου
7 Pakuti Mzimu amene Mulungu anatipatsa, si Mzimu wotipatsa manyazi, koma Mzimu wotipatsa mphamvu, chikondi ndi kudzisunga.
ου γαρ εδωκεν ημιν ο θεοσ πνευμα δειλιασ αλλα δυναμεωσ και αγαπησ και σωφρονισμου
8 Choncho usachite manyazi kuchitira umboni Ambuye athu, kapena kuchita manyazi chifukwa cha ine wamʼndende. Koma umve nane zowawa chifukwa cha Uthenga Wabwino, mothandizidwa ndi mphamvu za Mulungu.
μη ουν επαισχυνθησ το μαρτυριον του κυριου ημων μηδε εμε τον δεσμιον αυτου αλλα συγκακοπαθησον τω ευαγγελιω κατα δυναμιν θεου
9 Iye anatipulumutsa ndipo anatiyitanira ku moyo oyera mtima, osati chifukwa cha chilichonse chimene tinachita, koma chifukwa cha chikonzero ndi chisomo chake. Chisomo chimenechi anatipatsa ife mwa Khristu Yesu nthawi isanayambe. (aiōnios )
του σωσαντοσ ημασ και καλεσαντοσ κλησει αγια ου κατα τα εργα ημων αλλα κατ ιδιαν προθεσιν και χαριν την δοθεισαν ημιν εν χριστω ιησου προ χρονων αιωνιων (aiōnios )
10 Koma tsopano Mulungu watiwululira kudzera mʼkuoneka kwa Mpulumutsi wathu, Khristu Yesu, amene anathetsa mphamvu za imfa ndipo mwa Uthenga Wabwino anaonetsa poyera moyo umene sungafe.
φανερωθεισαν δε νυν δια τησ επιφανειασ του σωτηροσ ημων ιησου χριστου καταργησαντοσ μεν τον θανατον φωτισαντοσ δε ζωην και αφθαρσιαν δια του ευαγγελιου
11 Ine ndinasankhidwa kukhala wamthenga, ndi mtumwi ndi mphunzitsi wa Uthenga Wabwinowu.
εισ ο ετεθην εγω κηρυξ και αποστολοσ και διδασκαλοσ εθνων
12 Nʼchifukwa chake ndikuvutika monga ndililimu. Komabe zimenezi sizikundichititsa manyazi, popeza ndikumudziwa amene ndamukhulupirira ndipo ndikutsimikiza mtima kuti akhoza kusamalira chimene ndinamusungitsa mpaka tsiku lijalo.
δι ην αιτιαν και ταυτα πασχω αλλ ουκ επαισχυνομαι οιδα γαρ ω πεπιστευκα και πεπεισμαι οτι δυνατοσ εστιν την παραθηκην μου φυλαξαι εισ εκεινην την ημεραν
13 Zimene unamva kwa ine, uzisunge kuti zikhale chitsanzo cha chiphunzitso choona, mwa chikhulupiriro ndi chikondi mwa Khristu Yesu.
υποτυπωσιν εχε υγιαινοντων λογων ων παρ εμου ηκουσασ εν πιστει και αγαπη τη εν χριστω ιησου
14 Samalira bwino zokoma zimene anakusungitsa. Uzisamalire mothandizidwa ndi Mzimu Woyera amene amakhala mwa ife.
την καλην παραθηκην φυλαξον δια πνευματοσ αγιου του ενοικουντοσ εν ημιν
15 Iwe udziwa kuti onse a mʼchigawo cha Asiya anandithawa, kuphatikizapo Fugelo ndi Herimogene omwe.
οιδασ τουτο οτι απεστραφησαν με παντεσ οι εν τη ασια ων εστιν φυγελοσ και ερμογενησ
16 Mulungu achitire chifundo banja lonse la Onesiforo chifukwa ankandisangalatsa kawirikawiri ndipo sankachita nane manyazi ngakhale ndinali womangidwa ndi maunyolo.
δωη ελεοσ ο κυριοσ τω ονησιφορου οικω οτι πολλακισ με ανεψυξεν και την αλυσιν μου ουκ επαισχυνθη
17 Mʼmalo mwake, atangofika ku Roma, anandifunafuna ndipo anandipeza.
αλλα γενομενοσ εν ρωμη σπουδαιοτερον εζητησεν με και ευρεν
18 Ambuye amulole kuti adzalandire chifundo kwa Ambuye pa tsiku lijalo! Ukudziwa bwino momwe iye anandithandizira mʼnjira zosiyanasiyana ku Efeso.
δωη αυτω ο κυριοσ ευρειν ελεοσ παρα κυριου εν εκεινη τη ημερα και οσα εν εφεσω διηκονησεν βελτιον συ γινωσκεισ